Oweruza 1 – CCL & NSP

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Oweruza 1:1-36

Aisraeli Achita Nkhondo ndi Akanaani Otsala

1Atamwalira Yoswa Aisraeli anafunsa Yehova kuti, “Ndani mwa ife ayambe nkhondo yomenyana ndi Akanaani?”

2Yehova anayankha kuti, “Fuko la Yuda ndilo liyambe kupita. Ndawapatsa dzikolo mʼmanja mwawo.”

3Choncho Ayuda anawuza abale awo a fuko la Simeoni kuti, “Bwerani tipitire limodzi mʼdziko limene tapatsidwa kuti tikamenyane ndi Akanaani. Ifenso tidzapita nanu mʼdziko limene anakugawirani.” Ndipo Asimeoni anapita nawo.

4Choncho Ayuda ananyamuka, ndipo Yehova anapereka Akanaani ndi Aperezi mʼmanja mwawo. Ndipo anapha anthu 10,000 ku Bezeki. 5Ku Bezekiko anakumana ndi ankhondo a mfumu Adoni-Bezeki ndipo anamenyana nawo, ndipo Ayudawo anagonjetsa Akanaani ndi Aperezi. 6Adoni-Bezekiyo anathawa, koma anamuthamangira ndi kumupeza, namugwira. Atamugwira anamudula zala zake zazikulu za ku manja ndi miyendo.

7Tsono Adoni-Bezeki anati, “Mafumu 70 omwe anadulidwa zala zazikulu za ku manja ndi miyendo yawo ankatola nyenyeswa pansi pa tebulo langa. Mulungu tsopano wandibwezera zomwe ndinawachita.” Kenaka anapita naye ku Yerusalemu ndipo anafera komweko.

8Pambuyo pake Ayuda anakathira nkhondo mzinda wa Yerusalemu ndipo anawulanda. Anapha anthu ambiri ndi kutentha mzinda wonse.

9Kenaka Ayuda anapita kukamenyana ndi Akanaani omwe amakhala ku dziko la ku mapiri, dziko la Negevi kummwera ndiponso mu zigwa. 10Anakalimbananso ndi Akanaani amene ankakhala ku Hebroni (mzinda womwe kale unkatchedwa Kiriyati-Araba). Kumeneko anagonjetsa Sesai, Ahimani ndi Talimai.

11Kuchokera kumeneko, iwo anakathira nkhondo anthu amene ankakhala ku Debri (mzindawu poyamba unkatchedwa Kiriati Seferi). 12Tsono Kalebe anati, “Munthu amene angathire nkhondo mzinda wa Kiriati Seferi ndi kuwulanda, ndidzamupatsa mwana wanga Akisa kuti akhale mkazi wake.” 13Otanieli mwana wa Kenazi, mngʼono wake wa Kalebe, ndiye anawulanda. Choncho Kalebe anamupatsa mwana wake Akisa kuti akhale mkazi wake.

14Tsiku lina atafika Akisayo, Otanieli anamuwumiriza mkazi wakeyo kuti apemphe munda kwa Kalebe abambo ake. Pamene Akisa anatsika pa bulu wake, Kalebe anamufunsa kuti, “Kodi ukufuna ndikuchitire chiyani?”

15Iye anayankha kuti, “Mundikomere mtima. Popeza mwandipatsa ku Negevi, kumalo kumene kulibe madzi, mundipatsenso akasupe amadzi.” Choncho Kalebe anamupatsa akasupe a kumtunda ndi a kumunsi.

16Tsono zidzukulu za Hobabu, Mkeni uja, mpongozi wa Mose, zinachoka ku Yeriko mzinda wa migwalangwa pamodzi ndi anthu a fuko la Yuda mpaka ku chipululu chimene chili kummwera kwa Aradi ndi kukakhala ndi Aamaleki.

17Kenaka anthu a fuko la Yuda anapita pamodzi ndi abale awo a fuko la Simeoni ndi kukagonjetsa Akanaani amene amakhala ku Zefati, ndipo mzindawo anawuwononga kwambiri. Choncho mzindawo anawutcha Horima. 18Anthu a fuko la Yuda analandanso mzinda wa Gaza ndi dziko lonse lozungulira, mzinda wa Asikeloni pamodzi ndi dziko lake lonse lozungulira, ndi mzinda wa Ekroni pamodzi ndi dziko lonse lozungulira.

