Yeremia 1 – NEN & CCL

Kiswahili Contemporary Version (Neno: Bibilia Takatifu)

Yeremia 1:1-19

11:1 Yos 21:18; Yer 32:7-9Maneno ya Yeremia mwana wa Hilkia, mmoja wa makuhani katika mji wa Anathothi, katika nchi ya Benyamini. 2Neno la Bwana lilimjia katika mwaka wa kumi na tatu wa utawala wa Yosia mwana wa Amoni mfalme wa Yuda, 31:3 2Fal 24:17; Yer 29:2; 52:15; Ezr 5:12; 2Fal 23:34na pia wakati wa utawala wa Yehoyakimu mwana wa Yosia mfalme wa Yuda, mpaka mwezi wa tano wa mwaka wa kumi na moja wa utawala wa Sedekia mwana wa Yosia mfalme wa Yuda, wakati watu wa Yerusalemu walipopelekwa uhamishoni.

Wito Wa Yeremia

4Neno la Bwana lilinijia, kusema,

51:5 Yer 25:15-26; Za 139:13-16; Yn 10:36“Kabla sijakuumba ndani ya tumbo la mama yako, nilikujua;

kabla hujazaliwa nilikutenga kwa kazi maalum;

nilikuweka uwe nabii kwa mataifa.”

61:6 Kut 3:11; 4:10; 6:12; 1Fal 3:7Nami nikasema, “Aa, Bwana Mwenyezi, sijui kusema, kwani mimi ni mtoto mdogo tu.”

7Lakini Bwana akaniambia, “Usiseme, ‘Mimi ni mtoto mdogo tu.’ Utaenda popote nitakapokutuma na kunena lolote nitakalokuagiza. 81:8 Mwa 8:1; Kut 3:12; Eze 2:6; Yer 15:20; Hes 22:20; Mwa 26:3; Yer 26:24Usiwaogope, kwa maana niko pamoja nawe nikuokoe,” asema Bwana.

91:9 Isa 6:7; Kut 4:12Kisha Bwana akaunyoosha mkono wake na kugusa kinywa changu, akaniambia, “Sasa nimeyaweka maneno yangu kinywani mwako. 101:10 Yer 25:15; 18:7-10; 31:4, 28; 12:17; 24:6Tazama, leo nimekuweka juu ya mataifa na falme ili kungʼoa na kubomoa, kuharibu na kuangamiza, kujenga na kupanda.”

111:11 Yer 24:3; Amo 7:8-9Neno la Bwana likanijia kusema, “Je, Yeremia unaona nini?”

Nami nikajibu, “Naona tawi la mti wa mlozi.”

121:12 Ay 29:2; Yer 44:27Bwana akaniambia, “Umeona vyema kwa maana ninaliangalia neno langu ili kuona kwamba limetimizwa.”

131:13 Zek 4:2; 5:2; Yer 24:3Neno la Bwana likanijia tena, “Unaona nini?”

Nikajibu, “Naona chungu kinachochemka, kikiwa kimeinama kutoka kaskazini.”

141:14 Isa 14:31Bwana akaniambia, “Kutoka kaskazini maafa yatamwagwa kwa wote waishio katika nchi. 151:15 Yer 9:11; 10:22; 39:3; 4:16Nitawaita watu wote wa falme za kaskazini,” asema Bwana.

“Wafalme wao watakuja na kuweka viti vyao vya enzi

katika maingilio ya malango ya Yerusalemu,

watakuja dhidi ya kuta zake zote zinazouzunguka,

na dhidi ya miji yote ya Yuda.

161:16 Mwa 6:5; Yer 4:12; Kum 28:20; Yer 17:13; Kut 20:3; Yer 44:3-4; 19:4; Hes 25:3Nitatoa hukumu zangu kwa watu wangu

kwa sababu ya uovu wao wa kuniacha mimi,

kwa kufukiza uvumba kwa miungu mingine

na kuabudu kile ambacho mikono yao imekitengeneza.

171:17 Kum 31:6; 1Fal 18:46; Eze 2:6; Yer 7:27; 42:4“Jiandae! Simama useme chochote nitakachokuamuru. Usiwaogope, la sivyo nitakufanya uwaogope wao. 181:18 Isa 50:7Leo nimekufanya mji wenye ngome, nguzo ya chuma, na ukuta wa shaba ili kusimama dhidi ya nchi yote: dhidi ya wafalme wa Yuda, maafisa wake, makuhani wake na watu wa nchi hiyo. 191:19 Mwa 26:3; Isa 43:2; Mit 20:22; Hes 14:9; Mdo 26:17; Za 129:2Watapigana nawe lakini hawatakushinda, kwa kuwa niko pamoja nawe, nami nitakuokoa,” asema Bwana.

