Genesis 1 – CCL & NIRV

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Genesis 1:1-31

Chiyambi cha Chilengedwe

1Pachiyambi Mulungu analenga kumwamba ndi dziko lapansi. 2Dziko lapansi linali losakonzedwa ndi lopanda kanthu. Mdima wandiweyani unakuta nyanja ndipo Mzimu wa Mulungu unkayendayenda pamwamba pa madziwo.

3Pamenepo Mulungu anati, “Kuwale” ndipo kunawaladi. 4Mulungu anaona kuti kuwalako kunali bwino ndipo Iye analekanitsa kuwala ndi mdima. 5Mulungu anatcha kuwalako “usana” ndipo mdima anawutcha “usiku.” Ndipo panali madzulo ndiponso mmawa pa tsiku loyamba.

6Kenaka Mulungu anati, “Pakhale thambo pakati pa madzi kuti lilekanitse madzi a mʼmwamba ndi madzi a pansi.” 7Ndipo Mulungu anapanga thambo nalekanitsa madzi amene anali pansi ndi pamwamba pa thambo lija, ndipo zinachitikadi. 8Mulungu anatcha thambo lija “kumwamba.” Ndipo panali madzulo ndiponso mmawa pa tsiku lachiwiri.

9Mulungu anati, “Madzi a pansi pa thambo asonkhane pa malo amodzi kuti mtunda uwoneke,” ndipo zinachitikadi. 10Mulungu anawutcha mtundawo “dziko,” madzi osonkhana pamodziwo anawatcha “nyanja.” Ndipo Mulungu anaona kuti zinali bwino.

11Kenaka Mulungu anati, “Dziko libereke zomera zobala mbewu, mitengo yobala zipatso za mbewu, molingana ndi mitundu yake.” Ndipo zinachitikadi. 12Dziko linabereka zomera zokhala ndi mbewu monga mwa mitundu yake ndi mitengo yokhala ndi zipatso za mbewu mʼkati mwake monga mwa mitundu yake. Ndipo Mulungu anaona kuti zinali bwino. 13Ndipo panali madzulo ndiponso mmawa pa tsiku lachitatu.

14Mulungu anati, “Pakhale zowunikira kuthambo kuti zilekanitse usana ndi usiku. Ndipo zimenezi zikhale zizindikiro zoonetsa nyengo, masiku ndi zaka; 15zikhale kuthambo kuti ziwunikire pa dziko lapansi. Ndipo zinachitikadi.” 16Mulungu anapanga zowunikira zazikulu ziwiri; chachikulu chilamulire usana ndi chachingʼono chilamulire usiku. Iye anapanganso nyenyezi. 17Mulungu anaziyika mlengalenga kuti ziziwunikira pa dziko lapansi, 18kuti zilamulire usana ndi usiku, ndi kuti zilekanitse kuwala ndi mdima. Mulungu anaona kuti zinali bwino. 19Ndipo panali madzulo ndiponso mmawa pa tsiku lachinayi.

20Mulungu anati, “Mʼmadzi mukhale zamoyo zochuluka ndipo mbalame ziwuluke mlengalenga pamwamba pa dziko lapansi.” 21Choncho Mulungu analenga zamoyo zikuluzikulu za mʼnyanja ndi chamoyo chamtundu uliwonse chokhala mʼmadzi ndi mbalame iliyonse ya mapiko monga mwa mtundu wake. Mulungu anaona kuti zinali bwino. 22Mulungu anazidalitsa nati, “Muswane, ndi kudzaza mʼmadzi a mʼnyanja, ndipo mbalame zichuluke pa dziko lapansi.” 23Ndipo panali madzulo ndiponso mmawa pa tsiku lachisanu.

24Kenaka Mulungu anati, “Dziko lapansi litulutse zolengedwa zamoyo monga mwa mitundu yawo: ziweto, zolengedwa zokwawa ndi nyama zakuthengo, iliyonse monga mwa mtundu wake.” Ndipo zinaterodi. 25Mulungu anapanga nyama zakuthengo monga mwa mitundu yawo, nyama zoweta monga mwa mitundu yawo ndi nyama zokwawa monga mwa mitundu yawo. Ndipo Mulungu anaona kuti zinali bwino.

26Zitatha izi Mulungu anati, “Tipange munthu mʼchifanizo chathu, mofanana ndi ife kuti alamulire nsomba za mʼnyanja, mbalame zamlengalenga, nyama zonse zoweta ndi zonse zokwawa za pa dziko lapansi ndi zamoyo zonse zakutchire.”

27Ndipo Mulungu analenga munthu mʼchifanizo chake.

