Chivumbulutso 1:1-20
Mawu Oyamba
1Vumbulutso lochokera kwa Yesu Khristu, limene Mulungu anamupatsa kuti aonetse atumiki ake zimene zinayenera kuchitika posachedwa. Iye anatuma mngelo wake kuti adziwitse mtumiki wake Yohane, 2amene akuchitira umboni chilichonse chimene anachiona. Awa ndi Mawu a Mulungu ndi umboni wa Yesu Khristu. 3Ngodala munthu amene awerenga mawu oneneratu zamʼtsogolo ndi iwo amene amamva ndi kusunga zolembedwa mʼbukuli pakuti nthawi yayandikira.
Malonje kwa Mipingo Isanu ndi Iwiri
4Ndine Yohane,
Kupita ku mipingo isanu ndi iwiri ya mʼchigawo cha Asiya.
Chisomo ndi mtendere kwa inu, kuchokera kwa Iye amene ali, amene analipo ndi amene akubwera ndi kwa mizimu isanu ndi iwiri yokhala patsogolo pa mpando wake waufumu, 5ndiponso kuchokera kwa Yesu Khristu mboni yokhulupirika, woyamba kuukitsidwa, ndi wolamulira mafumu a dziko lapansi.
Kwa Iye amene amatikonda ndipo watimasula ku machimo athu ndi magazi ake, 6ndipo watisandutsa mafumu ndi ansembe kuti tizitumikira Mulungu ndi Atate ake. Kwa Iye kukhale ulemerero ndi mphamvu ku nthawi zosatha, Ameni.
7“Onani akubwera ndi mitambo,”
ndipo “Aliyense adzamuona,
ndi amene anamubaya omwe.”
Ndipo anthu a mitundu yonse ya pa dziko lapansi “adzalira chingʼangʼadza chifukwa cha Iye.”
Zidzakhaladi momwemo, Ameni.
8“Ine ndine Alefa ndi Omega,” akutero Ambuye Mulungu Wamphamvuzonseyo “amene muli, amene munalipo, ndi amene mudzakhalapo.”
Wina Wokhala ngati Mwana wa Munthu
9Ine Yohane mʼbale wanu ndi mnzanu mʼmasautso ndi mu ufumu ndi mukupirira kwambiri, zomwe ndi zathu mwa Yesu, ndinali pa chilumba cha Patimo chifukwa cha Mawu a Mulungu ndi umboni wa Yesu. 10Pa tsiku la Ambuye ndinanyamulidwa ndi Mzimu ndipo ndinamva kumbuyo kwanga mawu ofuwula ngati lipenga, 11amene anati, “Lemba mʼbuku zimene ukuziona ndipo uzitumize ku mipingo isanu ndi iwiri ya ku Efeso, Simurna, Pergamo, Tiyatira, Sarde, Filadefiya ndi ku Laodikaya.”
12Nditatembenuka kuti ndione amene amandiyankhulayo, ndinaona zoyikapo nyale zisanu ndi ziwiri zagolide. 13Pakati pa zoyikapo nyalezo ndinaona wina wooneka ngati Mwana wa Munthu atavala mkanjo wofika kumapazi ake ndipo anamangirira lamba wagolide pa chifuwa pake. 14Tsitsi lake linali loyera ngati thonje, kuyera ngati matalala, ndipo maso ake amawala ngati malawi amoto. 15Mapazi ake anali ngati chitsulo choti chili mʼngʼanjo yamoto, ndipo mawu ake anali ngati mkokomo wamadzi othamanga. 16Mʼdzanja lake lamanja ananyamula nyenyezi zisanu ndi ziwiri, ndipo mʼkamwa mwake munali lupanga lakuthwa konsekonse. Nkhope yake imawala ngati dzuwa lowala kwambiri.
17Nditamuona ndinagwa pa mapazi ake ngati wakufa. Kenaka Iye anasanjika dzanja lake lamanja pa ine nati, “Usachite mantha. Ndine Woyamba ndi Wotsiriza. 18Ine ndine Wamoyo; ndinali wakufa ndipo taona ndine wamoyo mpaka muyaya! Ndipo ndili ndi makiyi a imfa ndi Hade.
19“Chomwecho, lemba zimene waona, zimene zilipo panopa ndi zimene zidzachitike mʼtsogolo. 20Tanthauzo la nyenyezi zisanu ndi ziwiri zimene waziona mʼdzanja langa lamanja ndi la zoyikapo nyale zagolide zisanu ndi ziwiri ndi ili: Nyenyezi zisanu ndi ziwiri ndi angelo a mipingo isanu ndi iwiri ija, ndipo zoyikapo nyale zisanu ndi ziwiri zija ndi mipingo isanu ndi iwiri ija.”