19Yehova anathandiza anthu a fuko la Yuda. Iwo analanda dziko la kumapiri, koma sanathe kuwachotsa anthu ku zigwa, chifukwa anali ndi magaleta azitsulo. 20Monga analonjezera Mose, Kalebe anapatsidwa Hebroni. Kalebe anapirikitsa mafuko atatu a Anaki mu mzindamo. 21Koma fuko la Benjamini linalephera kuwachotsa Ayebusi, amene amakhala mu Yerusalemu. Choncho Ayebusiwo akukhalabe ndi fuko la Benjamini mu Yerusalemu mpaka lero.

22A banja la Yosefe nawonso anathira nkhondo mzinda wa Beteli, ndipo Yehova anali nawo. 23Anatumiza anthu kuti akazonde Beteli. Mzindawo kale unkatchedwa Luzi. 24Anthu okazondawo anaona munthu akutuluka mu mzindamo ndipo anamuwuza kuti, “Tisonyeze njira yolowera mu mzindamu, ndipo ife tidzakuchitira chifundo.” 25Choncho iye anawaonetsa njirayo, ndipo iwo anapha anthu onse mu mzindamo ndi lupanga koma munthu uja pamodzi ndi banja lake sanawaphe. 26Ndipo iye anapita ku dziko la Ahiti, kumene anamangako mzinda nawutcha dzina lake Luzi. Mpaka lero lino mzindawo dzina lake ndi lomwelo.

27Koma a fuko la Manase sanachotse nzika za mzinda wa Beti-Seani pamodzi ndi mʼmidzi yake yozungulira, kapena nzika za mzinda wa Taanaki ndi mʼmidzi yake yozungulira, kapenanso nzika za mzinda wa Dori ndi mʼmidzi yake yozungulira. Iwo sanapirikitse nzika za mzinda wa Ibuleamu ndi mʼmidzi yake yozungulira, kapena mzinda wa Megido ndi mʼmidzi yake yozungulira. Choncho Akanaani anapitirirabe kukhala mʼdzikomo. 28Aisraeli atakhala amphamvu, anawagwiritsa Akanaaniwo ntchito yakalavulagaga, koma sanawapirikitse. 29Nawonso Aefereimu sanathamangitse Akanaani amene amakhala mu Gezeri, choncho Akanaaniwo ankakhalabe pakati pawo ku Gezeriko. 30Azebuloni sanathamangitse Akanaani amene amakhala mu Kitironi kapena a ku Nahaloli. Iwo ankakhala pakati pawo ndipo ankawagwiritsa ntchito yakalavulagaga. 31A fuko la Aseri nawo sanathamangitse amene amakhala mu Ako, Sidoni, Ahilabu, Akizibu, Heliba, Afiki, ndi Rehobu. 32Choncho anthu a fuko la Aseri anakhala pakati pa Akanaani amene ankakhala mʼdzikomo popeza sanawapirikitse. 33Nalonso fuko la Nafutali silinathamangitse anthu amene ankakhala ku Beti Semesi kapena ku Beti Anati. Koma Anafutaliwo ankakhala pakati pa Akanaaniwo mʼdzikomo. Koma anthu amene ankakhala ku Beti Semesi ndi ku Beti Anati anawasandutsa kukhala ogwira ntchito yathangata. 34Aamori anapirikitsira anthu a fuko la Dani ku dziko la ku mapiri popeza sanawalole kuti atsikire ku chigwa. 35Aamori anatsimikiza mtima zokhalabe ku phiri la Hara-Heresi, ku Ayaloni, ndiponso ku Saalibimu. Koma a fuko la Yosefe anakula mphamvu ndipo anagwiritsa Aamoriwo ntchito yakalavulagaga. 36Malire a Aamori anayambira ku chikweza cha Akirabimu nʼkulowera ku Sela napitirira kumapita chakumapiri ndithu.

New Serbian Translation

Књига о судијама 1:1-36

Освајање остатка земље

1Након Исусове смрти, Израиљци упиташе Господа: „Ко ће од нас први поћи горе на Хананце да се бори против њих?“

2Господ одговори: „Нека горе пође Јуда. Ево, ја ћу предати земљу у његове руке.“

3Јуда рече своме брату Симеуну: „Пођи горе са мном у земљу која ми је додељена да се боримо против Хананаца, а онда ћу ја поћи с тобом у земљу која је теби додељена.“ И Симеун оде с њим.

