1 Yohane 2 – CCL & PCB

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

1 Yohane 2:1-29

1Inu Ana anga okondedwa, ndikukulemberani zimenezi kuti musachimwe. Koma wina akachimwa, tili nayo Nkhoswe yotinenera kwa Atate, Yesu Khristu, Wolungamayo. 2Iyeyo ndiye nsembe yopepesera machimo athu, ndipo osati athu okha, komanso machimo onse a dziko lapansi.

Chikondi ndi Chidani

3Ife timatsimikiza kuti tikumudziwa ngati tikusunga malamulo ake. 4Munthu akamanena kuti, “Ine ndimadziwa Mulungu,” koma samvera malamulo a Mulunguyo, ndi wabodza ameneyo ndipo mwa iye mulibe choonadi. 5Koma munthu aliyense akamvera mawu ake, ndiye kuti chikondi cha Mulungu chafikadi penipeni mwa iyeyo. Pamenepo timatsimikizadi kuti tili mwa Iye. 6Aliyense amene amati amakhala mwa Mulungu, ayenera kukhala moyo umene Yesu ankakhala.

7Okondedwa, sindikukulemberani lamulo latsopano koma lakale lomwe lija, limene munali nalo kuyambira pachiyambi. Lamulo la kalelo ndi mawu amene munawamva kale. 8Komabe ndi lamulo latsopano limene ndikukulemberani. Choonadi chake chikuoneka mwa Yesu ndiponso mwa inu, chifukwa mdima ukutha ndipo kuwunika kwenikweni kwayamba kale kuwala.

9Aliyense amene amati ali mʼkuwunika, koma nʼkumadana ndi mʼbale wake ali mu mdima. 10Aliyense amene amakonda mʼbale wake amakhalanso mʼkuwunika, ndipo mwa iye mulibe chokhumudwitsa. 11Koma aliyense wodana ndi mʼbale wake ali mu mdima ndipo akuyenda mu mdima. Iyeyo sakudziwa kumene akupita, chifukwa mdima wamudetsa mʼmaso mwake.

12Inu ana okondedwa, ndikukulemberani

popeza kuti machimo anu akhululukidwa chifukwa cha dzina la Yesu.

13Inu abambo, ndikukulemberani

popeza kuti munamudziwa Iye amene analipo kuyambira pachiyambi.

Inu anyamata, ndikukulemberani

popeza kuti munagonjetsa woyipayo.

14Ana okondedwa, ndikukulemberani

chifukwa mumawadziwa Atate.

Abambo, ndikukulemberani

chifukwa munamudziwa Iye amene analipo kuyambira pachiyambi.

Inu anyamata, ndikukulemberani

chifukwa ndinu amphamvu.

Mawu a Mulungu amakhala mwa inu

ndipo mumamugonjetsa woyipayo.

Musakonde Dziko Lapansi

15Musamakonde dziko lapansi kapena chilichonse cha dziko lapansi. Ngati munthu wina aliyense akonda dziko lapansi, mwa iyeyo mulibe chikondi chokonda Atate. 16Pakuti zonse za mʼdziko lapansi, zilakolako za thupi, zinthu zimene maso amakhumbira ndiponso kuyandikira zinthu za moyo uno, zonsezi sizichokera kwa Atate, koma ku dziko lapansi. 17Dziko lapansi likupita pamodzi ndi zilakolako zake, koma amene amachita chifuniro cha Mulungu amakhalapo mpaka muyaya.

Anthu Okana Khristu

18Ana anga, ino ndi nthawi yotsiriza, ndipo monga munamva kale kuti anthu okana Khristu akubwera, ngakhale tsopano okana Khristu ambiri afika kale. Zimenezi zikutisonyeza kuti ino ndi nthawi yotsiriza. 19Anthu amenewa anachoka pakati pathu, komatu sanali a mʼgulu lathu. Pakuti akanakhala a mʼgulu lathu, akanakhalabe nafe, koma kuchoka kwawo kunatisonyeza kuti sanali a mʼgulu lathu.

