Hagai 1 – CCL & PCB

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Hagai 1:1-15

Za Kumanga Nyumba ya Yehova

1Chaka chachiwiri cha Mfumu Dariyo, tsiku loyamba la mwezi wachisanu ndi chimodzi, Yehova anapatsa mneneri Hagai uthenga wopita kwa Zerubabeli mwana wa Sealatieli, bwanamkubwa wa Yuda, ndiponso kwa mkulu wa ansembe Yoswa mwana wa Yehozadaki:

2Yehova Wamphamvuzonse akuti, “Anthu awa amanena kuti, ‘Nthawi sinafike yoti nʼkumanga Nyumba ya Yehova.’ ”

3Tsono Yehova anayankhula ndi mneneri Hagai kuti, 4“Kodi ino ndi nthawi yoti inuyo muzikhala mʼnyumba zomanga bwino, pamene Nyumba yangayi ikanali bwinja?”

5Tsono zimene Yehova Wamphamvuzonse akunena ndi izi, “Ganizirani bwino njira zanu. 6Mwadzala zambiri, koma mwakolola zochepa. Mumadya, koma simukhuta. Mumamwa, koma ludzu lanu silitha. Mumavala, koma simumva kutentha. Mumalandira malipiro, koma ndalama zanu zimatha ngati mwaziyika mʼthumba lobowoka.”

7Yehova Wamphamvuzonse akuti, “Ganizirani bwino njira zanu. 8Pitani ku mapiri ndipo mukatenge matabwa oti mudzamangire Nyumba yanga, kuti ndikondwere nayo ndi kulandiramo ulemu,” akutero Yehova. 9“Mumayembekezera zambiri, koma taonani mwapeza pangʼono pokha. Zimene munazibweretsa ku nyumba, Ine ndinazimwaza. Nʼchifukwa chiyani?” Akutero Yehova Wamphamvuzonse. “Chifukwa Nyumba yanga ikanali bwinja, pamene aliyense wa inu watanganidwa kumanga nyumba yake. 10Choncho, chifukwa cha inu, mitambo yaleka kugwetsa mvula ndipo dziko lapansi laleka kutulutsa zomera. 11Ndabweretsa chilala pa minda ndi pa mapiri, chilala chawumitsa tirigu, mphesa, mafuta a olivi ndi chilichonse chimene chimamera pa nthaka, pa anthu ndi pa ngʼombe, ndi pa ntchito zonse za manja anu.”

12Pamenepo Zerubabeli mwana wa Sealatieli, mkulu wa ansembe Yoswa mwana wa Yehozadaki, ndi anthu onse otsala anamvera mawu a Yehova Mulungu wawo ndi uthenga wa Hagai, chifukwa anatumidwa ndi Yehova Mulungu wawo. Ndipo anthuwo anaopa Yehova.

13Tsono Hagai, mthenga wa Yehova, anapereka kwa anthuwo uthenga uwu wa Yehova: “Ine ndili nanu,” akutero Yehova. 14Kotero Yehova anakhudza mtima wa Zerubabeli mwana wa Sealatieli, bwanamkubwa wa Yuda, mtima wa Yoswa mwana wa Yehozadaki, mkulu wa ansembe, ndiponso mitima ya anthu onse otsala. Iwo anabwera ndi kuyamba ntchito yomanga Nyumba ya Yehova Wamphamvuzonse, Mulungu wawo, 15pa tsiku la 24 la mwezi wachisanu ndi chimodzi, wa chaka chachiwiri cha Mfumu Dariyo.

Persian Contemporary Bible

حجی 1:1-15

دعوت به بازسازی خانهٔ خدا

1در سال دوم سلطنت داريوش، در روز اول ماه ششم، خداوند پيامی توسط حجی نبی برای زروبابل (پسر شئلتیئيل) حاكم يهودا، و برای يهوشع (پسر يهوصادق) كاهن اعظم، فرستاد.

2خداوند قادر متعال به حجی نبی فرمود: «اين قوم می‌گويند كه اكنون وقت بازسازی خانهٔ خدا نيست.» 3سپس، خداوند اين پيام را توسط حجی نبی برای قوم فرستاد: 4«آيا اين درست است كه شما در خانه‌های نوساخته زندگی كنيد ولی خانهٔ من خراب بماند؟ 5به نتيجهٔ كارهايتان نگاه كنيد: 6بذر زياد می‌كاريد، ولی محصول كم برداشت می‌كنيد؛ می‌خوريد ولی سير نمی‌شويد؛ می‌نوشيد ولی تشنگی‌تان رفع نمی‌گردد؛ لباس می‌پوشيد اما گرم نمی‌شويد؛ مزد می‌گيريد ولی گويی آن را در جيبهای سوراخدار می‌گذاريد.

7«خوب فكر كنيد و ببينيد چه كرده‌ايد و نتيجه‌اش چه بوده است! 8حال به كوه رفته، چوب بياوريد و خانهٔ مرا دوباره بسازيد تا من از آن راضی شوم و در آنجا مردم احترام مرا بجا آورند.

9«انتظار محصول فراوانی داشتيد، اما خيلی كم به دست آورديد؛ و وقتی همان مقدار كم را هم به منزل آورديد، آن را از بين بردم. می‌دانيد چرا؟ چون خانهٔ من خراب مانده و شما فقط به فكر خانه‌های خود هستيد. 10به همين علت است كه آسمان نمی‌بارد و زمين محصول خود را نمی‌دهد. 11من در سرزمين شما خشكسالی پديد آورده‌ام و اين خشكسالی تمام كوهها، مزرعه‌ها، تاكستانها، باغهای زيتون و ساير محصولات و حتی انسان و حيوان و تمام حاصل دسترنج شما را فرا خواهد گرفت.»

12آنگاه زروبابل و يهوشع و تمام كسانی كه از اسارت برگشته بودند از خداوند ترسيدند و پيام حجی نبی را كه خداوند، خدايشان به او داده بود اطاعت كردند.

13سپس خداوند بار ديگر توسط نبی خود حجی به قوم فرمود: «من با شما هستم.» 14‏-15خداوند در زروبابل و يهوشع و تمام قوم علاقه و اشتياق ايجاد كرد تا خانهٔ او را بسازند. پس، در سال دوم سلطنت داريوش در روز بيست و چهارم ماه ششم همه جمع شده، به بازسازی خانهٔ خداوند قادر متعال، خدای خود پرداختند.