Psalm 121 – NIRV & CCL

New International Reader’s Version

Psalm 121:1-8

Psalm 121

A song for those who go up to Jerusalem to worship the Lord.

1I look up to the mountains.

Where does my help come from?

2My help comes from the Lord.

He is the Maker of heaven and earth.

3He won’t let your foot slip.

He who watches over you won’t get tired.

4In fact, he who watches over Israel

won’t get tired or go to sleep.

5The Lord watches over you.

The Lord is like a shade tree at your right hand.

6The sun won’t harm you during the day.

The moon won’t harm you during the night.

7The Lord will keep you from every kind of harm.

He will watch over your life.

8The Lord will watch over your life no matter where you go,

both now and forever.

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 121:1-8

Salimo 121

Nyimbo yoyimba pokwera ku Yerusalemu.

1Ndikweza maso anga ku mapiri;

kodi thandizo langa limachokera kuti?

2Thandizo langa limachokera kwa Yehova,

wolenga kumwamba ndi dziko lapansi.

3Sadzalola kuti phazi lako literereke;

Iye amene amakusunga sadzawodzera.

4Taonani, Iye amene amasunga Israeli

sadzawodzera kapena kugona.

5Yehova ndiye amene amakusunga;

Yehova ndiye mthunzi wako ku dzanja lako lamanja.

6Dzuwa silidzakupweteka nthawi ya masana,

kapena mwezi nthawi ya usiku.

7Yehova adzakuteteza ku zoyipa zonse;

adzasunga moyo wako.

8Yehova adzayangʼanira kutuluka kwako ndi kulowa kwako;

kuyambira tsopano mpaka muyaya.