Amosi 8 – NEN & CCL

Kiswahili Contemporary Version (Neno: Bibilia Takatifu)

Amosi 8:1-14

Maono Ya Nne: Kikapu Cha Matunda Yaliyoiva

1Hili ndilo alilonionyesha Bwana Mwenyezi katika maono: kikapu cha matunda yaliyoiva. 28:2 Mao 4:18; Yer 1:2, 13; 24:3; Eze 7:2-9; Amo 7:8; Mwa 40:16Akaniuliza, “Amosi, unaona nini?”

Nikajibu, “Kikapu chenye matunda yaliyoiva.”

Ndipo Bwana akaniambia, “Wakati umewadia kwa watu wangu Israeli; sitawahurumia zaidi.”

38:3 Amo 5:16-23; 6:10Bwana Mwenyezi asema, “Katika siku ile, nyimbo katika Hekalu zitageuka kuwa maombolezo. Miili mingi, mingi sana: itatupwa kila mahali! Kimya!”

48:4 Mit 30:14; Ay 20:19; Zek 14:4; Amo 2:7Lisikieni hili, ninyi ambao mnawagandamiza wahitaji,

na kuwaonea maskini wa nchi,

58:5 Kum 25:15; 2Fal 4:23; Neh 13:15-16; Hes 10:10; Isa 58:13; Mik 6:10; Mwa 31:7; Hos 12:7mkisema,

“Ni lini Mwezi Mwandamo utakapopita

ili tupate kuuza nafaka,

na Sabato itakwisha lini

ili tuweze kuuza ngano?”

Mkipunguza vipimo,

na kuongeza bei,

na kudanganya kwa mizani zisizo sawa,

68:6 Amo 2:6; 4:1; 5:11mkiwanunua maskini kwa fedha,

na wahitaji kwa jozi ya viatu,

na mkiuza hata takataka za ngano

pamoja na ngano.

78:7 Hos 8:13; Amo 6:8; Za 47:4; 68:34; Ay 35:15Bwana ameapa kwake mwenyewe, aliye Kiburi cha Yakobo: “Kamwe sitasahau chochote ambacho wamefanya.

88:8 Ay 9:6; Hos 4:3; Yer 46:8; 51:29; Za 18:7; Amo 9:5“Je, nchi haitatetemeka kwa ajili ya hili,

nao wote waishio ndani mwake hawataomboleza?

Nchi yote itainuka kama Naili;

itapanda na kushuka kama mto wa Misri.

98:9 Ay 5:14; Mk 15:33; Eze 32:7; Amo 4:13; 5:8; Isa 13:10; 59:9-10; Yer 15:9; Mik 3:6; 1The 5:2, 3; Mt 27:45“Katika siku ile,” asema Bwana Mwenyezi,

“Nitalifanya jua litue alasiri na kuifanya dunia

iwe giza wakati wa mchana mwangavu.

108:10 Yoe 1:8; Zek 12:10; Mwa 21:16; Hos 2:11; Lk 7:12, 13; Yer 6:26; 48:37; 2:19; Eze 7:18; Law 26:31; 13:40; Mao 5:15; Isa 3:17Nitageuza sikukuu zenu za kidini kuwa maombolezo,

na kuimba kwenu kote kuwe kilio.

Nitawafanya ninyi nyote mvae nguo ya gunia

na kunyoa nywele zenu.

Nitaufanya wakati ule uwe kama wa kuombolezea mwana wa pekee,

na mwisho wake kama siku ya uchungu.

118:11 1Sam 3:1; 28:6; Eze 7:26; Za 74:9; Mik 3:6; 2Nya 15:3; Yer 30:3; 31:27“Siku zinakuja,” asema Bwana Mwenyezi,

“wakati nitakapotuma njaa katika nchi yote:

si njaa ya chakula wala kiu ya maji,

lakini njaa ya kusikia maneno ya Bwana.

128:12 Eze 20:31Wanaume watayumbayumba kutoka bahari hadi bahari

na kutangatanga kutoka kaskazini mpaka mashariki,

wakitafuta neno la Bwana,

lakini hawatalipata.

