Yoweli 2 – CCL & CST

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Yoweli 2:1-32

Chilango cha Mulungu

1Lizani lipenga mu Ziyoni.

Chenjezani pa phiri langa loyera.

Onse okhala mʼdziko anjenjemere,

pakuti tsiku la Yehova likubwera,

layandikira;

2tsiku la mdima ndi chisoni,

tsiku la mitambo ndi la mdima wandiweyani.

Ngati mʼbandakucha umene wakuta mapiri,

gulu lalikulu ndi la ankhondo amphamvu likubwera,

gulu limene nʼkale lomwe silinaonekepo

ngakhale kutsogolo kuno silidzaonekanso.

3Patsogolo pawo moto ukupsereza,

kumbuyo kwawo malawi amoto akutentha zinthu.

Patsogolo pawo dziko lili ngati munda wa Edeni,

kumbuyo kwawo kuli ngati chipululu,

kulibe kanthu kotsalapo.

4Maonekedwe awo ali ngati akavalo;

akuthamanga ngati akavalo ankhondo.

5Akulumpha pamwamba pa mapiri

ndi phokoso ngati la magaleta,

ngati moto wothetheka wonyeketsa ziputu,

ngati gulu lalikulu la ankhondo lokonzekera nkhondo.

6Akangowaona, anthu a mitundu ina amazunzika mu mtima;

nkhope iliyonse imagwa.

7Amathamanga ngati ankhondo;

amakwera makoma ngati asilikali.

Onse amayenda pa mizere,

osaphonya njira yawo.

8Iwo sakankhanakankhana,

aliyense amayenda molunjika.

Amadutsa malo otchingidwa

popanda kumwazikana.

9Amakhamukira mu mzinda,

amathamanga mʼmbali mwa khoma.

Amakwera nyumba ndi kulowamo;

amalowera pa zenera ngati mbala.

10Patsogolo pawo dziko limagwedezeka,

thambo limanjenjemera,

dzuwa ndi mwezi zimachita mdima,

ndipo nyenyezi zimaleka kuwala.

11Yehova amabangula

patsogolo pawo,

gulu lake lankhondo ndi losawerengeka,

ndipo amphamvu ndi amene amamvera kulamula kwake.

Tsiku la Yehova ndi lalikulu;

ndi loopsa.

Ndani adzapirira pa tsikulo?

Ngʼambani Mtima Wanu

12“Ngakhale tsopano,

bwererani kwa Ine ndi mtima wanu wonse

posala zakudya ndi kukhetsa misozi,” akutero Yehova.

13Ngʼambani mtima wanu

osati zovala zanu.

Bwererani kwa Yehova Mulungu wanu,

pakuti Iye ndi wokoma mtima ndi wachifundo,

wosakwiya msanga ndi wachikondi chochuluka,

ndipo amaleka kubweretsa mavuto.

14Akudziwa ndani? Mwina adzasintha maganizo nʼkutimvera chisoni,

nʼkutisiyira madalitso,

a chopereka cha chakudya ndi cha chakumwa

kwa Yehova Mulungu wanu.

15Lizani lipenga mu Ziyoni,

lengezani tsiku losala zakudya,

itanitsani msonkhano wopatulika.

16Sonkhanitsani anthu pamodzi,

muwawuze kuti adziyeretse;

sonkhanitsani akuluakulu,

sonkhanitsani ana,

sonkhanitsani ndi oyamwa omwe.

Mkwati atuluke mʼchipinda chake,

mkwatibwi atuluke mokhala mwake.

17Ansembe amene amatumikira pamaso pa Yehova,

alire pakati pa guwa lansembe ndi khonde la Nyumba ya Yehova.

Azinena kuti, “Inu Yehova, achitireni chifundo anthu anu.

Musalole kuti cholowa chanu chikhale chinthu chonyozeka,

kuti anthu a mitundu ina awalamulire.

Kodi nʼchifukwa chiyani anthu a mitundu ina amanena kuti,

‘Ali kuti Mulungu wawo?’ ”

Yankho la Yehova

18Pamenepo Yehova adzachitira nsanje dziko lake

ndi kuchitira chisoni anthu ake.

19Yehova adzawayankha kuti,

“Ine ndikukutumizirani tirigu, vinyo watsopano ndi mafuta

ndipo mudzakhuta ndithu;

sindidzakuperekaninso kuti mukhale chitonzo

kwa anthu a mitundu ina.

