Luka 12 – CCL & PCB

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Luka 12:1-59

Chenjezo ndi Chilimbikitso

1Nthawi yomweyo, anthu miyandamiyanda atasonkhana, ndi kumapondanapondana, Yesu anayamba kuyankhula poyamba kwa ophunzira ake, nati, “Chenjereni ndi yisiti wa Afarisi, amene ndi chinyengo. 2Palibe chinthu chophimbika chimene sichidzawululika, kapena chobisika chimene sichidzadziwika. 3Chimene mwanena mu mdima chidzamveka dzuwa likuwala, ndipo zimene mwanongʼona mʼkhutu mʼchipinda chamʼkati, zidzayankhulidwa pa denga la nyumba.

4“Ine ndikuwuzani, abwenzi anga, musachite mantha ndi amene amapha thupi chifukwa akatero sangachitenso kanthu. 5Koma Ine ndidzakuonetsani amene muyenera kumuopa: Wopani Iye, amene pambuyo pakupha thupi, ali ndi mphamvu yakukuponyani ku gehena. Inde, Ine ndikuwuzani, muopeni Iye. 6Kodi atimba asanu samagulidwa ndi ndalama ziwiri? Ngakhale zili chomwecho palibe imodzi ya izo imene imayiwalika ndi Mulungu. 7Ndithudi, tsitsi lonse la mʼmutu mwanu ndi lowerengedwa. Musachite mantha; inu ndi oposa kwambiri mpheta zambiri.

8“Ine ndikukuwuza kuti, aliyense amene avomereza Ine pamaso pa anthu, Mwana wa Munthu adzamuvomerezanso pamaso pa angelo a Mulungu. 9Koma iye amene andikana Ine pamaso pa anthu adzakanidwanso pamaso pa angelo a Mulungu. 10Ndipo aliyense amene ayankhulira Mwana wa Munthu mawu oyipa adzakhululukidwa, koma iye wochitira mwano Mzimu Woyera sadzakhululukidwa.

11“Akadzakutengerani ku masunagoge pamaso pa oweruza ndi a maulamuliro, musadere nkhawa mmene mudzadzitchinjirizire nokha kapena chimene mudzayankhule, 12pakuti Mzimu Woyera nthawi imeneyo adzakuphunzitsani zoyenera kunena.”

Fanizo la Munthu Wachuma Wopusa

13Munthu wina mʼgulu la anthu anati kwa Iye, “Aphunzitsi, muwuzeni mʼbale wanga andigawireko chuma chamasiye.”

14Yesu anayankha kuti, “Munthu iwe, ndani anandiyika Ine kukhala woweruza kapena wogawa chuma pakati panu?” 15Kenaka Iye anawawuza kuti, “Chenjerani! Khalani tcheru ndi makhalidwe onse adyera; moyo wa munthu sukhala chifukwa cha kuchuluka kwa zimene ali nazo.”

16Ndipo Iye anawawuza fanizo ili, “Munda wa munthu wina wachuma unabereka kwambiri. 17Iye anaganiza kuti, ‘Ndichite chiyani? Ndilibe malo osungiramo mbewu zanga.’

18“Ndipo Iye anati, ichi ndi chimene ndidzachite: Ndidzaphwasula nkhokwe zanga zonse ndi kumanga zokulirapo, ndipo ndidzasungira mʼmenemo mbewu ndi katundu. 19Ndipo ndidzawuza moyo wanga kuti, ‘Uli nazo zinthu zabwino zambiri zimene zikhalepo zaka zambiri, usapupulume; idya, imwa ndi kukondwera.’ ”

20“Koma Mulungu anati kwa iye, ‘Iwe wopusa! Usiku womwe uno moyo wako udzachotsedwa kwa iwe, ndipo ndi ndani amene adzatenge zimene iwe wadzikonzera?’

21“Umu ndi mmene zidzakhalire ndi aliyense amene amadziwunjikira chuma, koma si wachuma pamaso pa Mulungu.”

Musadere Nkhawa

22Kenaka Yesu anati kwa ophunzira ake, “Choncho Ine ndikuwuzani kuti musadere nkhawa za moyo wanu, zimene mudzadya; kapena za thupi lanu, zimene mudzavala. 23Moyo uposa chakudya, ndi thupi liposa chovala. 24Taonani makwangwala: iwo safesa kapena kukolola, alibe nyumba zosungamo zinthu kapena nkhokwe; komabe, Mulungu amawadyetsa. Koposa kotani inu amene ndi ofunikira kuposa mbalame. 25Ndi ndani wa inu akhoza kuwonjeza ora pa moyo wake chifukwa cha kudandaula? 26Popeza simungathe kuchita kanthu kakangʼono aka, nʼchifukwa chiyani mumadandaula ndi zinazi?

