Deuteronomo 1 – CCL & NRT

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Deuteronomo 1:1-46

Mose Akumbutsa Aisraeli za ku Horebu

1Awa ndi mawu amene Mose anayankhula kwa Aisraeli onse mʼchipululu kummawa kwa Yorodani, ku Araba moyangʼanana ndi Sufi, pakati pa Parani ndi Tofeli, Labani, Heziroti ndi Dizahabu. 2(Kuyenda kuchokera ku Horebu kukafika ku Kadesi Barinea kudzera njira ya ku Phiri la Seiri ndi ulendo wa masiku khumi ndi limodzi).

3Mʼchaka cha makumi anayi, pa tsiku loyamba la mwezi 11, Mose anafotokozera Aisraeli zonse zimene Yehova anamulamula zokhudza iwowo. 4Apa nʼkuti atagonjetsa Sihoni mfumu ya Aamori, amene amalamulira ku Hesiboni, ndipo pa Ederi anagonjetsa Ogi mfumu ya ku Basani, amene amalamulira mu Asiteroti.

5Chakummawa kwa Yorodani mʼchigawo cha Mowabu, Mose anayamba kufotokozera lamulo ili kunena kuti:

6Ku Horebu, Yehova Mulungu wathu anati kwa ife, “Mwakhalitsa pa phiri lino. 7Sasulani msasa ndipo pitani ku dziko la mapiri la Aamori. Pitani kwa anthu onse oyandikana nawo ku Araba, ku mapiri, mʼmbali mwa mapiri a ku madzulo, ku Negevi ndiponso mʼmbali mwa nyanja, ku dziko la Akanaani ndi ku Lebanoni mpaka ku mtsinje waukulu wa Yufurate. 8Taonani, Ine ndakupatsani dziko ili. Lowani ndi kulilanda dziko limene Yehova analumbira kuti adzapereka kwa makolo anu, Abrahamu, Isake ndi Yakobo komanso kwa zidzukulu zawo.”

Kukhazikitsa Atsogoleri

9Pa nthawi imeneyi ine ndinati kwa inu, “Inu ndinu katundu olemera kwambiri woti sindingathe kumunyamula ndekha. 10Yehova Mulungu wanu wakuchulukitsani kotero kuti lero lino ndinu ochuluka ngati nyenyezi za kumwamba. 11Yehova Mulungu wa makolo anu wachulukitsa chiwerengero chanu ndipo wakudalitsani monga momwe analonjezera! 12Koma nanga ndekha ndidzasenza bwanji zovuta ndi zipsinjo zanu komanso milandu yanu? 13Sankhani amuna ena anzeru, ozindikira ndi amene mumawalemekeza kuchokera ku mtundu uliwonse wa mitundu yanu, ndipo ndidzawayika kuti akulamulireni.”

14Inu munandiyankha kuti, “Maganizo amenewa ndi abwino kuwachita.”

15Choncho ndinatenga anthu otsogolera mafuko anu, anzeru ndi omwe mumawalemekeza, ndipo ndinawayika kuti azikulamulirani mʼmagulu a 1,000, ena 100, ena makumi asanu ndi ena khumi, kuti akhalenso ngati akapitawo a mafuko. 16Ndipo pa nthawi imeneyo ndinawawuza olamula anu kuti, “Muzimva milandu ya pakati pa abale anu ndi kuweruza mosakondera, kaya mlanduwo uli pakati pa Aisraeli okhaokha kapena mmodzi wa iwo ndi mlendo. 17Osamayangʼana nkhope poweruza koma muzimvetsera aangʼono ndi aakulu omwe chimodzimodzi. Musamaope munthu aliyense, pakuti chiweruzo ndi cha Mulungu. Muzindibweretsera mlandu uliwonse wovuta ndipo ndidzaumva.” 18Ndipo nthawi imeneyo ndinakuwuzani chilichonse chimene munayenera kuchita.

