Deuteronomo 1 – CCL & NSP

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Deuteronomo 1:1-46

Mose Akumbutsa Aisraeli za ku Horebu

1Awa ndi mawu amene Mose anayankhula kwa Aisraeli onse mʼchipululu kummawa kwa Yorodani, ku Araba moyangʼanana ndi Sufi, pakati pa Parani ndi Tofeli, Labani, Heziroti ndi Dizahabu. 2(Kuyenda kuchokera ku Horebu kukafika ku Kadesi Barinea kudzera njira ya ku Phiri la Seiri ndi ulendo wa masiku khumi ndi limodzi).

3Mʼchaka cha makumi anayi, pa tsiku loyamba la mwezi 11, Mose anafotokozera Aisraeli zonse zimene Yehova anamulamula zokhudza iwowo. 4Apa nʼkuti atagonjetsa Sihoni mfumu ya Aamori, amene amalamulira ku Hesiboni, ndipo pa Ederi anagonjetsa Ogi mfumu ya ku Basani, amene amalamulira mu Asiteroti.

5Chakummawa kwa Yorodani mʼchigawo cha Mowabu, Mose anayamba kufotokozera lamulo ili kunena kuti:

6Ku Horebu, Yehova Mulungu wathu anati kwa ife, “Mwakhalitsa pa phiri lino. 7Sasulani msasa ndipo pitani ku dziko la mapiri la Aamori. Pitani kwa anthu onse oyandikana nawo ku Araba, ku mapiri, mʼmbali mwa mapiri a ku madzulo, ku Negevi ndiponso mʼmbali mwa nyanja, ku dziko la Akanaani ndi ku Lebanoni mpaka ku mtsinje waukulu wa Yufurate. 8Taonani, Ine ndakupatsani dziko ili. Lowani ndi kulilanda dziko limene Yehova analumbira kuti adzapereka kwa makolo anu, Abrahamu, Isake ndi Yakobo komanso kwa zidzukulu zawo.”

Kukhazikitsa Atsogoleri

9Pa nthawi imeneyi ine ndinati kwa inu, “Inu ndinu katundu olemera kwambiri woti sindingathe kumunyamula ndekha. 10Yehova Mulungu wanu wakuchulukitsani kotero kuti lero lino ndinu ochuluka ngati nyenyezi za kumwamba. 11Yehova Mulungu wa makolo anu wachulukitsa chiwerengero chanu ndipo wakudalitsani monga momwe analonjezera! 12Koma nanga ndekha ndidzasenza bwanji zovuta ndi zipsinjo zanu komanso milandu yanu? 13Sankhani amuna ena anzeru, ozindikira ndi amene mumawalemekeza kuchokera ku mtundu uliwonse wa mitundu yanu, ndipo ndidzawayika kuti akulamulireni.”

14Inu munandiyankha kuti, “Maganizo amenewa ndi abwino kuwachita.”

15Choncho ndinatenga anthu otsogolera mafuko anu, anzeru ndi omwe mumawalemekeza, ndipo ndinawayika kuti azikulamulirani mʼmagulu a 1,000, ena 100, ena makumi asanu ndi ena khumi, kuti akhalenso ngati akapitawo a mafuko. 16Ndipo pa nthawi imeneyo ndinawawuza olamula anu kuti, “Muzimva milandu ya pakati pa abale anu ndi kuweruza mosakondera, kaya mlanduwo uli pakati pa Aisraeli okhaokha kapena mmodzi wa iwo ndi mlendo. 17Osamayangʼana nkhope poweruza koma muzimvetsera aangʼono ndi aakulu omwe chimodzimodzi. Musamaope munthu aliyense, pakuti chiweruzo ndi cha Mulungu. Muzindibweretsera mlandu uliwonse wovuta ndipo ndidzaumva.” 18Ndipo nthawi imeneyo ndinakuwuzani chilichonse chimene munayenera kuchita.

