何西阿書 3 – CCBT & CCL

Chinese Contemporary Bible (Traditional)

何西阿書 3:1-5

何西阿贖回不貞之妻

1耶和華對何西阿說:「你要再去愛那個另有新歡的淫婦,像耶和華愛以色列人一樣愛她。儘管他們祭拜別的神明,喜愛葡萄餅,耶和華仍然愛他們。」 2於是,我用一百七十克銀子和一百五十公斤大麥贖回她, 3對她說:「你要和我住許多日子。這期間不可行淫,不可親近別的男人,我也不與你同房。」 4以色列人也要有許多日子沒有君王和首領,沒有祭祀和神柱,也沒有以弗得和家庭神像。 5之後,以色列人將回心轉意,尋求他們的上帝耶和華,歸向他們的君王大衛。在末後的日子,他們將懷著敬畏的心歸向耶和華,領受祂的恩惠。

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Hoseya 3:1-5

Hoseya Ayanjana ndi Mkazi Wake

1Yehova anati kwa ine, “Pita kamukondenso mkazi wako, ngakhale ali pa chibwenzi ndi wina ndi kuti ndi wachigololo. Mukonde iyeyo monga momwe Yehova amakondera Aisraeli, ngakhale iwo amapita kukapembedza milungu ina ndi kukonda nsembe za keke zamphesa zowuma.”

2Motero ndinamukwatira popereka ndalama khumi ndi zisanu zasiliva, ndiponso mitanga isanu ndi iwiri ya barele. 3Kenaka ndinamuwuza mkaziyo kuti, “Ukhale nane masiku ambiri; usachitenso zachiwerewere kapena chigololo ndi munthu wina, ndipo ine ndidzakhala nawe.”

4Pakuti Aisraeli adzakhala masiku ambiri opanda mfumu kapena kalonga, osapereka nsembe kapena kuyimika miyala yachipembedzo, wopanda efodi kapena fano. 5Pambuyo pake Aisraeli adzabwerera ndi kufunafuna Yehova Mulungu wawo ndi Davide mfumu yawo. Adzabwera kwa Yehova akunjenjemera ndipo adzalandira madalitso mʼmasiku awo otsiriza.