Amosi 9 – NEN & CCL

Kiswahili Contemporary Version (Neno: Bibilia Takatifu)

Amosi 9:1-15

Israeli Kuangamizwa

19:1 Za 68:21; Yer 11:11Nilimwona Bwana akiwa amesimama kando ya madhabahu, naye akasema:

“Piga vichwa vya nguzo

ili vizingiti vitikisike.

Viangushe juu ya vichwa vya watu wote;

na wale watakaosalia nitawaua kwa upanga.

Hakuna awaye yote atakayekimbia,

hakuna atakayetoroka.

29:2 Za 139:8-10; Ay 20:6; 7:9; Yer 51:33; Oba 1:4; Eze 26:20Wajapojichimbia chini mpaka kwenye vina vya kuzimu,

kutoka huko mkono wangu utawatoa.

Wajapopanda juu hadi kwenye mbingu,

kutoka huko nitawashusha.

39:3 Yer 23:24; 6:16-17; Za 139:8-10; 68:22; Mwa 49:17; Ay 11:20Wajapojificha juu ya kilele cha Karmeli,

huko nitawawinda na kuwakamata.

Wajapojificha kutoka kwenye uso wangu

katika vilindi vya bahari,

huko nako nitaamuru joka kuwauma.

49:4 Law 26:33; 17:10; Eze 5:12; 15:7; Kum 28:65; Yer 39:16; 21:10; 44:11Wajapopelekwa uhamishoni na adui zao,

huko nako nitaamuru upanga uwaue.

Nitawakazia macho yangu kwa mabaya

wala si kwa mazuri.”

59:5 Za 46:2; Amo 8:8; Mik 1:4Bwana, Bwana Mwenye Nguvu Zote,

yeye agusaye dunia nayo ikayeyuka,

na wote wakaao ndani mwake wakaomboleza:

nayo nchi yote huinuka kama Naili,

kisha hushuka kama mto wa Misri;

69:6 Za 104:1-3, 5-13; Amo 5:8; Yer 43:9yeye ambaye hujenga jumba lake la kifalme katika mbingu

na kuisimika misingi yake juu ya dunia,

yeye aitaye maji ya bahari

na kuyamwaga juu ya uso wa nchi:

Bwana ndilo jina lake.

79:7 2Nya 12:3; Kum 2:23; Isa 43:3; 22:6; 2Fal 16:9; Yer 47:4; Amo 1:5; Mwa 10:14“Je, Waisraeli,

ninyi si sawa kwangu kama Wakushi?”

asema Bwana.

“Je, sikuleta Israeli kutoka Misri,

Wafilisti kutoka Kaftori,9:7 Yaani Krete.

na Washamu kutoka Kiri?

89:8 Yer 30:11; 44:27; Za 11:4“Hakika macho ya Bwana Mwenyezi

yako juu ya ufalme wenye dhambi.

Nami nitauangamiza

kutoka kwenye uso wa dunia:

hata hivyo sitaiangamiza kabisa

nyumba ya Yakobo,”

asema Bwana.

99:9 Lk 22:31; Isa 30:28; Yer 31:36; Dan 9:7“Kwa kuwa nitatoa amri,

na nitaipepeta nyumba ya Israeli

miongoni mwa mataifa yote,

kama vile nafaka ipepetwavyo katika ungo,

na hakuna hata punje moja itakayoanguka chini.

109:10 Yer 5:12; 23:17; 49:37; Eze 20:38; Amo 6:3Watenda dhambi wote miongoni mwa watu wangu

watauawa kwa upanga,

wale wote wasemao,

‘Maafa hayatatupata wala kutukuta.’

Kurejezwa Kwa Israeli

119:11 Mdo 15:16; Mik 7:8-11; Zek 12:7; Isa 7:2; 49:8; Mwa 26:22; Eze 17:24“Katika siku ile nitaisimamisha

hema ya Daudi iliyoanguka.

Nitakarabati mahali palipobomoka

na kujenga upya magofu yake,

na kuijenga kama ilivyokuwa awali,

129:12 Hes 24:18; Isa 43:7; Oba 1:19; Yer 25:29; Mdo 15:16-17ili wapate kuyamiliki mabaki ya Edomu,

na mataifa yote yale yanayobeba Jina langu,”

asema Bwana ambaye atafanya mambo haya.

139:13 Law 26:5; Amu 9:27; Yoe 3:18; 2:24; Yer 31:38; 33:14; Rut 2:3“Siku zinakuja,” asema Bwana,

“wakati mvunaji atatanguliwa na mkulima,

naye mpanzi atatanguliwa na yeye akamuaye zabibu.

Divai mpya itadondoka kutoka milimani,

na kutiririka kutoka vilima vyote.

