Amosi 7 – CCL & NRT

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Amosi 7:1-17

Dzombe, Moto ndi Chingwe Chowongolera Khoma

1Zimene Ambuye Yehova anandionetsa ndi izi: Yehova ankasonkhanitsa gulu la dzombe nthawi imene gawo la zokolola za mfumu linali litakololedwa kale ndipo mbewu zachiwiri zinali zitangoyamba kumera kumene. 2Dzombelo litadya zomera zonse za mʼdzikomo, Ine ndinafuwula kuti, “Ambuye Yehova, khululukani! Kodi Yakobo adzapulumuka bwanji? Iye ndi wofowoka kwambiri!”

3Kotero Yehova anakhululuka.

Yehovayo anati, “Izi sizidzachitika.”

4Zimene Ambuye Yehova anandionetsa ndi izi: Ambuye Yehova ankayitana malawi a moto kuti alange anthu. Motowo unawumitsa nyanja yakuya ndi kupsereza dziko. 5Tsono ine ndinafuwula kuti, “Ambuye Yehova, chonde ndikukupemphani, lekani! Kodi Yakobo adzapulumuka bwanji? Iye ndi wofowoka kwambiri!”

6Kotero Yehova anakhululuka.

Ambuye Yehova anati, “Izinso sizidzachitika.”

7Zimene Iye anandionetsa ndi izi: Ambuye anayima pambali pa khoma lomangamanga, mʼmanja mwake muli chingwe chowongolera khoma. 8Ndipo Ambuye anandifunsa kuti, “Amosi, nʼchiyani ukuonachi?”

Ine ndinayankha kuti, “Chingwe chowongolera khoma.”

Ndipo Yehova anati, “Taona, Ine ndikuyika chingwe chowongolerachi pakati pa anthu anga, Aisraeli; sindidzawalekereranso.

9“Malo achipembedzo a Isake adzawonongedwa

ndipo malo opatulika a Israeli adzasanduka bwinja;

ndidzagwetsa nyumba ya Yeroboamu ndi lupanga langa.”

Amosi ndi Amaziya

10Pamenepo Amaziya wansembe wa ku Beteli anatumiza uthenga kwa Yeroboamu mfumu ya Israeli kuti, “Amosi akukuutsirani chiwembu pakati pa Aisraeli. Dziko silingalekerere zonena zake zonsezo. 11Pakuti zimene Amosi akunena ndi izi:

“ ‘Yeroboamu adzaphedwa ndi lupanga,

ndipo Israeli adzapita ndithu ku ukapolo,

kutali ndi dziko lake.’ ”

12Ndipo Amaziya anawuza Amosi kuti, “Choka, mlosi iwe! Bwerera ku dziko la Yuda. Uzikalosera kumeneko ndipo anthu a kumeneko azikakudyetsa. 13Usanenerenso ku Beteli, chifukwa kumeneko ndi malo opatulika a mfumu ndiponso ndi malo a nyumba yachipembedzo yaufumu.”

14Amosi anayankha Amaziya kuti, “Ine sindine mneneri kapena mwana wa mneneri; koma ndine woweta ziweto, ndiponso mlimi wa nkhuyu. 15Koma Yehova ananditenga ndikuweta nkhosa ndipo anati, ‘Pita ukanenere kwa anthu anga Aisraeli.’ 16Tsono imva mawu a Yehova. Iwe ukunena kuti,

“ ‘Usanenere zotsutsa Israeli,

ndipo siya kulalikira motsutsa nyumba ya Isake.’ ”

17“Tsono zimene akunena Yehova ndi izi:

“ ‘Mkazi wako adzasanduka wachiwerewere mu mzindamu,

ndipo ana ako aamuna ndi aakazi adzaphedwa ndi lupanga.

Munda wako udzayezedwa ndi chingwe ndi kugawidwa,

ndipo iwe mwini udzafera mʼdziko la anthu osapembedza Mulungu.

Ndipo Israeli adzatengedwa ndithu kupita ku ukapolo,

kutali ndi dziko lake.’ ”

New Russian Translation

Амос 7:1-17

Саранча, огонь и свинцовый отвес

1Вот что Владыка Господь, показал мне: Он готовил рои саранчи, когда царская доля была пожата, а поздняя трава начинала подниматься7:1 По-видимому, царь имел право на сбор первой травы, вероятно, на нужды армии (см. 3 Цар. 18:5). А поздняя трава – это зелень, выросшая вторично, после весенних дождей. После нее начиналась летняя засуха, и ничего вырасти не могло. Ее уничтожение саранчой могло значить только одно: повальный голод.. 2Когда они дочиста объели землю, я вскричал:

– Владыка Господи, молю Тебя, прости! Как выжить Иакову? Он так мал!

3И Господь смягчился.

– Не будет этого, – сказал Господь.

4Вот что Владыка Господь показал мне: Владыка Господь призвал огонь для суда, и тот иссушил великую пучину и пожрал землю7:4 Здесь говорится о том, что Бог навел испепеляющую жару, иссушившую подземные воды, которые по представлениям древних были источником всех вод, тем самым вызвав великую засуху на земле.. 5И я вскричал:

– О Владыка Господи, молю Тебя, остановись! Как выжить Иакову? Он ведь так мал!

6И Господь смягчился.

– Не будет и этого, – сказал Владыка Господь.

7Вот что Он показал мне: Владыка стоял у стены, построенной по отвесу, со свинцовым отвесом в руке. 8Господь спросил меня:

– Что ты видишь, Амос?

– Свинцовый отвес, – ответил я.

Владыка сказал:

– Вот, Я кладу отвес среди Моего народа, Израиля; Я больше не буду щадить их.

9– Возвышенности Исаака будут опустошены,

и святилища Израиля лягут руинами;

Я поднимусь с мечом против дома Иеровоама.

Амос и Амасия

10Амасия, священник из Вефиля, послал Иеровоаму, царю Израиля, весть: «Амос замышляет против тебя заговор в самом сердце Израиля. Земля не в силах терпеть всех его слов. 11Вот что говорит Амос:

„Иеровоам умрет от меча,

а Израиль непременно отправится в плен

со своей земли“».

12Амасия сказал Амосу:

– Уходи, провидец! Возвращайся в иудейскую землю. Там зарабатывай на хлеб, там и пророчествуй. 13Не пророчествуй больше в Вефиле – это капище царя и храм царства.

14Амос ответил Амасии:

– Я не пророк и не сын пророка. Я был пастухом и ухаживал за тутовыми деревьями. 15Но Господь забрал меня от овец и сказал мне: «Иди, пророчествуй Моему народу, Израилю». 16Итак, выслушай слово Господа. Ты говоришь:

«Не пророчествуй против Израиля,

перестань проповедовать против дома Исаака».

17Поэтому вот что говорит Господь:

«Городской блудницей станет твоя жена,

твои сыновья и дочери падут от меча.

Землю твою измерят и разделят,

а сам ты умрешь в нечистой земле.

Израиль же непременно пойдет в плен

со своей земли».