Atumizidwa Kukazonda Dziko

19Tsono monga Yehova Mulungu wathu anatilamulira, tinanyamuka kuchoka ku Horebu ndi kupita cha ku dziko lamapiri la Aamori kudzera ku chipululu chachikulu ndi choopsa chija munachionachi, kotero kuti tinakafika ku Kadesi Barinea. 20Ndipo ndinati kwa inu, “Mwafika ku dziko la mapiri la Aamori, limene Yehova Mulungu wathu akutipatsa. 21Taonani, Yehova Mulungu wanu wakupatsani dzikoli. Pitani ndi kulitenga monga Yehova, Mulungu wa makolo anu anakuwuzirani. Musaope kapenanso kugwa mphwayi.”

22Tsono nonse munabwera kwa ine ndi kuti, “Tiyeni titumize anthu ayambe apita kuti akazonde dzikolo ndi kutibweretsera mawu pa za njira yomwe tidzere ndi za mizinda imene tikafikireko.”

23Ndinaona kuti maganizo amenewa anali abwino, choncho ndinasankha anthu khumi ndi awiri, mmodzi ku fuko lililonse. 24Iwo ananyamuka napita mʼdziko la mapiri, ndipo anafika ku Chigwa cha Esikolo ndi kukazonda dzikolo. 25Pobwerera anatitengerako zipatso za mʼdzikomo ndipo anatipatsa mawu akuti, “Dziko limene Yehova Mulungu wathu akutipatsa ndi labwino.”

Awukira Yehova

26Koma inu simunafune kupitako ndipo munawukira lamulo la Yehova Mulungu wanu. 27Inu munanyinyirika mʼmatenti anu nʼkumati, “Mulungu amatida nʼchifukwa chake anatitulutsa ku Igupto kuti atipereke mʼmanja mwa Aamori kuti atiwononge. 28Tigwire mtengo wanji? Abale athu anatitayitsa mtima. Iwo akuti, ‘Anthuwo ndi amphamvu ndi aatali kuposa ife, mizindayo ndi yayikulu ndipo mipanda yake ndi yayitali yofika kumwamba. Ife tinaonanso Aanaki kumeneko.’ ”

29Ndipo ine ndinati kwa inu, “Musachite mantha kapena kuwaopa. 30Yehova Mulungu wanu, amene akukutsogolerani, adzakumenyerani nkhondo monga muja anachitira ku Igupto inu mukuona, 31ndi mʼchipululu muja. Kumeneko munaona mmene Yehova Mulungu wanu anakunyamulirani monga abambo anyamulira mwana wawo, njira yonse yomwe munayenda mpaka munafika pamalo ano.”

32Ngakhale zinali choncho, simunadalire Yehova Mulungu wanu 33amene anakutsogolerani pa ulendo wanu, ndi moto nthawi ya usiku ndi mtambo nthawi ya masana, kukufunirani malo woti mumange msasa ndi kukuonetsani njira yoti muyendemo.

34Yehova atamva zimene munanena anakwiya nalumbira kuti, 35“Palibe ndi mmodzi yemwe mwa mʼbado woyipawu amene adzaona dziko labwino limene ndinalumbira kupatsa makolo anu, 36kupatula Kalebe mwana wa Yefune. Iye adzaliona, ndipo ndidzamupatsa iye ndi adzukulu ake, dziko limene adzapondamo popeza anatsata Yehova ndi mtima wake wonse.”

37Chifukwa cha inu, Yehova anakwiyiranso ine ndipo anati, “Iwenso sudzalowa mʼdzikomo. 38Koma Yoswa mwana wa Nuni amene amakuthandiza, adzalowa mʼdzikomo. Umulimbikitse chifukwa adzatsogolera Israeli kukalandira dzikolo. 39Ndipo angʼonoangʼono amene munati adzagwidwa ukapolo, ana anu amene sanadziwe kusiyanitsa chabwino ndi choyipa, amenewo adzalowa mʼdzikolo. Ndidzalipereka kwa iwo ndipo lidzakhala lawo. 40Koma inu, tembenukani nyamukani kulowera cha ku chipululu kutsatira njira ya ku Nyanja Yofiira.”

