Isaya 22 – NEN & CCL

Kiswahili Contemporary Version (Neno: Bibilia Takatifu)

Isaya 22:1-25

Unabii Kuhusu Yerusalemu

122:1 Za 125:2; Yoe 3:2-14; Yos 2:8; Isa 13:1; Yer 48:38; 21:13Neno kuhusu Bonde la Maono:

Nini kinachokutaabisha sasa,

kwamba ninyi nyote mmepanda juu ya mapaa?

222:2 Isa 5:14; 32:13; Eze 22:5; Isa 21:5; 10:4; 2Fal 25:3Ewe mji uliojaa ghasia,

ewe mji wa makelele na sherehe!

Watu wenu waliokufa hawakuuawa kwa upanga,

wala hawakufa vitani.

322:3 Isa 13:14; 2Fal 25:6Viongozi wako wote wamekimbia pamoja,

wamekamatwa bila kutumia upinde.

Ninyi nyote mliokamatwa mlichukuliwa wafungwa pamoja,

mlikimbia wakati adui alipokuwa bado mbali.

422:4 Mao 1:16; Lk 19:41; Yer 9:1; Eze 21:6; Isa 15:3; Lk 19:41Kwa hiyo nilisema, “Geukia mbali nami,

niache nilie kwa uchungu.

Usijaribu kunifariji

juu ya maangamizi ya watu wangu.”

522:5 Amo 5:18-20; Es 3:15; Sef 1:15; Isa 2:12; Ay 40:12; 2Sam 22:43; Eze 8:17-18; 13:14; Mao 1:5Bwana, Bwana Mwenye Nguvu Zote, anayo siku

ya ghasia, ya kukanyaga, na ya kuogofya

katika Bonde la Maono,

siku ya kuangusha kuta

na ya kupiga kelele mpaka milimani.

622:6 Isa 21:2; 2Fal 16:9; Yer 51:56; 49:35; Za 46:9Elamu analichukua podo,

pamoja na waendesha magari ya vita na farasi.

Kiri anaifungua ngao.

722:7 Yos 15:18; 2Nya 32:1-2Mabonde yako yaliyo mazuri sana yamejaa magari ya vita,

nao wapanda farasi wamewekwa kwenye malango ya mji;

822:8 2Nya 32:5; 1Fal 7:2; Isa 2:12ulinzi wa Yuda umeondolewa.

Nawe ulitazama siku ile

silaha katika Jumba la Kifalme la Mwituni,

922:9 2Fal 18:17; 2Nya 32:4-5; Wim 4:4; 2Fal 20:20mkaona kuwa Mji wa Daudi

una matundu mengi katika ulinzi wake,

mkaweka akiba ya maji

kwenye Bwawa la Chini.

1022:10 Yer 33:4; 2Nya 32:15; 32:5; Yer 33:4Mlihesabu majengo katika Yerusalemu

nanyi mkabomoa nyumba ili kuimarisha ukuta.

1122:11 Yer 39:4; Neh 3:16; 2Fal 25:4; 19:25; 1Sam 12:24Mlijenga bwawa la maji katikati ya kuta mbili

kwa ajili ya maji ya Bwawa la Zamani,

lakini hamkumtazama Yule aliyelitengeneza,

au kuwa na heshima kwa Yule aliyeubuni tangu zamani za kale.

1222:12 Yoe 2:17; Law 13:40; Mik 1:16; Isa 3:24; Yoe 1:9-13Bwana, Bwana Mwenye Nguvu Zote,

aliwaita siku ile

ili kulia na kuomboleza,

kungʼoa nywele zenu na kuvaa nguo ya gunia.

1322:13 Mhu 8:15; Isa 5:12; 21:5; Lk 17:26-29; 1Kor 15:32; 1Sam 25:36; Isa 28:7-8Lakini tazama, kuna furaha na sherehe,

kuchinja ngʼombe na kuchinja kondoo,

kula nyama na kunywa mvinyo!

Mnasema, “Tuleni na kunywa,

kwa kuwa kesho tutakufa!”

