但以理書 1 – CCBT & CCL

Chinese Contemporary Bible (Traditional)

但以理書 1:1-21

但以理被擄到巴比倫

1猶大約雅敬執政第三年,巴比倫尼布甲尼撒前來圍攻耶路撒冷2主將猶大約雅敬及上帝殿中的部分器具交在他手中。他把器具擄到巴比倫1·2 巴比倫」希伯來文是「示拿」,巴比倫的別稱。的神廟,放在他神明的庫房裡。

3王吩咐太監長亞施毗拿以色列的王室貴族中選一些人, 4即毫無殘疾、相貌英俊、學問淵博、知識豐富、聰慧善學、能在王宮服侍的青年,教他們迦勒底的語言和文字。 5王安排他們每日享用一份御用的膳食和酒。他們要受教養三年,期滿後好在王身邊供職。 6被選的人中有猶大族的但以理哈拿尼雅米沙利亞撒利雅7太監長給他們起了名字:稱但以理伯提沙撒哈拿尼雅沙得拉米沙利米煞亞撒利雅亞伯尼歌

8然而,但以理決心不用王的膳食和酒,以免玷污自己。他請求太監長准許他不玷污自己。 9上帝使但以理得到太監長的恩待和同情。 10不過,太監長對但以理說:「我懼怕我主我王,因為這是他安排給你們的飲食。如果他看見你們比同齡的青年瘦弱,如何是好?你們會使我在王面前人頭難保。」 11但以理便對太監長派來監管他、哈拿尼雅米沙利亞撒利雅的人說: 12「求你試試看,十天內只讓僕人們吃素菜、喝清水, 13然後比較一下我們的面貌和那些用御膳的青年的面貌,看了之後再作決定。」 14監管同意試他們十天。 15十天後,但以理和他三個朋友看上去比那些用御膳的青年更俊美健康。 16於是,監管撤去了安排給他們的膳食和酒,只給他們素菜。

17上帝使這四個青年精通各樣學問和知識。但以理能明白各種異象和夢兆。 18到了尼布甲尼撒王規定青年們進宮的日子,太監長便帶他們去見王。 19王與他們談話,發現無人比得上但以理哈拿尼雅米沙利亞撒利雅,便把他們留在身邊供職。 20王詢問他們各樣的事,發現他們的智慧和聰明比全國的術士和巫師高十倍。 21直到塞魯士王元年,但以理仍在那裡供職。

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Danieli 1:1-21

Maphunziro a Danieli ku Babuloni

1Chaka chachitatu cha ufumu wa Yehoyakimu mfumu ya Yuda, Nebukadinezara mfumu ya ku Babuloni inabwera ndi kuzinga mzinda wa Yerusalemu ndi kuwuthira nkhondo. 2Ndipo Ambuye anapereka Yehoyakimu mfumu ya ku Yuda mʼdzanja lake, pamodzi ndi zina mwa zida zotumikira mʼNyumba ya Mulungu. Iye anazitenga napita nazo ku nyumba ya mulungu wake ku Babuloni ndi kuziyika mʼnyumba yosungiramo chuma cha mulungu wake.

3Tsono mfumu inalamula Asipenazi, mkulu wa nduna zake kuti abwere nawo ena mwa Aisraeli ochokera mʼbanja laufumu ndi la olemekezeka, 4achinyamata wopanda chilema, okongola, aluso mu nzeru zonse, okhala ndi chidziwitso, achangu pophunzira, odziwa kutumikira mʼnyumba ya mfumu. Ndipo anati awaphunzitsenso kuwerenga chiyankhulo cha Ababuloni. 5Ndipo mfumu imawapatsa tsiku ndi tsiku gawo la chakudya ndi vinyo wa ku nyumba yaufumu, ndi kuti awaphunzitse kwa zaka zitatu, ndipo kenaka adzayambe kutumikira mfumu.

6Pakati pa amenewa panali ena ochokera ku Yuda: Danieli, Hananiya, Misaeli ndi Azariya. 7Mkulu wa nduna za mfumu anawapatsa mayina atsopano: Danieli anamutcha Belitesezara; Hananiya anamutcha Sadirake; Misaeli anamutcha Mesaki; ndi Azariya anamutcha Abedenego.

8Koma Danieli anatsimikiza mtima kuti asadzidetse ndi chakudya ndi vinyo wa mfumu, ndipo anapempha chilolezo kwa mkulu wa nduna za mfumu kuti asadzidetse mwa njira imeneyi. 9Ndipo Mulungu anafewetsa mtima wa ndunayo kuti amukomere mtima ndi kumuchitira chifundo Danieli, 10koma ndunayo inamuwuza Danieli kuti, “Ine ndikuchita mantha ndi mbuye wanga mfumu, amene wapereka chakudya ndi chakumwa chanu. Kodi akuoneni inu owonda kuposa anzanu a misinkhu yanu pa chifukwa chanji? Mfumu ikhoza kundidula mutu chifukwa cha iwe.”

11Ndipo Danieli anati kwa kapitawo amene anali mkulu wa nduna za mfumu amene anamuyika kuti ayangʼanire Danieli, Hananiya, Misaeli ndi Azariya, 12“Chonde mutiyese ife akapolo anu pa masiku khumi: mutipatse masamba okha kuti tidye ndi madzi akumwa. 13Ndipo mudzafananize maonekedwe athu ndi a anyamata amene akudya chakudya cha mfumu, ndi kuti mudzachite ndi anyamata anu monga momwe mudzawaonere.” 14Choncho anawavomera ndipo anawayesa pa masiku khumi.

15Pakutha pa masiku khumi iwo anaoneka athanzi ndi odya bwino kuposa aliyense wa anyamata amene ankadya chakudya cha mfumu aja. 16Choncho kapitawo anawachotsera chakudya ndi vinyo za ku nyumba yaufumu zija nawapatsa ndiwo zamasamba basi.

17Kwa anyamata anayiwa Mulungu anapereka chidziwitso ndi kuzindikira bwino mitundu yonse ya zolembedwa ndi za maphunziro. Ndipo Danieli ankatanthauzira masomphenya ndi maloto a mitundu yonse.

18Ndipo kumapeto kwa masiku amene mfumu inayika kuti adzaonetse anyamatawa ku nyumba yake, mkulu wa nduna za mfumu uja anawapereka iwo kwa Nebukadinezara. 19Mfumu inayankhula nawo, ndipo panalibe wofanana ndi Danieli; Hananiya Misaeli ndi Azariya; Choncho analowa ndi kukhala otumikira mfumu. 20Nthawi zonse mfumu ikawafunsa zonse zofuna nzeru ndi chidziwitso, inkapeza kuti iwo anali oposa amatsenga ndi owombeza onse a mu ufumu wake wonse mopitirira muyeso.

21Ndipo Danieli anali kumeneko mpaka chaka choyamba cha ufumu wa Koresi.