Ezekieli 33 – CCL & BPH

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Ezekieli 33:1-33

Ezekieli Akhala Mlonda

1Yehova anandiyankhula nati: 2“Iwe mwana wa munthu awuze anthu a mtundu wako kuti, ‘Paja zimati ndikatumiza nkhondo mʼdziko anthu a mʼdzikomo amasankha munthu mmodzi pakati pawo kuti akhale mlonda. 3Tsono iyeyo amati akaona nkhondo ikubwera amaliza lipenga kuti achenjeze anthuwo. 4Wina aliyense akamva lipenga koma osasamala, mdani uja akabwera nʼkumupha, ndiye kuti wadziphetsa yekha. 5Iye anamva kulira kwa lipenga koma sanalabadire. Ndiye kuti wadziphetsa yekha. Akanasamala kuchenjeza kwa mlonda akanapulumuka. 6Koma ngati mlondayo aona lupanga likubwera ndipo osawomba lipengalo kuchenjeza anthu, ndipo lupanga libwera ndi kuchotsa moyo wa mmodzi mwa iwo, munthu ameneyo adzafa chifukwa cha tchimo lake, koma ndidzamuyimba mlandu mlondayo chifukwa cha imfa ya mnzakeyo.’

7“Tsono iwe mwana wa munthu, ndakuyika kuti ukhale mlonda wa Aisraeli. Choncho imva mawu amene ndikuyankhula ndipo uwachenjeze. 8Ndikawuza munthu woyipa kuti, ‘Iwe munthu woyipa, udzafa ndithu,’ ndipo iwe osayankhula kumuchenjeza kuti aleke njira zake, munthu wochimwayo adzafa chifukwa cha tchimo lake, koma Ine ndidzakuyimba mlandu chifukwa cha imfa yake. 9Koma ngati uchenjeza munthu woyipa kuti aleke njira zake, ndipo iye osatero, adzafa chifukwa cha tchimo lake, koma iwe udzapulumutsa moyo wako.

10“Iwe mwana wa munthu, akumbutse Aisraeli mawu awo akuti, ‘Ife talemedwa ndi zolakwa zathu ndi machimo athu, ndipo tikuwonda chifukwa cha zimene tachita. Kodi tingakhale ndi moyo bwanji?’ ” 11Uwawuze kuti, Ine Ambuye Yehova ndikuti: “Pali Ine wamoyo, sindikondwera ndi imfa ya munthu woyipa. Ndimakondwera ndikamaona munthu woyipa akuleka zoyipa zake kuti akhale ndi moyo. Tembenukani! Tembenukani, siyani makhalidwe anu oyipa! Muferanji, Inu Aisraeli?

12“Tsono iwe mwana wa munthu, awuze anthu a mtundu wako kuti, ‘Ngati munthu wolungama achimwa, ndiye kuti ntchito zake zabwino zija sizidzamupulutsa. Koma wochimwa akaleka ntchito zake zoyipazo, sadzalangidwa konse. Ndithu ngati munthu wolungama ayamba kuchimwa sadzatha kukhala ndi moyo chifukwa cha ntchito zake zabwino zija.’ 13Ngati ndiwuza munthu wolungama kuti adzafa ndithu, koma iyeyo nʼkumadalira ntchito zake zabwino zimene anachita kale ndi kuyamba kuchimwa, ndiye kuti ntchito zake zabwinozo zidzayiwalika. Iye adzafa chifukwa cha machimo ake. 14Ndipo ngati ndiwuza munthu woyipa kuti, ‘Udzafa ndithu,’ tsono iye nʼkutembenuka kuleka machimo ake ndi kuyamba kuchita zimene Yehova afuna, 15monga kubweza chimene anatenga ngati chikole cha ngongole, kubweza chimene anaba, kutsatira malamulo omwe amapereka moyo ndi kuleka kuchita zoyipa, iye adzakhala ndithu ndi moyo; sadzafa. 16Ndidzakhululuka machimo ake onse anachita. Iye wachita zimene ndi zolungama ndi zoyenera ndipo iye adzakhala ndi moyo ndithu.

17“Komabe anthu a mtundu wako akunena kuti, ‘Zimene Ambuye amachita ndi zopanda chilungamo.’ Ayi, koma makhalidwe awo ndiwo ali osalungama. 18Ngati munthu wolungama atembenuka ndi kuleka ntchito zake zolungama ndi kuyamba kuchita zoyipa, adzafa nazo. 19Ndipo ngati munthu woyipa atembenuka ndi kuleka ntchito zake zoyipa ndi kuyamba kuchita zolungama ndi zoyenera, iye adzakhala ndi moyo pochita zimenezo. 20Koma Inu Aisraeli, mukunena kuti, ‘Zimene Ambuye amachita ndi zopanda chilungamo.’ Ayi, inu Aisraeli, Ine ndidzaweruza aliyense wa inu potsata ntchito zake.”