1422:14 Eze 24:13; Isa 5:9; 1Sam 2:25; Isa 13:11; 30:13-14; 1Sam 3:14Bwana Mwenye Nguvu Zote amelifunua hili nikiwa ninasikia: Bwana, Bwana Mwenye Nguvu Zote, asema: “Mpaka siku ya kufa kwenu, dhambi hii haitafanyiwa upatanisho.”

1522:15 2Fal 6:30; 18:18; Mwa 41:40; Isa 36:3; 1Fal 4:6Hili ndilo Bwana, Bwana Mwenye Nguvu Zote, asemalo:

“Nenda ukamwambie huyu wakili Shebna,

ambaye ni msimamizi wa jumba la kifalme:

1622:16 Mt 27:60; Hes 32:42Unafanya nini hapa, na ni nani aliyekupa ruhusa

kujikatia kaburi lako mwenyewe,

ukichonga kaburi lako mahali palipo juu,

na kutoboa kwa patasi mahali pako pa kupumzikia katika mwamba?

1722:17 Yer 10:18; 13:18; 22:26“Jihadhari, Bwana yu karibu kukukamata thabiti,

na kukutupa mbali, ewe mtu mwenye nguvu.

1822:18 Ay 18:11; Isa 14:19; Mwa 41:43Atakuvingirisha uwe kama mpira

na kukutupa katika nchi kubwa.

Huko ndiko utakakofia,

na huko ndiko magari yako ya vita ya fahari yatabakia,

wewe unayeifedhehesha nyumba ya bwana wako!

1922:19 Za 52:5; Lk 16:3Nitakuondoa kutoka kazi yako,

nawe utaondoshwa kutoka nafasi yako.

2022:20 2Fal 18:18“Katika siku ile, nitamwita mtumishi wangu, Eliakimu mwana wa Hilkia. 2122:21 Ay 29:16Nitamvika joho lako, nami nitamfunga mshipi wako kiunoni mwake, na kumkabidhi mamlaka yako. Yeye atakuwa baba kwa wale wanaoishi Yerusalemu na kwa nyumba ya Yuda. 2222:22 1Nya 9:27; Mt 16:19; Ay 12:14; Ufu 3:7; Isa 7:2Nitaweka mabegani mwake ufunguo wa nyumba ya Daudi. Kile afunguacho hakuna awezaye kufunga, na kile afungacho hakuna awezaye kufungua. 2322:23 Eze 15:3; Zek 10:4; Ezr 9:8; Ay 6:25; 1Sam 2:7-8; Ay 36:7Nitamgongomea kama kigingi kilicho mahali palipo imara, naye atakuwa kiti cha enzi cha heshima kwa ajili ya nyumba ya baba yake. 24Utukufu wote wa jamaa yake utakuwa juu yake: Watoto wa jamaa hiyo na machipukizi yake, vyombo vyake vyote vidogo, tangu bakuli hadi magudulia yote.”

2522:25 Isa 46:11; Mik 4:4Bwana Mwenye Nguvu Zote asema, “Katika siku ile, kigingi kilichogongomewa mahali imara kitaachia njia. Kitakatwa, nacho kitaanguka na mzigo ulioningʼinia juu yake utaanguka chini.” Bwana amesema.

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Yesaya 22:1-25

Za Chilango cha Yerusalemu

1Uthenga wonena za Chigwa cha Masomphenya:

Kodi chachitika nʼchiyani,

kuti nonsenu mukwere pa madenga?

2Iwe mzinda wodzaza ndi chisangalalo chodzaza tsaya,

iwe mzinda waphokoso ndi wosokonekera?

Anthu ako ophedwa aja sanaphedwe ndi lupanga,

kapena kufera pa nkhondo.

3Atsogoleri ako onse ngakhale anathawa limodzi;

koma anagwidwa osadziteteza nʼkomwe.

Inu munapezeka ndipo nonse pamodzi munatengedwa ukapolo,

ngakhale munathawa pamene mdani akanali patali.

4Nʼchifukwa chake Ine ndinati, “Chokani pamaso panga;

ndilekeni ndilire ndi mtima wowawa.

Musayesere kunditonthoza

chifukwa cha kuwonongeka kwa anthu anga.”

5Lero Ambuye Yehova Wamphamvuzonse walola kuti tione

mavuto ndi kugonjetsedwa ndiponso chisokonezo

mʼChigwa cha Masomphenya.

