Mwanzo 2 – NEN & CCL

Kiswahili Contemporary Version

Mwanzo 2:1-25

12:1 Kum 4:19; 17:3; 2Fal 17:16; 21:3; Za 104:2; Isa 44:24; 45:12; 48:13; 51:13Kwa hiyo mbingu na dunia zikakamilika, pamoja na vyote vilivyomo.

22:2 Kum 5:14; Ebr 4:4; Kut 20:11; 31:17; 34:21; Yn 5:17Katika siku ya saba Mungu alikuwa amekamilisha kazi aliyokuwa akiifanya, hivyo siku ya saba akapumzika kutoka kazi zake zote. 32:3 Kut 16:23; 20:10; 23:12; 31:15; 35:2; Law 23:3; Ebr 4:11; Neh 9:14; Mwa 1:1; Za 95:11; Isa 58:13; Yer 17:22Mungu akaibariki siku ya saba akaifanya takatifu, kwa sababu katika siku hiyo alipumzika kutoka kazi zote za kuumba alizokuwa amefanya.

Adamu Na Eva

42:4 Mwa 5:1; 6:9; 1:1; 10:1; 11:10; 27:25; Ay 38:8-11Haya ndiyo maelezo ya mbingu na dunia wakati zilipoumbwa.

Bwana Mungu alipoziumba mbingu na dunia, 52:5 Mwa 1:11; Ay 38:28; Za 65:9-10; Yer 10:13hapakuwepo na mche wa shambani uliokuwa umejitokeza ardhini, wala hapakuwepo na mmea wa shamba uliokuwa umeota, kwa kuwa Bwana Mungu alikuwa hajanyeshea mvua juu ya nchi, na hapakuwepo mtu wa kuilima ardhi, 6lakini umande ulitokeza kutoka ardhini na kunyesha uso wote wa nchi: 72:7 Isa 29:16; 43:1, 21; 44:2; Mwa 1:27; 3:19; 18:27; 5:23; 4:2; Ay 4:19; 10:9; 17:16; 34:15; Za 103:14; 90:3; Mhu 3:20; 12:7Bwana Mungu alimuumba mtu kutoka mavumbi2:7 Neno la Kiebrania la mavumbi ya ardhi ndilo kiini cha jina Adamu. ya ardhi, akampulizia pumzi ya uhai puani mwake, naye mtu akawa kiumbe hai.

82:8 Mwa 3:23-24; 4:16; 13:10; Isa 51:3; Eze 28:13; 36:35; 31:9, 16; Yoe 2:3Basi Bwana Mungu alikuwa ameotesha bustani upande wa mashariki, katika Edeni, huko akamweka huyo mtu aliyemuumba. 92:9 Eze 31:8; 47:12; Mit 3:18; 11:30; Ufu 2:7; Mwa 3:22, 24Bwana Mungu akafanya aina zote za miti ziote kutoka ardhini, miti yenye kupendeza macho na mizuri kwa chakula. Katikati ya bustani ulikuwepo mti wa uzima na mti wa kujua mema na mabaya.

102:10 Hes 24:6; Eze 47:5; Za 46:4Mto wa kunyeshea bustani ulitiririka toka Edeni, kuanzia hapa ukagawanyika kuwa mito minne. 112:11 Mwa 10:7; 25:18Mto wa kwanza uliitwa Pishoni, nao huzunguka nchi yote ya Havila ambako kuna dhahabu. 122:12 Hes 11:7(Dhahabu ya nchi hiyo ni nzuri, bedola na vito shohamu pia hupatikana huko.) 13Jina la mto wa pili ni Gihoni, ambao huzunguka nchi yote ya Kushi. 142:14 Mwa 15:18; 41:1; 31:21; Dan 10:4; Kut 23:31; Hes 22:5; Ufu 9:14; 1Fal 4:21; 2Sam 8:3; Kum 11:24; 2Fal 23:29; 24:7; 1Nya 5:9; 18:3; 2Nya 35:20; Yer 13:4; 42:6; 51:63Jina la mto wa tatu ni Tigrisi, unaopita mashariki ya Ashuru. Mto wa nne ni Frati.

15Bwana Mungu akamchukua huyo mtu, akamweka kwenye Bustani ya Edeni ailime na kuitunza. 162:16 Mwa 3:1-2Bwana Mungu akamwagiza huyo mtu, akamwambia, “Uko huru kula matunda ya mti wowote katika bustani, 172:17 Mwa 3:11, 17; 9:29; Yer 42:16; Kum 30:15, 19; Eze 3:18; Rum 5:13; 6:23lakini kamwe usile matunda ya mti wa kujua mema na mabaya, kwa maana siku utakapokula matunda yake, hakika utakufa.”

182:18 Mit 11:31; 1Kor 11:9; 1Tim 2:13Bwana Mungu akasema, “Si vyema huyu mtu awe peke yake. Nitamfanyia msaidizi wa kumfaa.”

192:19 Za 8:7; Mwa 1:5, 20, 24Basi Bwana Mungu alikuwa amefanyiza kutoka ardhi wanyama wote wa porini na ndege wote wa angani. Akawaleta kwa huyu mtu aone atawaitaje, nalo jina lolote alilokiita kila kiumbe hai, likawa ndilo jina lake. 202:20 Mwa 3:20; 4:1Hivyo Adamu akawapa majina wanyama wote wa kufugwa, ndege wa angani, na wanyama wote wa porini.