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Yeremiya 1:1-19

1Mawu a Yeremiya mwana wa Hilikiya, mmodzi mwa ansembe a ku Anatoti, mʼdziko la Benjamini. 2Mawuwa Yehova anayankhula naye mʼchaka cha 13 cha ulamuliro wa Yosiya mwana wa Amoni mfumu ya Yuda. 3Yehova anayankhulanso naye pa nthawi yonse ya ulamuliro wa Yehoyakimu mwana wa Yosiya mfumu ya Yuda, mpaka mwezi wachisanu wa chaka cha 11 cha ufumu wa Zedekiya mwana wa Yosiya mfumu ya Yuda, pamene anthu a ku Yerusalemu anapita ku ukapolo.

Kuyitanidwa kwa Yeremiya

4Yehova anayankhula nane kuti,

5“Ndisanakuwumbe mʼmimba mwa amayi ako ndinali nditakudziwa kale,

iwe usanabadwe ndinali nditakupatula kale;

ndinakuyika kuti ukhale mneneri kwa anthu a mitundu yonse.”

6Ine ndinati, “Haa! Ambuye Yehova, ine sinditha kuyankhula; popeza ndikanali wamngʼono.”

7Koma Yehova anandiwuza kuti, “Usanene kuti, ‘Ndikanali wamngʼono’ popeza udzapita kwa munthu aliyense kumene ndidzakutuma ndi kunena chilichonse chimene ndidzakulamulira. 8Usawaope, pakuti Ine ndili nawe, ndipo ndidzakupulumutsa,” akutero Yehova.

9Pamenepo Yehova anatambalitsa dzanja lake nakhudza pakamwa panga, nandiwuza kuti, “Taona, tsopano ndayika mawu anga mʼkamwa mwako. 10Lero ndakusankha kuti ukhale ndi ulamuliro pa mitundu ya anthu ndi pa maufumu awo kuti uzule ndi kugwetsa, uwononge ndi kugumula, kuti uwamange ndi kudzala.”

11Yehova anandifunsa kuti, “Yeremiya, kodi ukuona chiyani?”

Ine ndinayankha kuti, “Ndikuona nthambi ya mtengo wa mtowo.”

12Yehova anandiwuza kuti, “Waona bwino, chifukwa Ine ndikuonetsetsa kuti mawu angawa akwaniritsidwe.”

13Yehova anandifunsanso kachiwiri kuti, “Kodi ukuona chiyani?”

Ine ndinayankha kuti, “Ndikuona mʼphika wa madzi owira, ndipo wagudukira kuno kummwera.”

14Yehova anandiwuza kuti, “Mavuto a anthu onse okhala mʼdziko lino adzachokera kumpoto. 15Ine ndikuyitana anthu onse a ku maufumu a kumpoto,” akutero Yehova.

“Mafumu awo adzabwera ndipo aliyense adzakhazika mpando wake waufumu

polowera pa zipata za Yerusalemu;

iwo adzabwera ndi kuzungulira makoma ake

ndiponso midzi yonse ya dziko la Yuda.

16Ndidzatulutsa mlandu wanga ndi iwo

chifukwa cha zoyipa zimene anachita pondisiya Ine.

Iwo anakafukiza lubani kwa milungu ina,

ndi kupembedza zimene anapanga ndi manja awo.

17“Koma iwe Yeremiya konzeka! Nyamuka ndipo ukawawuze zonse zimene ndakulamulira. Usachite nawo mantha, kuopa kuti Ine ndingakuchititse mantha iwo akuona. 18Taona, lero ndakupanga kukhala ngati mzinda wotetezedwa, ngati mzati wachitsulo ndiponso ngati makoma a mkuwa kuti usaopsedwe ndi munthu aliyense wa mʼdzikomo; kaya ndi mafumu a Yuda, akuluakulu ake, ansembe ake, kapena munthu wamba wa mʼdzikomo. 19Iwo adzalimbana nawe koma sadzakugonjetsa, popeza Ine ndili nawe ndipo ndidzakupulumutsa,” akutero Yehova.