27“Taonani mmene maluwa amakulira. Iwo sagwira ntchito kapena kusoka zovala. Koma Ine ndikuwuzani kuti, ngakhale Solomoni muulemelero wake wonse sanavalepo ngati limodzi la awa. 28Ngati umu ndi mmene Mulungu amavekera udzu wakuthengo, umene lero ulipo ndipo mawa uponyedwa pa moto, nanga Iye adzakuvekani inu motani. Haa! Inu achikhulupiriro chochepa! 29Ndipo musayike mtima wanu pa zimene mudzadye kapena kumwa; musade nazo nkhawa. 30Pakuti anthu akunja amathamanga kufunafuna zinthu zotere, ndipo Atate amadziwa kuti mumazifuna zimenezi. 31Koma funafunani ufumu wake, ndipo mudzapatsidwa zonsezi.

Chuma cha Kumwamba

32“Musachite mantha, inu kagulu kankhosa, pakuti zinakondweretsa Atate anu kuti akupatseni ufumu. 33Gulitsani zonse zimene muli nazo, ndipo ndalama zake mupereke kwa osauka. Dzipezereni zikwama zandalama zimene sizidzatha, ndi kudzikundikira chuma chomwe sichidzatha kumwamba, kumene mbala sizingafikeko, ndipo dzimbiri silingawononge. 34Popeza kumene kuli chuma chanu, mtima wanunso udzakhala komweko.”

Kukhala a Atcheru

35“Khalani okonzekeratu ndipo nyale zanu ziziyaka, 36ngati anthu oyembekezera kubwera kwa mbuye wawo kuchokera kuphwando la ukwati, kuti pamene afika ndi kugogoda akhoza nthawi yomweyo kumutsekulira chitseko. 37Zidzakhala bwino kwa antchitowo amene mbuye wawo pobwera adzawapeze akudikira. Zoonadi, Ine ndikuwuzani kuti adzakonzekera kuwatumikira, adzakhala nawo pa tebulo ndipo adzabwera ndi kuwatumikira. 38Zidzakhala bwino kwa antchitowo amene mbuye wawo adzawapeze ali okonzeka, ngakhale iye atabwera pa ora lachiwiri kapena lachitatu usiku. 39Koma zindikirani izi: Ngati mwini nyumba akanadziwa ora limene mbala ibwera, sakanalola kuti nyumba yake ithyoledwe. 40Inunso muyenera kukhala okonzeka, chifukwa Mwana wa Munthu adzabwera pa ora limene simukumuyembekezera Iye.”

Wantchito Wokhulupirika ndi Wosakhulupirika

41Petro anafunsa kuti, “Kodi mukunena fanizoli kwa ife, kapena kwa aliyense?”

42Ambuye anayankha kuti, “Kodi tsono woyangʼanira wokhulupirika ndi wanzeru ndani? Kodi ndi amene mbuye wake wamuyika kukhala oyangʼanira antchito ake kuti aziwapatsa ndalama yachakudya pa nthawi yake yoyenera? 43Zidzamukhalira bwino wantchito amene mbuye wake adzamupeza akuchita zimene pamene iye abwera. 44Zoonadi, Ine ndikukuwuzani kuti adzamuyika kukhala woyangʼanira katundu wake yense. 45Koma tiyerekeze kuti wantchitoyo aziganiza mu mtima mwake kuti, ‘Bwana wanga akuchedwa kwambiri kubwera,’ ndipo kenaka ndi kuyamba kumenya antchito aamuna ndi aakazi ndi kudya, kumwa ndi kuledzera. 46Mbuye wake adzabwera tsiku limene iye sakumuyembekezera ndi ora limene iye sakudziwa. Iye adzamulanga ndi kumusiya kumalo kumene kuli osakhulupirira.

47“Wantchito amene amadziwa chifuniro cha mbuye wake koma wosakonzeka kapena wosachita chimene mbuye wake akufuna adzakwapulidwa zikwapu zambiri. 48Koma wantchito amene sadziwa koma nʼkuchita zinthu zoyenera chilango, adzakwapulidwa zikwapu zochepa. Aliyense amene anapatsidwa zambiri, adzayenera kubwezanso zambiri; ndipo amene anamusungitsa zambiri, adzamulamula kuti abweze zambirinso.”

