Amosi 7 – NEN & CCL

Kiswahili Contemporary Version (Neno: Bibilia Takatifu)

Amosi 7:1-17

Maono Ya Kwanza: Nzige

17:1 Amo 8:1; Za 78:46; Yer 51:14; Yoe 1:4Hili ndilo alilonionyesha Bwana Mwenyezi katika maono: Alikuwa anaandaa makundi ya nzige baada ya kuvunwa fungu la mfalme na wakati ule tu mimea ya pili ilipokuwa ikichipua. 27:2 Kut 10:15; Eze 11:13; Isa 37:4; Amo 4:9Wakati nzige walikuwa wamekula mimea yote ya nchi, nililia kwa sauti kuu, “Bwana Mwenyezi, samehe! Je, Yakobo atawezaje kuendelea kuishi? Yeye ni mdogo sana!”

37:3 Kut 32:14; Yon 3:10; Kum 32:36; Za 106:45; 1Nya 21:15; Hos 11:8; Yoe 2:14; Yak 5:16; Yer 18:8; 26:19Kwa hiyo Bwana akaghairi.

Kisha Bwana akasema, “Hili halitatokea.”

Maono Ya Pili: Moto

47:4 Isa 66:16; Yoe 1:19; Kum 32:22Hili ndilo Bwana Mwenyezi alilonionyesha katika maono: Bwana Mwenyezi alikuwa akiita hukumu ya moto; nao ulikausha vilindi vikuu, ukateketeza nchi. 57:5 Yoe 2:17Ndipo nikalia, “Bwana Mwenyezi, nakusihi, zuia! Je, Yakobo atawezaje kuendelea kuishi? Yeye ni mdogo sana!”

67:6 Kut 32:14; Yer 18:8; 42:10; Za 102:17; Yon 3:10; Eze 9:8Kwa hiyo Bwana akaghairi.

Bwana Mwenyezi akasema, “Hili nalo halitatokea.”

Maono Ya Tatu: Timazi

7Hili ndilo alilonionyesha katika maono: Bwana alikuwa amesimama karibu na ukuta ambao ulikuwa umejengwa kwa timazi, akiwa na uzi wa timazi mkononi mwake. 87:8 Isa 28:17; Mao 2:8; 2Fal 21:13; Eze 7:2-9; Yer 1:11-13; 15:6; Mik 7:18Naye Bwana akaniuliza, “Je, Amosi unaona nini?”

Nikamjibu, “Uzi wa timazi.”

Kisha Bwana akasema, “Tazama, ninaweka uzi wa timazi miongoni mwa watu wangu Israeli; sitawahurumia tena.

97:9 Law 26:31; Mwa 26:23; 2Fal 14:23; 1Fal 13:34; 2Fal 15:9-10; Isa 63:18; Hos 10:8“Mahali pa Isaki pa juu pa kuabudia miungu pataangamizwa,

na mahali patakatifu pa Israeli pa kuabudia pataharibiwa;

kwa upanga wangu nitainuka

dhidi ya nyumba ya Yeroboamu.”

Amosi Na Amazia

107:10 1Fal 12:32; Yos 7:2; 2Fal 14:23-24; Yer 38:4; 26:8-11Kisha Amazia kuhani wa Betheli akatuma ujumbe kwa Yeroboamu mfalme wa Israeli, akisema: “Amosi analeta fitina juu yako katikati ya Israeli. Nchi haiwezi kuvumilia maneno yake yote. 117:11 Amo 5:27; Yer 36:16Kwa kuwa hili ndilo Amosi analosema:

“ ‘Yeroboamu atakufa kwa upanga,

na kwa hakika Israeli watakwenda uhamishoni,

mbali na nchi yao.’ ”

127:12 Mt 8:34; 1Sam 9:9Kisha Amazia akamwambia Amosi, “Nenda zako, ewe mwonaji! Urudi katika nchi ya Yuda. Ujipatie riziki yako huko na kutoa unabii wako. 137:13 Yer 20:2; 36:5; Amo 2:12; Mdo 4:18; Yos 7:2; 1Fal 12:29Usiendelee kutoa unabii katika Betheli, kwa sababu hapa ni mahali pa mfalme pa kuabudia na Hekalu la ufalme huu.”

147:14 1Sam 10:5; Zek 13:5; 2Fal 2:5; 4:38; Isa 9:10; 1Fal 10:27Amosi akamjibu Amazia, “Mimi sikuwa nabii wala mwana wa nabii, lakini nilikuwa mchungaji wa kondoo na mtunza mikuyu. 157:15 Mwa 37:5; 2Sam 7:8; Yer 7:1-2; 26:12; Eze 2:3-4; Isa 6:9Lakini Bwana akanitoa kutoka kuchunga kondoo na kuniambia, ‘Nenda, ukawatabirie watu wangu Israeli.’ 167:16 Isa 30:10; Eze 20:46; Mik 2:6; Yer 22:2Sasa basi, sikieni neno la Bwana. Ninyi mnasema,

“ ‘Usitabiri dhidi ya Israeli,

na uache kuhubiri dhidi ya nyumba ya Isaki.’

