Ezekieli 31 – CCL & BPH

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Ezekieli 31:1-18

Mkungudza mu Lebanoni

1Pa tsiku loyamba la mwezi wachitatu, chaka cha khumi ndi chimodzi, Yehova anandiyankhula kuti: 2“Iwe mwana wa munthu, unene kwa Farao mfumu ya Igupto ndi gulu lake lankhondo. Awawuze kuti,

“ ‘Kodi mu ukulu wanu ndani angafanane ndi inu?

3Taonani, ndidzakufanizirani ndi mtengo wa mkungudza wa ku Lebanoni,

wa nthambi zokongola zochititsa mthunzi mʼnkhalango.

Unali wautali,

msonga zake zooneka pamwamba pa nkhalango.

4Madzi ndiwo ankawukulitsa mkungudzawo,

akasupe ozama ankawutalikitsa.

Mitsinje yake inkayenda

mozungulira malo amene unaliwo

ndipo ngalande zake zinkafika

ku mitengo yonse ya mʼmunda.

5Choncho unatalika kwambiri

kupambana mitengo yonse ya mʼmunda.

Nthambi zake zinachuluka

ndi kutalika kwambiri,

chifukwa inkalandira madzi ambiri.

6Mbalame zonse zamlengalenga

zinkamanga zisa zake mʼnthambi za mtengowo.

Nyama zakuthengo zonse

zinkaswanirana mʼmunsi mwa nthambi zake.

Mitundu yotchuka ya anthu

inkakhala mu mthunzi wake.

7Unali wokongola kwambiri,

wa nthambi zake zotambalala,

chifukwa mizu yake inazama pansi

kumene kunali madzi ochuluka.

8Mʼmunda wa Mulungu munalibe

mkungudza wofanana nawo,

kapena mitengo ya payini

ya nthambi zofanafana ndi nthambi zake.

Munalibenso mtengo wa mkuyu

nthambi zofanafana ndi zake.

Mʼmunda wa Mulungu munalibe mtengo wina uliwonse

wofanana ndi iwo kukongola kwake.

9Ine ndinawupanga wokongola

wa nthambi zochuluka.

Mitengo yonse ya mu Edeni, mʼmunda wa

Mulungu inawuchitira nsanje.

10“ ‘Nʼchifukwa chake Ine Ambuye Yehova ndikuti: Chifukwa kuti mtengowo unatalika kwambiri, unatulutsa songa zake mpaka ku thambo, ndipo unadzikweza chifukwa cha msinkhu wake, 11ndinawupereka mʼdzanja la mfumu ya mitundu ya anthu kuti awulange molingana ndi kuyipa kwake. 12Anthu ankhanza kwambiri amitundu ya anthu achilendo adzawudula ndi kuwusiya. Nthambi zake zidzagwera pa mapiri ndi mu zigwa zonse. Nthambi zake zidzathyokera mʼmitsinje ya mʼdzikomo. Motero mitundu yonse ya anthu a dziko lapansi amene ankasangalala mu mthunzi wake idzawusiya. 13Mbalame zonse zamlengalenga zidzakhala pa mtengo wakugwawo, ndipo nyama zakuthengo zonse zidzakhala pa nthambi zake. 14Zidzakutero kuti pasakhalenso mitengo inanso ya mʼmbali mwa madzi yotalika kwambiri, imene idzatalike kwambiri ndi songa zake kufika mpaka ku mitambo. Komanso kuti pasadzakhalenso mitengo yolandira bwino madzi, imene idzatalika motero. Paja yonseyo kutha kwake ndi kufa, kupita ku dziko lapansi kukhala ndi anthu akufa amene analowa mʼmanda kale.

15“ ‘Ine Ambuye Yehova ndikuti: Pa nthawi imene mkungudzawo unatsikira ku manda, ndinawuza nyanja kuti iwulire maliro pakuwuphimba. Ndinawumitsa mitsinje ndipo madzi ambiri anaphwa. Ndinabweretsa mdima pa Lebanoni chifukwa cha mtengowo ndipo mitengo yonse ya mʼdzikomo inawuma. 16Mitundu ya anthu inagwedezeka pakumva mkokomo wa kugwa kwake, pamene ndinawutsitsira ku manda pamodzi ndi iwo amene anafa. Pamenepo ku dziko la akufa mitengo yonse ya ku Edeni pamodzi ndi ya ku Lebanoni yosankhidwa bwino inasangalatsidwa chifukwa cha zimenezi. 17Amene ankakhala mu mthunzi wake, amene ankayanjana nawo, iwonso anapita nawo pamodzi ku manda, kukakhala pamodzi ndi amene anaphedwa ndi lupanga pakati pa mitundu ya anthu.

