Amosi 9 – CCL & NRT

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Amosi 9:1-15

Israeli Adzawonongedwa

1Ine ndinaona Ambuye atayima pambali pa guwa lansembe, ndipo anati:

“Kantha mitu ya nsanamira

kuti ziwundo za nyumba zigwedezeke.

Muzigwetsere pa mitu ya anthu onse,

onse amene atsalira ndidzawapha ndi lupanga.

Palibe ndi mmodzi yemwe amene adzathawe,

palibe amene adzapulumuke.

2Ngakhale atakumba pansi mpaka ku malo a anthu akufa,

dzanja langa lidzawatulutsa kumeneko.

Ngakhale atakwera kumwamba

Ine ndidzawatsakamutsa kumeneko.

3Ngakhale atakabisala pamwamba pa phiri la Karimeli,

Ine ndidzawasaka kumeneko ndi kuwagwira.

Ngakhale atakabisala pansi pa nyanja yayikulu,

ndidzalamula njoka kuti iwalume kumeneko.

4Ngakhale adani awo awakusire ku ukapolo,

ndidzalamula lupanga kuti liwaphe kumeneko.

Ndidzawayangʼanitsitsa

kuti zoyipa ziwagwere; osati zabwino.”

5Ambuye Yehova Wamphamvuzonse

amene amakhudza dziko lapansi ndipo dzikolo limasungunuka,

onse amene amakhala mʼmenemo amalira.

Dziko lonse lidzadzaza ngati mtsinje wa Nailo,

kenaka nʼkuphwera ngati mtsinje wa ku Igupto.

6Iye amene amamanga malo ake okhalamo kumwamba,

ndi kuyika maziko ake pa dziko lapansi,

Iye amene amayitana madzi a ku nyanja

ndikuwakhuthulira pa dziko lapansi,

dzina lake ndiye Yehova.

7“Kodi kwa Ine, inu Aisraeli, simuli

chimodzimodzi ndi Akusi?”

Akutero Yehova.

“Kodi sindine amene ndinatulutsa Israeli ku Igupto,

Afilisti ku Kafitori

ndi Aaramu ku Kiri?

8“Taonani, maso a Ambuye Yehova

ali pa ufumu wochimwawu.

Ndidzawufafaniza

pa dziko lapansi.

Komabe sindidzawononga kotheratu

nyumba ya Yakobo,”

akutero Yehova.

9“Pakuti ndidzalamula,

ndipo ndidzagwedeza nyumba ya Israeli

pakati pa mitundu yonse ya anthu

monga momwe amasefera ufa mʼsefa,

koma palibe nʼkamwala kamodzi komwe kamene kadzagwe pansi.

10Anthu onse ochimwa pakati pa anthu anga

adzaphedwa ndi lupanga,

onse amene amanena kuti,

‘Tsoka silidzatigwera ife kapena kutiwononga.’

Kubwezeretsedwa kwa Israeli

11“Tsiku limenelo ndidzabwezeretsa

nyumba ya Davide imene inagwa.

Ndidzakonzanso malo amene anagumuka,

ndi kuyimanganso

monga inalili poyamba,

12kuti adzatengenso otsala a Edomu

ndi mitundu yonse imene imatchedwa ndi dzina langa,”

akutero Yehova amene adzachita zinthu izi.

13Yehova akunena kuti

“Nthawi ikubwera pamene mlimi wotipula adzapyola wokolola

ndipo woponda mphesa adzapyola wodzala mbewu.

Mapiri adzachucha vinyo watsopano

ndi kuyenderera pa zitunda zonse.

14Ndidzawabwezeranso pabwino anthu anga Aisraeli;

mizinda imene inali mabwinja idzamangidwanso ndipo azidzakhalamo.

Adzalima minda ya mpesa ndipo adzamwa vinyo wake;

adzalima minda ndipo adzadya zipatso zake.

15Ndidzakhazika Aisraeli mʼdziko mwawo,

ndipo sadzachotsedwamonso mʼdziko

limene Ine ndawapatsa,”

akutero Yehova Mulungu wako.

New Russian Translation

Амос 9:1-15

Гибель Израиля

1Я видел Владыку, стоящим у жертвенника9:1 Или: «на жертвеннике».. Он сказал:

– Бей по верхушкам колонн,

пусть задрожит порог.

Обрушь их на головы им всем,

а уцелевших Я перебью мечом.

Ни один не укроется,

никто не спасется.

2Пусть зароются хоть в мир мертвых9:2 Евр.: «шеол». –

и оттуда достанет их Моя рука.

Пусть взберутся на небеса –

и оттуда Я свергну их.

3Пусть укроются на вершине Кармила –

Я и там отыщу и схвачу их.

Пусть на дне морском спрячутся от Меня –

Я велю там змею, и он ужалит их.

4Пусть враги уведут их в плен –

прикажу там мечу, и он убьет их.

Обращу на них свои глаза –

им на беду, а не во благо.

5Владыка, Господь Сил,

касается земли – и она тает,

а все живущие на ней плачут.

Вся земля поднимается, словно Нил,

и опускается, словно река Египта.

6Он воздвиг Свой величественный дворец на небесах

и основания его9:6 Смысл этого места в еврейском тексте неясен. утвердил на земле,

призвал воды морские

и разлил их по лицу земли;

Господь Его имя.

7– Разве вы, израильтяне,

для Меня не то же, что и кушиты?9:7 Обитатели земель в верхнем течении Нила. –

возвещает Господь.

Да, Я вывел Израиль из Египта,

но Я вывел и филистимлян из Кафтора9:7 То есть из Крита.

и арамеев – из Кира.

8Несомненно, очи Владыки Господа

обращены на грешное царство.

– Я сотру его с лица земли,

но не истреблю до конца дом Иакова, –

возвещает Господь. –

9Я дам повеление просеять дом Израиля

среди всех народов,

как просеивают зерно9:9 Или: «просеивают песок». решетом,

и ни один камушек не достигнет земли.

10Все грешники среди Моего народа

умрут от меча,

все те, кто говорит:

«Беда нас не постигнет, нас не коснется».

Возрождение Израиля

11– В тот день

Я восстановлю павшую скинию Давида.

Заделаю в ней бреши,

восстановлю руины,

отстрою, как в дни древние,

12чтобы им обладать остатком Эдома

и всеми народами, которые были названы Моим именем, –

говорит Господь, Который сделает это.

13Близятся дни, – возвещает Господь, –

когда жнеца будет сменять пахарь,

а сажающего виноградник – топчущий ягоды.

Молодое вино будет сочиться из гор

и течь со всех холмов.

14Я возвращу из плена народ Мой, Израиль9:14 Или: «верну благополучие Моему народу, Израилю».;

они отстроят разрушенные города

и будут в них жить.

Они посадят виноградники и будут пить их вино;

разведут сады и будут есть их плоды.

15Насажу Мой народ на его земле,

и никогда впредь он не будет исторгнут

из земли, что Я дал ему, –

говорит Господь, твой Бог.