Marko 1 – CCL & PCB

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Marko 1:1-45

Yohane Mʼbatizi Akonza Njira

1Chiyambi cha Uthenga Wabwino wa Yesu Khristu, Mwana wa Mulungu, 2monga zalembedwera mʼbuku la mneneri Yesaya:

“Ine ndidzatuma mthenga wanga patsogolo panu,

amene adzakonza njira yanu,”

3“Mawu a wofuwula mʼchipululu,

‘Konzani njira ya Ambuye,

wongolani njira zake.’ ”

4Ndipo Yohane anabwera mʼmadera a mʼchipululu nabatiza, ndi kulalikira za ubatizo wa kutembenuka mtima ndi wa chikhululukiro cha machimo. 5Madera onse a ku Yudeya ndi anthu onse a ku Yerusalemu anatuluka napita kwa iye. Akavomereza machimo awo, amawabatiza mu mtsinje wa Yorodani. 6Yohane amavala zovala zopangidwa ndi ubweya wangamira, ndi lamba wachikopa mʼchiwuno mwake, ndipo amadya dzombe ndi uchi wamthengo. 7Ndipo uthenga wake unali uwu: “Pambuyo panga pakubwera wina wondiposa ine mphamvu. Ine si woyenera kuwerama ndi kumasula zingwe za nsapato zake. 8Ine ndikubatizani ndi madzi, koma Iye adzakubatizani ndi Mzimu Woyera.”

Kubatizidwa ndi Kuyesedwa kwa Yesu

9Pa nthawi imeneyo Yesu anabwera kuchokera ku Nazareti wa ku Galileya ndipo anabatizidwa ndi Yohane mu mtsinje wa Yorodani. 10Pamene Yesu ankatuluka mʼmadzi, anaona kumwamba kukutsekuka ndipo Mzimu Woyera akutsikira pa Iye ngati nkhunda. 11Ndipo Mawu anamveka kuchokera kumwamba: “Iwe ndiwe Mwana wanga wokondedwa; ndipo ndikondwera nawe.”

12Nthawi yomweyo Mzimu Woyera anamutumiza Iye ku chipululu, 13ndipo anali mʼchipululumo masiku makumi anayi, akuyesedwa ndi Satana. Anali pakati pa nyama zakuthengo; ndipo angelo anamutumikira.

Yesu Alengeza za Uthenga Wabwino

14Yohane atamutsekera mʼndende, Yesu anapita ku Galileya nalalikira Uthenga Wabwino wa Mulungu nati, 15“Nthawi yafika, ufumu wa Mulungu wayandikira. Tembenukani mtima ndi kukhulupirira Uthenga Wabwino!”

Yesu Ayitana Ophunzira ake Oyamba

16Pamene Yesu ankayenda mʼmbali mwa nyanja ya Galileya, anaona Simoni ndi mʼbale wake Andreya akuponya khoka mʼnyanja, popeza anali asodzi. 17Yesu anati, “Bwerani, tsateni Ine, ndipo ndidzakusandutsani asodzi a anthu.” 18Nthawi yomweyo anasiya makoka awo namutsata Iye.

19Atapita patsogolo pangʼono, anaona Yakobo ndi mʼbale wake Yohane ana a Zebedayo, ali mʼbwato akukonza makoka awo. 20Mosataya nthawi anawayitana, ndipo anasiya abambo awo Zebedayo ndi anyamata aganyu ali mʼbwatomo, namutsata Iye.

Yesu Atulutsa Mzimu Woyipa

21Iwo anapita ku Kaperenawo, ndipo tsiku la Sabata litafika, Yesu analowa mʼsunagoge nayamba kuphunzitsa. 22Anthu anadabwa ndi chiphunzitso chake, chifukwa anawaphunzitsa ngati munthu amene anali ndi ulamuliro, osati ngati aphunzitsi amalamulo. 23Pomwepo munthu wina mʼsunagogemo amene anali wogwidwa ndi mzimu woyipa anafuwula kuti, 24“Mukufuna chiyani kwa ife, Yesu wa ku Nazareti? Kodi mwabwera kudzatiwononga? Ndikudziwa kuti ndinu ndani, ndinu Woyerayo wa Mulungu!”