41Ndipo inuyo munati, “Tachimwa pamaso pa Yehova. Tipita ndi kukachita nkhondo monga Yehova Mulungu wathu watilamulira.” Choncho aliyense wa inu anavala zankhondo, ndi kuganiza kuti nʼkosavuta kupita mʼdziko la mapiri lija.

42Koma Yehova anandiwuza kuti, “Awuze anthuwa kuti, ‘Musapite kukachita nkhondo chifukwa Ine sindidzakhala nanu. Mudzagonjetsedwa ndi adani anu.’ ”

43Choncho ndinakuwuzani koma simunamve. Inu munawukira lamulo la Yehova ndipo mwamwano munayenda kulowa mʼdziko la mapiri. 44Aamori amene ankakhala mʼmapiriwo anatuluka kukakumana nanu ndipo anakuthamangitsani ngati gulu la njuchi ndipo anakukanthani kuchokera ku Seiri, njira yonse mpaka ku Horima. 45Munabwererako mukulira pamaso pa Yehova, koma Iye sanalabadire kulira kwanuko ndipo sanakumvetsereni. 46Pamenepo munakhala ku Kadesi masiku ambiri kwa nthawi yayitali ndithu.

New Russian Translation

Второзаконие 1:1-46

Воспоминания Моисея

1Вот слова, которые Моисей сказал всему Израилю в пустыне, что к востоку от Иордана – то есть в Иорданской долине – напротив Суфа, между Параном и Тофелом, Лаваном, Хацеротом и Ди-Загавом. 2(На расстоянии одиннадцати дней от Хорива по дороге от горы Сеир к Кадеш-Барнеа.)

3В сороковой год после выхода из Египта, в первый день одиннадцатого месяца Моисей объявил израильтянам все, что повелел ему о них Господь. 4Это было после того, как он разбил Сигона, царя аморреев, который правил в Хешбоне, а в Эдреи разбил Ога, царя Башана, который правил в Аштароте1:4 Букв.: «царя Башана, который правил в Аштароте в Эдреи»..

5К востоку от Иордана на земле Моава Моисей начал разъяснять этот Закон, говоря:

6– Господь, наш Бог, говорил нам в Хориве: «Довольно вам жить у этой горы. 7Сверните лагерь и идите в аморрейские нагорья и ко всем соседним народам, живущим в Иорданской долине, в горах, в западных предгорьях, в Негеве и вдоль побережья, идите в землю хананеев и на Ливан, даже до великой реки Евфрата. 8Смотрите, Я дал вам эту землю. Войдите и овладейте землей, которую Господь клялся отдать вашим отцам Аврааму, Исааку и Иакову – и их семени».

Назначение судей

(Исх. 18:13-27)

9В то время я сказал вам: «Вы – слишком тяжелое бремя для меня одного. 10Господь, ваш Бог, умножил ваше число, и сегодня вы многочисленны, как звезды на небе. 11Пусть Господь, Бог ваших отцов, умножит ваше число в тысячу раз больше и благословит вас, как обещал! 12Но как я могу нести тяжелое бремя ваших споров один? 13Изберите мудрых, понимающих и уважаемых людей от каждого вашего рода, а я поставлю их над вами».

14Вы отвечали мне: «То, что ты предлагаешь, хорошо».

15Я выбрал из ваших родов мудрых и уважаемых людей и поставил их вождями над вами: начальниками над тысячами, сотнями, полусотнями и десятками и старейшинами в родах. 16Я повелел в то время вашим судьям: выслушивайте споры между вашими братьями и судите справедливо, будет ли тяжба между израильтянами или между израильтянином и чужеземцем. 17Когда будете судить, не будьте пристрастны. Выслушивайте как великого, так и малого. Никого не бойтесь, потому что суд принадлежит Богу. Приносите мне всякое дело, которое слишком трудно для вас, и я выслушаю его. 18В то время я сказал вам все, что вы должны были делать.