Atumizidwa Kukazonda Dziko

19Tsono monga Yehova Mulungu wathu anatilamulira, tinanyamuka kuchoka ku Horebu ndi kupita cha ku dziko lamapiri la Aamori kudzera ku chipululu chachikulu ndi choopsa chija munachionachi, kotero kuti tinakafika ku Kadesi Barinea. 20Ndipo ndinati kwa inu, “Mwafika ku dziko la mapiri la Aamori, limene Yehova Mulungu wathu akutipatsa. 21Taonani, Yehova Mulungu wanu wakupatsani dzikoli. Pitani ndi kulitenga monga Yehova, Mulungu wa makolo anu anakuwuzirani. Musaope kapenanso kugwa mphwayi.”

22Tsono nonse munabwera kwa ine ndi kuti, “Tiyeni titumize anthu ayambe apita kuti akazonde dzikolo ndi kutibweretsera mawu pa za njira yomwe tidzere ndi za mizinda imene tikafikireko.”

23Ndinaona kuti maganizo amenewa anali abwino, choncho ndinasankha anthu khumi ndi awiri, mmodzi ku fuko lililonse. 24Iwo ananyamuka napita mʼdziko la mapiri, ndipo anafika ku Chigwa cha Esikolo ndi kukazonda dzikolo. 25Pobwerera anatitengerako zipatso za mʼdzikomo ndipo anatipatsa mawu akuti, “Dziko limene Yehova Mulungu wathu akutipatsa ndi labwino.”

Awukira Yehova

26Koma inu simunafune kupitako ndipo munawukira lamulo la Yehova Mulungu wanu. 27Inu munanyinyirika mʼmatenti anu nʼkumati, “Mulungu amatida nʼchifukwa chake anatitulutsa ku Igupto kuti atipereke mʼmanja mwa Aamori kuti atiwononge. 28Tigwire mtengo wanji? Abale athu anatitayitsa mtima. Iwo akuti, ‘Anthuwo ndi amphamvu ndi aatali kuposa ife, mizindayo ndi yayikulu ndipo mipanda yake ndi yayitali yofika kumwamba. Ife tinaonanso Aanaki kumeneko.’ ”

29Ndipo ine ndinati kwa inu, “Musachite mantha kapena kuwaopa. 30Yehova Mulungu wanu, amene akukutsogolerani, adzakumenyerani nkhondo monga muja anachitira ku Igupto inu mukuona, 31ndi mʼchipululu muja. Kumeneko munaona mmene Yehova Mulungu wanu anakunyamulirani monga abambo anyamulira mwana wawo, njira yonse yomwe munayenda mpaka munafika pamalo ano.”

32Ngakhale zinali choncho, simunadalire Yehova Mulungu wanu 33amene anakutsogolerani pa ulendo wanu, ndi moto nthawi ya usiku ndi mtambo nthawi ya masana, kukufunirani malo woti mumange msasa ndi kukuonetsani njira yoti muyendemo.

34Yehova atamva zimene munanena anakwiya nalumbira kuti, 35“Palibe ndi mmodzi yemwe mwa mʼbado woyipawu amene adzaona dziko labwino limene ndinalumbira kupatsa makolo anu, 36kupatula Kalebe mwana wa Yefune. Iye adzaliona, ndipo ndidzamupatsa iye ndi adzukulu ake, dziko limene adzapondamo popeza anatsata Yehova ndi mtima wake wonse.”

37Chifukwa cha inu, Yehova anakwiyiranso ine ndipo anati, “Iwenso sudzalowa mʼdzikomo. 38Koma Yoswa mwana wa Nuni amene amakuthandiza, adzalowa mʼdzikomo. Umulimbikitse chifukwa adzatsogolera Israeli kukalandira dzikolo. 39Ndipo angʼonoangʼono amene munati adzagwidwa ukapolo, ana anu amene sanadziwe kusiyanitsa chabwino ndi choyipa, amenewo adzalowa mʼdzikolo. Ndidzalipereka kwa iwo ndipo lidzakhala lawo. 40Koma inu, tembenukani nyamukani kulowera cha ku chipululu kutsatira njira ya ku Nyanja Yofiira.”