25Yesu anadzudzula chiwandacho mwamphamvu nati, “Khala chete! Tuluka mwa iye!” 26Mzimu woyipawo unamugwedeza mwamphamvu ndipo unatuluka mwa iye ukufuwula.

27Anthu anadabwa kwambiri kotero kuti anafunsana wina ndi mnzake kuti, “Ichi nʼchiyani? Chiphunzitso chatsopano ndi ulamuliro! Iye akulamula, ngakhale mizimu yoyipa ikumumvera.” 28Mbiri yake inafalikira kudera lonse la Galileya mofulumira.

Yesu Achiritsa Anthu Ambiri

29Atangochoka mu sunagoge, Yesu pamodzi ndi Yakobo ndi Yohane anakalowa mʼnyumba ya Simoni ndi Andreya. 30Mpongozi wa Simoni anali chigonere akudwala malungo, ndipo anamuwuza Yesu za iye. 31Ndipo Yesu anapita kwa iye, namugwira dzanja namuthandiza kudzuka. Malungo anachoka ndipo anayamba kuwatumikira.

32Madzulo omwewo dzuwa litalowa anthu anabweretsa kwa Yesu anthu onse odwala ndi ogwidwa ndi ziwanda. 33Anthu onse a mʼmudzimo anasonkhana pa khomo, 34Yesu anachiritsa ambiri amene anali ndi matenda osiyanasiyana, komanso anatulutsa ziwanda zambiri, ndipo sanalole kuti ziwandazo ziyankhule chifukwa zinkamudziwa Iye.

Yesu Apemphera Kumalo a Yekha

35Mmamawa, kukanali kamdima, Yesu anadzuka, nachoka pa nyumbapo kupita kumalo kwa yekha, kumene anakapemphera. 36Simoni ndi anzake anapita kokamufunafuna Iye, 37ndipo atamupeza, anamuwuza kuti, “Aliyense akukufunani!”

38Yesu anayakha kuti, “Tiyeni tipite kwina ku midzi ya pafupi kuti ndikalalikirenso kumeneko. Ichi ndi chifukwa chimene ndinabwerera.” 39Potero anayendayenda mu Galileya, kulalikira mʼmasunagoge awo ndi kutulutsa ziwanda.

Yesu Achiritsa Wakhate

40Munthu wakhate anabwera kwa Iye, nagwada, namupempha kuti, “Ngati mukufuna, mukhoza kundiyeretsa.”

41Yesu pomva naye chifundo, anatambasula dzanja lake namukhudza munthuyo nati, “Ndikufuna, yeretsedwa!” 42Nthawi yomweyo khate linachoka ndipo anachiritsidwa.

43Nthawi yomweyo Yesu anamuwuza kuti apite koma anamuchenjeza kuti, 44“Wonetsetsa kuti usawuze aliyense za zimenezi. Koma pita, kadzionetse wekha kwa wansembe ndi kukapereka nsembe zimene Mose analamulira zotsimikizira kuyeretsedwa kwanu, ngati umboni kwa iwo.” 45Mʼmalo mwake anapita nayamba kuyankhula momasuka, nafalitsa mbiriyo. Zotsatira zake, Yesu sanathe kulowa mʼmudzi moonekera, koma anakhala kunja kumalo kopanda anthu. Komabe anthu amabwera kwa Iye kuchokera kulikonse.

Persian Contemporary Bible

مَرقُس 1:1-45

ظهور نجات دهنده

1اِنجيل عيسی مسيح، فرزند خدا، اينچنين آغاز می‌شود:

2خدا به زبان اشعيای نبی خبر داده بود كه مسيح را به اين جهان خواهد فرستاد، و شخصی را نيز پيش از او گسيل خواهد داشت تا مردم جهان را برای آمدن او آماده سازد. 3اشعيا نوشت كه اين پيشرو مسيح، در بيابان خشک و سوزان زندگی خواهد كرد و مردم را به سوی زندگی خداپسندانه هدايت خواهد نمود، تا برای آمدن مسيح خداوند آماده باشند.