20Koma inu muli ndi kudzoza kochokera kwa Woyerayo, ndipo nonsenu mukudziwa choonadi. 21Sindikukulemberani chifukwa choti simudziwa choonadi ayi, koma chifukwa choti mumadziwa choonadicho, ndipo mukudziwanso kuti bodza silichokera pa choonadi. 22Wabodzayo ndani? Ndi munthu aliyense amene amanena kuti Yesu si Mpulumutsi. Munthu woteroyo ndi wokana Khristu, ndiponso amakana Atate, ndi Mwana. 23Aliyense wokana Mwana alibenso Atate. Wovomereza Mwana alinso ndi Atate.

24Onetsetsani kuti zimene munazimva kuyambira pachiyambi zikhalebe mwa inu. Ngati zikhala mwa inu, inunso mudzakhala mwa Mwana ndiponso mwa Atate. 25Ndipo chimene anatilonjeza nʼchimenechi: moyo wosatha.

26Ine ndikukulemberani zimenezi kuti ndikuwuzeni za amene akufuna kukusocheretsani. 27Koma za inu, kudzoza kumene munalandira kwa Khristu kuli mwa inu, ndipo sipafunika wina aliyense kuti akuphunzitseni. Koma kudzozako kumakuphunzitsani zinthu zonse, ndipo popeza kudzoza kwakeko nʼkoona osati konama, monga munaphunzira, khalani mwa Iyeyo.

Ana a Mulungu

28Tsopano ana okondedwa, khalani mwa Yesu, kuti pamene adzaonekera, ife tidzakhale otsimikizika mu mtima ndi wopanda manyazi pamaso pake akamadzabwera.

29Popeza mukudziwa kuti Khristu ndi wolungama, choncho mukudziwanso kuti aliyense amene amachita chilungamo ndi mwana wa Mulungu.

Persian Contemporary Bible

اول يوحنا 2:1-29

1فرزندان عزيزم، اينها را به شما می‌نويسم تا گناه نكنيد. اما اگر گناهی از شما سر زند، كسی هست كه برای ما نزد خدای پدر وساطت كند و بخشايش ما را از او درخواست نمايد. اين شخص عيسی مسيح است كه مظهر راستی و عدالت است. 2او كسی است كه تاوان گناهان ما را داده تا خدا ما را هلاک نسازد؛ او با اين كار، رابطه‌ای دوستانه ميان خدا و ما بوجود آورده است. او نه فقط برای گناهان ما، بلكه برای گناهان تمام مردم جهان فدا شد.

3چگونه می‌توانيم مطمئن باشيم كه خدا را می‌شناسيم؟ راهش اينست كه به قلب خود نگاه كنيم و ببينيم كه آيا مايل هستيم احكام خدا را بجا بياوريم. 4كسی كه می‌گويد خدا را می‌شناسد اما احكام خدا را نگاه نمی‌دارد و خواست او را بجا نمی‌آورد، دروغ می‌گويد و از حقيقت به دور است. 5فقط كسی می‌تواند واقعاً خدا را بشناسد و با او رابطهٔ نزديک داشته باشد كه او را هر روز بيشتر دوست داشته، كلام او را بجا آورد. 6كسی كه ادعا می‌كند مسيحی است، بايد مانند مسيح زندگی كند.

حکمی تازه

7ای برادران، به شما می‌گويم كه يكديگر را محبت نماييد. اين يک حكم تازه نيست، بلكه همان حكم قديمی است كه از ابتدا به شما داده شده و همهٔ شما آن را شنيده‌ايد. 8با اين حال هميشه تازه است، و همانگونه كه مسيح به آن عمل كرد، شما نيز بايد چنين كنيد، زيرا در همان حال كه به يكديگر محبت می‌نماييد، لكه‌های تيره و تار زندگی از ميان می‌رود، و نور تازهٔ زندگی مسيحايی شروع به تابيدن می‌كند.

9كسی كه می‌گويد: «من در نور مسيح هستم»، ولی همنوع خود را دوست نمی‌دارد، هنوز در تاريكی است. 10اما هر كه همنوع خود را محبت نمايد، در نور زندگی می‌كند و می‌تواند راه خود را ببيند، بدون آنكه گرفتار تاريكی و گناه گردد. 11ولی كسی كه همنوع خود را دوست ندارد، در تاريكی سرگردان است و نمی‌داند به كجا می‌رود، زيرا تاريكی چشمانش را كور كرده است تا راه را نبيند.

