Yoweli 1 – CCL & CST

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Yoweli 1:1-20

1Yehova anayankhula ndi Yoweli mwana wa Petueli.

Kubwera kwa Dzombe

2Inu akuluakulu, imvani izi;

mvetserani, nonse amene mumakhala mʼdziko.

Kodi zinthu zokhala ngati izi zinayamba zaonekapo mʼnthawi yanu,

kapena mʼnthawi ya makolo anu?

3Muwafotokozere ana anu,

ndipo ana anuwo afotokozere ana awo,

ndipo ana awo adzafotokozere mʼbado winawo.

4Chimene dzombe losamera mapiko lasiya

dzombe lowuluka ladya;

chimene dzombe lowuluka lasiya

dzombe lalingʼono ladya;

chimene dzombe lalingʼono lasiya

chilimamine wadya.

5Dzukani, inu zidakwa ndipo mulire!

Lirani mofuwula, inu nonse amene mumamwa vinyo;

lirani mofuwula chifukwa cha vinyo watsopano,

pakuti wachotsedwa pakamwa panu.

6Mtundu wa anthu wathira nkhondo dziko langa,

wamphamvu ndi wosawerengeka;

uli ndi mano a mkango,

zibwano za mkango waukazi.

7Wawononga mphesa zanga

ndipo wathyola mitengo yanga ya mkuyu.

Wakungunula makungwa ake

ndi kuwataya,

kusiya nthambi zake zili mbee.

8Lirani ngati namwali wovala chiguduli,

chifukwa cha mwamuna wa utsikana wake.

9Chopereka cha chakudya ndi cha chakumwa

sizikuperekedwa ku nyumba ya Yehova.

Ansembe akulira,

amene amatumikira pamaso pa Yehova.

10Minda yaguga,

nthaka yauma;

tirigu wawonongeka,

vinyo watsopano watha,

mitengo ya mafuta yauma.

11Khalani ndi nkhawa, inu alimi,

lirani mofuwula inu alimi a mphesa;

imvani chisoni chifukwa cha tirigu ndi barele,

pakuti zokolola za mʼmunda zawonongeka.

12Mpesa wauma

ndipo mtengo wamkuyu wafota;

makangadza, kanjedza ndi mitengo ya apulosi,

mitengo yonse ya mʼmunda yauma.

Ndithudi chimwemwe cha anthu

chatheratu.

Mulungu Ayitana Anthu kuti Atembenuke

13Inu ansembe, valani ziguduli ndipo lirani;

lirani mofuwula, inu amene mumatumikira pa guwa lansembe.

Bwerani, fundani ziguduli usiku wonse,

inu amene mumatumikira pamaso pa Mulungu wanga;

pakuti chopereka cha chakudya ndi cha chakumwa

sizikupezekanso mʼnyumba ya Mulungu wanu.

14Lengezani tsiku lopatulika losala zakudya,

itanani msonkhano wopatulika.

Sonkhanitsani akuluakulu

ndi anthu onse okhala mʼdziko

ku nyumba ya Yehova Mulungu wanu

ndipo alirire Yehova.

15Kalanga ine tsikulo!

Pakuti tsiku la Yehova layandikira;

lidzabwera ngati chiwonongeko chochokera kwa Wamphamvuzonse.

16Kodi chakudya chathu sichachotsedwa

ife tikuona?

Kodi mʼnyumba ya Mulungu wathu

simulibe chimwemwe ndi chisangalalo?

17Mbewu zikunyala

poti pansi ndi powuma.

Nyumba zosungiramo zinthu zawonongeka;

nkhokwe zapasuka

popeza tirigu wauma.

18Taonani mmene zikulirira ziweto;

ngʼombe zikungoyenda uku ndi uku

chifukwa zilibe msipu;

ngakhalenso nkhosa zikusauka.

19Kwa Inu Yehova ndilirira,

pakuti moto wapsereza msipu wakuthengo,

malawi amoto apsereza mitengo yonse ya mʼtchire.

20Ngakhale nyama zakuthengo zikulirira Inu;

timitsinje tonse taphwa

ndipo moto wapsereza msipu wa kuthengo.

Nueva Versión Internacional (Castilian)

Joel 1:1-20

1Esta es la palabra del Señor, que vino a Joel hijo de Petuel.

La invasión de langostas

2¡Oíd esto, ancianos del pueblo!

¡Prestad atención, habitantes todos del país!

¿Alguna vez sucedió cosa semejante

en vuestros tiempos o en los de vuestros antepasados?

3Contádselo a vuestros hijos,

y que ellos se lo cuenten a los suyos,

y estos a la siguiente generación.

4Lo que dejaron las langostas grandes

lo devoraron las langostas pequeñas;

lo que dejaron las langostas pequeñas

se lo comieron las larvas;

y lo que dejaron las larvas

se lo comieron las orugas.1:4 El texto hebreo en este versículo usa cuatro términos que se refieren a langostas y que son de difícil traducción; también en 2:25.

5¡Despertad, borrachos, y llorad!

Gemid, todos los entregados al vino,

porque el vino dulce os fue arrebatado de los labios.

6Una nación poderosa e innumerable

ha invadido mi país:

tiene dientes de león,

colmillos de leona.

7Asoló mis vides,

desgajó mis higueras.

Las peló hasta dejar blancas sus ramas;

¡las derribó por completo!

8Mi pueblo gime como virgen vestida de luto

por la muerte de su prometido.

9Las ofrendas de cereales y las libaciones

no se ofrecen ya en la casa del Señor.

Hacen duelo los sacerdotes,

los ministros del Señor.

10Los campos yacen devastados,

reseca está la tierra;

han sido arrasados los cereales,

se ha secado el vino nuevo

y agotado el aceite.

11Secaos también vosotros, labradores;

gemid, viñadores,

por el trigo y la cebada,

porque se ha perdido la cosecha de los campos.

12La vid se marchitó;

languideció la higuera;

se marchitaron los granados,

las palmeras, los manzanos,

¡todos los árboles del campo!

¡Y hasta la alegría de la gente acabó por marchitarse!

Llamado al arrepentimiento

13Vestíos de duelo y gemid, sacerdotes;

lamentaos, ministros del altar.

Venid, ministros de mi Dios,

y pasad la noche vestidos de luto,

porque las ofrendas de cereales y las libaciones

han sido suspendidas en la casa de vuestro Dios.

14Proclamad ayuno,

convocad una asamblea solemne.

Reunid a los ancianos del pueblo

en la casa del Señor vuestro Dios;

reunid a todos los habitantes del país,

y clamad al Señor.

15¡Ay de aquel día, el día del Señor, que ya se aproxima!

Vendrá como devastación de parte del Todopoderoso.

16¿No se nos arrebató el alimento

ante nuestros propios ojos,

y la alegría y el regocijo

de la casa de nuestro Dios?

17La semilla se pudrió

a pesar de haber sido cultivada.1:17 La semilla … cultivada. Texto de difícil traducción.

Los silos están en ruinas

y los graneros, derribados

porque la cosecha se perdió.

18¡Cómo brama el ganado!

Vagan sin rumbo las vacas

porque no tienen donde pastar,

y sufren también las ovejas.

19A ti clamo, Señor,

porque el fuego ha devorado los pastizales de la estepa;

las llamas han consumido todos los árboles silvestres.

20Aun los animales del campo te buscan con ansiedad,

porque se han secado los arroyos

y el fuego ha devorado los pastizales de la estepa.