Obadiya 1 – CCL & NRT

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Obadiya 1:1-21

Masomphenya a Obadiya

1Masomphenya a Obadiya.

Ambuye Yehova akunena kwa Edomu kuti,

Tamva uthenga wochokera kwa Yehova:

Nthumwi yatumidwa kupita kwa anthu a mitundu kukanena kuti,

“Konzekani, tiyeni tikachite nkhondo ndi Edomu.”

2“Taona, ndidzakuchepetsani pakati pa anthu a mitundu ina;

udzanyozedwa kwambiri.

3Kudzikuza kwa mtima wako kwakusocheretsa,

iwe amene umakhala mʼmapanga a mʼmatanthwe

ndipo umamanga nyumba zako pa mapiri ataliatali,

iwe amene umanena mu mtima mwako kuti,

‘Ndani anganditsitse pansi?’

4Koma ngakhale umawuluka ngati chiwombankhanga

ndi kumanga chisa chako pakati pa nyenyezi,

ndidzakutsitsa pansi kuchokera kumeneko,”

akutero Yehova.

5“Anthu akuba akanabwera kwa iwe,

kapena anthu olanda zinthu akanafika usiku,

aa, tsoka lanji limene likukudikira iwe!

Kodi akanangotengako zimene akuzifuna zokha?

Ngati anthu othyola mphesa akanafika,

kodi akanakusiyiraniko mphesa pangʼono pokha?

6Koma Esau adzalandidwa zinthu zonse,

chuma chake chobisika chidzabedwa!

7Anthu onse ogwirizana nawo adzakupirikitsira kumalire;

abwenzi ako adzakunyenga ndi kukugonjetsa;

amene amadya chakudya chako adzakutchera msampha,

koma iwe sudzazindikira zimenezi.”

8Yehova akunena kuti, “Tsiku limenelo,

kodi sindidzawononga anthu onse anzeru a ku Edomu,

anthu odziwa zinthu mʼmapiri a Esau?

9Ankhondo ako, iwe Temani, adzachita mantha,

ndipo aliyense amene ali mʼphiri la Esau

adzaphedwa pa nkhondo.

10Chifukwa cha nkhanza zimene unachitira mʼbale wako Yakobo,

udzakhala wamanyazi;

adzakuwononga mpaka muyaya.

11Pamene adani

ankamulanda chuma chake

pamene alendo analowa pa zipata zake

ndi kuchita maere pa Yerusalemu,

pa tsikulo iwe unali ngati mmodzi wa iwo.

12Iwe sunayenera kunyoza mʼbale wako

pa nthawi ya tsoka lake,

kapena kunyogodola Ayuda

chifukwa cha chiwonongeko chawo,

kapena kuwaseka pa nthawi ya

mavuto awo.

13Iwe sunayenera kudutsa pa zipata za anthu anga

pa nthawi ya masautso awo,

kapena kuwanyogodola

pa tsiku la tsoka lawo,

kapena kulanda chuma chawo

pa nthawi ya masautso awo.

14Sunayenera kudikirira pamphambano ya misewu

kuti uphe Ayuda othawa,

kapena kuwapereka kwa adani awo Ayuda opulumuka

pa nthawi ya mavuto awo.”

15“Tsiku la Yehova layandikira

limene adzaweruza mitundu yonse ya anthu.

Adzakuchitira zomwe unawachitira ena;

zochita zako zidzakubwerera wekha.

16Iwe unamwa pa phiri langa loyera,

koteronso mitundu ina yonse idzamwa kosalekeza;

iwo adzamwa ndi kudzandira

ndipo adzayiwalika pa mbiri ya dziko lapansi.

17Koma pa Phiri la Ziyoni padzakhala chipulumutso;

phirilo lidzakhala lopatulika,

ndipo nyumba ya Yakobo

idzalandira cholowa chake.

18Nyumba ya Yakobo idzasanduka moto

ndipo nyumba ya Yosefe idzasanduka lawi la moto;

nyumba ya Esau idzasanduka chiputu,

ndipo adzayitenthe pa moto ndi kuyipsereza.

Sipadzakhala anthu opulumuka

kuchokera mʼnyumba ya Esau.”

Yehova wayankhula.

19Anthu ochokera ku Negevi adzakhala

ku mapiri a Esau,

ndipo anthu ochokera mʼmbali mwa mapiri

adzatenga dziko la Afilisti.

Adzakhala mʼminda ya Efereimu ndi Samariya,

ndipo Benjamini adzatenga Giliyadi.