Mbiri ya Kuwonongeka kwa Yerusalemu

21Pa tsiku lachisanu la mwezi wakhumi, chaka chakhumi ndi chiwiri cha ukapolo wathu, munthu wina amene anapulumuka ku Yerusalemu anabwera kudzandiwuza kuti, “Mzinda wagwa!” 22Tsono madzulo ake munthuyo asanafike, dzanja la Yehova linali pa ine. Koma mmawa mwake munthuyo atabwera Yehova anatsekula pakamwa panga, motero kuti sindinakhalenso wosayankhula.

23Ndipo Yehova anandiyankhula kuti: 24“Iwe mwana wa munthu, anthu amene akukhala mʼmizinda ya mabwinja ya dziko la Israeli akunena kuti, ‘Abrahamu anali munthu mmodzi yekha, ndipo anamupatsa dziko lonse. Koma ife tilipo ambiri, motero tsono dzikolo ndi lathu.’ 25Choncho iwe uwawuze kuti Ine Ambuye Yehova ndikuti, ‘Inu mumadya nyama ili ndi magazi ake, ndipo mumapembedza mafano ndi kukhetsa magazi, kodi tsono inu nʼkulandira dzikoli? 26Mumadalira lupanga lanu, mumachita zinthu zonyansa, ndipo aliyense wa inu amachita chigololo ndi mkazi wa mnzake. Kodi inu nʼkulandira dzikoli?’

27“Uwawuze kuti Ine Ambuye Yehova ndikuti, ‘Ndithu pali Ine wamoyo, anthu amene anatsala mʼmizinda ya mabwinja adzaphedwa ndi lupanga, amene ali ku midzi ndidzawapereka kuti adzadyedwe ndi zirombo zakuthengo, ndipo amene ali mʼmalinga ndi mʼmapanga adzafa ndi mliri. 28Ndidzalisandutsa chipululu dzikolo, ndipo mphamvu zake zimene amanyadira zidzatheratu, ndipo mapiri a Yerusalemu adzasanduka chipululu, kotero kuti palibe amene adzatha kudutsako. 29Ndikadzasandutsa dzikolo chipululu chifukwa cha zonyansa zimene ankachita, pamenepo ndiye adzadziwa kuti ndine Yehova.’

30“Koma kunena za iwe, mwana wa munthu, anthu a mtundu wako akumayankhula za iwe akakhala pa makoma a mzinda ndi pa makomo a nyumba zawo. Akumawuzana kuti, ‘Tiyeni tikamve uthenga umene wachokera kwa Yehova.’ 31Anthu anga amabwera kwa iwe, monga momwe amachitira nthawi zonse anthu anga, ndipo amakhala pansi pamaso pako kumvetsera mawu ako. Koma zimene akumvazo sazichita. Zokamba zawo zimaonetsa chikondi, koma mitima yawo imakhala pa phindu lawo. 32Kunena zoona, kwa iwowo sindiwe kanthu konse, ndiwe munthu wamba chabe womangoyimba nyimbo zachikondi ndi liwu lokoma poyimba zeze. Kumva amamva mawu ako koma sawagwiritsa ntchito.

33“Koma zonsezi zikadzachitika, ndipo zidzachitika ndithu, pamenepo adzadziwa kuti mneneri anali pakati pawo.”

Bibelen på hverdagsdansk

Ezekiels Bog 33:1-33

Ezekiel som Guds vagtpost i Israel

1Herren sagde til mig: 2„Du menneske, tal til dit folk og giv dem følgende budskab: Når jeg sender en fjendtlig hær imod et land, udpeger landets befolkning en vagtpost. 3Og når vagtposten får øje på den fremstormende hær, blæser han straks alarm, så folket er advaret. 4Hvis der nu er nogle, der ikke tager advarslen alvorligt, og derfor senere bliver dræbt, så er det deres egen skyld. 5For de hørte jo alarmen, men rettede sig ikke efter den. De er selv skyld i deres død, for hvis de havde lyttet til advarslen, kunne de have reddet livet. 6Men hvis nu vagtposten ser den fremstormende hær og ikke blæser alarm for at advare folket, så er det vagtposten, der er skyld i, at de omkommer. Folket dør godt nok på grund af deres egne synder, men jeg vil kræve vagtposten til regnskab for deres død.

