Luka 13 – CCL & PCB

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Luka 13:1-35

Za Kutembenuka Mtima

1Nthawi yomweyo panali ena amene analipo omwe amamuwuza Yesu za Agalileya amene magazi awo Pilato anawasakaniza ndi nsembe zawo. 2Yesu anayankha kuti, “Kodi mukuganiza kuti Agalileya amenewa anali ochimwa kwambiri kuposa Agalileya ena onse chifukwa anavutika mʼnjira iyi? 3Ine ndikuti, ayi! Koma ngati inu simutembenuka mtima, inunso mudzawonongeka nonse. 4Kapena anthu 18 aja amene anafa nsanja ya Siloamu itawagwera, kodi mukuganiza kuti iwo aja anali ochimwa kwambiri kuposa onse amene amakhala mu Yerusalemu? 5Ine ndikuti, ayi! Koma ngati inu simutembenuka mtima, inunso mudzawonongeka nonse.”

6Kenaka Iye anawawuza fanizo kuti, “Munthu wina anali ndi mtengo wamkuyu, umene anadzala mʼmunda wamphesa, ndipo Iye anapita kukayangʼana zipatso, koma sanazipeze. 7Tsono kwa munthu amene amasamalira munda wamphesawo anati, ‘Kwa zaka zitatu tsopano ndakhala ndikubwera kudzafuna chipatso pa mtengo uwu ndipo sindinachipeze. Udule! Nʼchifukwa chiyani ukuwononga nthaka?’

8“Munthuyo anayankha kuti, ‘Bwana, tawusiyani kwa chaka chimodzi chokha ndipo ine ndikumba ngalande mozungulira ndi kuthira manyowa. 9Ngati udzabale zipatso chaka chamawa, zili bwino! Koma ngati sudzabala, pamenepo mudzawudule.’ ”

Mayi Wokhota Msana Achiritsidwa pa Sabata

10Pa Sabata Yesu ankaphunzitsa mʼsunagoge ina, 11ndipo momwemo munali mayi amene anali ndi mzimu woyipa umene unamudwalitsa zaka 18. Iye anali wokhota msana ndipo samatha kuweramuka ndi pangʼono pomwe. 12Yesu atamuona anamuyitana kutsogolo ndipo anati kwa iye, “Amayi, mwamasulidwa ku mavuto.” 13Kenaka anasanjika manja ake pa iye, ndipo nthawi yomweyo anawongoka nayamika Mulungu.

14Chifukwa cha kuyipidwa kuti Yesu anachiritsa pa Sabata, wolamulira sunagoge anati kwa anthu, “Pali masiku asanu ndi limodzi ogwira ntchito. Choncho bwerani kuti mudzachiritsidwe masiku amenewo osati pa Sabata.”

15Ambuye anamuyankha kuti, “Iwe wachiphamaso! Kodi nonsenu simumasula pa Sabata ngʼombe zanu kapena bulu kumuchotsa mʼkhola ndi kupita naye kukamupatsa madzi? 16Nanga mayiyu, amene ndi mwana wa Abrahamu, ndipo anamangidwa ndi Satana zaka 18, kodi siwoyenera kuti amasulidwe msinga imeneyi pa tsiku la Sabata?”

17Atanena izi, onse omutsutsa anachititsidwa manyazi, koma anthu anakondwera ndi zodabwitsa zonse zimene Iye anazichita.

Fanizo la Mbewu ya Mpiru ndi la Yisiti

18Kenaka Yesu anafunsa kuti, “Kodi ufumu wa Mulungu uli ngati chiyani? Kodi Ine ndingawufanizire ndi chiyani? 19Uli ngati mbewu ya mpiru, imene munthu anatenga ndi kudzala mʼmunda mwake. Inakula, nʼkukhala mtengo, ndipo mbalame zamlengalenga zinakhala mʼnthambi zake.”

20Iye anafunsanso kuti, “Kodi ufumu wa Mulungu ndingawufanizire ndi chiyani? 21Uli ngati yisiti amene mayi anatenga ndi kusakaniza ndi ufa wambiri mpaka anafufumitsa ufawo.”

Khomo Lopapatiza

22Ndipo Yesu anayendayenda mʼmizinda ndi mʼmidzi, kumaphunzitsa pamene Iye ankapita ku Yerusalemu. 23Wina anamufunsa Iye kuti, “Ambuye, kodi ndi anthu ochepa okha amene adzapulumutsidwe?”

Iye anawawuza kuti, 24“Yesetsani kulowa pa khomo lopapatiza, chifukwa ndikukuwuzani kuti ambiri adzafuna kulowa koma sadzatha kutero. 25Nthawi yomwe mwini nyumba adzayimirira ndi kutseka chitseko, inu mudzayima kunja kugogoda ndi kudandaula kuti, ‘Bwana, tatitsekulirani khomo.’