177:17 Hos 4:13; 9:3; Eze 4:13; Yer 28:12; 29:21; Mao 5:11; Amo 5:27; 2:12-13; 2Fal 17:6“Kwa hiyo hili ndilo asemalo Bwana:

“ ‘Mke wako atakuwa kahaba mjini,

nao wana wako na binti zako watauawa kwa upanga.

Shamba lako litapimwa na kugawanywa,

na wewe mwenyewe utafia katika nchi ya kipagani.

Nayo Israeli kwa hakika itakwenda uhamishoni,

mbali na nchi yao.’ ”

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Amosi 7:1-17

Dzombe, Moto ndi Chingwe Chowongolera Khoma

1Zimene Ambuye Yehova anandionetsa ndi izi: Yehova ankasonkhanitsa gulu la dzombe nthawi imene gawo la zokolola za mfumu linali litakololedwa kale ndipo mbewu zachiwiri zinali zitangoyamba kumera kumene. 2Dzombelo litadya zomera zonse za mʼdzikomo, Ine ndinafuwula kuti, “Ambuye Yehova, khululukani! Kodi Yakobo adzapulumuka bwanji? Iye ndi wofowoka kwambiri!”

3Kotero Yehova anakhululuka.

Yehovayo anati, “Izi sizidzachitika.”

4Zimene Ambuye Yehova anandionetsa ndi izi: Ambuye Yehova ankayitana malawi a moto kuti alange anthu. Motowo unawumitsa nyanja yakuya ndi kupsereza dziko. 5Tsono ine ndinafuwula kuti, “Ambuye Yehova, chonde ndikukupemphani, lekani! Kodi Yakobo adzapulumuka bwanji? Iye ndi wofowoka kwambiri!”

6Kotero Yehova anakhululuka.

Ambuye Yehova anati, “Izinso sizidzachitika.”

7Zimene Iye anandionetsa ndi izi: Ambuye anayima pambali pa khoma lomangamanga, mʼmanja mwake muli chingwe chowongolera khoma. 8Ndipo Ambuye anandifunsa kuti, “Amosi, nʼchiyani ukuonachi?”

Ine ndinayankha kuti, “Chingwe chowongolera khoma.”

Ndipo Yehova anati, “Taona, Ine ndikuyika chingwe chowongolerachi pakati pa anthu anga, Aisraeli; sindidzawalekereranso.

9“Malo achipembedzo a Isake adzawonongedwa

ndipo malo opatulika a Israeli adzasanduka bwinja;

ndidzagwetsa nyumba ya Yeroboamu ndi lupanga langa.”

Amosi ndi Amaziya

10Pamenepo Amaziya wansembe wa ku Beteli anatumiza uthenga kwa Yeroboamu mfumu ya Israeli kuti, “Amosi akukuutsirani chiwembu pakati pa Aisraeli. Dziko silingalekerere zonena zake zonsezo. 11Pakuti zimene Amosi akunena ndi izi:

“ ‘Yeroboamu adzaphedwa ndi lupanga,

ndipo Israeli adzapita ndithu ku ukapolo,

kutali ndi dziko lake.’ ”

12Ndipo Amaziya anawuza Amosi kuti, “Choka, mlosi iwe! Bwerera ku dziko la Yuda. Uzikalosera kumeneko ndipo anthu a kumeneko azikakudyetsa. 13Usanenerenso ku Beteli, chifukwa kumeneko ndi malo opatulika a mfumu ndiponso ndi malo a nyumba yachipembedzo yaufumu.”

14Amosi anayankha Amaziya kuti, “Ine sindine mneneri kapena mwana wa mneneri; koma ndine woweta ziweto, ndiponso mlimi wa nkhuyu. 15Koma Yehova ananditenga ndikuweta nkhosa ndipo anati, ‘Pita ukanenere kwa anthu anga Aisraeli.’ 16Tsono imva mawu a Yehova. Iwe ukunena kuti,

“ ‘Usanenere zotsutsa Israeli,

ndipo siya kulalikira motsutsa nyumba ya Isake.’ ”

17“Tsono zimene akunena Yehova ndi izi:

“ ‘Mkazi wako adzasanduka wachiwerewere mu mzindamu,

ndipo ana ako aamuna ndi aakazi adzaphedwa ndi lupanga.

Munda wako udzayezedwa ndi chingwe ndi kugawidwa,

ndipo iwe mwini udzafera mʼdziko la anthu osapembedza Mulungu.

Ndipo Israeli adzatengedwa ndithu kupita ku ukapolo,

kutali ndi dziko lake.’ ”