4Јуда оде горе и Господ му предаде у руке Хананце и Фережане. Побили су у Везеку десет хиљада људи. 5У Везеку су наишли на Адони-Везека, ступили у бој против њега, и поразили Хананце и Фережане. 6Адони-Везек се дао у бег, али су га гонили и ухватили, па су му одсекли палце на рукама и на ногама.

7Тада рече Адони-Везек: „Седамдесет царева одсечених палчева на рукама и на ногама купило је мрвице под мојим столом. Како сам чинио, тако ми је Бог вратио.“ Одвели су га у Јерусалим и тамо је умро.

8Јудејци нападну Јерусалим и освоје га. Град су ударили оштрицом мача и запалили га.

9После тога су сишли Јудејци да се боре против Хананаца који су живели у горју, Негеву и равници. 10Јудејци оду на Хананце коју су живели у Хеврону (Хеврон се некада звао „Киријат-Арва“) и поразе Сесаја, Ахимана и Талмаја. 11Оданде су отишли на становнике Давира, који се некада звао „Киријат-Сефер“.

12Халев рече: „Ономе ко нападне и освоји Киријат-Сефер, даћу своју ћерку Ахсу за жену.“ 13Освојио га је Готонило, син Кенеза, млађег брата Халевова. Зато му је Халев дао своју ћерку Ахсу за жену.

14Кад је дошла к њему, Готонило је наговори да тражи поље од њеног оца. Кад је сишла с магарца, Халев је упита: „Шта желиш?“

15Она му одговори: „Дај ми благослов! Кад си ми већ дао земљу у Негеву, дај ми и који извор воде.“ Халев јој је дао Горње и Доње изворе.

16А потомци Кенеја, таста Мојсијевог, оду горе с Јудејцима из Палмовог града у Јудејску пустињу која лежи у Негеву код Арада. Отишли су и населили се међу тамошњим народом.

17Јуда оде са својим братом Симеуном и поби Хананце који су живели у Сефату. Град су изручили клетом уништењу. Зато се град прозвао Орма1,17 Орма, односно уништење.. 18Јуда је, такође, освојио Газу са њеним подручјем, Аскалон са његовим подручјем и Акарон са његовим подручјем.

19Господ је био с Јудом, те је овај освојио горје. Житеље долине није могао да протера, јер су имали гвоздена бојна кола. 20Халеву су, по Мојсијевој наредби, дали Хеврон, одакле је протерао три Енаковца. 21Синови Венијаминови нису протерали Јевусејце који живе у Јерусалиму. Зато Јевусејци све до данас живе у Јерусалиму са синовима Венијаминовим.

22Тако су и синови Јосифови отишли горе у Ветиљ, и Господ је био с њима. 23Синови Јосифови извиде Ветиљ, који се некада звао „Луз“. 24Тамо су уходе виделе једног човека како излази из града. Они му рекоше: „Покажи нам улаз у град, па ћемо ти се смиловати.“ 25Он им покаже улаз у град. Онда ударе град оштрицом мача, а оног човека са његовом породицом пусте. 26Човек оде у земљу Хетита и тамо подигне град. Назвао га је Луз, а тако се зове и данас.

27Синови Манасијини нису освојили Вет-Сан и његова насеља, ни Танах и његова насеља, ни житеље Дора са његовим насељима, ни житеље Јивлеама са његовим насељима, ни житеље Мегида са његовим насељима, јер су Хананци били решени да живе у земљи. 28Али кад је Израиљ ојачао, наметнуо је Хананцима принудни рад. Ипак, нису их сасвим протерали. 29Ни Јефрем није протерао Хананце, становнике Гезера; Хананци су наставили да живе међу њима у Гезеру. 30Завулон није протерао ни становнике Китрона ни становнике Налола. Тако су Хананци остали међу њима, али им је био наметнут принудни рад. 31Асир није протерао становнике Акоа, Сидона, Ахлава, Ахзива, Хелбе, Афека и Реова. 32Пошто их нису протерали, Асировци су остали међу Хананцима, житељима земље. 33Ни Нефталим није протерао становнике Вет-Семеса и Вет-Аната, те је живео усред Хананаца, становника земље. Становницима Вет-Семеса и Вет-Аната био је наметнут принудни рад. 34Аморејци су потиснули Дановце у горски крај; нису им давали да силазе у долину. 35Аморејци су били решени да остану да живе на гори Херес, у Ајалону и у Са̂лвиму. Али притисла их је рука дома Јосифовог, па им је био наметнут принудни рад. 36Аморејска граница се пружала од узвишице Акравим, од Селе, па навише.