4اين شخص همان يحيای پيامبر بود كه در بيابان زندگی می‌كرد و به مردم می‌گفت: «توبه كنيد و غسل تعميد بگيريد تا به همه نشان دهيد كه از گناهانتان دست كشيده‌ايد. آنگاه خدا از سر تقصيراتتان خواهد گذشت و شما را خواهد بخشيد.» 5مردم از شهر اورشليم و از تمام سرزمين يهوديه به آن بيابان می‌شتافتند تا سخنان او را بشنوند. آنان به اعمال و رفتار بد خود اعتراف می‌كردند و از يحيی در رود اردن غسل تعميد می‌گرفتند. 6لباس يحيی از پشم شتر و كمربند او از چرم و خوراكش نيز ملخ و عسل صحرايی بود. 7او به مردم چنين می‌گفت: «بزودی شخصی خواهد آمد كه از من خيلی بزرگتر است، به طوری كه من حتی لياقت خدمتگزاری او را ندارم. 8من شما را با آب تعميد می‌دهم، ولی او شما را به روح‌القدس تعميد خواهد داد.»

تعميد عيسی

9يكی از همان روزها، عيسی از شهر ناصره، واقع در ايالت جليل، نزد يحيی رفت و از او در رود اردن تعميد گرفت. 10هنگامی كه عيسی از آب بيرون می‌آمد، ديد كه آسمان باز شد و روح‌القدس به شكل كبوتری فرود آمد و بر او قرار گرفت، 11و ندايی از آسمان در رسيد و گفت: «تو فرزند عزيز من هستی كه از تو بسيار خشنودم.»

آزمايش عيسی

12‏-13بلافاصله پس از اين رويداد، روح خدا، عيسی را به بيابان برد. در آنجا چهل روز تنها ماند. فقط حيوانات وحشی با او بودند. در اين مدت شيطان او را وسوسه می‌كرد، اما فرشتگان از او مراقبت می‌نمودند.

آغاز خدمت عيسی

14مدتی بعد، پس از آنكه يحيی به دستور هيروديس پادشاه، زندانی شد، عيسی به ايالت جليل آمد تا پيام خدا را به مردم برساند. 15او فرمود: «زمان موعود فرا رسيده است. بزودی خداوندْ ملكوت خود را برقرار خواهد ساخت. پس، از گناهان خود دست بكشيد و به اين خبر خوش ايمان بياوريد.»

16روزی عيسی در كنارهٔ درياچهٔ جليل قدم می‌زد كه چشمش به شمعون و برادرش اندرياس افتاد. ايشان تور به دريا انداخته، مشغول صيد ماهی بودند، چون كارشان ماهيگيری بود. 17عيسی ايشان را صدا زد و فرمود: «از من پيروی كنيد تا شما را صياد مردم سازم.» 18ايشان نيز بی‌درنگ تورهای خود را بر زمين گذاشتند و به دنبال او به راه افتادند. 19كمی جلوتر، يعقوب و يوحنا، پسران زبدی را ديد كه در قايق، تورهای ماهيگيری خود را تعمير می‌كردند. 20ايشان را نيز دعوت كرد تا پيروی‌اش كنند، كه بلافاصله پدر خود زبدی را با كارگران گذاشتند و به دنبال او رفتند.

عيسی روح پليد را اخراج می‌کند

21سپس همگی وارد شهر كفرناحوم شدند، و صبح روز شنبه به عبادتگاه يهود كه آن را كنيسه می‌ناميدند، رفتند. در آنجا عيسی پيغام خدا را برای مردم بيان فرمود. 22مردم از موعظهٔ او تعجب كردند چون هرگز نشنيده بودند كه كسی با چنين قدرت و اقتداری سخن گويد و برای اثبات گفته‌های خود، نيازی نداشته باشد كه گفتار بزرگان را شاهد بياورد.