Malinga agumuka,

komanso anthu akanalira mofuwula ku mapiri.

6Ankhondo a ku Elamu anadza pa magaleta

ndi akavalo ali ndi mivi mʼmanja.

Ankhondo a ku Kiri anakonzeka ndi zishango.

7Zigwa zanu zachonde ndi zodzaza ndi magaleta,

ndipo asilikali okwera pa akavalo ayikidwa pa zipata za mzinda;

8zonse zoteteza Yuda zachotsedwa.

Ndipo tsiku limenelo munayangʼanayangʼana

zida zankhondo zomwe zinali mʼnyumba yaufumu ya nkhalango;

9inu munaona kuti makoma ambiri a mzinda wa Davide

anali ndi malo ambiri ogumuka;

munasunga madzi

mu chidziwe chakumunsi.

10Munawerenga nyumba zonse za mu Yerusalemu

ndipo munagwetsa nyumba zina kuti mulimbitse linga logumuka lija.

11Pakati pa makoma awiri munamanga chitsime

chosungiramo madzi ochokera ku dziwe lakale,

koma inu simunadalire Mulungu amene anapanga zimenezi,

kapena kusamalako za Iye amene anazilenga kale lomwe.

12Pa tsiku limenelo, Ambuye Yehova Wamphamvuzonse

anakuyitanani kuti mulire ndi kukhetsa misozi;

kumeta mutu wanu mpala

ndi kuvala ziguduli.

13Koma mʼmalo mwake inu munakondwa ndi kusangalala;

munapha ngʼombe ndi nkhosa;

munadya nyama ndi kumwa vinyo.

Inu mumati, “Tiyeni tidye ndi kumwa

pakuti mawa tifa!”

14Yehova Wamphamvuzonse wandiwululira mondinongʼoneza kuti, “Tchimo limeneli sindidzakhululuka mpaka tsiku la kufa kwanu,” akutero Ambuye, Yehova Wamphamvuzonse.

15Chimene Ambuye, Yehova Wamphamvuzonse akuti,

“Pita, ukanene kwa Sabina kapitawo,

amene amayangʼanira nyumba yaufumu:

16Kodi ukuchita chiyani kuno, nanga ndani anakupatsa chilolezo

kuti udzikumbire manda kuno,

kudzikumbira manda pa phiri

ndi kudzisemera malo opumulira mʼthanthwe?

17“Samalira, Yehova watsala pangʼono kukugwira zolimba

ndi kukuponya mwamphamvu, iwe munthu wamphamvu.

18Iye adzakukulunga kwambiri ngati mpira

ndipo adzakuponyera mʼdziko lalikulu.

Kumeneko ndiko ukafere

ndipo kumeneko ndiko kudzatsalire magaleta ako.

Ndipo udzasanduka wochititsa manyazi nyumba ya mbuye wako.

19Ine ndidzakuchotsa pa ukapitawo wako

ndipo ndidzakutsitsa pa udindo wako.

20“Tsiku limenelo ndidzayitanitsa mtumiki wanga, Eliyakimu mwana wa Hilikiya. 21Ndidzamuveka mkanjo wako ndi kumangira lamba wako mʼchiwuno mwake ndi kumupatsa ulamuliro wako. Iye adzakhala kholo la amene amakhala mu Yerusalemu ndiponso a fuko la Yuda. 22Ndidzamupatsa ulamuliro wa banja la Davide. Adzatsekula ndipo palibe adzatseke, adzatseka popanda wina kutsekula. 23Ufumu wake udzakhala wokhazikika ngati chikhomo chokhomedwa pa malo olimba. Anthu adzalemekeza nyumba ya abale ake chifukwa cha iye. 24Ana ndi abale a nyumba ya abambo ake adzakhala ngati katundu pa iye ngati ziwiya zopanda ntchito zimene zapachikidwa pa chikhomo.

25“Yehova Wamphamvuzonse akunena kuti, ‘Tsiku limeneli chikhomo chokhomedwa kwambiri chija sichidzalimbanso; chidzazuka ndipo chidzagwa ndipo zonse zopachikidwa zidzawonongedwa.’ ” Yehova wayankhula chomwechi.