41Ndipo inuyo munati, “Tachimwa pamaso pa Yehova. Tipita ndi kukachita nkhondo monga Yehova Mulungu wathu watilamulira.” Choncho aliyense wa inu anavala zankhondo, ndi kuganiza kuti nʼkosavuta kupita mʼdziko la mapiri lija.

42Koma Yehova anandiwuza kuti, “Awuze anthuwa kuti, ‘Musapite kukachita nkhondo chifukwa Ine sindidzakhala nanu. Mudzagonjetsedwa ndi adani anu.’ ”

43Choncho ndinakuwuzani koma simunamve. Inu munawukira lamulo la Yehova ndipo mwamwano munayenda kulowa mʼdziko la mapiri. 44Aamori amene ankakhala mʼmapiriwo anatuluka kukakumana nanu ndipo anakuthamangitsani ngati gulu la njuchi ndipo anakukanthani kuchokera ku Seiri, njira yonse mpaka ku Horima. 45Munabwererako mukulira pamaso pa Yehova, koma Iye sanalabadire kulira kwanuko ndipo sanakumvetsereni. 46Pamenepo munakhala ku Kadesi masiku ambiri kwa nthawi yayitali ndithu.

New Serbian Translation

5. Мојсијева 1:1-46

Увод

1Ово су речи које је Мојсије изговорио свем Израиљу с оне стране Јордана, у пустињи у Арави1,1 Арава, или пољана, пустињска равница. насупрот Суфу, између Фарана и Тофела, Лавана, Асирота и Ди Захава. 2А од Хорива до Кадис-Варније преко горе Сир има једанаест дана хода.

3Четрдесете године првога дана једанаестога месеца, Мојсије је рекао Израиљцима све што му је Господ заповедио да им каже. 4Након што је поразио аморејског цара Сихона који је владао у Есевону и васанског цара Ога који је владао у Астароту у Едрајину, 5с оне стране Јордана, у земљи моавској, Мојсије је почео да објашњава овај Закон. Говорио је:

6„Господ, наш Бог, рекао нам је на Хориву: ’Доста сте боравили на овој гори. 7Запутите се у горски крај Аморејаца и свих њихових суседа, у Араву, у горје, у равницу1,7 Сефела. и Негев, у Приморје, у земљу Хананаца, и у Ливан све до велике реке, реке Еуфрата. 8Погледајте! Предао сам вам ову земљу. Идите и заузмите ту земљу за коју се Господ заклео вашим оцима Аврахаму, Исаку и Јакову, да ће је дати њима и њиховом потомству после њих.’

Постављење вођа

9У то време сам вам рекао: ’Не могу сам управљати вама. 10Господ вас је толико умножио да вас је данас као звезда на небу. 11Господ, Бог ваших отаца, нека вас умножи хиљаду пута више! Нека вас благослови, као што вам је обећао! 12Како бих, иначе, ја сам могао да носим ваш терет, ваша бремена и спорове? 13Изаберите себи из свакога племена људе мудре, разумне и искусне да вам их поставим за главаре.’

14А ви сте ми одговорили: ’Добро је то што си рекао да ћеш учинити!’

15Тада сам узео главаре племена, људе мудре и искусне, па сам их поставио вама за главаре, за заповеднике јединица од хиљаду, стотину, педесет и десет, и за племенске заповеднике. 16У то време сам заповедио вашим судијама: ’Саслушајте своју браћу и судите праведно кад неко има спор са својим сународником, или са странцем. 17Не будите пристрани у суђењу, него саслушавајте како малог, тако великог. Не плашите се никога, јер суд припада Богу. Ако је спор сувише тежак за вас, донесите га мени да чујем.’ 18У то време сам вам заповедио све што имате да чините.

