1Yehova anayankhula ndi Zefaniya mwana wa Kusi, mwana wa Gedaliya, mwana wa Amariya, mwana wa Hezekiya pa nthawi ya Yosiya, mwana wa Amoni, mfumu ya Yuda.
Yehova Adzaweruza Dziko Lapansi
2“Ndidzawononga kotheratu zinthu zonse
pa dziko lapansi,”
akutero Yehova.
3“Ndidzawononga anthu pamodzi ndi nyama zomwe;
ndidzawononga mbalame zamlengalenga
ndi nsomba za mʼnyanja.
Ndidzawononga anthu oyipa,
ndipo ndidzafafaniza mtundu wa anthu pa dziko lonse lapansi,”
akutero Yehova.
Chenjezo kwa Yuda
4Ndidzatambasula dzanja langa pa Yuda
ndi onse okhala mu Yerusalemu.
Ndidzawononga pamalo pano otsalira opembedza Baala,
mayina a anthu osapembedza pamodzi ndi ansembe a mafano:
5amene amagwada pa madenga a nyumba zawo
kupembedza zolengedwa zamumlengalenga,
amene amagwada ndi kulumbira mʼdzina la Yehova,
komanso mʼdzina la Moleki,
6amene abwerera mʼmbuyo osatsata Yehova,
osafunafuna kapena kupempha nzeru kwa Yehova.
7Khalani chete pamaso pa Ambuye Yehova,
chifukwa tsiku la Yehova layandikira.
Yehova wakonzekera kupereka nsembe;
wapatula iwo amene wawayitana.
8Pa tsiku la nsembe ya Yehova
ndidzalanga akalonga
ndi ana aamuna a mfumu
ndi onse amene amavala
zovala zachilendo.
9Pa tsiku limenelo ndidzalanga
onse amene safuna kuponda pa chiwundo,
amene amadzaza nyumba ya ambuye awo
ndi chiwawa ndi chinyengo.
10“Pa tsiku limenelo,” akutero Yehova,
“Kufuwula kwakukulu kudzamveka pa Chipata cha Nsomba,
kulira kwa chisoni kuchokera mʼChigawo Chatsopano,
ndi phokoso la kugumuka kochokera ku mapiri.
11Lirani mwachisoni, inu amene mumakhala kumene kuli msika;
a malonda anu onse adzapululidwa,
ndiponso onse amene ali ndi siliva adzawonongedwa.
12Pa nthawi imeneyo ndidzafufuzafufuza mu Yerusalemu ndi nyale
ndi kulanga onse amene sakulabadira,
amene ali ngati vinyo wosakhutchumulidwa,
amene amaganiza kuti, ‘Yehova sadzachita chilichonse,
chabwino kaya choyipa.’
13Chuma chawo chidzafunkhidwa,
nyumba zawo zidzagwetsedwa.
Adzamanga nyumba,
koma osakhalamo;
adzadzala minda ya mpesa
koma sadzamwako vinyo wake.”
Tsiku Lalikulu la Yehova
14Tsiku lalikulu la Yehova layandikira,
layandikira ndipo lifika msanga.
Tamverani! Kulira kwa pa tsiku la Yehova kudzakhala kowawa,
ngakhale munthu wolimba mtima adzalira kwambiri.
15Tsiku limenelo lidzakhala la ukali,
tsiku losautsa ndi lomvetsa chisoni,
tsiku la mavuto ndi la chiwonongeko,
tsiku la mdima ndi lachisoni,
tsiku la mitambo ndi la mdima wandiweyani.
16Tsiku loliza lipenga ndi la mfuwu wankhondo,
tsiku la kugwa kwa mizinda yotetezedwa
ndi nsanja za pa ngodya.
17Ndidzabweretsa msautso pa anthu
ndipo adzayenda ngati anthu osaona,
chifukwa achimwira Yehova,
magazi awo adzamwazika ngati fumbi
ndi mnofu wawo ngati ndowe.
18Ngakhale siliva wawo kapena golide wawo
sadzatha kuwapulumutsa
pa tsiku la ukali wa Yehova.
