Oweruza 1 – CCL & NRT

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Oweruza 1:1-36

Aisraeli Achita Nkhondo ndi Akanaani Otsala

1Atamwalira Yoswa Aisraeli anafunsa Yehova kuti, “Ndani mwa ife ayambe nkhondo yomenyana ndi Akanaani?”

2Yehova anayankha kuti, “Fuko la Yuda ndilo liyambe kupita. Ndawapatsa dzikolo mʼmanja mwawo.”

3Choncho Ayuda anawuza abale awo a fuko la Simeoni kuti, “Bwerani tipitire limodzi mʼdziko limene tapatsidwa kuti tikamenyane ndi Akanaani. Ifenso tidzapita nanu mʼdziko limene anakugawirani.” Ndipo Asimeoni anapita nawo.

4Choncho Ayuda ananyamuka, ndipo Yehova anapereka Akanaani ndi Aperezi mʼmanja mwawo. Ndipo anapha anthu 10,000 ku Bezeki. 5Ku Bezekiko anakumana ndi ankhondo a mfumu Adoni-Bezeki ndipo anamenyana nawo, ndipo Ayudawo anagonjetsa Akanaani ndi Aperezi. 6Adoni-Bezekiyo anathawa, koma anamuthamangira ndi kumupeza, namugwira. Atamugwira anamudula zala zake zazikulu za ku manja ndi miyendo.

7Tsono Adoni-Bezeki anati, “Mafumu 70 omwe anadulidwa zala zazikulu za ku manja ndi miyendo yawo ankatola nyenyeswa pansi pa tebulo langa. Mulungu tsopano wandibwezera zomwe ndinawachita.” Kenaka anapita naye ku Yerusalemu ndipo anafera komweko.

8Pambuyo pake Ayuda anakathira nkhondo mzinda wa Yerusalemu ndipo anawulanda. Anapha anthu ambiri ndi kutentha mzinda wonse.

9Kenaka Ayuda anapita kukamenyana ndi Akanaani omwe amakhala ku dziko la ku mapiri, dziko la Negevi kummwera ndiponso mu zigwa. 10Anakalimbananso ndi Akanaani amene ankakhala ku Hebroni (mzinda womwe kale unkatchedwa Kiriyati-Araba). Kumeneko anagonjetsa Sesai, Ahimani ndi Talimai.

11Kuchokera kumeneko, iwo anakathira nkhondo anthu amene ankakhala ku Debri (mzindawu poyamba unkatchedwa Kiriati Seferi). 12Tsono Kalebe anati, “Munthu amene angathire nkhondo mzinda wa Kiriati Seferi ndi kuwulanda, ndidzamupatsa mwana wanga Akisa kuti akhale mkazi wake.” 13Otanieli mwana wa Kenazi, mngʼono wake wa Kalebe, ndiye anawulanda. Choncho Kalebe anamupatsa mwana wake Akisa kuti akhale mkazi wake.

14Tsiku lina atafika Akisayo, Otanieli anamuwumiriza mkazi wakeyo kuti apemphe munda kwa Kalebe abambo ake. Pamene Akisa anatsika pa bulu wake, Kalebe anamufunsa kuti, “Kodi ukufuna ndikuchitire chiyani?”

15Iye anayankha kuti, “Mundikomere mtima. Popeza mwandipatsa ku Negevi, kumalo kumene kulibe madzi, mundipatsenso akasupe amadzi.” Choncho Kalebe anamupatsa akasupe a kumtunda ndi a kumunsi.

16Tsono zidzukulu za Hobabu, Mkeni uja, mpongozi wa Mose, zinachoka ku Yeriko mzinda wa migwalangwa pamodzi ndi anthu a fuko la Yuda mpaka ku chipululu chimene chili kummwera kwa Aradi ndi kukakhala ndi Aamaleki.

17Kenaka anthu a fuko la Yuda anapita pamodzi ndi abale awo a fuko la Simeoni ndi kukagonjetsa Akanaani amene amakhala ku Zefati, ndipo mzindawo anawuwononga kwambiri. Choncho mzindawo anawutcha Horima. 18Anthu a fuko la Yuda analandanso mzinda wa Gaza ndi dziko lonse lozungulira, mzinda wa Asikeloni pamodzi ndi dziko lake lonse lozungulira, ndi mzinda wa Ekroni pamodzi ndi dziko lonse lozungulira.

