Ezekieli 32 – CCL & BPH

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Ezekieli 32:1-32

Nyimbo ya Maliro a Farao

1Pa tsiku loyamba la mwezi wa khumi ndi chiwiri, chaka chakhumi ndi chiwiri, Yehova anandiyankhula kuti: 2“Iwe mwana wa munthu imba nyimbo ya maliro a Farao mfumu ya Igupto ndipo uyiwuze kuti,

“Iwe umadziyesa ngati mkango pakati pa mitundu ya anthu.

Koma iwe uli ngati ngʼona mʼnyanja.

Umakhuvula mʼmitsinje yako,

kuvundula madzi ndi mapazi ako

ndi kudetsa madzi mʼmitsinje.

3“Tsono Ine Ambuye Yehova ndikuti,

“ ‘Pogwiritsa ntchito gulu la anthu a mitundu yambiri,

ndidzakuponyera khoka langa

ndi kukugwira mu ukonde wanga.

4Ndidzakuponya ku mtunda

ndi kukutayira pansi.

Ndidzabweretsa mbalame zamumlengalenga kuti zidzatere pa iwe,

ndipo zirombo zonse za dziko lapansi zidzakudya.

5Ndidzayanika mnofu wako pa mapiri

ndipo zigwa zidzadzaza ndi zotsalira zako.

6Ndidzanyowetsa dziko ndi magazi ako,

mpaka kumapiri komwe,

ndipo mitsinje idzadzaza ndi mnofu wako.

7Ndikadzakuwononga, ndidzaphimba miyamba

ndikudetsa nyenyezi zake.

Ndidzaphimba dzuwa ndi mtambo,

ndipo mwezi sudzawala.

8Zowala zonse zamumlengalenga

ndidzazizimitsa;

ndidzachititsa mdima pa dziko lako,

akutero Ambuye Yehova.

9Ndidzasautsa mitima ya anthu a mitundu yambiri

pamene ndidzakupititsa ku ukapolo pakati pa mitundu ya anthu,

ku mayiko amene iwe sunawadziwe.

10Ine ndidzachititsa kuti anthu a mitundu yambiri adabwe nawe,

ndipo mafumu awo adzanjenjemera ndi mantha aakulu chifukwa cha iwe

pamene ndidzaonetsa lupanga langa pamaso pawo.

Pa nthawi ya kugwa kwako,

aliyense wa iwo adzanjenjemera

moyo wake wonse.

11“ ‘Pakuti ndikunena Ine Ambuye Yehova kuti,

“ ‘Lupanga la mfumu ya ku Babuloni

lidzabwera kudzalimbana nawe.

12Ndidzachititsa gulu lako lankhondo kuti ligwe

ndi lupanga la anthu amphamvu,

anthu ankhanza kwambiri pakati pa mitundu yonse ya anthu.

Adzathetsa kunyada kwa Igupto,

ndipo gulu lake lonse la nkhondo lidzagonjetsedwa.

13Ndidzawononga ziweto zake zonse

zokhala mʼmbali mwa madzi ambiri.

Ku madziko sikudzaonekanso phazi la munthu

kapena kudetsedwa ndi phazi la ziweto.

14Pambuyo pake ndidzayeretsa madzi ake

ndipo mitsinje yake idzayenda mokometsera ngati mafuta,

akutero Ambuye Yehova.

15Ndikadzasandutsa dziko la Igupto kukhala bwinja;

ndikadzawononga dziko lonse

ndi kukantha onse okhala kumeneko,

adzadziwa kuti ndine Yehova.’

16“Mawu angawa adzakhala nyimbo ya maliro. Ana a akazi amitundu ya anthu adzayimba, kuyimbira Igupto ndi gulu lake lonse la nkhondo, akutero Ambuye Yehova.”

17Pa tsiku la 15 la mwezi woyamba, chaka cha khumi ndi chiwiri, Yehova anayankhula kuti: 18“Iwe mwana wa munthu, lirira gulu lankhondo la Igupto ndipo uwalowetse pamodzi ndi anthu ena amphamvu a mayiko ena ku dziko la anthu akufa. 19Ufunse kuti, ‘Ndani amene akukuposa kukongola? Tsikirani ku manda ndi kukhala pamodzi ndi anthu osachita mdulidwe.’ 20Aigupto adzagwa pakati pa amene akuphedwa ndi lupanga. Lupanga ndi losololedwa kale. Iye adzaphedwa pamodzi ndi gulu lake lankhondo. 21Mʼkati mwa manda atsogoleri amphamvu pamodzi ndi ogwirizana nawo azidzakambirana za Igupto nʼkumati, ‘Afika kuno anthu osachita mdulidwe aja! Ndi awa agona apawa, ophedwa pa nkhondo.’