149:14 Isa 32:18; 49:8; 62:9; 61:4; Eze 34:13-14; Yer 29:14; 33:7; 30:18Nitawarejesha tena watu wangu Israeli waliohamishwa;

wataijenga tena miji iliyoachwa magofu,

nao wataishi ndani mwake.

Watapanda mizabibu na kunywa divai yake;

watalima bustani na kula matunda yake.

159:15 Kut 15:17; Isa 60:21; 65:9; Yer 18:9; 23:8; 3:18; 24:6; 32:15; Eze 28:26; 34:28; Yoe 3:20Nitaipanda Israeli katika nchi yao wenyewe,

hawatangʼolewa tena

kutoka nchi ambayo nimewapa,”

asema Bwana Mungu wenu.

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Amosi 9:1-15

Israeli Adzawonongedwa

1Ine ndinaona Ambuye atayima pambali pa guwa lansembe, ndipo anati:

“Kantha mitu ya nsanamira

kuti ziwundo za nyumba zigwedezeke.

Muzigwetsere pa mitu ya anthu onse,

onse amene atsalira ndidzawapha ndi lupanga.

Palibe ndi mmodzi yemwe amene adzathawe,

palibe amene adzapulumuke.

2Ngakhale atakumba pansi mpaka ku malo a anthu akufa,

dzanja langa lidzawatulutsa kumeneko.

Ngakhale atakwera kumwamba

Ine ndidzawatsakamutsa kumeneko.

3Ngakhale atakabisala pamwamba pa phiri la Karimeli,

Ine ndidzawasaka kumeneko ndi kuwagwira.

Ngakhale atakabisala pansi pa nyanja yayikulu,

ndidzalamula njoka kuti iwalume kumeneko.

4Ngakhale adani awo awakusire ku ukapolo,

ndidzalamula lupanga kuti liwaphe kumeneko.

Ndidzawayangʼanitsitsa

kuti zoyipa ziwagwere; osati zabwino.”

5Ambuye Yehova Wamphamvuzonse

amene amakhudza dziko lapansi ndipo dzikolo limasungunuka,

onse amene amakhala mʼmenemo amalira.

Dziko lonse lidzadzaza ngati mtsinje wa Nailo,

kenaka nʼkuphwera ngati mtsinje wa ku Igupto.

6Iye amene amamanga malo ake okhalamo kumwamba,

ndi kuyika maziko ake pa dziko lapansi,

Iye amene amayitana madzi a ku nyanja

ndikuwakhuthulira pa dziko lapansi,

dzina lake ndiye Yehova.

7“Kodi kwa Ine, inu Aisraeli, simuli

chimodzimodzi ndi Akusi?”

Akutero Yehova.

“Kodi sindine amene ndinatulutsa Israeli ku Igupto,

Afilisti ku Kafitori

ndi Aaramu ku Kiri?

8“Taonani, maso a Ambuye Yehova

ali pa ufumu wochimwawu.

Ndidzawufafaniza

pa dziko lapansi.

Komabe sindidzawononga kotheratu

nyumba ya Yakobo,”

akutero Yehova.

9“Pakuti ndidzalamula,

ndipo ndidzagwedeza nyumba ya Israeli

pakati pa mitundu yonse ya anthu

monga momwe amasefera ufa mʼsefa,

koma palibe nʼkamwala kamodzi komwe kamene kadzagwe pansi.

10Anthu onse ochimwa pakati pa anthu anga

adzaphedwa ndi lupanga,

onse amene amanena kuti,

‘Tsoka silidzatigwera ife kapena kutiwononga.’

Kubwezeretsedwa kwa Israeli

11“Tsiku limenelo ndidzabwezeretsa

nyumba ya Davide imene inagwa.

Ndidzakonzanso malo amene anagumuka,

ndi kuyimanganso

monga inalili poyamba,

12kuti adzatengenso otsala a Edomu

ndi mitundu yonse imene imatchedwa ndi dzina langa,”

akutero Yehova amene adzachita zinthu izi.

13Yehova akunena kuti

“Nthawi ikubwera pamene mlimi wotipula adzapyola wokolola

ndipo woponda mphesa adzapyola wodzala mbewu.

Mapiri adzachucha vinyo watsopano

ndi kuyenderera pa zitunda zonse.

14Ndidzawabwezeranso pabwino anthu anga Aisraeli;

mizinda imene inali mabwinja idzamangidwanso ndipo azidzakhalamo.

Adzalima minda ya mpesa ndipo adzamwa vinyo wake;

adzalima minda ndipo adzadya zipatso zake.

15Ndidzakhazika Aisraeli mʼdziko mwawo,

ndipo sadzachotsedwamonso mʼdziko

limene Ine ndawapatsa,”

akutero Yehova Mulungu wako.