19Yehova anathandiza anthu a fuko la Yuda. Iwo analanda dziko la kumapiri, koma sanathe kuwachotsa anthu ku zigwa, chifukwa anali ndi magaleta azitsulo. 20Monga analonjezera Mose, Kalebe anapatsidwa Hebroni. Kalebe anapirikitsa mafuko atatu a Anaki mu mzindamo. 21Koma fuko la Benjamini linalephera kuwachotsa Ayebusi, amene amakhala mu Yerusalemu. Choncho Ayebusiwo akukhalabe ndi fuko la Benjamini mu Yerusalemu mpaka lero.

22A banja la Yosefe nawonso anathira nkhondo mzinda wa Beteli, ndipo Yehova anali nawo. 23Anatumiza anthu kuti akazonde Beteli. Mzindawo kale unkatchedwa Luzi. 24Anthu okazondawo anaona munthu akutuluka mu mzindamo ndipo anamuwuza kuti, “Tisonyeze njira yolowera mu mzindamu, ndipo ife tidzakuchitira chifundo.” 25Choncho iye anawaonetsa njirayo, ndipo iwo anapha anthu onse mu mzindamo ndi lupanga koma munthu uja pamodzi ndi banja lake sanawaphe. 26Ndipo iye anapita ku dziko la Ahiti, kumene anamangako mzinda nawutcha dzina lake Luzi. Mpaka lero lino mzindawo dzina lake ndi lomwelo.

27Koma a fuko la Manase sanachotse nzika za mzinda wa Beti-Seani pamodzi ndi mʼmidzi yake yozungulira, kapena nzika za mzinda wa Taanaki ndi mʼmidzi yake yozungulira, kapenanso nzika za mzinda wa Dori ndi mʼmidzi yake yozungulira. Iwo sanapirikitse nzika za mzinda wa Ibuleamu ndi mʼmidzi yake yozungulira, kapena mzinda wa Megido ndi mʼmidzi yake yozungulira. Choncho Akanaani anapitirirabe kukhala mʼdzikomo. 28Aisraeli atakhala amphamvu, anawagwiritsa Akanaaniwo ntchito yakalavulagaga, koma sanawapirikitse. 29Nawonso Aefereimu sanathamangitse Akanaani amene amakhala mu Gezeri, choncho Akanaaniwo ankakhalabe pakati pawo ku Gezeriko. 30Azebuloni sanathamangitse Akanaani amene amakhala mu Kitironi kapena a ku Nahaloli. Iwo ankakhala pakati pawo ndipo ankawagwiritsa ntchito yakalavulagaga. 31A fuko la Aseri nawo sanathamangitse amene amakhala mu Ako, Sidoni, Ahilabu, Akizibu, Heliba, Afiki, ndi Rehobu. 32Choncho anthu a fuko la Aseri anakhala pakati pa Akanaani amene ankakhala mʼdzikomo popeza sanawapirikitse. 33Nalonso fuko la Nafutali silinathamangitse anthu amene ankakhala ku Beti Semesi kapena ku Beti Anati. Koma Anafutaliwo ankakhala pakati pa Akanaaniwo mʼdzikomo. Koma anthu amene ankakhala ku Beti Semesi ndi ku Beti Anati anawasandutsa kukhala ogwira ntchito yathangata. 34Aamori anapirikitsira anthu a fuko la Dani ku dziko la ku mapiri popeza sanawalole kuti atsikire ku chigwa. 35Aamori anatsimikiza mtima zokhalabe ku phiri la Hara-Heresi, ku Ayaloni, ndiponso ku Saalibimu. Koma a fuko la Yosefe anakula mphamvu ndipo anagwiritsa Aamoriwo ntchito yakalavulagaga. 36Malire a Aamori anayambira ku chikweza cha Akirabimu nʼkulowera ku Sela napitirira kumapita chakumapiri ndithu.

New Russian Translation

Судей 1:1-36

Израиль ведет войну с оставшимися хананеями

(Нав. 15:15-19)

1После смерти Иисуса израильтяне спросили Господа:

– Кому из нас первым идти воевать с хананеями?

2Господь ответил:

– Первым пусть идет Иуда; Я отдаю землю в его руки.

3Тогда воины Иуды сказали своим братьям симеонитам:

– Идите с нами в землю, которая нам досталась, воевать с хананеями. А потом мы, в свой черед, пойдем с вами в вашу землю.

И симеониты пошли с ними. 4Когда Иуда со своими людьми вышел на бой, Господь отдал хананеев и ферезеев в их руки, и они сразили в Везеке десять тысяч человек. 5Там они и нашли Адони-Везека, сразились с ним и разбили хананеев и ферезеев. 6Адони-Везек бежал, но они погнались за ним, схватили его и отрубили ему большие пальцы на руках и на ногах.