12ای فرزندان، اين چيزها را برای شما می‌نويسم، زيرا گناهانتان به خاطر نام عيسی مسيح آمرزيده شده است. 13ای پدران، اين مطالب را به شما نيز می‌نويسم، زيرا مسيح را كه از ازل بوده است، می‌شناسيد. ای جوانان، روی سخنم با شما نيز هست، زيرا در نبرد روحانی، بر شيطان پيروز شده‌ايد. به شما خردسالان نيز می‌نويسم، كه پدرمان خدا را می‌شناسيد.

14پس اين را می‌خواهم بگويم به شما پدرانی كه خدای ازلی را می‌شناسيد، و به شما جوانانی كه كلام خدا را در دل خود حفظ می‌كنيد و قوی هستيد و بر شيطان پيروز شده‌ايد؛ 15به اين دنيای گناه‌آلود و به آنچه به آن تعلق دارد، دل نبنديد. كسی كه به اين چيزها دل ببندد، در واقع نشان می‌دهد كه به خدا دلبستگی ندارد. 16زيرا وابستگی‌های اين دنيا و خواسته‌های ناپاک، ميل به داشتن و تصاحب هر آنچه كه به نظر جالب می‌آيد، و غرور ناشی از ثروت و مقام، هيچيک از خدا نيست؛ بلكه از اين دنيای گناه‌آلود می‌باشد. 17دنيا نابود خواهد شد و چيزهای گناه‌آلود آن نيز از بين خواهند رفت، اما هر كه طبق خواست خدا زندگی كند، هميشه برقرار خواهد ماند.

18فرزندان عزيزم، پايان دنيا نزديک شده است. شما حتماً دربارهٔ ظهور دَجّال كه دشمن مسيح است چيزهايی شنيده‌ايد. حتی الان نيز مخالفين مسيح همه جا ديده می‌شوند، و از همين متوجه می‌شويم كه پايان دنيا نزديک شده است. 19اين مخالفين مسيح بين ما بودند، اما در واقع از ما نبودند، چه در غير اين صورت نزد ما می‌ماندند. وقتی از ما جدا شدند، معلوم شد كه اصلاً از ما نبودند.

20اما شما مانند اينها نيستيد، زيرا روح‌القدس بر شما قرار گرفته و حقيقت را می‌دانيد. 21اگر اين چيزها را می‌نويسم، منظورم اين نيست كه حقيقت را نمی‌دانيد، بلكه فقط می‌خواهم به شما هشدار داده باشم، زيرا شما فرق ميان راست و دروغ را تشخيص می‌دهيد.

22دروغگوی واقعی كيست؟ هر كه بگويد عيسی همان مسيح نيست، دروغگوست؛ او همان دَجّال است، زيرا نه به خدای پدر ايمان دارد و نه به فرزند خدا. 23كسی كه به عيسی مسيح، فرزند خدا، ايمان نداشته باشد، امكان ندارد بتواند خدای پدر را بشناسد. اما كسی كه به فرزند خدا ايمان دارد، خدای پدر را نيز می‌شناسد.

24ايمان خود را به آنچه كه از اول شنيديد، حفظ نماييد زيرا اگر چنين كنيد، هميشه با خدای پدر و فرزندش، رابطه‌ای نزديک خواهيد داشت، 25و زندگی جاويد كه او وعده داده است، نصيب شما خواهد شد.

26اين مطالب را دربارهٔ اين اشخاص می‌نويسم تا بدانيد كه ايشان می‌خواهند شما را گمراه كنند. 27اما می‌دانم كه روح خدا در شماست و به همين جهت نيازی نداريد كسی به شما بياموزد كه چه بكنيد، زيرا روح خدا همه چيز را به شما تعليم خواهد داد؛ هر چه او می‌گويد حقيقت محض است و دروغ در آن يافت نمی‌شود. پس، همانگونه كه به شما تعليم داده است، هميشه در مسيح بمانيد و هرگز از او دور نشويد.

28بلی فرزندان من، بكوشيد تا با مسيح رابطه‌ای صميمی داشته باشيد، تا به هنگام بازگشت او، بتوانيم با اطمينان او را استقبال كنيم، نه با ترس و خجالت. 29همهٔ شما به خوبی می‌دانيد كه خدا به طور مطلق نيک است. پس اين را نيز بدانيد كه هر كه نيكی می‌كند، فرزند خداست.