مکاشفه 1:1-20
مقدمه
1این است مکاشفۀ عیسی مسیح که خدا به او داد تا آنچه را که میبایست به زودی واقع شود، به خادمانش نشان دهد. او فرشتۀ خود را فرستاد تا این مکاشفه را بر خادم خود یوحنا آشکار سازد. 2یوحنا نیز تمام سخنان خدا و عیسی مسیح و هر آنچه را که خود دید و شنید، به نگارش درآورد.
3خوشا به حال کسی که این کلام نبوّت را میخواند و خوشا به حال آنان که به آن گوش فرا میدهند، و آنچه را در آن نوشته شده، نگاه میدارند، زیرا زمان وقوع این رویدادها نزدیک است.
سلام یوحنا بر هفت کلیسا
4از طرف یوحنا، به هفت کلیسا که در ایالت آسیا1:4 ایالت رومی آسیا در ترکیۀ غربی امروزه قرار داشت. هستند. فیض و آرامش بر شما باد، از جانب پروردگاری که هست و بود و میآید، و از جانب روح هفتگانه1:4 یونانی: هفت روح. که در پیشگاه تخت الهی است، 5و از جانب عیسی مسیح که تمام حقیقت را به طور کامل بر ما آشکار میفرماید. مسیح نخستین کسی است که پس از مرگ زنده شد، و برتر از تمام پادشاهان این جهان است.
سپاس و ستایش بر او که ما را محبت مینماید و با خون خود ما را شست و از گناهانمان رهانید؛ 6او ما را در پادشاهی خود، کاهنان منصوب کرده تا خدا یعنی پدر او را خدمت نماییم. او را تا ابد قدرت و جلال باد! آمین.
7بنگرید! او سوار بر ابرها میآید. هر چشمی او را خواهد دید؛ حتی آنانی که به او نیزه زدند، او را خواهند دید؛ و تمام قومهای جهان برای او سوگواری خواهند کرد. بله، آمین! بگذار چنین باشد. 8خدا میفرماید: «من الف و یا هستم. من ابتدا و انتها هستم.» این را خداوندی میفرماید که صاحب تمام قدرتهاست، و هست و بود و میآید.
رویای پسر انسان
9من، یوحنا، که این نامه را برای شما مینویسم، مانند شما در راه خداوند رنج میکشم. اما او به ما صبر و تحمل عطا فرموده و ما را در ملکوت خود سهیم نموده است.
من به علّت اعلام پیغام انجیل و بشارت دربارهٔ عیسی، به جزیرهٔ پطموس تبعید شدم. 10در روزِ خداوند، روح خدا مرا فرو گرفت1:10 یونانی: در روح شدم.. ناگهان از پشت سر خود، صدایی بلند همچون صدای شیپور شنیدم، 11که میگفت: «من الف و یا هستم. من ابتدا و انتها هستم. هر چه میبینی، در نامهای بنویس و آن را برای هفت کلیسا بفرست، یعنی برای کلیساهای اَفِسُس، اِسمیرنا، پِرگاموم، تیاتیرا، ساردِس، فیلادِلفیه و لائودیکیه.»
12هنگامی که برگشتم تا کسی را که با من سخن میگفت ببینم، در پشت سر خود هفت شمعدان طلا دیدم. 13در میان شمعدانها، مردی را دیدم شبیه پسر انسان1:13 عیسی لقب «پسر انسان» را برای خودش به کار میبرد. دانیال ۷:۱۳. که ردایی بلند بر تن داشت و کمربندی طلایی دور سینهاش بود. 14سر و موی او سفید بود چون برف و پشم، و چشمانش تیز و نافذ بود همچون شعلههای آتش. 15پاهای او میدرخشید، مانند مسی که در کورۀ آتش صیقل داده باشند. صدای او مثل آبشار طنینافکن بود. 16در دست راست او، هفت ستاره بود، و شمشیر دو دمِ تیزی هم در دهانش قرار داشت. صورت او همچون خورشید بود در درخشش کاملش.
17-18وقتی چشمم به او افتاد، مانند مرده جلوی پای او افتادم. اما او دست راست خود را بر من گذاشت و فرمود: «نترس! من ابتدا و انتها هستم! من زنده بودم و مُردم، و حال تا به ابد زندهام، و کلیدهای مرگ و عالم مردگان را در دست دارم.
19«پس آنچه دیدهای، یعنی آنچه الان در حال وقوع است و آنچه از این پس خواهد شد، همه را بنویس. 20معنی هفت ستارهای که در دست راست من دیدی و همچنین هفت شمعدان طلا این است: هفت ستاره، فرشتگان1:20 یا: پیامآوران. هفت کلیسا هستند، و هفت شمعدان، خود هفت کلیسا میباشند.