7Адони-Везек сказал:

– Семьдесят царей с отрубленными большими пальцами на руках и на ногах собирали крохи под моим столом. Теперь Бог воздал мне за то, что я сделал.

Его отвели в Иерусалим, где он и умер.

8Воины Иуды напали на Иерусалим и взяли его. Они предали город мечу и огню.

9После этого воины Иуды отправились на битву с хананеями, которые жили в нагорьях, в Негеве и в западных предгорьях. 10Они выступили против хананеев Хеврона (прежде он назывался Кирьят-Арба) и разбили Шешая, Ахимана и Талмая1:10 Это были потомки Анака (см. ст. 20), род которого был известен своим высоким ростом и наводил страх на израильтян (см. Чис. 13:22; Нав. 15:14).. 11Оттуда они пошли на жителей Давира (который прежде назывался Кирьят-Сефер).

12Халев сказал:

– Я отдам свою дочь Ахсу в жены тому, кто нападет на Кирьят-Сефер и возьмет его.

13Отниил, сын младшего брата Халева Кеназа1:13 Или: «Отниил, потомок Кеназа, младший брат Халева»., взял его, и Халев отдал ему в жены свою дочь Ахсу.

14В день, когда была назначена свадьба, она говорила с Отниилом, чтобы просить у ее отца поле. Когда она слезла со своего осла, Халев спросил ее:

– Чего ты хочешь?

15Она ответила:

– Окажи мне особую милость. Ты дал мне землю в Негеве – так дай мне и источники воды.

И Халев дал ей верхние и нижние источники.

16Потомки тестя Моисея, кенея, пошли с народом Иуды из города Пальм1:16 То есть Иерихона. в пустыню Иуды, что в Негеве рядом с городом Арадом, и поселились среди народа.

17Воины Иуды пошли со своими братьями симеонитами, напали на хананеев, которые жили в Цефате, и полностью уничтожили1:17 На языке оригинала стоит слово, которое говорит о полном посвящении предметов или людей Господу, часто осуществлявшемся через их уничтожение. город. Поэтому он получил название Хорма1:17 По-еврейски это название означает «уничтожение».. 18Еще воины Иуды взяли Газу, Ашкелон и Экрон с их окрестностями.

19Господь был с воинами Иуды. Они овладели нагорьями, но не смогли прогнать жителей долин, потому что у тех были железные колесницы. 20Как и обещал Моисей, Хеврон был отдан Халеву, который прогнал оттуда троих сыновей Анака.

21Вениамитяне не смогли выселить иевусеев, которые жили в Иерусалиме; иевусеи живут там с вениамитянами до сегодняшнего дня.

22Дом Иосифа напал на Вефиль, и Господь был с ними. 23Когда они послали лазутчиков разведать Вефиль (прежде он назывался Луз), 24лазутчики увидели мужчину, выходящего из города, и сказали ему:

– Покажи нам, как попасть в город, и мы обойдемся с тобой хорошо.

25Он показал им, и они предали город мечу, но пощадили того человека и всю его семью. 26Этот человек пошел в землю хеттов, где построил город, который назвал Луз – так он называется и до сегодняшнего дня.

27Но Манассия не прогнал жителей Бет-Шеана, Таанаха, Дора, Ивлеама и Мегиддо и окрестных деревень, и в этой земле продолжали жить хананеи. 28Когда Израиль окреп, они сделали хананеев подневольными, но не изгнали их полностью. 29И Ефрем не прогнал хананеев, которые жили в городе Гезере, и хананеи продолжали жить там среди них. 30И Завулон не прогнал хананеев, живших в Китроне и в Нагалоле, которые остались среди них, но сделались подневольными. 31И Асир не изгнал жителей Акко, Сидона, Ахлава, Ахзива, Хелвы, Афека и Рехова; 32и поэтому народ Асира жил среди хананеев, обитателей той земли. 33И Неффалим не прогнал жителей Бет-Шемеша и Бет-Анафа: неффалимиты жили среди хананеев, обитателей той земли, а жителей Бет-Шемеша и Бет-Анафа сделали подневольными. 34Данитянам аморреи отрезали путь с нагорий в долину. 35Аморреи продолжали жить на горе Херес, в городе Айялоне и поселении Шаалвиме, но когда сила дома Иосифа возросла, они тоже стали подневольными. 36Граница аморреев шла от Скорпионовой возвышенности1:36 Или: «возвышенности Акраббим»., от Селы и далее.