約珥書 1 – CCBT & CCL

Chinese Contemporary Bible (Traditional)

約珥書 1:1-20

1以下是耶和華對毗土珥的兒子約珥所說的話。

嚴重的蝗災

2長老們啊,請聽我說!

地上的所有居民啊,要留心聽!

在你們或你們祖先的時代可曾發生過這樣的事?

3要把這事告訴你們的子子孫孫,

傳到世世代代!

4蝗蟲吃剩的,蝻子來吃;

蝻子吃剩的,蚱蜢來吃;

蚱蜢吃剩的,螞蚱來吃1·4 蝗蟲蝻子蚱蜢螞蚱」四個詞希伯來語的確切意思很難考證。

5醉漢啊,醒過來哭泣吧!

貪杯的人啊,哀號吧!

你們再無美酒可飲了。

6有一群兇猛的蝗蟲侵犯我的國土,

牠們不計其數,

有雄獅的獠牙和母獅的利齒。

7牠們毀壞我的葡萄樹和無花果樹,

剝光樹皮,

只留下光禿的樹枝。

8我的子民啊,你們要像死了未婚夫的少女,

穿上喪服痛哭哀號。

9耶和華殿中的素祭1·9 素祭就是獻上五穀、麵粉之類的供物,參見利未記2章。和奠祭1·9 奠祭就是獻上新釀的酒。都停止了,

事奉耶和華的祭司都哀傷。

10田園荒廢,遍地淒涼,

五穀盡毀,

再也沒有新酒和油了。

11農夫啊,你們要憂傷!

照料葡萄園的人啊,

你們要哀號!

因為田間的大麥和小麥全毀了。

12葡萄樹枯死,

無花果樹凋殘,

石榴樹、棕樹、蘋果樹等田野的一切樹木枯乾。

人間的歡樂消逝了。

13祭司啊,穿著喪服痛哭吧;

在祭壇前事奉的人啊,要哀號;

我上帝的僕人啊,要披上麻衣過夜;

因為再無素祭和奠祭獻到你們上帝的殿中了。

14你們要定一個禁食的日子,

舉行莊嚴的聚會,

召集全國的長老和人民,

到你們的上帝耶和華的殿中,

向耶和華呼求。

15太可怕了!耶和華的日子近了,

那是全能者施行毀滅的日子。

16我們的糧食斷絕了,

我們上帝殿中的歡樂消失了。

17種子在土裡腐爛,

五穀乾死,倉庫荒廢,

穀倉被拆毀。

18牲畜哀鳴,

牛群因找不到草場而四處亂竄,

羊群也受苦。

19耶和華啊,我向你呼求,

因為火焰吞滅了曠野的草場,

烈火燒光了田野的樹木。

20田野的走獸向你呼求,

因為溪水已經枯乾,

火也燒盡了曠野的草場。

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Yoweli 1:1-20

1Yehova anayankhula ndi Yoweli mwana wa Petueli.

Kubwera kwa Dzombe

2Inu akuluakulu, imvani izi;

mvetserani, nonse amene mumakhala mʼdziko.

Kodi zinthu zokhala ngati izi zinayamba zaonekapo mʼnthawi yanu,

kapena mʼnthawi ya makolo anu?

3Muwafotokozere ana anu,

ndipo ana anuwo afotokozere ana awo,

ndipo ana awo adzafotokozere mʼbado winawo.

4Chimene dzombe losamera mapiko lasiya

dzombe lowuluka ladya;

chimene dzombe lowuluka lasiya

dzombe lalingʼono ladya;

chimene dzombe lalingʼono lasiya

chilimamine wadya.

5Dzukani, inu zidakwa ndipo mulire!

Lirani mofuwula, inu nonse amene mumamwa vinyo;

lirani mofuwula chifukwa cha vinyo watsopano,

pakuti wachotsedwa pakamwa panu.

6Mtundu wa anthu wathira nkhondo dziko langa,

wamphamvu ndi wosawerengeka;

uli ndi mano a mkango,

zibwano za mkango waukazi.

7Wawononga mphesa zanga

ndipo wathyola mitengo yanga ya mkuyu.

Wakungunula makungwa ake

ndi kuwataya,

kusiya nthambi zake zili mbee.

8Lirani ngati namwali wovala chiguduli,

chifukwa cha mwamuna wa utsikana wake.

9Chopereka cha chakudya ndi cha chakumwa

sizikuperekedwa ku nyumba ya Yehova.

Ansembe akulira,

amene amatumikira pamaso pa Yehova.

10Minda yaguga,

nthaka yauma;

tirigu wawonongeka,

vinyo watsopano watha,

mitengo ya mafuta yauma.

11Khalani ndi nkhawa, inu alimi,

lirani mofuwula inu alimi a mphesa;

imvani chisoni chifukwa cha tirigu ndi barele,

pakuti zokolola za mʼmunda zawonongeka.

12Mpesa wauma

ndipo mtengo wamkuyu wafota;

makangadza, kanjedza ndi mitengo ya apulosi,

mitengo yonse ya mʼmunda yauma.

Ndithudi chimwemwe cha anthu

chatheratu.

Mulungu Ayitana Anthu kuti Atembenuke

13Inu ansembe, valani ziguduli ndipo lirani;

lirani mofuwula, inu amene mumatumikira pa guwa lansembe.

Bwerani, fundani ziguduli usiku wonse,

inu amene mumatumikira pamaso pa Mulungu wanga;

pakuti chopereka cha chakudya ndi cha chakumwa

sizikupezekanso mʼnyumba ya Mulungu wanu.

14Lengezani tsiku lopatulika losala zakudya,

itanani msonkhano wopatulika.

Sonkhanitsani akuluakulu

ndi anthu onse okhala mʼdziko

ku nyumba ya Yehova Mulungu wanu

ndipo alirire Yehova.

15Kalanga ine tsikulo!

Pakuti tsiku la Yehova layandikira;

lidzabwera ngati chiwonongeko chochokera kwa Wamphamvuzonse.

16Kodi chakudya chathu sichachotsedwa

ife tikuona?

Kodi mʼnyumba ya Mulungu wathu

simulibe chimwemwe ndi chisangalalo?

17Mbewu zikunyala

poti pansi ndi powuma.

Nyumba zosungiramo zinthu zawonongeka;

nkhokwe zapasuka

popeza tirigu wauma.

18Taonani mmene zikulirira ziweto;

ngʼombe zikungoyenda uku ndi uku

chifukwa zilibe msipu;

ngakhalenso nkhosa zikusauka.

19Kwa Inu Yehova ndilirira,

pakuti moto wapsereza msipu wakuthengo,

malawi amoto apsereza mitengo yonse ya mʼtchire.

20Ngakhale nyama zakuthengo zikulirira Inu;

timitsinje tonse taphwa

ndipo moto wapsereza msipu wa kuthengo.