22“Asiriya ali komweko ndipo ankhondo ake onse ali mʼmanda omuzungulira. Onsewo anaphedwa pa nkhondo. 23Manda awo ali kumalo ozama a dzenje, ndipo ankhondo ake azungulira manda ake. Onse amene anaopseza dziko la anthu amoyo aphedwa, agwa ndi lupanga.

24“Elamu ali komweko ndipo ankhondo ake ali mʼmanda omuzungulira. Onsewa anaphedwa pa nkhondo, natsikira ku manda ali osachita mdulidwe. Iwowa kale ankaopseza anthu pa dziko lapansi. Tsopano akuchita manyazi pamodzi ndi amene ali mʼmanda. 25Amukonzera pogona pakati pa anthu ophedwa, pamodzi ndi gulu lake lonse la nkhondo litazungulira manda ake. Onsewo ndi anthu osachita mdulidwe ophedwa ndi lupanga. Paja anthuwa ankaopsa mʼdziko la anthu a moyo. Koma tsopano akuchita manyazi pamodzi ndi amene ali mʼmanda. Iwo ayikidwa pakati pa anthu ophedwa.

26“Mesaki ndi Tubala ali komweko, pamodzi ndi gulu lonse la nkhondo litazungulira manda awo. Onsewo ndi anthu osachita mdulidwe, ophedwa ndi lupanga. Paja ankaopsa mʼdziko la anthu amoyo. 27Iwo sanayikidwe mwaulemu ngati ankhondo amphamvu amakedzana, amene anatsikira ku dziko la anthu akufa ndi zida zawo zomwe za nkhondo. Malupanga awo anawayika ku mitu yawo, ndipo zishango zawo anaphimba mafupa awo. Kale anthu amphamvu amenewa ankaopsa dziko la anthu amoyo.

28“Iwenso Farao, udzaphwanyidwa ndi kuyikidwa pakati pa anthu osachita mdulidwe, amene anaphedwa ndi lupanga.

29“Edomu ali kumeneko pamodzi ndi mafumu ake ndi akalonga ake onse. Ngakhale anali amphamvu, koma anayikidwa. Ayikidwa pamodzi ndi anthu osachita mdulidwe, pamodzi ndi iwo amene akutsikira ku dzenje.

30“Akalonga onse akumpoto pamodzi ndi anthu onse a ku Sidoni ali kumeneko. Anatsikira ku dziko la anthu akufa mwamanyazi ngakhale anali owopsa ndi mphamvu zawo. Iwo akugona osachita mdulidwe pamodzi ndi amene anaphedwa ndi lupanga ndipo akuchita manyazi pamodzi ndi iwo amene anatsikira kale ku manda.

31“Farao ndi gulu lake lankhondo akadzawaona iwowa adzathunza mtima pokumbukira kuchuluka kwa gulu lake lankhondo limene linaphedwa pa nkhondo. Ndikutero Ine Ambuye Yehova. 32Paja ankaopsa mʼdziko la anthu amoyo. Koma Faraoyo pamodzi ndi ankhondo ake onse adzayikidwa pamodzi ndi anthu osachita mdulidwe, pamodzi ndi amene anaphedwa pa nkhondo. Ndikutero Ine Ambuye Yehova.”

Bibelen på hverdagsdansk

Ezekiels Bog 32:1-32

Dommen over Egyptens konge

1På den første dag i den 12. måned i det 12. år af vores eksil sagde Herren til mig: 2„Du menneske, syng en sørgesang for Egyptens konge:

Du var som en løve blandt nationerne,

som et uhyre fra havet fór du frem,

piskede Nilens vande op

og trampede bredderne til mudder.

3Men hør, hvad Herren siger til dig:

Jeg fanger dig i mit fiskenet,

sender min hær og trækker dig op,

4lader dig ligge på bredden og dø,

slænger dig ud i den øde ørken,

så himlens fugle slår ned på dig,

og jordens rovdyr mættes med dit kød.

