Yoswa 23 – CCL & NRT

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Yoswa 23:1-16

Kutsanzika kwa Yoswa

1Panapita nthawi yayitali kuchokera pamene Yehova anakhazikitsa mtendere pakati pa Aisraeli ndi adani awo owazungulira. Nthawi imeneyi nʼkuti Yoswa atakalamba, ali ndi zaka zambiri. 2Yoswayo anayitanitsa Aisraeli onse pamodzi ndi akuluakulu, atsogoleri, oweruza, ndi oyangʼanira anthu antchito ndipo anawawuza kuti, “Ine ndakalamba ndipo ndili ndi zaka zambiri. 3Inu mwaona zonse zimene Yehova Mulungu wanu wachita kwa mitundu yonseyi chifukwa cha inu. Ndi Yehova Mulungu wanu amene anakumenyerani nkhondo. 4Tsono onani! Mitundu ya anthu otsalawa ndayipereka kwa mafuko anu pamodzi ndi mitundu ya anthu ya pakati pa Yorodani ndi Nyanja Yayikulu ya kumadzulo imene ndinayigonjetsa. 5Yehova Mulungu wanu ndiye adzawathamangitsa pamaso panu. Mudzatenga dziko lawo monga Yehova anakulonjezerani.

6“Choncho khalani amphamvu, ndipo samalani kuti mumvere zonse zimene zalembedwa mʼbuku la malamulo a Mose. Musapatuke pa malamulo onse amene alembedwamo. 7Musagwirizane ndi mitundu ya anthu imene yatsala pakati panu. Musatchule mayina a milungu yawo kapena kuyitchula polumbira. Musayitumikire kapena kuyigwadira. 8Koma mukuyenera kugwiritsa Yehova Mulungu wanu, monga mwachitira mpaka lero lino.

9“Yehova wapirikitsa patsogolo panu mitundu ya anthu ikuluikulu ndi yolimba. Mpaka lero palibe amene watha kulimbana nanu. 10Aliyense wa inu atha kuthamangitsa anthu 1,000 chifukwa Yehova Mulungu wanu ndiye amakumenyerani nkhondo, monga momwe analonjezera. 11Choncho samalitsani kuti mukonde Yehova Mulungu wanu.

12“Koma ngati mubwerera mʼmbuyo ndi kuphatikizana ndi mitundu yotsalayi imene ili pakati panu ndi kumakwatirana nayo, 13pamenepo mudziwe kuti Yehova, Mulungu wanu, sadzapirikitsa mitundu imeneyi pamaso panu, koma idzakhala ngati msampha kwa inu kapenanso khwekhwe lokukolani. Idzakhala ngati zikwapu pa msana panu kapenanso ngati minga mʼmaso mwanu mpaka mutatha psiti mʼdziko labwinoli limene Yehova Mulungu wanu wakupatsani.

14“Aliyense wa inu akudziwa mu mtima mwake komanso mʼmoyo mwake kuti zabwino zonse zimene Yehova Mulungu wanu anakulonjezani zachitika. Palibe lonjezo ndi limodzi lomwe limene silinakwaniritsidwe. 15Monga momwe Yehova Mulungu wanu wakuchitirani zabwino zonse zimene ananena kuti adzachita, Yehovayo angathenso kukuchitirani zoyipa zonse zimene waopseza, mpaka kukuchotsani mʼdziko lokoma limene anakupatsani. 16Ngati muphwanya pangano la Yehova Mulungu wanu, limene anakulamulirani nʼkumapita kukatumikira milungu ina ndi kuyigwadira, Yehova adzakukwiyirani, ndiye mudzachotsedwa mʼdziko labwinoli limene Yehova wakupatsani.”

New Russian Translation

Навин 23:1-16

Иисус прощается с вождями

1Спустя много времени после того, как Господь дал Израилю покой от всех окружающих его врагов, Иисус, уже состарившийся и достигший преклонного возраста, 2созвал всех старейшин, вождей, судей и начальников Израиля и сказал им:

– Я состарился, достиг преклонного возраста. 3Вы сами видели все, что Господь, ваш Бог, сделал ради вас со всеми этими народами. Господь, ваш Бог, Сам сражался за вас. 4Помните, что я по жребию разделил между вашими родами всю землю между Иорданом и Великим морем на западе, которая принадлежала народам еще оставшимся и тем, которых я уже искоренил. 5Господь, ваш Бог, Сам прогонит их с вашего пути. Он вытеснит их перед вами, и вы завладеете их землей, как Господь, ваш Бог, вам и обещал.

6Будьте тверды, соблюдайте и исполняйте все, что написано в книге Закона Моисея, не уклоняясь ни вправо, ни влево. 7Не смешивайтесь с этими народами, которые остаются среди вас, не упоминайте имен их богов и не клянитесь ими. Не служите и не поклоняйтесь им. 8Крепко держитесь Господа, вашего Бога, как вы делали до сегодняшнего дня.

9Господь прогнал от вас великие и сильные народы. До сегодняшнего дня никто не мог устоять перед вами. 10Один из вас рассеивает тысячу, потому что Господь, ваш Бог, Сам сражается за вас, как Он и обещал. 11Поэтому всеми силами старайтесь любить Господа, вашего Бога.

12Но если вы отступите и объединитесь с уцелевшим остатком этих народов среди вас, и станете заключать с ними браки, 13то знайте наверняка: Господь, ваш Бог, уже не станет прогонять от вас эти народы. Вместо этого они станут для вас ловушкой и западней, плетью для ваших спин и колючками для ваших глаз, пока вы не будете искоренены из этой хорошей земли, которую дал вам Господь, ваш Бог.

14Я собираюсь отправиться путем всей земли. Всем вашим сердцем и всей душой вы знаете, что из всех добрых обещаний Господа, вашего Бога, не осталось ни одного неисполненного – все сбылись, ни одно не оказалось ложным. 15Но как сбылось для вас все доброе, что обещал Господь, ваш Бог, так наведет Господь на вас и все злое, о котором предупреждал, пока не истребит вас с этой хорошей земли, которую Он вам дал. 16Если вы преступите завет Господа, вашего Бога, который Он с вами заключил, и пойдете служить другим богам и поклоняться им, то гнев Господа вспыхнет на вас, и вы будете быстро искоренены из этой хорошей земли, которую Он вам дал.