Dengu la Zipatso Zakupsa
1Zimene Ambuye Yehova anandionetsa ndi izi: dengu la zipatso zakupsa. 2Iye anandifunsa kuti, “Amosi nʼchiyani ukuona?”
Ine ndinayankha kuti, “Dengu la zipatso zakupsa.”
Ndipo Yehova anati kwa ine, “Nthawi yachimaliziro yawakwanira anthu anga Aisraeli; sindidzawakhululukiranso.
3“Tsiku limenelo,” Ambuye Yehova akulengeza kuti, “Nyimbo za mʼNyumba ya Mulungu zidzasanduka kulira kofuwula. Mitembo ya anthu idzachuluka, ndipo adzayiponya ponseponse! Kudzangoti zii!”
4Imvani izi, inu amene mumapondereza anthu osowa
ndipo simulabadira anthu osauka a mʼdzikomu.
5Mumanena kuti,
“Kodi chikondwerero cha mwezi watsopano chidzatha liti
kuti tigulitse zinthu?
Ndipo tsiku la Sabata litha liti
kuti tigulitse tirigu,
kuti tichepetse miyeso,
kukweza mitengo
kuti tibere anthu ndi miyeso ya chinyengo,
6tigule osauka ndi ndalama zasiliva
ndi osowa powapatsa nsapato,
tigulitse ngakhale mungu wa tirigu?”
7Yehova amene Yakobo amamunyadira, walumbira kuti: Ine sindidzayiwala chilichonse chimene anachita.
8“Kodi dziko silidzagwedezeka chifukwa cha zimenezi,
ndi onse okhala mʼmenemo kulira mwachisoni?
Dziko lonse lidzavunduka ngati mtsinje wa Nailo;
lidzagwedezeka kenaka nʼkukhala bata
ngati mtsinje wa ku Igupto.
9“Tsiku limenelo,” Ambuye Yehova akunena kuti,
“Ndidzadetsa dzuwa masana
ndi kugwetsa mdima pa dziko lapansi dzuwa likuswa mtengo.
10Maphwando anu achipembedzo ndidzawasandutsa kulira kwa chisoni
ndipo kuyimba kwanu konse ndidzakusandutsa maliro.
Ndidzakuvekani chiguduli nonsenu
ndi kumeta mipala mitu yanu.
Nthawi imeneyo idzakhala ngati yolira mwana wamwamuna mmodzi yekhayo,
ndipo tsikulo lidzakhala lowawa mpaka kutha kwake.
11“Nthawi ikubwera,” Ambuye Yehova akunena kuti,
“Ndidzagwetsa njala mʼdziko lonse;
osati njala ya chakudya kapena ludzu la madzi,
koma njala yofuna kumva mawu a Yehova.
12Anthu azidzangoyendayenda kuchoka ku nyanja ina kupita ku nyanja ina.
Azidzangoyendayenda kuchoka kumpoto kupita kummawa,
kufunafuna mawu a Yehova,
koma sadzawapeza.
13“Tsiku limenelo
“anamwali okongola ndi anyamata amphamvu
adzakomoka ndi ludzu.
14Onse amene amalumbira pa tchimo la Samariya,
kapena kumanena kuti, ‘Iwe Dani, pali mulungu wako wamoyo,’
kapena, ‘Pali mulungu wamoyo wa ku Beeriseba.’
Iwowo adzagwa
ndipo sadzadzukanso.”
Корзина со спелыми плодами
1Вот что показал мне Владыка Господь: корзину со спелыми плодами.
2– Что ты видишь, Амос? – спросил Он.
– Корзину со спелыми плодами, – ответил я.
Тогда сказал мне Господь:
– Пришел конец8:2 На языке оригинала наблюдается игра слов: «спелые плоды» (кайиц) и «конец» (кец). Моему народу, Израилю; Я больше не буду их щадить. 3Храмовые песни в тот день станут воплем, – возвещает Владыка Господь. – Повсюду разбросано множество трупов! Молчи!
4Слушайте это, топчущие бедных,
уничтожающие нищих страны,
5говоря: «Когда же пройдет праздник Новолуния8:5 Новолуние – израильтяне, пользовавшиеся лунным календарем, праздновали начало каждого месяца, которое совпадало с новолунием.,
чтобы нам продавать зерно,
и суббота закончится,
чтобы нам торговать пшеницей?» –
урезая меру,
завышая цену
и обманывая неточными весами,
6покупая нищего за серебро
и бедного за пару сандалий,
продавая даже шелуху от зерна.
7Гордостью Иакова поклялся Господь:
– Никогда не забуду ничего из их дел.
8– Разве не содрогнется от этого земля,
и не заплачет всякий живущий на ней?
Вся земля поднимется, как Нил,
будет вздыматься и убывать, как река Египта.
9В тот день, – возвещает Владыка Господь, –
Я сделаю так, что солнце закатится в полдень
и накрою землю мраком средь ясного дня.
10Праздники ваши обращу в скорбь
и все ваши песни – в плач.
Я заставлю всех вас одеться в рубище
и обрить свои головы.
Произведу в то время плач, как о единственном сыне,
и горьким будет день, когда наступит конец.
11Близятся дни, – возвещает Владыка Господь, –
когда Я пошлю на землю голод –
не пищи голод, не жажду воды,
а голод и жажду услышать слова Господа.
12Будут скитаться от моря до моря
и от севера метаться к востоку
в поисках слова Господня,
но не найдут его.
13В тот день
красивые девушки и юноши
ослабеют от жажды.
14Те, кто клянется виной Самарии8:14 Или: «Ашимой, богиней самарийской»; или: «идолом Самарии».,
и говорит: «Верно, как и то, что бог твой жив, о Дан» –
или: «Верно, как и то, что живо паломничество в Вирсавию»8:14 Жив путь в Вирсавию – смысл этого места в еврейском тексте неясен.,
падут и больше не встанут.