18“ ‘Ndi mitengo iti ya mu Edeni imene ingafanane ndi kukongola kwako ndi ulemerero wako? Komabe iwenso, udzatsikira ku dziko la anthu akufa pamodzi ndi mitengo ya mu Edeni. Udzagona pamodzi ndi anthu osachita mdulidwe, anthu amene anaphedwa pa nkhondo.

“ ‘Mtengowo ndi Farao ndi gulu lake lankhondo, akutero Ambuye Yehova.’ ”

Bibelen på hverdagsdansk

Ezekiels Bog 31:1-18

Egyptens stolthed og indbildskhed

1På den første dag i den tredje måned i det 11. år af vores eksil sagde Herren til mig: 2-3„Du menneske, giv egypterkongen og hele hans folk følgende budskab:

Hvem skal jeg sammenligne dig med? Med Assyrien?

Det land var engang som et af Libanons majestætiske cedertræer

med smukke grene og skyggefuld krone.

Det ragede højt op, helt til skyerne.

4Vandet fra jordens dyb gav det vækst,

og små floder strømmede tæt forbi det,

før de fortsatte til skovens andre træer.

5Cedertræet knejsede over alle de andre træer,

og det fik mange og lange grene,

fordi det havde rigeligt med vand.

6Fugle byggede rede i dets grene,

de vilde dyr ynglede i dets skygge.

Alle verdens folkeslag levede i skyggen af dets storhed.

7Det var et stærkt og smukt træ,

hvis rødder nåede ned til grundvandet.

8Ingen andre træer i Edens have kunne måle sig med det,

hverken cedre, fyr eller platantræer.

9Jeg gjorde det cedertræ så smukt,

at alle træer i Guds have misundte det.

10Herren siger om Assyrien: Fordi din stamme blev høj og din krone strakte sig op mellem skyerne, blev du stolt og indbildsk. 11Derfor udleverede jeg dig til en mægtig nation, der kunne straffe dig for din gudløshed og ondskab. Jeg forkastede dig. 12Et grusomt folk fældede dig og lod dig ligge på bjergsiden. Dit løv faldt ned i dalene, og dine grene lå knækkede ved alle landets vandløb. Alle de folkeslag, som havde søgt ly under din skygge, forlod dig. 13Fuglene slog sig ned på din faldne stamme, og de vilde dyr lagde sig oven på dine splintrede grene. 14Ingen træer har lov at få så høje stammer, at de når til skyerne, uanset hvor dybt ned deres rødder når, og hvor meget vand de får. Ingen skal sætte lid til deres egen styrke og storhed. Alle skal forgå og ende i dødsriget. Selv de stærkeste ender i graven.

15Gud Herren siger: Den dag du endte i dødsriget, holdt jeg vandstrømmene tilbage. Jeg klædte Libanon i sørgedragt, og alle landets træer hang med bladene. 16Ved braget fra dit fald skælvede folkeslagene af skræk, for jeg styrtede dig i graven til dem, der gik forud for dig. Dernede fandt de andre stolte træer fra Guds have trøst, for du delte skæbne med dem, alle disse engang så ranke cedre, hvis rødder nåede ned til grundvandet. 17Dine forbundsfæller, som sad i din skygge, endte samme sted, for de blev hugget ned af fjendens sværd og fulgte dig i dødsriget. De sluttede sig til dem, der tidligere var blevet fældet.

18Egypten, du er større og prægtigere end alle andre træer i Guds have, men du skal alligevel ende i graven som Assyrien og de andre. Du kommer til at ligge side om side med de folkeslag, du foragtede og besejrede i krig. Det er egypterkongens og hans folks skæbne, siger Gud Herren.”