1Masomphenya wonena za Yuda ndi Yerusalemu, amene Yesaya mwana wa Amozi, anaona pa nthawi ya ulamuliro wa Uziya, Yotamu, Ahazi ndi Hezekiya, mafumu a Yuda.
Anthu Owukira
2Tamverani, miyamba inu! Tchera khutu, iwe dziko lapansi!
Pakuti Yehova wanena kuti,
“Ndinabala ana ndi kuwalera,
koma anawo andiwukira Ine.
3Ngʼombe imadziwa mwini wake,
bulu amadziwa kumene kuli gome la mbuye wake,
koma Israeli sadziwa,
anthu anga samvetsa konse.”
4Haa, mtundu wochimwa,
anthu olemedwa ndi machimo,
obadwa kwa anthu ochita zoyipa,
ana odzipereka ku zoyipa!
Iwo asiya Yehova;
anyoza Woyerayo wa Israeli
ndipo afulatira Iyeyo.
5Chifukwa chiyani mukufuna kuti muzingolangidwabe?
Chifukwa chiyani mukupitirira kukhala mʼmoyo wowukira?
Mutu wanu wonse uli ndi mabala,
mtima wanu wonse wafowokeratu.
6Kuchokera ku phazi mpaka ku mutu
palibe pabwino,
paliponse pali mikwingwirima ndi zilonda,
mabala ali magazi chuchuchu,
mabala ake ngosatsuka, ngosamanga
ndiponso ngosapaka mafuta ofewetsa.
7Dziko lanu lasanduka bwinja,
mizinda yanu yatenthedwa ndi moto;
minda yanu ikukololedwa ndi alendo
inu muli pomwepo,
dziko lanu lasanduka bwinja monga ngati lagonjetsedwa ndi alendo.
8Mwana wamkazi wa Ziyoni watsala yekha
ngati nsanja mʼmunda wampesa,
ngati chisimba mʼmunda wa minkhaka,
ngati mzinda wozingidwa ndi nkhondo.
9Yehova Wamphamvuzonse akanapanda
kutisiyira opulumuka,
tikanawonongeka ngati Sodomu,
tikanakhala ngati anthu a ku Gomora.
10Imvani mawu a Yehova,
inu olamulira Sodomu;
mverani lamulo la Mulungu wathu,
inu anthu a ku Gomora!
11Yehova akuti, “Kodi ndili nazo chiyani
nsembe zanu zochuluka?”
“Zandikola nsembe zanu zopsereza
za nkhosa zazimuna ndiponso mafuta a nyama zonenepa;
sindikusangalatsidwanso
ndi magazi angʼombe zamphongo ndi a ana ankhosa ndi ambuzi zazimuna.
12Ndani anakulamulirani kuti
mubwere nazo pamaso panga?
Ndani anakuwuzani kuti muzipondaponda mʼmabwalo a nyumba yanga?
13Siyani kubweretsa nsembe zachabechabezo!
Nsembe zanu zofukiza zimandinyansa Ine.
Sindingapirire misonkhano yanu yoyipa,
kapenanso zikondwerero za Mwezi Watsopano ndi Masabata.
14Zikondwerero zanu za Mwezi Watsopano ndi masiku anu opatulika
ndimadana nazo.
Zasanduka katundu wondilemera;
ndatopa kuzinyamula.
15Mukamatambasula manja anu popemphera,
Ine sindidzakuyangʼanani;
ngakhale muchulukitse mapemphero anu,
sindidzakumverani.
Manja anu ndi odzaza ndi magazi;
16sambani, dziyeretseni.
Chotsani pamaso panu
ntchito zanu zoyipa!
Lekani kuchita zoyipa,
17phunzirani kuchita zabwino!
Funafunani chilungamo,
thandizani oponderezedwa.
Tetezani ana amasiye,
muwayimirire akazi amasiye pa milandu yawo.”
18Yehova akuti,
“Tiyeni tsono tikambe mlandu wanu.
Ngakhale machimo anu ali ofiira,
adzayera ngati thonje.