20“Ine ndidzachotsa ankhondo akumpoto kuti apite kutali ndi inu,

kuwapirikitsira ku dziko lowuma ndi lachipululu,

gulu lawo lakutsogolo ndidzalipirikitsira ku nyanja ya kummawa

ndi gulu lawo lakumbuyo, ku nyanja ya kumadzulo.

Ndipo mitembo yawo idzawola,

fungo lake lidzamveka.”

Zoonadi Yehova wachita zinthu zazikulu.

21Iwe dziko usachite mantha;

sangalala ndipo kondwera.

Zoonadi Yehova wachita zinthu zazikulu.

22Inu nyama zakuthengo, musachite mantha,

pakuti msipu wa ku chipululu ukuphukira.

Mitengo ikubala zipatso zake;

mitengo ya mkuyu ndi mpesa ikubereka kwambiri.

23Inu anthu a ku Ziyoni sangalalani,

kondwerani mwa Yehova Mulungu wanu,

pakuti wakupatsani

mvula yoyambirira mwachilungamo chake.

Iye wakutumizirani mivumbi yochuluka,

mvula yoyambirira ndi mvula ya nthawi ya mphukira, monga poyamba paja.

24Pa malo opunthira padzaza tirigu;

mʼmitsuko mudzasefukira vinyo watsopano ndi mafuta.

25“Ine ndidzakubwezerani zonse zimene zinawonongedwa ndi dzombe,

dzombe lalikulu ndi dzombe lalingʼono,

dzombe lopanda mapiko ndi dzombe lowuluka;

gulu langa lalikulu la nkhondo limene ndinalitumiza pakati panu.

26Mudzakhala ndi chakudya chambiri, mpaka mudzakhuta,

ndipo mudzatamanda dzina la Yehova Mulungu wanu,

amene wakuchitirani zodabwitsa;

ndipo anthu anga sadzachitanso manyazi.

27Pamenepo inu mudzadziwa kuti Ine ndili mu Israeli,

kuti Ine ndine Yehova Mulungu wanu,

ndi kuti palibenso wina;

ndipo anthu anga sadzachitanso manyazi.

Tsiku la Yehova

28“Ndipo patapita nthawi,

ndidzakhuthulira Mzimu wanga pa anthu onse.

Ana anu aamuna ndi ana anu aakazi adzanenera,

nkhalamba zanu zidzalota maloto,

anyamata anu adzaona masomphenya.

29Ngakhalenso pa antchito anga aamuna ndi aakazi

ndidzakhuthulira Mzimu wanga masiku amenewo.

30Ndidzaonetsa zodabwitsa mlengalenga

ndi pa dziko lapansi,

ndizo magazi, moto ndi utsi watolotolo.

31Dzuwa lidzadetsedwa

ndipo mwezi udzaoneka ngati magazi

lisanafike tsiku lalikulu ndi loopsa la Ambuye.

32Ndipo aliyense amene adzayitana

pa dzina la Ambuye adzapulumuka;

pakuti chipulumutso chidzakhala pa Phiri la Ziyoni

ndi mu Yerusalemu,

monga Yehova wanenera,

pakati pa otsala

amene Yehova wawayitana.

Nueva Versión Internacional (Castilian)

Joel 2:1-32

Un ejército de langostas

1Tocad la trompeta en Sión;

dad la voz de alarma en mi santo monte.

Tiemblen todos los habitantes del país,

pues ya viene el día del Señor;

en realidad ya está cerca.

2Día de tinieblas y oscuridad,

día de nubes y densos nubarrones.

Como la aurora que se extiende sobre los montes,

así avanza un pueblo fuerte y numeroso,

pueblo como nunca lo hubo en la antigüedad

ni lo habrá en las generaciones futuras.

3El fuego devora delante de ellos;

detrás, las llamas lo queman todo.

Antes de su llegada, el país se parece al jardín del Edén;

después, queda un desolado desierto;

¡nada escapa a su poder!

4Tienen aspecto de caballos;

galopan como corceles.

5Y al saltar sobre las cumbres de los montes,

producen un estruendo como el de carros de guerra,

como el crepitar del fuego al consumir la hojarasca.

¡Son como un ejército poderoso en formación de batalla!

6Ante él se estremecen las naciones;

todo rostro palidece.

7Atacan como guerreros,

escalan muros como soldados.

Cada uno mantiene la marcha

sin romper la formación.

8No se atropellan entre sí;

cada uno marcha en línea.

Se lanzan entre las flechas

sin romper filas.

