Zekariya 13 – CCL & NRT

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Zekariya 13:1-9

Kuyeretsedwa ku Tchimo

1“Pa tsiku limenelo nyumba ya Davide adzayitsekulira kasupe wa madzi pamodzi ndi okhala mu Yerusalemu, kuti awachotsere tchimo lawo ndi chodetsa chawo.

2“Pa tsiku limenelo, ndidzafafaniziratu mayina a mafano mʼdziko, ndipo sadzawakumbukiranso,” akutero Yehova Wamphamvuzonse. “Ndidzachotsa mʼdziko aneneri pamodzi ndi mzimu wonyansa. 3Ndipo ngati wina aliyense adzafuna kunenera, abambo ndi amayi ake amene anamubereka, adzamuwuza kuti, ‘Uyenera kufa, chifukwa wayankhula bodza mʼdzina la Yehova.’ Pamene anenera, makolo ake omwe adzamubaya.

4“Pa tsiku limenelo mneneri aliyense adzachita manyazi chifukwa cha masomphenya ake. Sadzavala chovala chake chaubweya ndi cholinga chonamiza anthu. 5Iye adzati, ‘Sindine mneneri. Ndine mlimi; ndakhala ndi kulima munda kuyambira ubwana wanga.’ 6Ngati wina adzamufunsa, ‘Zilonda zili mʼthupi lakoli ndi chiyani?’ Iye adzayankha kuti, ‘Zilondazi ndinazilandira mʼnyumba ya abwenzi anga.’

Kukantha Mʼbusa, Nkhosa Kubalalika

7“Dzambatuka iwe lupanga, ukanthe mʼbusa wanga,

ukanthe munthu amene ali pafupi ndi Ine!”

akutero Yehova Wamphamvuzonse.

Kantha mʼbusa

ndipo nkhosa zidzabalalika,

ndipo ndidzatambalitsa dzanja langa kuwononga zazingʼono.

8Mʼdziko monse, akutero Yehova Wamphamvuzonse,

“zigawo ziwiri mwa zigawo zitatu za anthu zidzakanthidwa ndi kuwonongeka;

koma chigawo chimodzi chidzatsala mʼdzikomo.

9Chigawo chachitatuchi ndidzachiyika pa moto;

ndidzawayeretsa monga momwe amayeretsera siliva

ndi kuwayesa monga momwe amayesera golide.

Adzayitana pa dzina langa

ndipo Ine ndidzawayankha;

Ine ndidzanena kuti, ‘Awa ndi anthu anga,’

ndipo iwo adzanena kuti, ‘Yehova ndiye Mulungu wathu.’ ”

New Russian Translation

Захария 13:1-9

Очищение страны от осквернения

1– В тот день для дома Давида и жителей Иерусалима пробьется родник, чтобы очистить их от греха и скверны.

2В тот день Я искореню в стране имена идолов, и их больше не будут вспоминать, – возвещает Господь Сил. – Еще Я удалю из страны лжепророков13:2 Букв.: «пророков». и дух скверны, 3а если кто-нибудь снова примется пророчествовать, тогда отец и мать, которые его родили, скажут ему: «Смерть тебе за то, что ты лгал во имя Господа» – и пронзят его, когда он будет пророчествовать.

4В тот день каждый пророк постыдится своего пророческого видения и никто не наденет косматого плаща, чтобы обманывать. 5Каждый скажет: «Я не пророк, я земледелец, ведь с юности моим уделом была земля». 6А если кто спросит его: «Что же это за раны у тебя между руками?»13:6 Вероятный смысл: «Что же это за раны у тебя на груди?» – он ответит: «Эти раны я получил в доме друзей»13:6 Лжепророки, из-за широко распространенной антипатии к ним в упомянутый период времени, скрывали то, кем они на самом деле были, выдавая себя за земледельцев. Если у них были раны, которые они сами себе наносили, как это часто было принято в экстатических языческих ритуалах, то они утверждали, что эти раны были нанесены им их друзьями..

Народ – отара без пастуха

7– Меч, поднимись на Моего Пастуха,

на Того, Кто Мне близок! –

возвещает Господь Сил. –

Порази Пастуха

и разбегутся овцы,

а Я на ягнят обращу Свою руку13:7 См. Мат. 26:31, 56..

8Во всей стране, – возвещает Господь, –

две трети будут поражены и погибнут,

но треть уцелеет.

9Эту треть Я проведу сквозь огонь;

Я очищу их, как серебро,

и испытаю, как золото.

Они будут призывать Мое имя,

а Я буду им отвечать;

Я скажу: «Это Мой народ»,

а они скажут: «Господь – наш Бог».