5Jeg spreder dit kød ud over bjergene,

kaster dine knogler i dalenes kløfter.

6Jeg lader jorden drikke dit blod,

og bjergenes kløfter fyldes deraf.

7Når dommens dag rammer dig,

tildækker jeg himlens stjerner.

Solen bliver gemt bag sorte skyer,

og månens lys forsvinder.

8Jeg slukker alle himlens lys,

så hele dit land opsluges af mørke.

9Rygtet om din skæbne vil nå ud til lande,

som du aldrig har set eller hørt om,

og folkene dér vil fyldes af frygt.

10Mange folkeslag bliver lammet af rædsel,

og deres konger ryster af skræk,

når de ser, hvordan jeg svinger mit sværd

og lader det ramme dig med frygtelig kraft.

11For det er, hvad Gud Herren siger:

Babyloniens konges sværd skal ramme dig.

12Jeg sender verdens vældigste hær imod dig,

den er berømt for sin grusomhed.

Den raserer det, du er allermest stolt af,

og udrydder både folk og husdyr.

13Kvæget, der græsser langs floden, bliver udryddet.

Ingen hove skal længere mudre vandet til,

ingen menneskefødder forstyrre flodens ro.

14Nilens vand bliver klart og gennemsigtigt,

floden skal flyde som olivenolie, siger Herren.

15Når jeg lægger dit land øde

og udrydder din befolkning,

da vil folk indse, at jeg er Herren.

16Da skal denne klagesang synges.

Alle folkeslag skal stemme i

og sørge over Egyptens skæbne, siger Herren.”

17På den 15. dag i samme måned sagde Herren til mig: 18„Du menneske, sørg over Egypten, for jeg styrter landet ned i dødsriget sammen med andre, mægtige nationer.

19Du Egypten, er du mon bedre end de andre?

Kom ned og lig blandt de andre gudløse!

20Egypterne skal dø som alle andre.

Sværdet er draget og vil ramme dem alle.

21Dødsrigets helte tager imod dem med skadefryd,

giver dem plads iblandt alle de faldne.

‚Nu er de gudløse egyptere faldet,’ råber de.

‚Heltene er pludselig blevet så tavse.’

22Der ligger Assyriens mægtige fyrster.

Alle blev dræbt, de faldt for sværdet.

23De ligger i dødsrigets inderste kroge.

Skønt de spredte rædsel på jorden,

endte dog alle som offer for sværdet.

24Elams mægtige konger er der,

omgivet af deres faldne krigere.

Alle blev dræbt, de faldt for sværdet.

I live spredte de rædsel omkring sig.

Nu ligger de mellem de andre gudløse.

Deres skæbne blev som alle andres.

25Blandt dødsrigets dræbte fik de et hvilested,

omgivet af deres faldne krigere.

Alle de gudløse segnede for sværdet,

for de spredte rædsel i de levendes land.

Nu må de bide skammen i sig,

for de faldt selv for sværdet til sidst.

26Der ligger Mesheks og Tubals fyrster,

omgivet af deres faldne krigere.

I live spredte de rædsel omkring sig.

Nu ligger de mellem de andre gudløse.

27De ligger ikke blandt de gamle helte,

som fik en ærefuld begravelse

og fik deres våben med i dødsriget,

sværdet under hovedet og skjoldet over kroppen,

for de spredte rædsel i de levendes land.

28Egypten, dine krigere må ligge mellem de gudløse,

side om side med alle de andre dræbte.

29Der ligger Edoms konger og fyrster,

som fik deres grav blandt de slagne,

blandt de gudløse, der endte i døden.

30Alle nordens fyrster ligger slagne dernede,

side om side med folkene fra Sidon.

Alle de gudløse segnede for sværdet.

De spredte skræk og rædsel omkring sig,

men nu må de bide skammen i sig

sammen med de andre gudløse i graven.

31Når egypterkongen ender på det sted,

kan han se på de andre og trøste sig med,

at han ikke er den eneste, der tabte en krig.

32Egypterkongen og hele hans hær

spredte skræk og rædsel i de levendes land.

Nu ligger han blandt de gudløse og dræbte,

der faldt for sværdet, siger Gud Herren.”