Anawalengadi mʼchifanizo cha Mulungu;

analenga iwo, mwamuna ndi mkazi.

28Mulungu anawadalitsa nati kwa iwo, “Muberekane, muchulukane, mudzaze dziko lapansi ndipo muligonjetse. Mulamulire nsomba zamʼnyanja, mbalame zamlengalenga ndi cholengedwa chamoyo chilichonse chimene chimayenda mokwawa pa dziko lapansi.”

29Kenaka Mulungu anati, “Ine ndakupatsani chomera chilichonse cha pa dziko lapansi chimene chili ndi mbewu komanso mtengo uliwonse wobala zipatso zokhala ndi mbewu mʼkati mwake kuti zikhale chakudya chanu. 30Ndaperekanso msipu kwa nyama zonse za pa dziko lapansi ndi kwa mbalame zamlengalenga ndi kwa cholengedwa chamoyo chilichonse chimene chimakwawa, chilichonse chimene chili ndi moyo.” Ndipo zinachitikadi.

31Mulungu anaona zonse zimene anazilenga kuti zinali zabwino kwambiri. Ndipo panali madzulo ndiponso mmawa, tsiku lachisanu ndi chimodzi.

New International Reader’s Version

Genesis 1:1-31

The Beginning

1In the beginning, God created the heavens and the earth. 2The earth didn’t have any shape. And it was empty. There was darkness over the surface of the waves. At that time, the Spirit of God was hovering over the waters.

3God said, “Let there be light.” And there was light. 4God saw that the light was good. He separated the light from the darkness. 5God called the light “day.” He called the darkness “night.” There was evening, and there was morning. It was day one.

6God said, “Let there be a huge space between the waters. Let it separate water from water.” 7And that’s exactly what happened. God made the huge space between the waters. He separated the water under the space from the water above it. 8God called the huge space “sky.” There was evening, and there was morning. It was day two.

9God said, “Let the water under the sky be gathered into one place. Let dry ground appear.” And that’s exactly what happened. 10God called the dry ground “land.” He called all the water that was gathered together “seas.” And God saw that it was good.

11Then God said, “Let the land produce plants. Let them produce their own seeds. And let there be trees on the land that grow fruit with seeds in it. Let each kind of plant or tree have its own kind of seeds.” And that’s exactly what happened. 12So the land produced plants. Each kind of plant had its own kind of seeds. And the land produced trees that grew fruit with seeds in it. Each kind of tree had its own kind of seeds. God saw that it was good. 13There was evening, and there was morning. It was day three.

14God said, “Let there be lights in the huge space of the sky. Let them separate the day from the night. Let the lights set the times for the holy celebrations and the days and the years. 15Let them be lights in the huge space of the sky to give light on the earth.” And that’s exactly what happened. 16God made two great lights. He made the larger light to rule over the day and the smaller light to rule over the night. He also made the stars. 17God put the lights in the huge space of the sky to give light on the earth. 18He put them there to rule over the day and the night. He put them there to separate light from darkness. God saw that it was good. 19There was evening, and there was morning. It was day four.

20God said, “Let the seas be filled with living things. Let birds fly above the earth across the huge space of the sky.” 21So God created the great sea creatures. He created every kind of living thing that fills the seas and moves about in them. He created every kind of bird that flies. And God saw that it was good. 22God blessed them. He said, “Have little ones so that there will be many of you. Fill the water in the seas. Let there be more and more birds on the earth.” 23There was evening, and there was morning. It was day five.

24God said, “Let the land produce every kind of living creature. Let there be livestock, and creatures that move along the ground, and wild animals.” And that’s exactly what happened. 25God made every kind of wild animal. He made every kind of livestock. He made every kind of creature that moves along the ground. And God saw that it was good.

26Then God said, “Let us make human beings so that they are like us. Let them rule over the fish in the seas and the birds in the sky. Let them rule over the livestock and all the wild animals. And let them rule over all the creatures that move along the ground.”

27So God created human beings in his own likeness.

He created them to be like himself.

He created them as male and female.

28God blessed them. He said to them, “Have children so that there will be many of you. Fill the earth and bring it under your control. Rule over the fish in the seas and the birds in the sky. Rule over every living creature that moves along the ground.”

29Then God said, “I am giving you every plant on the face of the whole earth that produces its own seeds. I am giving you every tree that has fruit with seeds in it. All of them will be given to you for food. 30I am giving every green plant as food for all the land animals and for all the birds in the sky. I am also giving the plants to all the creatures that move along the ground. I am giving them to every living thing that breathes.” And that’s exactly what happened.

31God saw everything he had made. And it was very good. There was evening, and there was morning. It was day six.