Yoswa 6 – CCL & NSP

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Yoswa 6:1-27

1Tsono mzinda wa Yeriko unali utatsekedwa kuti Aisraeli asalowe. Palibe amene amatuluka kapena kulowa.

2Kenaka Yehova anati kwa Yoswa, “Taona ndapereka Yeriko, pamodzi ndi mfumu yake ndi ankhondo ake mʼmanja mwako. 3Tsono iwe pamodzi ndi ankhondo ako onse muzizungulira mzindawu masiku asanu ndi limodzi, kamodzi pa tsiku. 4Ansembe asanu ndi awiri, atanyamula malipenga a nyanga za nkhosa zazimuna, akhale patsogolo pa Bokosi la Chipangano. Pa tsiku lachisanu ndi chiwiri mudzazungulire mzindawu kasanu ndi kawiri ansembe akuliza malipenga. 5Ansembe adzalize malipenga kosalekeza. Tsono anthu onse akadzamva kuliza kumeneku adzafuwule kwambiri, ndipo makoma a mzindawo adzagwa. Zikadzatero ankhondo adzalowe mu mzindawo.”

6Ndipo Yoswa mwana wa Nuni anayitana ansembe ndipo anawawuza kuti, “Nyamulani Bokosi la Chipangano cha Yehova ndipo ansembe asanu ndi awiri anyamule malipenga. Iwowa akhale patsogolo pake.” 7Ndipo analamulira anthu kuti, “Yambani kuyenda! Yendani mozungulira mzinda ndipo ankhondo akhale patsogolo pa Bokosi la Yehova.”

8Mofanana ndi mmene Yoswa anayankhulira kwa anthu aja, ansembe asanu ndi awiri anapita patsogolo pa Bokosi la Chipangano la Yehova akuliza malipenga a nyanga za nkhosa zija, ndipo Bokosi la Chipangano cha Yehova limabwera pambuyo pawo. 9Ankhondo amayenda patsogolo pa ansembe amene amayimba malipenga, ndiponso gulu lina pambuyo pa Bokosilo. Nthawi yonseyi nʼkuti malipenga akulira. 10Koma Yoswa nʼkuti atalamulira anthu kuti, “Musafuwule, musakweze mawu anu kapena kuyankhula mpaka tsiku limene ndidzakuwuzani kuti mufuwule. Pamenepo mudzafuwule!” 11Ansembe onyamula Bokosi la Chipangano la Yehova anazungulira mzindawo kamodzi. Kenaka anthu anabwerera ku msasa wawo kukagona.

12Yoswa anadzuka mmawa tsiku linalo ndipo ansembe ananyamula Bokosi la Yehova. 13Ansembe asanu ndi awiri onyamula malipenga asanu ndi awiri anakhala patsogolo pa Bokosi la Yehova akuyimba malipenga. Ankhondo anali patsogolo pawo ndipo gulu lina linatsatira Bokosi la Yehova. Apa nʼkuti malipenga akulira. 14Tsiku lachiwiri anazunguliranso mzinda kamodzi ndi kubwerera ku misasa. Iwo anachita izi kwa masiku asanu ndi limodzi.

15Pa tsiku lachisanu ndi chiwiri, anadzuka mʼbandakucha ndipo anazungulira mzindawo kasanu ndi kawiri. Ndi pa tsiku lokhali limene anazungulira mzindawu kasanu ndi kawiri. 16Pomwe amazungulira kachisanu ndi chiwiri, ansembe akuliza malipenga mokweza, Yoswa analamulira anthu kuti “Fuwulani pakuti Yehova wakupatsani mzindawu! 17Mzindawu ndi zonse zimene zili mʼmenemo muziwononge. Rahabe yekha, mayi wadama, ndi aliyense amene ali pamodzi naye mʼnyumba mwake asaphedwe, chifukwa anabisa anthu odzazonda, amene ife tinawatuma 18Koma musatenge kanthu kalikonse koyenera kuwonongedwa. Mukadzangotenga kanthu kalikonse koyenera kuwonongedwa, mudzaputa mavuto, misasa ya Israeli idzawonongedwa. 19Zonse za siliva ndi golide, ziwiya zamkuwa ndi zachitsulo, ndi zake za Yehova ndipo ziyenera kukasungidwa mosungiramo chuma chake.”

20Ansembe analiza malipenga. Anthu atamva kulira kwa malipenga, anafuwula kwambiri ndipo makoma a Yeriko anagwa. Choncho ankhondo anabwera ku mzinda uja nawulanda. 21Iwo analowa mu mzindawo nawononga ndi lupanga chilichonse chamoyo kuyambira amuna, akazi, ana ndi akulu, ngʼombe, nkhosa ndi abulu.

22Yoswa anawuza anthu awiri amene anakazonda dziko aja kuti, “Pitani ku nyumba ya mkazi wadama uja ndipo mukamutulutse iye pamodzi ndi onse amene ali naye ndipo mukabwere nawo kuno, munamulumbirira.” 23Choncho iwo anapita nakatenga Rahabe, abambo ake ndi amayi ake, abale ake ndi onse amene anali naye. Iwo anatulutsa banja lake lonse ndipo analiyika kuseri kwa msasa wa Aisraeli.