20Aisraeli amene ali ku ukapolo

adzalandira dziko la Kanaani mpaka ku Zarefati;

a ku Yerusalemu amene ali ku ukapolo ku Sefaradi

adzalandira mizinda ya ku Negevi.

21Opulumukawo adzapita ku Phiri la Ziyoni

ndipo adzalamulira mapiri a Esau.

Koma ufumuwo udzakhala wa Yehova.

New Russian Translation

Авдий 1:1-21

1Видение, которое было к пророку Авдию.

Эдом будет низвергнут

Так говорит Владыка Господь об Эдоме:

Мы услышали весть от Господа,

что отправлен посланник к народам,

чтобы объявить им:

«Вставайте! Выступим войной против Эдома!»

2– Вот, Я сделаю тебя, Эдом, малым среди народов,

ты будешь в большом презрении.

3Гордость сердца твоего обольстила тебя.

Ты живешь в расщелинах скал1:3 Или: «в расщелинах Селы». На языке оригинала наблюдается игра слов: села означает «скала», но это также название столицы Эдома.,

высоко строишь свой дом

и говоришь в сердце своем:

«Кто низвергнет меня на землю?»

4Но даже если ты, подобно орлу,

поднимешься ввысь

и устроишь гнездо свое среди звезд,

то и оттуда Я низвергну тебя, –

возвещает Господь. –

5О, как ты будешь разрушен!

Если воры и грабители в ночи придут к тебе,

разве они не украдут только то, что пожелают?

Если проникнут к тебе собиратели винограда,

разве не оставят они несколько виноградин?

6Как все будет обыскано у Исава,

будут ограблены его тайники!

7Все твои союзники

вытеснят тебя до границы,

все твои друзья

обманут и одолеют тебя.

Те, кто ест твой хлеб, поставят на тебя западни,

но ты не догадаешься.

8В тот день, – возвещает Господь, –

Я истреблю мудрых в Эдоме

и благоразумных на горе Исава.

9Воины твои, Теман1:9 Теман – важный эдомитский город, получивший свое название от имени внука Исава, родоначальника Эдома (см. Быт. 36:15). Здесь под именем Теман подразумевается вся страна Эдом.,

будут трепетать от страха,

и все на горе Исава будут истреблены.

10Из-за насилия над своим братом Иаковом

будешь покрыт позором,

будешь уничтожен навсегда.

11Ты стоял в стороне в тот день,

когда чужие народы уносили его богатства,

когда иноземцы входили в его ворота

и бросали жребий об Иерусалиме.

Ты был как один из них!

12Тебе не следовало смотреть сверху вниз на своего брата

в день его несчастья,

не стоило торжествовать над народом Иуды

в день его гибели

и хвастаться

в день его страдания.

13Тебе не следовало входить

в ворота Моего народа

в день его бедствия,

смотреть на его горе

в день его бедствия

и касаться его богатства

в день его бедствия.

14Тебе не стоило стоять на перекрестках

и убивать беглецов,

не стоило выдавать уцелевших

в день их страдания.

Спасение Израиля

15– Близок день Господень для всех народов:

как ты поступал, так и с тобою поступят,

то, что ты делал, падет на твою же голову.

16Как вы пили на святой горе Моей,

так и все народы будут пить всегда,

будут пить, не переставая,

и проглотят, и исчезнут, будто их и не было.

17Будет на горе Сион спасение,

и будет она святой обителью,

а дом Иакова вернет свое наследие.

18Дом Иакова будет огнем,

дом Иосифа – пламенем,

а дом Исава будет соломою,

которую они подожгут и уничтожат;

никто из дома Исава не выживет, –

сказал Господь.

19Люди из Негева завладеют горой Исава,

а люди из предгорий – землей филистимлян.

Они захватят поля Ефрема и Самарии,

а Вениамин завладеет Галаадом.

20Войска сынов израилевых, те, что были в изгнании,

завладеют землей ханаанской до города Сарепты1:20 Сарепта – финикийский город, находившийся на территории современного государства Ливан.,

а изгнанники Иерусалима, живущие в Сефараде1:20 Сефарад – вероятно другое название Сардиса, столицы Лидии, но также возможно, что это местность Спарда в Малой Азии, или Шапарда в северо-западной Мидии, или же Испания, так, например, потомков евреев, изгнанных из Испании называют «сефардами».,

получат во владения города Негева.

21Спасители взойдут на гору1:21 Или: «сойдут с горы». Сион,

чтобы править горою Исава,

и наступит царствование Господа.