Za Kugawikana

49“Ine ndabwera kudzayatsa moto pa dziko lapansi, ndipo ndikanakonda ukanayaka kale. 50Koma Ine ndiyenera kubatizidwa, ndipo ndikusautsika mu mtima mpaka utachitika! 51Kodi mukuganiza kuti Ine ndinabwera kudzabweretsa mtendere pa dziko lapansi? Ayi, Ine ndikukuwuzani kuti, ndinabweretsa kugawikana. 52Kuyambira tsopano mpaka mʼtsogolo mʼbanja limodzi mudzakhala anthu asanu ndipo adzawukirana wina ndi mnzake, atatu kuwukira awiri, ndipo awiri kuwukira atatu. 53Anthu adzawukirana. Abambo kudzawukira mwana wawo wamwamuna, mwana wawoyo adzawukira abambo ake. Amayi adzawukira mwana wawo wamkazi, mwana wawoyo adzawukira amayi ake. Amayi adzawukira mpongozi wawo wamkazi, mpongoziyo adzawukira amayiwo.”

Kumasulira Nthawi

54Iye anati kwa gulu la anthu, “Pamene mukuona mtambo ukukwera kummawa, nthawi yomweyo inu mumati, ‘kugwa mvula,’ ndipo imagwadi. 55Ndipo pamene mphepo yakummwera ikuwomba, inu mumati ‘kutentha’ ndipo kumaterodi. 56Achiphamaso inu! Inu mumadziwa kutanthauzira maonekedwe a dziko lapansi ndi thambo. Zikutheka bwanji kuti simukudziwa kumasulira kwa nthawi ino?

57“Bwanji simukuzindikira nokha zoyenera kuchita? 58Pamene mukupita kwa woweruza ndi amene munalakwirana naye, yesetsani kwambiri kuti muyanjane naye mʼnjiramo, chifukwa mukapanda kutero akhoza kukutengerani ku bwalo la milandu ndipo woweruzayo adzakuperekani kwa woyangʼanira ndende, ndipo woyangʼanira ndendeyo adzakuponyani mʼndende. 59Ine ndikuwuzani kuti, simudzatulukamo mpaka mutalipira ndalama zonse.”

Persian Contemporary Bible

لوقا 12:1-59

هشدار عليه رياکاری

1هنگامی كه هزاران نفر ازدحام نموده بودند، به طوری كه يكديگر را پايمال می‌كردند، عيسی نخست رو به شاگردان كرد و به ايشان فرمود: «از فريسی‌های خوش‌ظاهر و بدباطن برحذر باشيد! زيرا همانگونه كه خميرمايه در تمام خمير اثر می‌كند، همانطور رياكاری فريسيان نيز انسان را آلوده می‌سازد. 2بدانيد كه چيزی پنهان نيست كه روزی آشكار و عيان نگردد. 3بنابراين، آنچه ايشان در تاريكی گفته‌اند، در روشنايی شنيده خواهد شد، و آنچه در اتاقهای در بسته در گوش گفته‌اند، بر بامها اعلام خواهد شد تا همه بشنوند!

توكل و اعتماد به خدا

4«ای دوستان من، از آنانی نترسيد كه قادرند فقط جسمتان را بكشُند، چون نمی‌توانند به روحتان آسيبی برسانند! 5اما به شما خواهم گفت از كه بترسيد: از خدايی بترسيد كه هم قدرت دارد بكشد و هم به جهنم بيندازد. بلی، از او بايد ترسيد.

6«مگر پنج گنجشک به قيمتی ارزان خريد و فروش نمی‌شوند؟ با وجود اين، خدا حتی يكی از آنها را فراموش نمی‌كند! 7او حتی حساب موهای سر شما را نيز دارد! پس هرگز نترسيد! چون در نظر خدا، شما بسيار عزيزتر از گنجشكان هستيد.

8«يقين بدانيد كه اگر نزد مردم اعلام نماييد كه پيرو من می‌باشيد، من نيز در حضور فرشتگان خدا، شما را دوست خود اعلام خواهم نمود. 9اما كسانی كه پيش مردم مرا انكار كنند، من نيز ايشان را در حضور فرشتگان خدا انكار خواهم نمود. 10با اين حال، آنانی كه بر ضد من چيزی بگويند، در صورت توبه بخشيده خواهند شد، اما آنانی كه بر ضد روح‌القدس سخنی گويند، هرگز بخشيده نخواهند شد.

