Zefaniya 2 – CCL & PCB

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Zefaniya 2:1-15

1Sonkhanani pamodzi, sonkhanani pamodzi,

inu mtundu wochititsa manyazi,

2isanafike nthawi yachiweruzo,

nthawi yanu isanawuluke ngati mungu,

usanakufikeni mkwiyo woopsa wa Yehova,

tsiku la ukali wa Yehova lisanafike pa inu.

3Funafunani Yehova, inu nonse odzichepetsa a mʼdziko,

inu amene mumachita zimene amakulamulani.

Funafunani chilungamo, funafunani kudzichepetsa;

mwina mudzatetezedwa

pa tsiku la mkwiyo wa Yehova.

Za Afilisti

4Gaza adzasiyidwa

ndipo Asikeloni adzasanduka bwinja.

Nthawi yamasana Asidodi adzakhala wopanda anthu

ndipo Ekroni adzazulidwa.

5Tsoka inu okhala mʼmbali mwa nyanja,

inu mtundu wa Akereti;

mawu a Yehova akutsutsa

iwe Kanaani, dziko la Afilisti.

“Ndidzakuwononga

ndipo palibe amene adzatsale.”

6Dziko la mʼmbali mwa nyanja, kumene kumakhala Akereti,

lidzakhala malo a abusa ndi la makola a nkhosa.

7Malowa adzakhala a anthu otsala a nyumba ya Yuda;

adzapezako msipu.

Nthawi ya madzulo adzagona

mʼnyumba za Asikeloni.

Yehova Mulungu wawo adzawasamalira;

adzabwezeretsa mtendere wawo.

Za Mowabu ndi Amoni

8“Ndamva kunyoza kwa Mowabu

ndi chipongwe cha Amoni,

amene ananyoza anthu anga

ndi kuopseza kuti alanda dziko lawo.

9Choncho, pali Ine Wamoyo,”

akutero Yehova Wamphamvuzonse, Mulungu wa Israeli,

“Ndithu, Mowabu adzasanduka ngati Sodomu,

Amoni adzasanduka ngati Gomora;

malo a zomeramera ndi maenje a mchere,

dziko la bwinja mpaka muyaya.

Anthu anga otsala adzawafunkha;

opulumuka a mtundu wanga adzalandira dziko lawo.”

10Ichi ndi chimene adzalandire chifukwa cha kunyada kwawo,

chifukwa chonyoza ndi kuchitira chipongwe anthu a Yehova Wamphamvuzonse.

11Yehova adzawachititsa mantha kwambiri

pamene adzawononga milungu yonse ya mʼdzikomo.

Ndipo mitundu ya anthu pa dziko lonse idzamulambira,

uliwonse ku dziko la kwawo.

Za Kusi

12“Inunso anthu a ku Kusi,

mudzaphedwa ndi lupanga.”

Za Asiriya

13Yehova adzatambasulira dzanja lake kumpoto

ndi kuwononga Asiriya,

kusiya Ninive atawonongekeratu

ndi owuma ngati chipululu.

14Nkhosa ndi ngʼombe zidzagona pansi kumeneko,

pamodzi ndi nyama zakuthengo za mtundu uliwonse.

Akadzidzi a mʼchipululu ndi akanungu

adzakhala pa nsanamira zake.

Kulira kwawo kudzamveka mʼmazenera,

mʼmakomo mwawo mudzakhala zinyalala zokhazokha,

nsanamira za mkungudza zidzakhala poonekera.

15Umenewu ndiye mzinda wosasamala

umene kale unali wotetezedwa.

Unkanena kuti mu mtima mwake,

“Ine ndine, ndipo palibenso wina wondiposa.”

Taonani lero wasanduka bwinja,

kokhala nyama zakutchire!

Onse owudutsa akuwunyoza

ndi kupukusa mitu yawo.

Persian Contemporary Bible

صفنيا 2:1-15

1ای قومی كه حيا نداريد، به خود آييد، 2پيش از آنكه داوری آغاز گردد و فرصت شما چون كاه بر باد رود، قبل از آنكه خشم خداوند فرو ريزد و روز هولناک غضب او فرا رسد. 3ای تمام متواضعانی كه احكام او را بجا می‌آوريد، به سوی خداوند بازگشت نماييد؛ به راستی عمل كنيد و در حضور خداوند فروتن شويد تا شايد شما را از غضب خود در آن روز هلاكت مصون بدارد.

نابودی قومهای مجاور اسرائيل

4شهرهای غزه، اشقلون، اشدود و عقرون، ريشه‌كن و ويران خواهند شد. 5وای بر شما ای فلسطينی‌هايی كه در ساحل دريا و در سرزمين كنعان زندگی می‌كنيد، زيرا شما هم داوری خواهيد شد. خداوند شما را به هلاكت خواهد رساند و حتی يک نفر از شما هم باقی نخواهد ماند. 6زمينهای ساحلی شما مكانی برای شبانان و آغل گوسفندان خواهد شد. 7بازماندگان قبيلهٔ يهودا، سرزمين شما را اشغال كرده گله‌های خود را در آنجا خواهند چرانيد و خود در خانه‌های اشقلون خواهند خوابيد؛ زيرا خداوند با مهربانی از قوم خود ياد نموده خوشبختی آنها را باز خواهد گردانيد.

8طعنه‌های مردم موآب و عمون را شنيده‌ام كه قوم مرا مسخره نموده، تهديد به اشغال سرزمينشان می‌كنند. 9بنابراين، خداوند قادر متعال، خدای اسرائيل می‌فرمايد: «به حيات خود قسم، موآب و عمون مثل سدوم و عموره از بين خواهند رفت و به محلی از خارها، گودالهای نمک و ويرانی ابدی تبديل خواهند شد و بازماندگان قوم من آنها را غارت نموده، سرزمينهاشان را تصرف خواهند كرد.» 10آنها مزد غرور خود را دريافت خواهند كرد، زيرا به قوم خداوند قادر متعال اهانت نموده، ايشان را مسخره كردند. 11خداوند بلاهای هولناكی بر سرشان خواهد آورد. او تمامی خدايان جهان را به تباهی خواهد كشانيد و آنگاه همهٔ اقوام در سرزمينهای خود او را عبادت خواهند نمود.

12ای حبشی‌ها، شما هم به شمشير او كشته خواهيد شد.

13خداوند قدرت خود را بر ضد آشور به کار خواهد برد و پايتخت بزرگ آن، نينوا را ويران نموده، به بيابانی خشک مبدل خواهد كرد. 14آن شهر، چراگاه گوسفندان خواهد شد و انواع حيوانات وحشی در آن جای خواهند گرفت. خفاشها و جغدها در ميان ويرانه‌هايش لانه می‌كنند و صدايشان از پنجره‌های خانه‌های متروک شنيده می‌شود. در آستانهٔ خانه‌ها زباله جمع می‌شود و روكش زيبای ستونهای شهر كه از چوب سرو بود، از بين می‌رود. 15اين شهر مستحكم كه چنان در امنيت بود كه با خود می‌گفت: «در تمام دنيا شهری مانند من وجود ندارد!» ويران شده، لانهٔ حيوانات خواهد گرديد! هر كه از آنجا بگذرد سر خود را از بهت و حيرت تكان خواهد داد.