Isaya 21 – NEN & CCL

Kiswahili Contemporary Version (Neno: Bibilia Takatifu)

Isaya 21:1-17

Unabii Dhidi Ya Babeli

1Neno kuhusu Jangwa kando ya Bahari:

Kama upepo wa kisulisuli unaopita katika nchi hadi kusini,

mshambuliaji anakuja kutoka jangwani,

kutoka nchi inayotisha.

221:2 1Sam 24:13-16; Mwa 10:22; Za 60:3; Yer 49:34; Isa 22:6; 13:3; Yer 25:25Nimeonyeshwa maono ya kutisha:

Msaliti anasaliti, mteka nyara anateka nyara.

Elamu, shambulia! Umedi, izunguke kwa jeshi!

Nitakomesha huzuni zote alizosababisha.

321:3 Mwa 3:16; Yn 16:2; Ay 14:22; Za 48:6; Isa 26:17; Yer 30:6; Dan 7:28Katika hili mwili wangu umeteswa na maumivu,

maumivu makali ya ghafula yamenishika,

kama yale ya mwanamke mwenye utungu wa kuzaa.

Nimeduwazwa na lile ninalolisikia,

nimeshangazwa na lile ninaloliona.

421:4 Isa 7:4; 35:4; 13:8; Dan 5:9; Za 55:5Moyo wangu unababaika,

woga unanifanya nitetemeke,

gizagiza la jioni nililolitamani sana,

limekuwa hofu kuu kwangu.

521:5 Yer 25:16, 27; Dan 5:2-5; Isa 5:12; 23:7; Yer 46:3; 1Sam 1:21Wanaandaa meza,

wanatandaza mazulia,

wanakula, wanakunywa!

Amkeni, enyi maafisa,

zitieni ngao mafuta!

621:6 2Fal 9:17Hili ndilo Bwana analoniambia:

“Nenda, weka mlinzi,

na atoe taarifa ya kile anachokiona.

721:7 Amu 6:5; Isa 21:9Anapoona magari ya vita

pamoja na kundi la farasi,

wapanda punda au wapanda ngamia,

na awe macho, awe macho kikamilifu.”

821:8 Mik 7:7; Hab 2:1Naye mlinzi alipaza sauti,

“Mchana baada ya mchana, bwana wangu, ninasimama katika mnara wa ulinzi,

kila usiku ninakaa mahali pangu nilipoamriwa.

921:9 Isa 13:19; Ufu 14:8; Dan 5:30; Ufu 18:2; Yer 50:2; Isa 47:11; Yer 51:8Tazama, yuaja mtu anayepanda gari la vita

pamoja na kundi la farasi.

Naye anajibu:

‘Babeli umeanguka, umeanguka!

Vinyago vyote vya miungu yake

vimelala chini vikiwa vimevunjwa!’ ”

1021:10 Yer 51:33; Mt 3:12; Mik 4:13; Isa 27:12; Hab 3:12Ee watu wangu, mliopondwa kwenye sakafu ya kupuria,

ninawaambia kile nilichokisikia

kutoka kwa Bwana Mwenye Nguvu Zote,

kutoka kwa Mungu wa Israeli.

Unabii Dhidi Ya Edomu

1121:11 Mwa 32:3; 1Nya 1:30; Eze 35:2; Oba 1:1Neno kuhusu Duma:

Mtu fulani ananiita kutoka Seiri,

“Mlinzi, usiku utaisha lini?

Mlinzi, usiku utaisha lini?”

12Mlinzi anajibu,

“Asubuhi inakuja, lakini pia usiku.

Kama ungeliuliza, basi uliza;

bado na urudi tena.”

Unabii Dhidi Ya Arabia

1321:13 Isa 13:1; 2Nya 9:14; Mwa 10:7; 25:3; 1Nya 1:9Neno kuhusu Arabia:

Enyi misafara ya Wadedani,

mnaopiga kambi katika vichaka vya Arabia,

1421:14 Mwa 25:15; Ay 6:19leteni maji kwa wenye kiu,

ninyi mnaoishi Tema,

leteni chakula kwa ajili ya wakimbizi.

1521:15 Isa 13:14; 31:8Wanaukimbia upanga,

kutoka upanga uliochomolewa alani,

kutoka upinde uliopindwa,

na kutoka kwenye joto la vita.