23در آن عبادتگاه، ديوانه‌ای حضور داشت كه با ديدن عيسی فرياد زد: 24«ای عيسای ناصری، چرا ما را آسوده نمی‌گذاری؟ آيا آمده‌ای ما را هلاک سازی؟ تو را می‌شناسم؛ تو فرستادهٔ مقدس خدا هستی.»

25عيسی حرف روح پليد را قطع كرد و دستور داد تا از او بيرون بيايد. 26همان دم، روح پليد او را به زمين زد، نعره‌ای برآورد و از او خارج شد. 27حيرت همهٔ حاضرين را فرو گرفت؛ ايشان با هيجان به يكديگر می‌گفتند: «اين ديگر چه نوع مكتب جديدی است؟ كلام او به قدری قدرت دارد كه حتی ارواح پليد نيز از او فرمان می‌برند!» 28طولی نكشيد كه در تمام ايالت جليل خبر معجزهٔ عيسی پيچيد.

عيسی بيماران بسياری را شفا می‌بخشد

29عيسی از كنيسه خارج شد، و به اتفاق يعقوب و يوحنا به خانهٔ شمعون و اندرياس رفت. 30وقتی به خانه رسيدند، ديدند كه مادر زن شمعون تب كرده و خوابيده است؛ فوری به عيسی خبر دادند. 31عيسی نزد او رفت، دستش را گرفت و او را برخيزاند. همان لحظه تبش قطع شد و برخاست و مشغول پذيرايی گرديد.

32هنگام غروب، مردم بيماران و ديوانگان را نزد عيسی آوردند تا شفايشان دهد. 33تمام اهالی شهر نيز برای تماشا جلو در خانه گرد آمده بودند. 34پس عيسی بيماران زيادی را شفا بخشيد و روحهای ناپاک بسياری را از ديوانه‌ها بيرون كرد، اما اجازه نداد ارواح ناپاک چيزی بگويند زيرا او را می‌شناختند.

عيسی در جليل موعظه می‌کند

35صبح روز بعد، وقتی هنوز هوا تاريک بود، عيسی برخاست و تنها به صحرا رفت تا در آنجا دعا كند. 36كمی بعد شمعون با سايرين به جستجوی او رفتند. 37وقتی او را يافتند، گفتند: «همه به دنبال شما می‌گردند.» 38ولی عيسی در جواب ايشان فرمود: «بايد به شهرهای ديگر هم بروم، تا به اهالی آنجا نيز پيغامم را برسانم، چون به خاطر همين به اينجا آمده‌ام.» 39پس در تمام ايالت جليل سفر كرد و در كنيسه‌ها به تعليم و راهنمايی مردم پرداخت و ارواح پليد را از ديوانه‌ها بيرون كرد.

عيسی جذامی را شفا می‌بخشد

40روزی يک جذامی آمده، نزد عيسی زانو زد و التماس‌كنان گفت: «اگر بخواهيد می‌توانيد مرا شفا دهيد.» 41عيسی دلش بر او سوخت، دست خود را بر او گذاشت و فرمود: «البته كه می‌خواهم! شفا بياب.» 42بلافاصله جذام او برطرف شد و شفا يافت. 43هنگامی كه عيسی او را مرخص می‌نمود، با تأكيد زياد به او فرمود: 44«بی‌درنگ نزد كاهن برو تا تو را معاينه كند. بين راه نيز با كسی صحبت نكن. آن هديه را هم كه موسی برای جذامی‌های شفا يافته تعيين كرده، با خودت ببر تا به همه ثابت شود كه شفا يافته‌ای.» 45اما او همانطور كه می‌رفت، فرياد می‌زد كه شفا يافته است. در نتيجه، مردم دور عيسی جمع شدند، به طوری كه از آن به بعد ديگر نتوانست آزادانه وارد شهری شود. او مجبور بود پس از آن در بيابانها بماند، ولی مردم از همه جا نزد او می‌شتافتند.