Dziko lonse lapansi lidzanyeka
mʼmoto wa nsanje yake
chifukwa adzakantha modzidzimutsa
onse okhala pa dziko lapansi.
1اين است پيامی كه خداوند در دوران سلطنت يوشيا (پسر آمون)، پادشاه يهودا، به صفنيا داد. (صفنيا پسر كوشی، كوشی پسر جدليا، جدليا پسر امريا، و امريا پسر حزقيای پادشاه بود.)
روز داوری خدا
2خداوند میفرمايد: «همه چيز را از روی زمين محو و نابود خواهم كرد. 3انسانها و حيوانات، پرندگان هوا و ماهيان دريا را از بين خواهم برد. انسان شرور با همهٔ بتهايی كه میپرستد نابود خواهد شد.
4«يهودا و اورشليم را مجازات میكنم. آثار و بقايای پرستش بعل را از بين میبرم به طوری كه ديگر اسمی از كاهنان بت بعل باقی نماند. 5آنانی را كه بر بامها، آفتاب و ماه و ستارگان را پرستش میكنند و نيز كسانی را كه مرا میپرستند و به من سوگند وفاداری ياد میكنند ولی در عين حال بت مولک را نيز میپرستند، هلاک خواهم كرد. 6آنانی را كه از پيروی من برگشتهاند و كسانی را كه نزد من نمیآيند و از من راهنمايی نمیخواهند از بين خواهم برد.»
7در حضور خداوند خاموش باش، زيرا روز داوری او فرا رسيده است. خداوند قوم خود را برای كشته شدن آماده میسازد. او دشمنان آنها را دعوت كرده تا سرزمين يهودا را غارت كنند. 8خداوند میفرمايد: «در آن روز داوری، رهبران و رؤسای يهودا و تمام كسانی را كه از رسوم بتپرستان پيروی میكنند مجازات خواهم كرد. 9آری، آنانی را كه در پرستش خود، روشهای كافران را به کار میبرند و نيز كسانی را كه كشتار و غارت میكنند تا معابد خدايان خود را پر سازند، مجازات خواهم كرد. 10در آن روز صدای ناله و فرياد از دروازههای اورشليم به گوش خواهد رسيد و صدای نعرهٔ دشمن از تپهها شنيده خواهد شد.
11«ای بازاريان اورشليم، از غم و غصه شيون كنيد، زيرا تمام تاجران حريص شما نابود خواهند شد.
12«در آن روز، با چراغ در اورشليم خواهم گشت و كسانی را كه با خيال راحت گناه میورزند و گمان میكنند كه من كاری به كارشان ندارم، پيدا كرده مجازات خواهم نمود. 13اموالشان را به دست دشمن خواهم داد و خانههايشان را با خاک يكسان خواهم كرد. خانهها خواهند ساخت، ولی نخواهند توانست در آنها ساكن شوند. تاكستانها غرس خواهند كرد، ولی هرگز شراب آنها را نخواهند نوشيد.»
14آن روز هولناک نزديک است و به سرعت فرا میرسد. در آن روز مردان قدرتمند به تلخی خواهند گريست. 15آن روز، روزی است كه غضب خداوند افروخته میشود. روز سختی و اضطراب است، روز خرابی و ويرانی، روز تاريكی و ظلمت، روز ابرها و سياهیها! 16شيپور به صدا در میآيند، جنگ شروع میشود، شهرهای حصاردار و برجهای بلند واژگون میگردند.
17خداوند میفرمايد: «شما را مثل آدم كوری كه به دنبال راه میگردد، درمانده خواهم نمود، چون نسبت به من گناه ورزيدهايد. بنابراين، خون شما بر خاک ريخته خواهد شد و بدنهايتان همانجا روی زمين خواهد گنديد.»
18در آن روزِ غضبِ خدا، طلا و نقرهٔ شما نخواهد توانست جان شما را از مرگ برهاند، زيرا تمام زمين از آتش غيرت او گداخته خواهد شد. او به سرعت زمين را از وجود ساكنان آن پاک خواهد ساخت.