“Koma Iye adzayankha kuti, ‘Ine sindikukudziwani ndipo sindikudziwanso kumene mwachokera.’

26“Ndipo inu mudzati, tinkadya ndi kumwa ndi inu ndipo munkaphunzitsa mʼmisewu yathu.

27“Koma Iye adzayankha kuti, ‘Ine sindikukudziwani ndipo sindikudziwanso kumene mwachokera. Chokereni inu nonse ochita zoyipa!’

28“Mudzalira ndi kukuta mano mukadzaona Abrahamu, Isake ndi Yakobo ndi aneneri onse ali mu ufumu wa Mulungu koma inuyo mutaponyedwa kunja. 29Anthu adzachokera kummawa ndi kumadzulo, kumpoto ndi kummwera, kudzakhala pa phwando mu ufumu wa Mulungu. 30Ndithudi otsirizira ndiye adzakhale oyambirira, ndipo oyambirira ndiye adzakhale otsirizira.”

Yesu Amvera Chisoni Yerusalemu

31Pa nthawi imeneyo Afarisi anabwera kwa Yesu ndipo anati kwa Iye, “Chokani malo ano ndipo pitani kumalo ena aliwonse. Herode akufuna kukuphani.”

32Iye anayankha kuti, “Pitani kawuzeni nkhandweyo, Ine ndikutulutsa ziwanda ndi kuchiritsa anthu lero ndi mawa ndipo tsiku lachitatu ndidzakwaniritsa cholinga changa.” 33Mʼnjira ina iliyonse, Ine ndiyenera kupitirira ulendo wanga lero, mawa ndi mkuja. Zoona nʼzakuti mneneri sangafere kunja kwa Yerusalemu.

34Iwe Yerusalemu, Yerusalemu! Umapha aneneri ndi kuwagenda miyala anthu amene atumizidwa kwa iwe. Nthawi zambiri ndakhala ndikufuna kusonkhanitsa ana ako pamodzi, monga nkhuku imasonkhanitsira anapiye pansi pa mapiko ake, koma iwe sunafune! 35Taona, nyumba yako yasanduka bwinja. Ine ndikukuwuza kuti, sudzandionanso mpaka pamene udzati, “Wodala amene akubwera mʼdzina la Ambuye!”

Persian Contemporary Bible

لوقا 13:1-35

توبه يا هلاكت

1در همين وقت به عيسی اطلاع دادند كه پيلاطوس، عده‌ای از زائران جليلی را در اورشليم به هنگام تقديم قربانی در خانهٔ خدا، قتل عام كرده است.

2عيسی با شنيدن اين خبر فرمود: «آيا تصور می‌كنيد اين عده، از ساير مردم جليل گناهكارتر بودند، كه اين گونه رنج ديدند و كشته شدند؟ 3به هيچ وجه! شما نيز اگر از راههای بد خويش باز نگرديد و به سوی خدا بازگشت ننماييد، مانند ايشان هلاک خواهيد شد! 4يا آن هجده نفری كه برج ”سلوام“ بر روی ايشان فرو ريخت و كشته شدند، آيا از همه ساكنان اورشليم، گناهكارتر بودند؟ 5هرگز! شما نيز اگر توبه نكنيد، همگی هلاک خواهيد شد!»

عبرت از درخت انجير

6سپس اين داستان را بيان فرمود: «شخصی در باغ خود، درخت انجيری كاشته بود. اما هر بار كه به آن سر می‌زد، می‌ديد كه ميوه‌ای نياورده است. 7سرانجام صبرش به پايان رسيد و به باغبان خود گفت: اين درخت را ببر، چون سه سال تمام انتظار كشيده‌ام و هنوز يک دانه انجير هم نداده است! نگه داشتنش چه فايده‌ای دارد؟ زمين را نيز بيهوده اشغال كرده است!

8«باغبان جواب داد: باز هم به آن فرصت بدهيد! بگذاريد يک سال ديگر هم بماند تا از آن به خوبی مواظبت كنم و كود زياد به آن بدهم. 9اگر سال آينده ميوه داد كه چه بهتر؛ اما اگر نداد، آنگاه آن را خواهم بريد.»

شفای بيمار در روز شنبه

10يک روز شنبه، عيسی در عبادتگاه كلام خدا را تعليم می‌داد. 11در آنجا زنی حضور داشت كه مدت هجده سال، روحی پليد او را عليل ساخته بود به طوری که پشتش خميده شده، به هيچ وجه نمی‌توانست راست بايستد.

12وقتی عيسی او را ديد، به او فرمود: «ای زن، تو از اين مرض شفا يافته‌ای!» 13در همان حال كه اين را می‌گفت، دستهای خود را بر او گذاشت. بلافاصله آن زن شفا يافت و راست ايستاد و شروع به ستايش خداوند نمود!