Послање ухода

19Затим смо отишли с Хорива, па смо прешли сву ону велику и застрашујућу пустињу коју сте видели на путу према горском крају Аморејаца, како нам је заповедио Господ, наш Бог. Тако смо дошли у Кадис-Варнију. 20Ја сам вам тада рекао: ’Дошли сте у горски крај Аморејаца, који вам даје Господ, Бог ваш. 21Види, Господ, Бог твој, предао ти је ову земљу. Успни се и освоји је, као што ти је рекао Господ, Бог твојих отаца. Не бој се и не страхуј!’

22Тада сте ми сви ви приступили и рекли: ’Хајде да пошаљемо људе испред нас да извиде земљу и донесу нам извештај о путу којим ћемо ићи и градовима у које ћемо доћи.’

23Овај предлог ми се допао. Зато сам одабрао између вас дванаесторицу људи, из сваког племена по једног. 24Они су кренули, успели се у горје, те дошли у долину Есхол и извидели је. 25Онда су понели у својим рукама плодове те земље, па су се спустили к нама и донели нам извештај. Рекли су: ’Земља коју нам Господ даје је добра.’

Побуна против Господа

26Међутим, ви нисте хтели да пођете горе, него сте се побунили против наредбе Господа, свога Бога. 27Гунђали сте у својим шаторима и говорили: ’Господ нас мрзи! Извео нас је из Египта да нас преда Аморејцима у руке, како би нас истребили. 28Куда да идемо? Наша браћа су напунила наше срце страхом, говорећи: „тај народ је већи и виши растом од нас, а градови су им огромни и опасани зидинама до небеса. И Енаковце смо тамо видели!“’

29Тада сам вам рекао: ’Не страхујте! Не бојте их се! 30Господ, Бог ваш, који иде пред вама, ратоваће за вас, као што је то чинио у Египту на ваше очи. 31У пустињи си видео да те је Господ, Бог твој, носио као што отац носи свога сина током целог пута који сте превалили све док нисте дошли до овог места.’

32Али и поред тога нисте се поуздали у Господа, Бога свога, 33који иде пред вама да вам потражи место за таборовање – ноћу у огњу да видите пут на који сте кренули, а дању у облаку.

34Кад је Господ чуо шта сте рекли, разгневио се и заклео: 35’Ниједан од ових људи из овог злог нараштаја неће видети добру земљу за коју сам се заклео да ћу је дати вашим оцима, 36осим Халева, сина Јефонијина. Он ће је видети! Њему и његовим синовима ћу дати земљу у коју је ступио, зато што се потпуно поуздао у Господа.’

37Због вас се Господ разгневио и на мене, па је рекао: ’Ни ти нећеш ући тамо! 38Исус, син Навинов, који стоји пред тобом, ући ће тамо. Охрабри га, јер ће он увести Израиља да прими земљу у посед. 39А ваша деца, за коју сте рекли да ће постати плен, они ће ући тамо. Њима ћу дати да заузму земљу. 40Ви, пак, крените натраг и идите у пустињу према Црвеном мору.’

41Ви сте ми одговорили: ’Згрешили смо Господу. Кренућемо горе и ратовати како је заповедио Господ, Бог наш.’ Сваки човек је припасао своје оружје мислећи да је лако успети се у горски крај.

42Тада ми је Господ рекао: ’Реци им: „Не пењите се и не ратујте, јер нећу бити међу вама; иначе ћете бити потучени од својих непријатеља!“’

43Ја сам вам то рекао, али ви нисте послушали. Побунили сте се против онога што је Господ рекао, па сте се припасали и успели у горје. 44Тада су изашли Аморејци који живе у горју и пресрели вас гонећи вас као пчеле. Тукли су вас од Сира до Орме. 45Онда сте се вратили и плакали пред Господом. Али Господ није слушао ваш вапај, нити се обазрео на вас. 46Зато сте остали у Кадису много дана – онолико колико сте остали тамо.