Lakini kwa Adamu hakupatikana msaidizi wa kumfaa. 212:21 Mwa 15:12; 1Sam 26:12; Ay 33:15Hivyo Bwana Mungu akamfanya Adamu kulala usingizi mzito, naye alipokuwa amelala akachukua moja ya mbavu zake, akapafunika mahali pale kwa nyama. 222:22 1Kor 11:8-9, 12; 1Tim 2:12Kisha Bwana Mungu akamfanya mwanamke kutoka kwenye ule ubavu aliouchukua kutoka kwa huyo mwanaume, akamleta huyo mwanamke kwa huyo mwanaume.

232:23 Mwa 29:14; Efe 5:28-30; 1Kor 11:8Huyo mwanaume akasema,

“Huyu sasa ni mfupa wa mifupa yangu

na nyama ya nyama yangu,

ataitwa ‘mwanamke,’2:23 Jina la Kiebrania la mwanamke linafanana na lile la mwanaume.

kwa kuwa alitolewa katika mwanaume.”

242:24 Mal 2:15; Mt 19:5; Mk 10:7-8; Efe 5:31; 1Kor 6:16Kwa sababu hii mwanaume atamwacha baba yake na mama yake na kuambatana na mkewe, nao watakuwa mwili mmoja.

252:25 Mwa 3:7, 10-11; Isa 47:3; Mao 1:8Adamu na mkewe wote wawili walikuwa uchi, wala hawakuona aibu.

The Word of God in Contemporary Chichewa

Genesis 2:1-25

1Motero kumwamba, dziko lapansi ndi zonse za mʼmenemo zinatha kulengedwa monga mwa kuchuluka kwawo.

2Pofika tsiku lachisanu ndi chiwiri Mulungu anamaliza ntchito zonse zimene ankagwira ndipo pa tsiku lachisanu ndi chiwiri anapumula ku ntchito zake zonse. 3Ndipo Mulungu anadalitsa tsiku lachisanu ndi chiwiri nalipatula, chifukwa pa tsiku limeneli Iye anapumula ku ntchito yonse yolenga imene anayigwira.

Adamu ndi Hava

4Mbiri ya momwe kumwamba ndi dziko lapansi zinalengedwera pa tsiku lija Yehova Mulungu ankazilenga ndi iyi:

Yehova Mulungu atapanga dziko lapansi ndi kumwamba, 5zitsamba zinali zisanamere ndipo chomera chilichonse chinali chisanamerenso popeza Yehova Mulungu anali asanagwetse mvula pa dziko lapansi. Panalibe munthu wolima nthaka, 6koma kasupe ankatuluka mʼnthaka ndi kuthirira pa dziko lonse. 7Tsono Yehova Mulungu anawumba munthu kuchokera ku dothi nawuziramo mpweya wamoyo mʼmphuno mwake ndipo munthuyo anakhala wamoyo.

8Kenaka Yehova Mulungu anatsekula munda wa Edeni chakummawa; kumeneko anayikako munthu amene anamupanga uja. 9Ndipo Yehova Mulungu anameretsa mʼmundamo mitengo ya mitundu yonse. Inali mitengo yokongola ndi ya zipatso zokoma. Pakati pa munda uja panali mtengo wopatsa moyo ndi mtengo wopatsa nzeru zodziwitsa chabwino ndi choyipa.

10Mtsinje wothirira mundawo unkatuluka mu Edeni; kuchokera apo unkagawikana kukhala mitsinje inayi. 11Dzina la mtsinje woyamba ndi Pisoni; uwu umazungulira dziko lonse la Havila, kumene kuli golide. 12(Golide wa ku dziko ili ndi wabwino. Kulinso miyala yokongola ya bedola ndi onikisi). 13Dzina la mtsinje wachiwiri ndi Gihoni; uwu umazungulira dziko lonse la Kusi. 14Dzina la mtsinje wachitatu ndi Tigirisi; umayenda chakummawa kwa Asiriya. Ndipo mtsinje wachinayi ndi Yufurate.

15Yehova Mulungu anatenga munthu uja ndi kumuyika mʼmunda wa Edeni kuti awulime ndi kuwusamalira. 16Ndipo Yehova Mulungu analamula munthu uja kuti, “Uzidya zipatso za mu mtengo wina uliwonse mʼmundamu; 17koma usadye zipatso za mu mtengo wodziwitsa chabwino ndi choyipa, popeza ukadzadya za mu mtengowu udzafa ndithu.”

18Ndipo Yehova Mulungu anati, “Sibwino kuti munthu akhale yekha. Ndidzamupangira mnzake womuthandiza.”

19Kenaka Yehova Mulungu anawumba ndi dothi nyama zonse zakuthengo ndi mbalame zonse zamlengalenga. Ndipo Iye anapita nazo kwa munthu uja kuti akazipatse mayina; ndipo dzina lililonse limene Adamu anapereka ku chamoyo chilichonse, lomwelo linakhala dzina lake. 20Choncho Adamu anazitcha mayina ziweto zonse, mbalame zamlengalenga ndi nyama zakuthengo zonse.

Komabe munthu uja analibe mnzake womuthandiza. 21Tsono Yehova Mulungu anamugonetsa munthu uja tulo tofa nato; ali mtulo chomwecho, Mulungu anachotsa imodzi mwa nthiti zake ndi kutseka pamalopo ndi mnofu. 22Motero Yehova Mulungu anapanga mkazi ndi nthiti ija imene anatenga kwa munthu uja nabwera naye kwa iye.

23Munthu uja anati,

“Uyu ndiye fupa lochokera ku mafupa anga

ndi mnofu wochokera ku mnofu wanga;

adzatchedwa ‘mkazi,’

popeza wachokera mwa mwamuna.”

24Nʼchifukwa chake, mwamuna amasiya abambo ndi amayi ake nakaphatikana ndi mkazi wake ndipo awiriwo amakhala thupi limodzi.

25Munthu uja ndi mkazi wakeyo, onse awiri anali maliseche ndipo analibe manyazi.