14اما سرپرست عبادتگاه غضبناک شد، چون عيسی آن زن را روز شنبه شفا داده بود. پس با خشم به حضار گفت: «در هفته شش روز بايد كار كرد. در اين شش روز بياييد و شفا بگيريد، اما نه در روز شنبه.»

15اما عيسای خداوند در جواب او فرمود: «ای رياكار! مگر تو خود روز شنبه كار نمی‌كنی؟ مگر روز شنبه، گاو يا الاغت را از آخور باز نمی‌كنی تا برای آب دادن بيرون ببری؟ 16پس حال چرا از من ايراد می‌گيری كه در روز شنبه، اين زن را رهايی دادم، زنی كه همچون ما از نسل ابراهيم است، و هجده سال در چنگ شيطان اسير بود؟»

17با شنيدن اين سخن، دشمنان او همه شرمگين شدند، اما مردم از معجزات او غرق شادی گشتند.

مثال درباره ملكوت خدا

18آنگاه عيسی درباره ملكوت خدا مثالی آورد و فرمود: «ملكوت خدا به چه می‌ماند؟ آن را به چه تشبيه كنم؟ 19مانند دانهٔ كوچک خردل است كه در باغی كاشته می‌شود و پس از مدتی تبديل به چنان بوته بزرگی می‌شود كه پرندگان در ميان شاخه‌هايش آشيانه می‌كنند.»

مثال خميرمايه

20باز گفت: «ملکوت خدا را به چه تشبیه کنم؟ 21مانند خمير مايه‌ای است كه هنگام تهيه خمير با آرد مخلوط می‌شود و كم‌كم اثر آن نمايان می‌گردد.»

تا فرصت باقی است بايد به سوی خدا بازگشت نمود

22عيسی بر سر راه خود به اورشليم، به شهرها و دهات مختلف می‌رفت و كلام خدا را به مردم تعليم می‌داد.

23روزی، شخصی از او پرسيد: «خداوندا، آيا تعداد نجات يافتگان كم خواهد بود؟»

عيسی فرمود: 24«درِ آسمان تنگ است. پس بكوشيد تا داخل شويد، زيرا يقين بدانيد كه بسياری تلاش خواهند كرد كه داخل گردند، اما نخواهند توانست. 25زمانی خواهد رسيد كه صاحب خانه در را خواهد بست. آنگاه شما بيرون ايستاده، در خواهيد زد و التماس خواهيد كرد كه: خداوندا، خداوندا، در را به روی ما باز كن! اما او جواب خواهد داد كه: من شما را نمی‌شناسم!

26«شما خواهيد گفت: ما با تو غذا خورديم! تو در كوچه‌های شهر ما تعليم دادی! چگونه ما را نمی‌شناسی؟

27«اما او باز خواهد گفت: من به هيچ وجه شما را نمی‌شناسم! ای بدكاران از اينجا دور شويد!

28«آنگاه وقتی ببينيد كه ابراهيم و اسحاق و يعقوب و همه انبیا در ملكوت خدا هستند و خودتان بيرون مانده‌ايد، از شدت ناراحتی خواهيد گريست و لبهايتان را خواهيد گزيد. 29مردم از تمام نقاط جهان آمده، در ضيافت ملكوت خدا شركت خواهند كرد، اما شما محروم خواهيد ماند. 30بلی، يقين بدانيد آنانی كه اكنون خوار و حقير شمرده می‌شوند، در آن زمان بسيار سرافراز خواهند گرديد و آنانی كه حالا مورد احترام و تمجيد هستند، در آن زمان، حقير و ناچيز به حساب خواهند آمد.»

سوگواری برای اورشليم

31همان موقع چند نفر از فريسی‌ها آمدند و به او گفتند: «اگر می‌خواهی زنده بمانی، هر چه زودتر از جليل برو، چون هيروديس پادشاه قصد دارد تو را بكشد!»

32عيسی جواب داد: «برويد و به آن روباه بگوييد كه من امروز و فردا، ارواح پليد را بيرون می‌كنم و بيماران را شفا می‌بخشم و روز سوم، خدمتم را به پايان خواهم رساند. 33بلی، امروز و فردا و پس فردا، بايد به راه خود ادامه دهم، چون محال است كه نبی خدا در جای ديگری به غیر از اورشليم كشته شود!

34«ای اورشليم، ای اورشليم، ای شهری كه كشتارگاه انبیا می‌باشی! ای شهری كه انبيايی را كه خدا به سويت فرستاد، سنگسار كردی! چند بار خواستم فرزندانت را دور هم جمع كنم، همانطور كه مرغ جوجه‌هايش را زير پروبالش می‌گيرد، اما نخواستی. 35پس اكنون خانه‌ات ويران خواهد ماند و ديگر هرگز مرا نخواهی ديد تا زمانی كه بگويی: مبارک باد قدم كسی كه به نام خداوند می‌آيد.»