Ngakhale ali ofiira ngati kapezi,
adzayera ngati ubweya wankhosa.
19Ngati muli okonzeka kundimvera
mudzadya zinthu zabwino za mʼdziko;
20koma mukakana ndi kuwukira
mudzaphedwa ndi lupanga.”
Pakuti Yehova wayankhula.
21Taonani momwe mzinda wokhulupirika
wasandukira wadama!
Mzinda umene kale unali wodzaza ndi chiweruzo cholungama;
mu mzindamo munali chilungamo,
koma tsopano muli anthu opha anzawo!
22Siliva wako wasanduka wachabechabe,
vinyo wako wabwino wasungunulidwa ndi madzi.
23Atsogoleri ako ndi owukira,
anthu ogwirizana ndi mbala;
onse amakonda ziphuphu
ndipo amathamangira mphatso.
Iwo sateteza ana amasiye;
ndipo samvera madandawulo a akazi amasiye.
24Nʼchifukwa chake Ambuye Yehova Wamphamvu,
Wamphamvuyo wa Israeli, akunena kuti,
“Haa, odana nane ndidzawatha,
ndipo ndidzawabwezera ndekha adani anga.
25Ndidzatambasula dzanja langa kuti ndilimbane nawe;
ndidzasungunula machimo ako nʼkuwachotsa,
monga mmene amachotsera dzimbiri ndi mankhwala.
26Ndidzabwezeretsa oweruza ako ngati masiku amakedzana,
aphungu ako ndidzawabwezeretsa ngati poyamba paja.
Kenaka iweyo udzatchedwa
mzinda wolungama,
mzinda wokhulupirika.”
27Ziyoni adzawomboledwa mwa chiweruzo cholungama,
anthu ake olapadi adzapulumutsidwa mwachilungamo.
28Koma owukira ndi ochimwa adzawawonongera pamodzi,
ndipo amene asiya Yehova adzatheratu.
29“Mudzachita nayo manyazi mitengo ya thundu
imene inkakusangalatsani;
mudzagwetsa nkhope chifukwa cha minda
imene munayipatula.
30Mudzakhala ngati mtengo wa thundu umene masamba ake akufota,
mudzakhala ngati munda wopanda madzi.
31Munthu wamphamvu adzasanduka ngati udzu wowuma,
ndipo ntchito zake zidzakhala ngati mbaliwali;
motero zonse zidzayakira limodzi,
popanda woti azimitse motowo.”
1اين كتاب شامل پيامهايی است كه خدا در دوران سلطنت عزيا و يوتام و آحاز و حزقيا، پادشاهان سرزمين يهودا، در عالم رؤيا به اشعيا پسر آموص داد. اين پيامها دربارهٔ يهودا و پايتخت آن اورشليم است.
ياغيگری قوم اسرائيل
2ای آسمان و زمين، به آنچه خداوند میفرمايد گوش كنيد: «فرزندانی كه بزرگ كردهام بر ضد من برخاستهاند. 3گاو مالک خود را و الاغ صاحب خويش را میشناسد، اما قوم اسرائيل شعور ندارد و خدای خود را نمیشناسد.»
4وای بر شما قوم گناهكار كه پشتتان زير بار گناهانتان خم شده است. وای بر شما مردم شرور و فاسد كه از خداوند مقدس بنیاسرائيل روگردانده و او را ترک گفتهايد. 5چرا از گناهان خود دست برنمیداريد؟ آيا به اندازهٔ كافی مجازات نشدهايد؟ ای اسرائيل، فكر و دلت تمام بيمار است. 6از سر تا پا مجروح و مضروب هستی؛ جای سالم در بدنت نمانده است. زخمهايت باز مانده و عفونی شده، كسی آنها را بخيه نزده و مرهم نماليده است.
7ای قوم اسرائيل، سرزمينتان ويران گشته و شهرهايتان به آتش كشيده شده است. بيگانگان هر چه را كه میبينند، در برابر چشمانتان به غارت میبرند و نابود میكنند. 8اورشليم همچون كلبهای در مزرعه و مانند سايبانی در جاليز، بیدفاع و تنها مانده است.