11«هنگامی كه شما را برای محاكمه، به عبادتگاه‌های يهود و نزد بزرگان و حاكمان می‌برند، نگران نباشيد كه برای دفاع از خود، چه بگوييد، 12چون روح‌القدس همان لحظه به شما خواهد آموخت كه چه بگوييد.»

وارستگی از طمع و ماديات

13در اين هنگام، شخصی از ميان جمعيت گفت: «استاد، به برادرم بفرما كه ارث پدرم را با من تقسيم كند!»

14عيسی جواب داد: «ای مرد، چه كسی تعيين كرده كه من قاضی شما باشم تا دربارهٔ اين موضوع حكم كنم؟ 15اما اگر از من می‌شنويد، از طمع فرار كنيد، چون زندگی حقيقی به ثروت بستگی ندارد.»

16سپس اين داستان را برای ايشان بيان كرد: «شخصی ثروتمند از مزرعه خود محصول فراوانی به دست آورد، 17‏-18به طوری كه تمام انبارهايش پر شد، اما هنوز مقدار زيادی غَلّه باقی مانده بود. پس از تفكر بسيار، بالاخره با خود گفت: ”انبارهايم را خراب می‌كنم و انبارهای بزرگتری می‌سازم تا جای كافی برای محصول خود داشته باشم. 19آنگاه به خود خواهم گفت: ای مرد خوشبخت، تو برای چندين سال، محصول فراوان ذخيره كرده‌ای! حالا ديگر راحت باش و به عيش و نوش بپرداز و خوش بگذران!“

20«اما خدا به او فرمود: ”ای نادان! همين امشب جانت را خواهم گرفت. آنگاه اموالی كه اندوخته‌ای، به چه كسی خواهد رسيد؟“

21«بلی، نادان است هر كه در اين دنيا مال و ثروت جمع كند، اما توشه‌ای برای آخرت نيندوزد!»

تعليم درباره مال و ثروت

22آنگاه به شاگردان خود فرمود: «هرگز برای خوراک و پوشاک غصه نخوريد، 23زيرا زندگی بسيار با ارزشتر از خوراک و پوشاک است! 24كلاغها را ملاحظه كنيد! نه می‌كارند، نه درو می‌كنند و نه انبار دارند تا خوراک را ذخيره كنند، زيرا روزی آنها را خدا می‌رساند. اما شما در نظر خدا بسيار عزيزتر از پرندگان هستيد! 25به علاوه، با نگرانی و غصه خوردن چه كاری از پيش می‌بريد؟ آيا می‌توانيد حتی يک لحظه به عمر خود بيفزاييد؟ هرگز! 26پس اگر با غصه خوردن، حتی قادر به انجام كوچكترين كار هم نيستيد، پس چرا برای امور بزرگتر نگران و مضطرب می‌شويد؟

27«گلهای وحشی را بنگريد كه چگونه رشد و نمو می‌كنند! نه نخ می‌ريسند و نه می‌بافند. با وجود اين، حتی سليمان پادشاه نيز با آن همه شكوه و جلال، همچون يكی از اين گلها آراسته نبود! 28پس اگر خدا به فكر پوشاک گلهاست، گلهايی كه امروز سبز و خرّمند و فردا پژمرده می‌شوند، آيا به فكر پوشاک شما نخواهد بود، ای سست ايمانان؟! 29برای خوراک نيز نگران نباشيد كه چه بخوريد و چه بنوشيد! غصه نخوريد، چون خدا روزی شما را می‌رساند. 30مردم بی‌ايمان تمام زندگی خود را صرف به دست آوردن اين چيزها می‌كنند، اما پدر آسمانی شما به خوبی می‌داند كه شما به همه اينها نياز داريد. 31بنابراين، ملكوت خدا را هدف زندگی خود قرار دهيد، و خدا خودش همه نيازهای شما را برآورده خواهد ساخت.

32«پس ای گله كوچک من، نترسيد! چون رضای خاطر پدر شما در اينست كه ملكوت را به شما عطا فرمايد. 33بنابراين، هر چه داريد بفروشيد و به فقرا بدهيد تا برای آخرت خود، گنج و ثروتی اندوخته باشيد، ثروتی كه هرگز تلف نمی‌شود و دزدها به آن دستبرد نمی‌زنند و بيد، آن را تباه نمی‌سازد. 34زيرا گنجتان هر كجا باشد، فكر و دلتان نيز همانجا خواهد بود.

