Miyambo 2 – CCL & NEN

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Miyambo 2:1-22

Ubwino Wanzeru

1Mwana wanga, ngati ulandira mawu anga

ndi kusunga malamulo anga mu mtima mwako,

2ndiponso kutchera khutu lako ku nzeru

ndi kuyikapo mtima pa kumvetsa zinthu;

3ngati upempha kuti uzindikire zinthu

inde kupempha ndi mtima wonse kuti ukhale womvetsa zinthu,

4ngati ufunafuna nzeruyo ngati siliva

ndi kuyisakasaka ngati chuma chobisika,

5ndiye udzamvetsa bwino tanthauzo la kuopa Yehova;

ndipo udzapezanso tanthauzo la kumudziwa Yehova.

6Pakuti Yehova ndiye amapereka nzeru,

ndipo mʼkamwa mwake mumachokera chidziwitso ndi kumvetsa zinthu.

7Anthu olungama zinthu zimawayendera bwino chifukwa Yehova amakhala nawo.

Paja Yehova ndiye chishango cha amene amayenda mwangwiro,

8pakuti ndiye mlonda wa njira zolungama.

Iye amasamala mayendedwe a anthu ake okhulupirika.

9Choncho udzamvetsa tanthauzo la ungwiro, chilungamo,

kusakondera ndi njira iliyonse yabwino.

10Pakuti nzeru idzalowa mu mtima mwako,

kudziwa zinthu kudzakusangalatsa.

11Kuganizira bwino za mʼtsogolo kudzakusunga;

kumvetsa zinthu bwino kudzakuteteza.

12Nzeru idzakupulumutsa ku mayendedwe oyipa,

kwa anthu amabodza,

13amene amasiya njira zolungama

namayenda mʼnjira zamdima,

14amene amakondwera pochita zoyipa

namasangalala ndi kuyipa kwa ntchito zawo zonyansa.

15Amenewa ndi anthu a njira zawo zokhotakhota,

ndipo makhalidwe awo ndi achinyengo.

16Nzeruyo idzakupulumutsanso kwa mkazi wachigololo;

kwa mkazi wachilendo woyankhula moshashalika,

17amene wasiya mwamuna wa chitsikana wake

ndi kuyiwala pangano limene anachita pamaso pa Mulungu wake.

18Pakuti nyumba yake imatsetserekera ku imfa;

njira zake zimamufikitsa ku manda.

19Opita kwa iye palibe ndi mmodzi yemwe amabwerera

kapena kupezanso njira zamoyo.

20Choncho iwe uziyenda mʼnjira za anthu abwino,

uzitsata njira za anthu ochita chilungamo.

21Pakuti anthu olungama ndiwo ati adzakhale mʼdziko

ndipo anthu angwiro ndiwo ati adzakhazikike mʼmenemo;

22Koma anthu oyipa adzachotsedwa mʼdzikomo,

ndipo anthu onyenga adzachotsedwamo.

Kiswahili Contemporary Version (Neno: Bibilia Takatifu)

Mithali 2:1-22

Faida Za Hekima

12:1 Mit 1:8Mwanangu, kama utayakubali maneno yangu

na kuyaweka akiba maagizo yangu ndani mwako,

22:2 Mit 22:17kutega sikio lako kwenye hekima

na kuweka moyo wako katika ufahamu,

32:3 Yak 1:5na kama ukiita busara

na kuita kwa sauti ufahamu,

42:4 Ay 3:21; Mt 13:44; 6:19-21na kama utaitafuta kama fedha

na kuitafuta sana kama hazina iliyofichwa,

52:5 Kum 4:6ndipo utakapoelewa kumcha Bwana

na kupata maarifa ya Mungu.

62:6 Ay 12:13; Lk 21:15; Yak 1:5Kwa maana Bwana hutoa hekima,

na kinywani mwake hutoka maarifa na ufahamu.

72:7 Mwa 6:9; 15:1; Mit 30:5-6; Za 84:11Anahifadhi ushindi kwa ajili ya mwadilifu,

yeye ni ngao kwa wale wasio na lawama,

82:8 1Sam 2:9; Za 18:25kwa kuwa hulinda mwenendo wa mwenye haki

na kuhifadhi njia ya waaminifu wake.

92:9 Kum 1:16Ndipo utafahamu lipi lililo kweli na haki

na sawa: yaani kila njia nzuri.

102:10 Mit 14:33Kwa maana hekima itaingia moyoni mwako,

nayo maarifa yataifurahisha nafsi yako.

112:11 Mit 4:6Busara itakuhifadhi

na ufahamu utakulinda.

122:12 Mit 2:16; 3:13-18; 4:5Hekima itakuokoa kutoka njia za waovu,

kutoka kwa watu ambao maneno yao yamepotoka,

132:13 Mit 4:19; Yn 3:19; Efe 4:18wale waachao mapito yaliyonyooka

wakatembea katika njia za giza,

142:14 Mit 15:21; Yer 11:15wale wapendao kutenda mabaya

na kufurahia upotovu wa ubaya,

152:15 Za 125:5; Mit 21:8ambao mapito yao yamepotoka

na ambao ni wapotovu katika njia zao.

162:16 Mit 6:20-29; 7:5-27Itakuokoa pia kutokana na mwanamke kahaba,

kutokana na mke aliyepotoka mwenye maneno

ya kushawishi kutenda ubaya,

172:17 Mal 2:14; Mwa 2:24aliyemwacha mwenzi wa ujana wake

na kupuuza agano alilofanya mbele ya Mungu.

182:18 Mit 5:5; 7:27; 9:18Kwa maana nyumba yake huelekea kwenye kifo

na mapito yake kwenye roho za waliokufa.

192:19 Mit 5:8; Mhu 7:26; Ebr 13:4Hakuna yeyote aendaye kwake akarudi,

au kufikia mapito ya uzima.

202:20 Ebr 6:12Hivyo utatembea katika njia za watu wema

na kushikamana na mapito ya wenye haki.

212:21 Za 37:29Kwa maana wanyofu wataishi katika nchi,

nao wasio na lawama watabakia ndani yake.

222:22 Ay 18:17; Za 37:38; Kum 29:28Bali waovu watakatiliwa mbali kutoka nchi,

nao wasio waaminifu watangʼolewa kutoka humo.