9اگر خداوند قادر متعال به داد قوم ما نمیرسيد اين عدهٔ كم نيز از ما باقی نمیماند و اورشليم مثل شهرهای سدوم و عموره به کلی از بين میرفت.
10ای حاكمان و ای مردم اورشليم كه چون اهالی سدوم و عموره فاسد هستيد، به كلام خداوند گوش دهيد. 11او میفرمايد: «از قربانیهای شما بيزارم. ديگر آنها را به حضور من نياوريد. قوچهای فربهٔ شما را نمیخواهم. ديگر مايل نيستم خون گاوها و برهها و بزغالهها را ببينم. 12چه كسی از شما خواسته كه وقتی به حضور من میآييد اين قربانیها را با خود بياوريد؟ چه كسی به شما اجازه داده كه اينچنين آستان خانهٔ مرا پايمال كنيد؟ 13ديگر اين هدايای باطل را نياوريد. من از بخوری كه میسوزانيد نفرت دارم و از اجتماعات مذهبی و مراسمی كه در اول ماه و در روز سَبَت بجا میآوريد بيزارم. نمیتوانم اين اجتماعات گناهآلود را تحمل كنم. 14از همهٔ آنها متنفرم و تحمل ديدن هيچكدام را ندارم. 15هرگاه دستهايتان را به سوی آسمان دراز كنيد، روی خود را از شما برخواهم گرداند و چون دعای بسيار كنيد، اجابت نخواهم نمود؛ زيرا دستهای شما به خون آلوده است.
16«خود را بشوييد و طاهر شويد! گناهانی را كه در حضور من مرتكب شدهايد از خود دور كنيد. 17نيكوكاری را بياموزيد و با انصاف باشيد. به مظلومان و يتيمان و بيوهزنان كمک كنيد.»
18خداوند میفرمايد: «بحث و جدل من با شما اين است: اگرچه لكههای گناهانتان به سرخی خون است، اما من آنها را مانند پشم پاک میكنم و شما را همچون برف سفيد میسازم! 19كافی است مرا اطاعت كنيد تا شما را از محصول زمين سير كنم. 20اما اگر به سرپيچی از من ادامه دهيد، به دست دشمن كشته خواهيد شد.» اين كلام خداوند است.
21ای اورشليم، زمانی تو نسبت به خداوند وفادار بودی، اما اينک همچون يک فاحشه به دنبال خدايان ديگر میروی. زمانی شهر عدل و انصاف بودی، اما اكنون شهر جنايتكاران شدهای. 22زمانی چون نقره خالص بودی، ولی اينک فلزی بیمصرف شدهای. زمانی همچون شراب ناب بودی، ولی اكنون همانند آب شدهای. 23رهبرانت ياغی و شريک دزدانند؛ همه رشوهخوارند؛ از يتيمان حمايت نمیكنند و به دادخواهی بيوهزنان گوش نمیدهند. 24بنابراين خداوند، خدای قادر متعال اسرائيل به آنها میگويد: «شما دشمن من هستيد؛ تا از شما انتقام نگيرم آرام نمیشوم. 25به دست خود، شما را مثل فلز در كوره میگدازم تا از كثافت خود پاک شويد.
26«مانند گذشته، رهبران و مشاورانی لايق به شما خواهم بخشيد تا اورشليم را به شهر عدالت و امانت مشهور سازند.»
27خداوند عادل، اورشليم و اهالی توبهكار آن را نجات خواهد داد. 28اما گناهكاران و عصيانگران را به هلاكت خواهد رساند و كسانی را كه او را ترک كنند نابود خواهد كرد.
29شما از بتپرستی خود در زير درختان بلوط باغهايتان پشيمان خواهيد شد، 30و مانند بلوطی خشک و باغی بیآب، از بين خواهيد رفت. 31زورمندانتان با اعمالشان مانند كاه در آتش خواهند سوخت و كسی قادر نخواهد بود آنها را نجات دهد.