آماده باشيد

35«همواره لباس بر تن، برای خدمت آماده باشيد! 36مانند خدمتكارانی كه منتظرند اربابشان از جشن عروسی بازگردد، و حاضرند هر وقت كه برسد و در بزند، در را به رويش باز كنند. 37خوشا به حال آن خدمتكارانی كه وقتی اربابشان می‌آيد، بيدار باشند. يقين بدانيد كه او خود لباس كار بر تن كرده، آنان را بر سر سفره خواهد نشاند و به پذيرايی از ايشان خواهد پرداخت. 38بلی، خوشا به حال آن غلامانی كه وقتی اربابشان می‌آيد، بيدار باشند، خواه نيمه شب باشد، خواه سپيده دم! 39اگر صاحب خانه می‌دانست كه دزد چه وقت می‌آيد، بيدار می‌ماند و نمی‌گذاشت وارد خانه‌اش شود. همانگونه نيز زمان دقيق بازگشت ارباب معلوم نيست. 40بنابراين، شما نيز آماده باشيد، زيرا من، مسيح موعود، هنگامی باز خواهم گشت كه كمتر انتظارش را داريد.»

41پطرس از عيسی پرسيد: «خداوندا، آيا اين را فقط برای ما می‌گويی يا برای همه؟»

42عيسای خداوند در جواب فرمود: «اين را به هر خدمتكار امين و آگاهی می‌گويم كه اربابش او را بر ساير خدمتكاران می‌گمارد تا در غياب خود، خوراک و آذوقه را به موقع به ايشان بدهد. 43خوشا به حال چنين خدمتكاری كه وقتی اربابش باز می‌گردد، او را در حال انجام وظيفه ببيند. 44يقين بدانيد كه او را ناظر تمام دارايی خود خواهد ساخت.

45«ولی ممكن است آن شخص با اين تصور كه اربابش به اين زودی باز نخواهد گشت، به اذيت و آزار افراد زير دست خود بپردازد و وقت خود را به عيش و نوش بگذراند. 46آنگاه در روزی كه انتظارش را ندارد، اربابش باز خواهد گشت و او را از مقامش بركنار كرده، به جايی خواهد فرستاد كه افراد نادرست و خائن فرستاده می‌شوند.

47«آن خدمتكاری كه وظيفه خود را بداند و به آن عمل نكند، به سختی مجازات خواهد شد. 48اما اگر كسی ندانسته عمل خلافی انجام دهد، كمتر مجازات خواهد شد. به هر كه مسئوليت بزرگتری سپرده شود، بازخواست بيشتری نيز از او به عمل خواهد آمد، و نزد هر كه امانت بيشتری گذاشته شود، مطالبه بيشتری نيز خواهد شد.

اختلاف به خاطر عيسی

49«من آمده‌ام تا بر روی زمين آتش داوری بيفروزم، و كاش هر چه زودتر اين كار انجام شود! 50اما پيش از آن، بايد از تجربياتی سخت بگذرم، و چقدر در اندوه هستم، تا آنها به پايان برسند!

51«آيا تصور می‌كنيد كه آمدن من باعث صلح و آشتی مردم با يكديگر می‌شود؟ نه! بلكه به خاطر من، مردم با يكديگر اختلاف پيدا خواهند كرد، 52و خانواده‌ها از هم پاشيده خواهند شد! دو نفر به جانب من خواهند بود و سه نفر بر ضد من. 53نظر پدر خانواده درباره من، با نظر پسرش متفاوت خواهد بود. همچنين مادر با دختر، و عروس با مادر شوهر اختلاف نظر پيدا خواهند كرد.»

54سپس رو به جماعت كرد و فرمود: «وقتی می‌بينيد ابرها از سوی مغرب می‌آيند، می‌گوييد كه باران خواهد آمد و همانطور نيز می‌شود. 55و هنگامی كه باد جنوبی می‌وزد، می‌گوييد كه امروز هوا گرم خواهد شد، و همانگونه نيز می‌شود. 56ای رياكاران، شما قادريد وضع آب و هوا را پيش‌بينی كنيد، اما نمی‌خواهيد تشخيص دهيد كه در چه زمانی زندگی می‌كنيد، و نمی‌خواهيد درک كنيد كه رويدادهای حاضر چه بلايايی را هشدار می‌دهند! 57چرا نمی‌خواهيد حقيقت را بپذيريد؟

58«وقتی كسی از تو شاكی است و تو را به دادگاه می‌برد، سعی كن پيش از رسيدن به نزد قاضی، با او صلح كنی، مبادا تو را به زندان بيفكند. 59چون اگر به زندان بيفتی، از آنجا بيرون نخواهی آمد، مگر آنكه تا دينار آخر را بپردازی!»