Mika 1 – CCL & NIRV

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Mika 1:1-16

1Yehova anayankhula ndi Mika wa ku Moreseti pa nthawi ya ulamuliro wa Yotamu, Ahazi ndi Hezekiya, mafumu a ku Yuda. Awa ndi masomphenya amene iye anaona onena za Samariya ndi Yerusalemu.

2Tamverani, inu anthu a mitundu yonse,

mvetsera iwe dziko lapansi ndi okhala mʼmenemo,

pakuti Ambuye Yehova achitira umboni wokutsutsani,

Ambuye akuyankhula ali mʼnyumba yake yopatulika.

Chiweruzo cha Samariya ndi Yerusalemu

3Taonani! Yehova akubwera kuchokera ku malo ake;

Iye akutsika ndipo akuponda pa malo okwera a dziko lapansi.

4Mapiri akusungunuka pansi pake,

ndipo zigwa zikugawikana

ngati phula pa moto,

ngati madzi ochokera mʼphiri.

5Zonsezi ndi chifukwa cha cholakwa cha Yakobo,

chifukwa cha machimo a nyumba ya Israeli.

Kodi cholakwa cha Yakobo nʼchiyani?

Kodi si Samariya?

Kodi malo achipembedzo a Yuda ndi ati?

Kodi si Yerusalemu?

6“Choncho Ine ndidzasandutsa Samariya kukhala bwinja,

malo odzalamo mphesa.

Miyala yake ndidzayitaya ku chigwa

ndipo ndidzafukula maziko ake.

7Mafano ake onse ndidzawaphwanyaphwanya;

mphatso zake zonse ndidzazitentha ndi moto;

ndidzawononga zifanizo zonse za milungu yake.

Popeza analandira mphatso zake kuchokera ku malipiro a akazi achiwerewere,

mphatsozonso zidzagwiritsidwa ntchito ndi ena ngati malipiro a akazi achiwerewere.”

Kulira ndi Kumva Chisoni

8Chifukwa cha zimenezi ine ndidzalira momvetsa chisoni;

ndidzayenda wopanda nsapato ndi wamaliseche.

Ndidzafuwula ngati nkhandwe

ndi kulira ngati kadzidzi.

9Pakuti chilonda cha Samariya nʼchosachizika;

chafika ku Yuda.

Chafika pa chipata chenicheni cha anthu anga,

mpaka mu Yerusalemu mwenimwenimo.

10Musanene zimenezi ku Gati;

musalire nʼkomwe.

Mugubuduzike mu fumbi

ku Beti-Leafura.

11Inu anthu okhala ku Safiro,

muzipita ku ukapolo muli amaliseche ndi amanyazi.

Iwo amene akukhala ku Zanaani

sadzatuluka.

Beti-Ezeli akulira mwachisoni;

chitetezo chake chakuchokerani.

12Anthu amene amakhala ku Maroti akubuwula ndi ululu,

akuyembekezera thandizo,

chifukwa Yehova wabweretsa tsoka,

lafika mpaka pa chipata cha Yerusalemu.

13Inu anthu okhala ku Lakisi

mangani akavalo ku magaleta.

Inu amene munayamba kuchimwitsa

mwana wamkazi wa Ziyoni,

pakuti zolakwa za Israeli

zinapezeka pakati panu.

14Chifukwa chake perekani mphatso zolawirana

ndi a ku Moreseti Gati.

Mzinda wa Akizibu udzaonetsa kunama

kwa mafumu a Israeli.

15Ndidzabweretsa mgonjetsi kudzalimbana ndi inu

okhala mu Maresa.

Ulemerero wa Israeli udzafika

ku Adulamu.

16Metani mipala mitu yanu kuonetsa kuti mukulirira

ana anu amene mumawakonda;

mudzichititse dazi ngati dembo,

pakuti anawo adzatengedwa pakati panu kupita ku ukapolo.

New International Reader’s Version

Micah 1:1-16

1A message from the Lord came to Micah. He was from the town of Moresheth. The message came while Jotham, Ahaz and Hezekiah were kings of Judah. This is the vision Micah saw concerning Samaria and Jerusalem. Here is what he said.

2Listen to me, all you nations!

Earth and everyone who lives in it, pay attention!

The Lord and King will be a witness against you.

The Lord will speak from his holy temple in heaven.

The Lord Will Judge Samaria and Jerusalem

3The Lord is about to come down

from his home in heaven.

He rules over even the highest places on earth.

4The mountains will melt under him

like wax near a fire.

The valleys will be broken apart

by water rushing down a slope.

5All this will happen because

Jacob’s people have done what is wrong.

The people of Israel

have committed many sins.

Who is to blame

for the wrong things Jacob has done?

Samaria!

Who is to blame for the high places

where Judah’s people worship other gods?

Jerusalem!

6So the Lord says,

“I will turn Samaria into a pile of trash.

It will become a place for planting vineyards.

I will dump its stones down into the valley.

And I will destroy it

down to its very foundations.

7All the statues of Samaria’s gods

will be broken to pieces.

All the gifts its people gave to temple prostitutes

will be burned with fire.

I will destroy all the statues of its gods.

Samaria collected gifts that were paid to temple prostitutes.

So the Assyrians will use the gifts

to pay their own temple prostitutes.”

Micah Weeps Over His People

8I will weep and mourn because Samaria will be destroyed.

I’ll walk around barefoot and naked.

I’ll bark like a wild dog.

I’ll hoot like an owl.

9Samaria’s plague can’t be healed.

The plague has spread to Judah.

It has spread right up to the gate of my people.

It has spread to Jerusalem itself.

10Don’t tell the people of Gath about it.

Don’t let them see you weep.

People in Beth Ophrah, roll in the dust.

11You who live in the town of Shaphir,

leave naked and in shame.

Those who live in Zaanan

won’t come out to help you.

The people in Beth Ezel will mourn.

They won’t be able to help keep you safe any longer.

12Those who live in Maroth will groan with pain

as they wait for help.

That’s because the Lord will bring trouble on them.

It will reach the very gate of Jerusalem.

13You who live in Lachish,

get your fast horses ready to pull their chariots.

You trust in military power.

Lachish was where sin began

for the people of Zion.

The wrong things Israel did

were also done by you.

14People of Judah, you might as well say goodbye

to Moresheth near Gath.

The town of Akzib won’t give any help

to the kings of Israel.

15An enemy will attack

you who live in Mareshah.

Israel’s nobles will have to run away

and hide in the cave of Adullam.

16The children you enjoy so much

will be taken away as prisoners.

So shave your heads and mourn.

Make them as bare as the head of a vulture.