1621:16 Law 25:50; Mwa 25:13; 25:13; Isa 17:3; 16:14; Za 120:5; Law 25:50; Wim 1:5; Mwa 25:13Hili ndilo Bwana analoniambia: “Katika muda wa mwaka mmoja, kama vile mtumishi aliyefungwa na mkataba angeihesabu, majivuno yote ya Kedari yatafikia mwisho. 1721:17 Hes 23:19; Kum 4:27; Isa 10; 19; 1:20; 16:14; Lk 21:33; 1Sam 15:29; Mt 24:35; Mk 13:31; 1Pet 1:25Wanaume wavutao pinde walionusurika, mashujaa wa Kedari, watakuwa wachache.” Bwana, Mungu wa Israeli, amesema.

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Yesaya 21:1-17

Za Chilango cha Babuloni

1Uthenga wonena za chipululu cha mʼmbali mwa Nyanja.

Ankhondo a ku Elamu ndi Mediya adzabwera ngati kamvuluvulu amene akuwomba modutsa mʼmbali ya nyanja,

kuchokera ku chipululu,

dziko lochititsa mantha.

2Ine ndaona zinthu zoopsa mʼmasomphenya:

Wonyenga akunyenga, wofunkha akufunkha komanso owononga akuwononga.

Elamu, yambani nkhondo! Mediya, zingani mzinda!

Ine ndidzathetsa mavuto onse amene anayambitsa Ababuloni.

3Chifukwa cha zimenezi thupi langa likunjenjemera ndi mantha,

ndikumva ululu ngati wa mayi amene akubereka;

ndikuvutika kwambiri ndi zimene ndikumva,

ndathedwa nzeru ndi zimene ndikuziona.

4Mtima wanga ukugunda,

ndipo ndikunjenjemera ndi mantha;

chisisira chimene ndakhala ndikuchifuna

chasanduka chinthu choopsa kwa ine.

5Ankhondo a ku Elamu ndi Mediya akukonza matebulo,

akuyala mphasa,

akudya komanso kumwa!

Mwadzidzidzi anamva mawu akuti, “Dzukani inu ankhondo,

pakani mafuta zishango zanu!”

6Zimene Ambuye akunena kwa ine ndi izi;

“Pita, kayike mlonda

kuti azinena zimene akuziona.

7Taonani, anthu akubwera ali pa akavalo

ndipo akuyenda awiriawiri,

okwera pa bulu

kapena okwera pa ngamira,

mlondayo akhale tcheru kwambiri.”

8Ndipo mlondayo anafuwula kuti,

“Ambuye anga, tsiku ndi tsiku ndimakhala pa nsanja yolondera;

Usiku uliwonse ndimakhala pa malo anga olondera.

9Taonani, uyo munthu akubwera atakwera pa galeta

ali ndi gulu la akavalo.

Mmodzi wa iwo akuti,

‘Babuloni wagwa, wagwa!

Mafano onse a milungu yake

agwa pansi ndipo aphwanyika!’ ”

10Inu anthu anga opunthidwa ndi kupetedwa ngati tirigu,

ine ndikukuwuzani zimene ndamva

ndikukuwuzani Uthenga wochokera kwa Yehova Wamphamvuzonse,

Mulungu wa Israeli.

Za Chilango cha Edomu

11Uthenga wonena za Duma:

Munthu wina akundiyitana kuchokera ku Seiri kuti,

“Iwe mlonda, usikuwu utha liti?

Iwe mlonda, utha liti kodi usikuwu?”

12Mlonda akuyankha kuti,

“Kukucha, koma kudanso.

Ngati ukufuna kufunsa, funsa tsopano;

ndipo ubwerenso udzafunse.”

Za Chilango cha Arabiya

13Uthenga wonena za Arabiya:

Inu anthu amalonda a ku Dedani,

amene usiku mumagona mʼzithukuluzi za ku Arabiya,

14perekani madzi kwa anthu aludzu.

Inu anthu a ku Tema

perekani chakudya kwa anthu othawa nkhondo.

15Iwo akuthawa malupanga,

lupanga losololedwa,

akuthawa uta wokokakoka

ndiponso nkhondo yoopsa.

16Zimene Ambuye akunena kwa ine ndi izi: “Chaka chimodzi chisanathe, potsata mmene amawerengera munthu waganyu, ulemerero wonse wa Kedara udzatheratu. 17Mwa anthu okoka uta, ankhondo a ku Kedara opulumuka adzakhala owerengeka.” Wayankhula ndi Yehova Mulungu wa Israeli.