Посланные лазутчики

(Чис. 13:1-33)

19Затем мы тронулись в путь, как повелел нам Господь. Вышли из Хорива, и пошли к аморрейским нагорьям через всю огромную и ужасную пустыню, которую вы видели, и достигли Кадеш-Барнеа. 20Тогда я сказал вам: «Вы достигли аморрейских нагорий, которые Господь, наш Бог, отдает нам. 21Смотри, Господь, твой Бог, отдал тебе землю. Поднимись и завладей ею, как сказал тебе Господь, Бог твоих отцов. Не бойся; не будь малодушным».

22Тогда вы все пришли ко мне и сказали: «Пошлем вперед людей, пусть они разведают нам эту землю и расскажут о дороге, по которой нам идти, и о городах, куда мы вступим».

23Мне понравилось это предложение, и я выбрал из вас двенадцать человек, по одному из каждого рода. 24Они пошли, поднялись в нагорья, пришли в долину Эшкол и исследовали ее. 25Взяв с собой плоды с той земли, они принесли их вниз к нам и доложили: «Хорошую землю дает нам Господь, наш Бог».

Восстание против Господа

(Чис. 14:1-45)

26Но вы не захотели подниматься; вы взбунтовались против повеления Господа, вашего Бога. 27Вы роптали у себя в шатрах и говорили: «Господь ненавидит нас. Поэтому Он вывел нас из Египта, чтобы отдать в руки аморреев и погубить. 28Куда нам идти? Наши братья лишили нас смелости1:28 Букв.: «размягчили наше сердце».. Они говорят: „Тот народ сильнее и выше ростом; города там большие, со стенами до небес. Мы даже видели там потомков Анака“».

29Тогда я сказал вам: «Не страшитесь, не бойтесь их. 30Господь, ваш Бог, идет впереди, чтобы сражаться за вас, как Он сделал в Египте у вас на глазах 31и в пустыне, где вы видели, как Господь, ваш Бог, носил вас, словно отец своего сына, на всем вашем пути вплоть до этого места».

32Но вы не доверились Господу, вашему Богу, 33Который шел перед вами во время путешествия ночью в огне, а днем в облаке, чтобы найти вам места для остановки и показать путь, которым вы должны идти.

34Когда Господь услышал ваши речи, Он разгневался и поклялся: 35«Ни один человек из этого злого поколения не увидит благодатной земли, которую Я клялся отдать вашим отцам, 36кроме Халева, сына Иефоннии. Он увидит ее, и Я дам ему и его потомкам землю, через которую он проходил, потому что он от всего сердца последовал Господу».

37Из-за вас Господь разгневался и на меня и сказал: «Ты тоже не войдешь туда. 38Но твой помощник Иисус, сын Навин, войдет в эту землю. Ободряй его, потому что он поведет Израиль, чтобы унаследовать ее. 39А дети, о которых вы говорили, что они попадут в плен, – ваши дети, которые еще не отличают хорошее от плохого, войдут в землю. Я отдам ее им, и они овладеют ею. 40А вы повернитесь и отправляйтесь в пустыню, что на пути к Красному морю».

41Тогда вы отвечали: «Мы согрешили против Господа. Мы поднимемся и сразимся, как повелел нам Господь, наш Бог». Вы взяли оружие, думая, что подняться в нагорья легко.

42Но Господь сказал мне: «Скажи им: „Не поднимайтесь и не сражайтесь, потому что Меня не будет с вами. Ваши враги разобьют вас“».

43Я сказал вам, но вы не послушали. Вы взбунтовались против повеления Господа и в своей гордыне поднялись в нагорья. 44Аморреи, жившие в тех нагорьях, вышли против вас. Они преследовали вас, как пчелиный рой, и били вас от Сеира до самого города Хормы. 45Вы вернулись и плакали перед Господом, но Он не внял вашему плачу и отказался услышать вас. 46И много дней вы оставались в Кадеше – все то время, которое вы там провели.