24Kenaka iwo anawotcha mzinda wonse ndi chilichonse chimene chinali mʼmenemo, kupatulapo zasiliva ndi zagolide pamodzi ndi ziwiya zamkuwa ndi zachitsulo zimene anakaziyika mʼnyumba yosungiramo chuma cha Yehova. 25Koma Yoswa sanaphe Rahabe, mkazi wadamayo pamodzi ndi banja lake ndi onse amene anali naye, chifukwa anabisa anthu amene iye anawatuma kukazonda Yeriko. Zidzukulu zake za Rahabeyo zikukhala pakati pa Aisraeli mpaka lero.

26Pa nthawi imeneyo Yoswa anapereka chenjezo motemberera kuti, “Akhale wotembereredwa pamaso pa Yehova munthu amene adzamangenso mzinda uwu wa Yeriko:

“Aliyense amene adzayike maziko ake,

mwana wake wamwamuna wachisamba adzafa,

aliyense womanga zipata zake

mwana wake wamngʼono adzafa.”

27Motero Yehova anali ndi Yoswa, ndipo mbiri yake inafalikira dziko lonse.

New Serbian Translation

Књига Исуса Навина 6:1-27

Пад Јерихона

1А Јерихон је био затворен и јако утврђен пред Израиљцима; нико није излазио нити улазио.

2Тада Господ рече Исусу: „Погледај, предаћу у твоје руке Јерихон, његовог цара и његове ратнике. 3Сви ви, ратници, обиђите око града једанпут. Тако чините шест дана. 4Нека седам свештеника носе седам труба од овнујских рогова пред Ковчегом. Седмога дана обиђите око града седам пута, а свештеници нека затрубе у трубе. 5Кад се труба од овнујског рога огласи отегнутим звуком, нека сав народ, чим чује глас трубе, викне у сав глас, па ће пасти зидови града. Тада сав народ нека крене у напад, сваки оданде где се задеси.“

6Исус, син Навинов, позва свештенике и рече им: „Понесите Ковчег савеза, а седам свештеника нека понесу седам труба од овнујских рогова испред Ковчега Господњег.“ 7А народу рече: „Пођите и обиђите око града, а ратници нека иду испред Ковчега Господњег.“

8Кад је Исус то заповедио народу, кренуше свештеници који носе седам труба од овнујских рогова пред Господом. Трубили су у рогове, а Ковчег савеза је ишао за њима. 9Ратници су ишли испред свештеника који су трубили у рогове, док је остали народ ишао за Ковчегом. Ишли су тако док је одзвањао звук труба. 10Исус је био заповедио народу: „Не вичите и не дижите глас, и нека реч не пређе преко ваших усана, све до дана када вам кажем: ’Вичите!’ Тада вичите.“

11Онда је наредио да Ковчег Господњи обиђе једном око града, па су се вратили у табор и преноћили у њему. 12Следећег дана Исус порани, а свештеници подигну Ковчег Господњи. 13Седам свештеника који су носили седам труба од овнујских рогова ишли су пред Ковчегом Господњим и трубили у рогове. Ратници су ступали пред њима, а остали народ је ишао за Ковчегом Господњим док су трубе одјекивале. 14И другог дана су једном обишли око града, па су се вратили у табор. Тако су чинили шест дана.

15Седмога дана у освит зоре поране и на исти начин обиђу седам пута око града. Само су тога дана обишли око града седам пута. 16Кад су свештеници седми пут затрубили у рогове, Исус рече народу: „Вичите, јер вам је Господ предао град! 17Нека град и све што је у њему буде посвећено Господу за уништење. Само Рахава блудница нека остане у животу, она и сви који су са њом у кући, зато што је сакрила уходе које смо послали. 18А ви се држите даље од онога што је посвећено за уништење, да не бисте сами били изручени уништењу: ако узмете нешто од онога што је посвећено за уништење, изложићете уништењу израиљски табор и навући на њега пропаст. 19Све сребро, злато, бронзано и гвоздено посуђе посвећено је Господу; нека се донесе у ризницу Господњу.“

20Тако је народ повикао на глас труба. Чим је чуо глас труба, народ кликну громким гласом, а зидине града падоше. Народ онда крену на град, свако оданде где се задесио, па освојише град. 21Изручили су клетом уништењу све који су се нашли у граду: побили су мачем мушкарце и жене, младо и старо, волове, овце и магарце.

22А оној двојици што су уходили земљу, Исус рече: „Идите у кућу оне жене блуднице и изведите је оданде, њу и све њене, као што сте јој се заклели!“ 23Младићи, уходе, оду и изведу Рахаву, њеног оца и њену мајку, њену браћу и све њене. Извели су сву њену родбину и сместили их изван израиљског табора.

24А град и све што је у њему су спалили огњем. Само су сребро и злато, те бронзано и гвоздено посуђе ставили у ризницу Дома Господњег. 25Исус је поштедео блудницу Рахаву и дом њеног оца, и све што је било њено. Она је остала међу Израиљцима све до дана данашњега, јер је сакрила уходе које је Исус послао да уходе Јерихон.

26У то време је Исус изрекао ову клетву: „Проклет био човек пред Господом, који поново подигне и сазида овај град, Јерихон.

Положио му темеље по цену

свога првенца,

а врата по цену

свога најмлађега!“

27Господ је био са Исусом и глас о њему се прочуо по целој земљи.