138:13 Isa 41:17; 9:17; Hos 2:3; 8:14; Kum 9:21; 1Fal 12:29, 30; Hos 8:5, 6; 10:5; Mik 1:5; Za 46:2; Amo 5:2-5“Katika siku ile

“wasichana wazuri na vijana wanaume wenye nguvu

watazimia kwa sababu ya kiu.

14Wale waapao kwa aibu ya Samaria,

au kusema, ‘Hakika kama miungu yenu iishivyo, ee Dani,’

au ‘Hakika kama mungu wa Beer-Sheba aishivyo’:

wataanguka, wala hawatasimama tena.”

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Amosi 8:1-14

Dengu la Zipatso Zakupsa

1Zimene Ambuye Yehova anandionetsa ndi izi: dengu la zipatso zakupsa. 2Iye anandifunsa kuti, “Amosi nʼchiyani ukuona?”

Ine ndinayankha kuti, “Dengu la zipatso zakupsa.”

Ndipo Yehova anati kwa ine, “Nthawi yachimaliziro yawakwanira anthu anga Aisraeli; sindidzawakhululukiranso.

3“Tsiku limenelo,” Ambuye Yehova akulengeza kuti, “Nyimbo za mʼNyumba ya Mulungu zidzasanduka kulira kofuwula. Mitembo ya anthu idzachuluka, ndipo adzayiponya ponseponse! Kudzangoti zii!”

4Imvani izi, inu amene mumapondereza anthu osowa

ndipo simulabadira anthu osauka a mʼdzikomu.

5Mumanena kuti,

“Kodi chikondwerero cha mwezi watsopano chidzatha liti

kuti tigulitse zinthu?

Ndipo tsiku la Sabata litha liti

kuti tigulitse tirigu,

kuti tichepetse miyeso,

kukweza mitengo

kuti tibere anthu ndi miyeso ya chinyengo,

6tigule osauka ndi ndalama zasiliva

ndi osowa powapatsa nsapato,

tigulitse ngakhale mungu wa tirigu?”

7Yehova amene Yakobo amamunyadira, walumbira kuti: Ine sindidzayiwala chilichonse chimene anachita.

8“Kodi dziko silidzagwedezeka chifukwa cha zimenezi,

ndi onse okhala mʼmenemo kulira mwachisoni?

Dziko lonse lidzavunduka ngati mtsinje wa Nailo;

lidzagwedezeka kenaka nʼkukhala bata

ngati mtsinje wa ku Igupto.

9“Tsiku limenelo,” Ambuye Yehova akunena kuti,

“Ndidzadetsa dzuwa masana

ndi kugwetsa mdima pa dziko lapansi dzuwa likuswa mtengo.

10Maphwando anu achipembedzo ndidzawasandutsa kulira kwa chisoni

ndipo kuyimba kwanu konse ndidzakusandutsa maliro.

Ndidzakuvekani chiguduli nonsenu

ndi kumeta mipala mitu yanu.

Nthawi imeneyo idzakhala ngati yolira mwana wamwamuna mmodzi yekhayo,

ndipo tsikulo lidzakhala lowawa mpaka kutha kwake.

11“Nthawi ikubwera,” Ambuye Yehova akunena kuti,

“Ndidzagwetsa njala mʼdziko lonse;

osati njala ya chakudya kapena ludzu la madzi,

koma njala yofuna kumva mawu a Yehova.

12Anthu azidzangoyendayenda kuchoka ku nyanja ina kupita ku nyanja ina.

Azidzangoyendayenda kuchoka kumpoto kupita kummawa,

kufunafuna mawu a Yehova,

koma sadzawapeza.

13“Tsiku limenelo

“anamwali okongola ndi anyamata amphamvu

adzakomoka ndi ludzu.

14Onse amene amalumbira pa tchimo la Samariya,

kapena kumanena kuti, ‘Iwe Dani, pali mulungu wako wamoyo,’

kapena, ‘Pali mulungu wamoyo wa ku Beeriseba.’

Iwowo adzagwa

ndipo sadzadzukanso.”