Hoseya 14 – CCL & CST

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Hoseya 14:1-9

Kulapa Kubweretsa Madalitso

1Iwe Israeli bwerera kwa Yehova Mulungu wako.

Machimo anu ndi amene akugwetsani!

2Bweretsani zopempha zanu

ndipo bwererani kwa Yehova.

Munene kwa Iye kuti,

“Tikhululukireni machimo athu onse

ndi kutilandira mokoma mtima,

kuti tithe kukuyamikani ndi mawu a pakamwa pathu.

3Asiriya sangatipulumutse;

ife sitidzakwera pa akavalo ankhondo,

sitidzanenanso kuti, ‘Milungu yathu’

kwa zimene manja athu omwe anazipanga,

pakuti ndinu amene mumachitira chifundo ana amasiye.”

4Ine ndidzachiza kusakhulupirika kwawo

ndipo ndidzawakonda mwaufulu

pakuti ndaleka kuwakwiyira.

5Ndidzakhala ngati mame kwa Israeli

Ndipo iye adzachita maluwa ngati kakombo.

Adzazika mizu yake pansi

ngati mkungudza wa ku Lebanoni;

6mphukira zake zidzakula.

Kukongola kwake kudzakhala ngati mtengo wa olivi,

kununkhira kwake ngati mkungudza wa ku Lebanoni.

7Anthu adzakhalanso mu mthunzi wake.

Iye adzakula bwino ngati tirigu.

Adzachita maluwa ngati mphesa

ndipo kutchuka kwake kudzakhala ngati vinyo wochokera ku Lebanoni.

8Efereimu adzati, “Ndidzachita nawonso chiyani mafano?

Ine ndidzamuyankha ndi kumusamalira.

Ine ndili ngati mtengo wa payini wobiriwira;

zipatso zako zimachokera kwa Ine.”

9Ndani ali ndi nzeru? Adzazindikire zinthu izi.

Ndani amene amamvetsa zinthu? Adzamvetse izi.

Njira za Yehova ndi zolungama;

anthu olungama amayenda mʼmenemo,

koma anthu owukira amapunthwamo.

Nueva Versión Internacional (Castilian)

Oseas 14:1-9

Arrepentimiento para traer bendición

1Vuélvete, Israel, al Señor tu Dios.

¡Tu perversidad te ha hecho caer!

2Piensa bien lo que le dirás,

y vuélvete al Señor con este ruego:

«Perdónanos nuestra perversidad,

y recíbenos con benevolencia,

pues queremos ofrecerte

el fruto de nuestros labios.

3Asiria no podrá salvarnos;

no montaremos caballos de guerra.

Nunca más llamaremos “dios nuestro”

a cosas hechas por nuestras manos,

pues en ti el huérfano halla compasión».

Respuesta de Dios

4«Yo corregiré su rebeldía

y los amaré de pura gracia,

porque mi ira contra ellos se ha calmado.

5Yo seré para Israel como el rocío,

y lo haré florecer como lirio.

¡Hundirá sus raíces como cedro del Líbano!

6Sus vástagos crecerán,

y tendrán el esplendor del olivo

y la fragancia del cedro del Líbano.

7Volverán a habitar bajo mi sombra,

y crecerán como el trigo.

Echarán renuevos, como la vid,

y serán tan famosos como el vino del Líbano.

8Efraín, ¿qué tengo yo que ver con las imágenes?

¡Soy yo quien te responde y cuida de ti!

Soy como un pino siempre verde;

tu fruto procede de mí».

9El que es sabio entiende estas cosas;

el que es inteligente las comprende.

Ciertamente son rectos los caminos del Señor:

en ellos caminan los justos,

mientras que allí tropiezan los rebeldes.