9Se abalanzan contra la ciudad,

arremeten contra los muros,

trepan por las casas,

se meten por las ventanas como ladrones.

10Ante este ejército tiembla la tierra

y se estremece el cielo,

el sol y la luna se oscurecen

y las estrellas dejan de brillar.

11Truena la voz del Señor

al frente de su ejército;

son innumerables sus tropas

y poderosos los que ejecutan su palabra.

El día del Señor es grande y terrible.

¿Quién lo podrá resistir?

Exhortación al arrepentimiento

12«Ahora bien —afirma el Señor—,

volveos a mí de todo corazón,

con ayuno, llantos y lamentos».

13Rasgaos el corazón

y no las vestiduras.

Volveos al Señor vuestro Dios,

porque él es bondadoso y compasivo,

lento para la ira y lleno de amor,

cambia de parecer y no castiga.

14Tal vez Dios reconsidere y cambie de parecer,

y deje tras de sí una bendición.

Las ofrendas de cereales y las libaciones

son del Señor vuestro Dios.

15Tocad la trompeta en Sión,

proclamad el ayuno,

convocad una asamblea solemne.

16Congregad al pueblo,

purificad la asamblea;

juntad a los ancianos del pueblo,

reunid a los pequeños

y a los niños de pecho.

Que salga de su alcoba el recién casado,

y la recién casada de su cámara nupcial.

17Lloren, sacerdotes, ministros del Señor,

entre el pórtico y el altar;

y digan: «Compadécete, Señor, de tu pueblo.

No entregues tu propiedad al oprobio,

para que las naciones no se burlen de ella.2:17 no se burlen de ella. Alt. no la sometan.

¿Por qué habrán de decir entre los pueblos:

“Dónde está su Dios?”»

La respuesta del Señor

18Entonces el Señor mostró amor por su tierra

y perdonó a su pueblo.

19Y les respondió el Señor:

«Mirad, os enviaré cereales, vino nuevo y aceite,

hasta dejaros plenamente satisfechos;

y no volveré a entregaros

al oprobio entre las naciones.

20»Alejaré de vosotros al que viene del norte,

arrojándolo hacia una tierra seca y desolada:

lanzaré su vanguardia hacia el mar oriental,

y su retaguardia hacia el mar occidental.2:20 el mar oriental … el mar occidental. Es decir, el Mar Muerto y el Mediterráneo.

Subirá su hedor

y se elevará su fetidez».

¡El Señor hará grandes cosas!

21No temas, tierra,

sino alégrate y regocíjate,

porque el Señor hará grandes cosas.

22No temáis, animales del campo,

porque los pastizales de la estepa reverdecerán;

los árboles producirán su fruto,

y la higuera y la vid darán su riqueza.

23Alegraos, hijos de Sión,

regocijaos en el Señor vuestro Dios,

que a su tiempo os dará las lluvias de otoño.

Os enviará la lluvia,

la de otoño y la de primavera,

como en tiempos pasados.

24Las eras se llenarán de grano;

los lagares rebosarán de vino nuevo y de aceite.

25«Yo os compensaré a vosotros

por los años en que todo lo devoró

ese gran ejército de langostas

que envié contra vosotros:

las grandes, las pequeñas,

las larvas y las orugas.2:25 Véase nota en 1:4.

26Comeréis en abundancia, hasta saciaros,

y alabaréis el nombre del Señor vuestro Dios,

que hará maravillas con vosotros.

¡Nunca más será avergonzado mi pueblo!

27Entonces sabréis que yo estoy en medio de Israel,

que yo soy el Señor vuestro Dios,

y no hay otro fuera de mí.

¡Nunca más será avergonzado mi pueblo!

El día del Señor

28»Después de esto,

derramaré mi Espíritu sobre todo ser humano.

Vuestros hijos y vuestras hijas profetizarán,

tendrán sueños los ancianos

y visiones los jóvenes.

29En esos días derramaré mi Espíritu

aun sobre los siervos y las siervas.

30En el cielo y en la tierra mostraré prodigios:

sangre, fuego y columnas de humo.

31El sol se convertirá en tinieblas

y la luna en sangre

antes que llegue el día del Señor,

día grande y terrible.

32Y todo el que invoque el nombre del Señor

escapará con vida,

porque en el monte Sión y en Jerusalén

habrá escapatoria,

como lo ha dicho el Señor.

Y entre los sobrevivientes

estarán los llamados del Señor.