7Du menneske, jeg har udvalgt dig til vagtpost for Israels folk. Derfor skal du høre godt efter, hvad jeg siger, og så advare folket. 8Hvis jeg siger, at nogle onde mennesker skal dø for deres ondskabs skyld, og hvis du ikke advarer dem, så de får mulighed for at omvende sig, da skal de onde mennesker godt nok dø på grund af deres egne synder, men jeg vil kræve dig til regnskab for deres død. 9Advarer du dem derimod, og de nægter at omvende sig, skal de dø på grund af deres synder, men du er uden skyld i deres død.

10Du menneske, du skal sige til Israels folk: I er klar over, at I lider på grund af jeres synder og overtrædelser, og at det snart er ude med jer. I spørger, om I ikke kan gøre noget for at overleve. 11Sig til dem: Så sandt jeg lever, siger Herren, jeg har ingen glæde af, at de onde skal dø. Jeg vil meget hellere se dem omvende sig fra deres ondskab, så de kan redde livet. Åh Israel, omvend jer dog fra jeres synder! Hvorfor ønsker I at dø?

12Du menneske, sig til mit folk: Hvis retskafne mennesker vender sig bort fra mig og gør oprør, kan alle deres tidligere gode gerninger ikke redde dem fra straffen. Og hvis syndige mennesker omvender sig, skal de ikke dø på grund af deres tidligere synder.

13Godt nok har jeg sagt, at retskafne mennesker får et godt liv. Men hvis de bliver for selvsikre og begynder at synde, kan alle deres tidligere gode gerninger ikke redde dem. De skal dø, fordi de har gjort oprør og syndet imod mig. 14Men hvis onde mennesker lytter til min advarsel, omvender sig fra deres synd og begynder at handle retfærdigt, bliver de ikke straffet med døden. 15Hvis de betaler det tilbage, de har stjålet, hvis de udleverer et pant, de har taget i sikkerhed, og hvis de begynder at følge mine love, som sigter på et godt liv, og holder sig fra uretfærdighed, så skal de leve og ikke dø. 16De vil ikke blive dømt på grund af deres tidligere synder, for de har besluttet at gøre det rigtige, og derfor har de ret til at leve.

17‚Det er ikke fair!’ siger I. Hør lige her, Israels folk: Er det mig, der ikke er fair? Er det ikke snarere jer? 18Når retskafne mennesker holder op med at handle ret og i stedet vælger at synde, er det så ikke fair, at de må bære straffen for deres synd og dø? 19Og når onde mennesker tager afstand fra deres tidligere synder og i stedet vælger at adlyde min lov, er det så ikke fair, at de redder livet? 20Hvordan kan I påstå, at det ikke er fair? Bør jeg ikke dømme jer efter jeres handlinger?”

21På den femte dag i den tiende måned i det 12. år af vores eksil ankom en flygtning fra Jerusalem og meddelte, at byen var faldet. 22Aftenen før havde jeg oplevet Herrens kraft over mig, så da manden fra Jerusalem ankom, kunne jeg igen tale.33,22 Jf. 3,26 og 24,25-27. 23Herren sagde da til mig:

24„Du menneske, de overlevende fra Judas folk, som bor spredt mellem ruinerne i Israels land, siger: ‚Abraham var kun én person, men han fik lovning på at få hele det hellige land i eje. Vi er alle sammen hans efterkommere, så det løfte må også gælde os.’ 25Men jeg, Herren, siger: I spiser kød med blod i, dyrker jeres afskyelige afguder og begår mord. Tror I så, at jeg vil give jer landet i eje? 26I stoler på jeres egne våben. I begår de frygteligste synder og er ægteskabsbrydere alle sammen. Og I vil have landet tilbage?

27Sig til dem: Så sandt jeg lever, siger Herren, skal de overlevende blandt Judas ruiner også falde for sværdet! De, som prøver at skjule sig i det fri, skal ædes af de vilde dyr, og de, som gemmer sig i fæstninger og huler, skal dø af sygdom. 28Jeg gør landet til en ødemark og knækker dets stolthed. Jeg gør bjergene så øde, at ingen tør rejse gennem dem. 29Når jeg har lagt hele landet i ruiner som følge af folkets synder, vil de indse, at jeg er Herren.

30Du menneske, dine landsmænd taler om dig, når de mødes ved murene og i døråbningerne. ‚Kom, lad os gå hen og høre, hvilke budskaber Herren har til os,’ siger de. 31Så stimler de sammen hos dig og sætter sig ned for at høre på dig. Men de har ikke tænkt sig at adlyde mine ord, for de taler altid om deres egne ønsker, og de er mest optaget af at søge efter penge og profit. 32For dem er du blot underholdning. Du er som en, der synger kærlighedssange med en smuk stemme og spiller på harpe for dem. De hører ordene, men de vil ikke adlyde. 33Men når profetierne bliver til virkelighed—og vær sikker på, at hvert eneste ord vil gå i opfyldelse—vil de indse, at det var en Herrens profet, der talte til dem.”