Kuchita Zabwino kwa Onse
1Abale, ngati munthu agwa mʼtchimo lililonse, inu amene Mzimu amakutsogolerani, mumuthandize munthuyo ndi mtima wofatsa kuti akonzekenso. Koma mukhale maso kuti inu nomwe mungayesedwe. 2Thandizanani kusenza zolemetsa zanu, ndipo mʼnjira imeneyi mudzakwanitsa lamulo la Khristu. 3Ngati wina adziyesa kanthu pamene iyeyo sali kanthu konse, akudzinamiza yekha. 4Munthu aliyense aziyesa yekha ntchito zake mmene zilili. Ngati zili bwino, adzatha kunyadira chifukwa cha ntchito zake zokhazo, iyeyo asadzifanizire ndi munthu wina wake, 5pakuti aliyense ayenera kusenza katundu wake.
6Koma munthu amene akuphunzira mawu, agawireko mphunzitsi wake zinthu zonse zabwino zimene iye ali nazo.
7Musanamizidwe: nʼkosatheka kupusitsa Mulungu. Munthu amakolola zimene wafesa. 8Pakuti amene amafesa zokondweretsa thupi lake la uchimo, kuchokera ku khalidwe limenelo adzakolola chiwonongeko; amene amafesa zokondweretsa Mzimu, kuchokera kwa Mzimu adzakolola moyo wosatha. 9Tisatope nʼkuchita zabwino, pakuti pa nthawi yoyenera tidzakolola ngati sititopa. 10Nʼchifukwa chake ngati tapeza mpata, tiyenera kuchitira zabwino anthu onse, makamaka amene ndi a banja la okhulupirira.
Osati Mdulidwe koma Kulengedwa Mwatsopano
11Onani zilembo zazikulu zimene ine ndikulemba ndi dzanja langa.
12Onse amene akufuna kuoneka abwino pamaso pa anthu akukukakamizani kuti muchite mdulidwe. Akuchita izi ndi cholinga chimodzi chokha, chakuti apewe kuzunzidwa chifukwa cha mtanda wa Khristu. 13Pakuti ngakhale iwowa amene anachita mdulidwe satsata Malamulo, komabe akufuna kuti muchite mdulidwe kuti anyadire mdulidwe wanuwo. 14Ine sindingathe kunyadira kanthu kena koma mtanda wa Ambuye athu Yesu Khristu, kudzera mwa mtandawo dziko lapansi linapachikidwa kwa ine ndi ine ku dziko lapansi. 15Pakuti kaya mdulidwe kapena kusachita mdulidwe, sizitanthauza kanthu; chofunika ndi kulengedwa mwatsopano. 16Mtendere ndi chifundo zikhale kwa onse amene amatsata chiphunzitso ichi, ndi pa Israeli wa Mulungu.
17Pomaliza wina asandivutitse, pakuti mʼthupi mwanga muli zizindikiro za Yesu.
18Chisomo cha Ambuye athu Yesu Khristu zikhale ndi mzimu wanu abale. Ameni.
Do Good to Everyone
1Brothers and sisters, what if someone is caught in a sin? Then you who live by the Spirit should correct that person. Do it in a gentle way. But be careful. You could be tempted too. 2Carry one another’s heavy loads. If you do, you will fulfill the law of Christ. 3If anyone thinks they are somebody when they are nobody, they are fooling themselves. 4Each person should test their own actions. Then they can take pride in themselves. They won’t be comparing themselves to someone else. 5Each person should carry their own load. 6But those who are taught the word should share all good things with their teacher.
7Don’t be fooled. You can’t outsmart God. A man gathers a crop from what he plants. 8Some people plant to please their desires controlled by sin. From these desires they will harvest death. Others plant to please the Holy Spirit. From the Spirit they will harvest eternal life. 9Let us not become tired of doing good. At the right time we will gather a crop if we don’t give up. 10So when we can do good to everyone, let us do it. Let’s try even harder to do good to the family of believers.
Not Circumcision but the New Creation
11Look at the big letters I’m using as I write to you with my own hand!
12Some people are worried about how things look on the outside. They are trying to force you to be circumcised. They do it for only one reason. They don’t want to suffer by being connected with the cross of Christ. 13Even those who are circumcised don’t obey the law. But they want you to be circumcised. Then they can brag about what has been done to your body. 14I never want to brag about anything except the cross of our Lord Jesus Christ. Through that cross the ways of the world have been crucified as far as I am concerned. And I have been crucified as far as the ways of the world are concerned. 15Circumcision and uncircumcision don’t mean anything. What really counts is that the new creation has come. 16May peace and mercy be given to all who follow this rule. May peace and mercy be given to the Israel that belongs to God.
17From now on, let no one cause trouble for me. My body has marks that show I belong to Jesus.
18Brothers and sisters, may the grace of our Lord Jesus Christ be with your spirit. Amen.