Yoswa 1 – CCL & NRT

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Yoswa 1:1-18

Yehova Asankha Yoswa Kukhala Mtsogoleri

1Atamwalira Mose mtumiki wa Mulungu, Yehova anati kwa Yoswa mwana wa Nuni mthandizi wa Mose: 2“Mose mtumiki wanga wamwalira. Ndipo iwe ndi anthu onsewa, tsopano konzekani kuwoloka mtsinje wa Yorodani kupita ku dziko limene ndiwapatse Aisraeli onse. 3Paliponse pamene phazi lanu liponde, ndikupatsani monga momwe ndinalonjezera Mose. 4Dziko lanu lidzayambira ku chipululu kummwera mpaka ku mapiri a Lebanoni kumpoto, kuchokeranso ku mtsinje waukulu wa Yufurate kummawa, mpaka dziko lonse la Ahiti, kukafika ku Nyanja Yayikulu ya kumadzulo. 5Palibe munthu amene adzatha kukugonjetsa masiku onse a moyo wako. Monga Ine ndinakhalira ndi Mose, chomwechonso ndidzakhala nawe. Sindidzakusiya kapena kukataya.

6“Ukhale wamphamvu ndi wolimba mtima, chifukwa iwe udzatsogolera anthu awa kukalandira dziko limene Ine ndinalonjeza makolo awo kuti ndidzawapatsa. 7Ukhale wamphamvu ndi wolimba mtima kwambiri. Usamale ndithu kuti umvere malamulo onse amene mtumiki wanga Mose anakupatsa. Usachoke pa malamulo anga ndipo kulikonse kumene udzapite udzapambana. 8Uziwerenga Buku la Malamuloli, uzilingalira zolembedwa mʼmenemo usana ndi usiku, kuti uchite zonse zimene zinalembedwamo. Ukamatero udzapeza bwino ndi kupambana. 9Paja ndinakulamula kuti ukhale wamphamvu ndi wolimba mtima. Choncho usamachite mantha kapena kutaya mtima popeza Ine Yehova Mulungu wako ndidzakhala nawe kulikonse kumene udzapite.”

10Tsono Yoswa analamula atsogoleri a Aisraeli nawawuza kuti, 11“Pitani ku misasa yonse ndipo muwuze anthu kuti, ‘Konzekani, mangani katundu wanu, popeza pakapita masiku atatu kuyambira lero mudzawoloka Yorodani kupita kukatenga dziko limene Yehova Mulungu wanu akukupatsani.’ ”

12Koma Yoswa anawuza fuko la Rubeni, fuko la Gadi ndi theka la fuko la Manase kuti, 13“Kumbukirani zimene Mose mtumiki wa Yehova anakulamulani kuti, ‘Yehova Mulungu wanu akukupatsani mpumulo, ndi dziko ili kuti likhale lanu.’ 14Tsono akazi anu, ana anu ndi ziweto zanu zitsale mʼdziko lino limene Mose anakupatsani kummawa kwa Yorodani. Koma ankhondo anu okha ndiwo awoloke atatenga zida zawo ndi kupita patsogolo pa abale anu kukawathandiza. 15Abale anuwo akadzalandira dziko limene Yehova Mulungu wanu akuwapatsa monga inu mwachitira, inu mudzabwerera kudzakhazikika mʼdziko lanu limene Mose mtumiki wa Yehova anakupatsani tsidya la kummawa kwa Yorodani.”

16Kenaka iwo anayankha Yoswa kuti, “Ife tidzachita chilichonse chimene mwatilamula, ndipo kulikonse kumene mudzatitume tidzapita. 17Monga momwe tinamvera Mose kwathunthu, chomwechonso tidzakumvera iwe. Yehova Mulungu wanu akhale nanu monga momwe anachitira ndi Mose. 18Aliyense wotsutsana ndi inu kapena wosamvera zimene mutilamula adzaphedwa. Inu mukhale wamphamvu ndi wolimba mtima!”

New Russian Translation

Навин 1:1-18

Господь повелевает Иисусу завоевать Ханаан

1После смерти слуги Господнего, Моисея, Господь сказал Иисусу, сыну Навину, помощнику Моисея:

2– Мой слуга Моисей умер. Итак, приготовься вместе со всем этим народом переправиться через реку Иордан в землю, которую Я даю им – израильтянам. 3Я отдам вам всякое место, на которое ступит ваша нога, как Я обещал Моисею. 4Ваша земля будет простираться от пустыни до Ливана, от великой реки, реки Евфрата (включая всю землю хеттов), до Великого1:4 То есть до Средиземного. Также в других местах книги. моря на западе. 5Никто не сможет противостоять тебе во все дни твоей жизни. Как Я был с Моисеем, так буду и с тобой; Я никогда тебя не оставлю и никогда не покину.

6Будь тверд и мужествен, потому что ты поведешь этих людей, чтобы им унаследовать землю, которую Я клялся дать их отцам. 7Будь тверд и очень мужествен. Тщательно исполняй весь Закон, который дал тебе Мой слуга Моисей. Не уклоняйся от него ни вправо, ни влево, чтобы тебе иметь успех везде, куда бы ты ни пошел. 8Пусть слова книги Закона всегда будут у тебя на устах; размышляй над ними день и ночь, чтобы в точности исполнять все, что написано. Тогда ты будешь процветать и иметь успех. 9Итак, Я повелеваю тебе: будь тверд и мужествен. Не страшись и не падай духом, потому что Господь, твой Бог, будет с тобой, куда бы ты ни пошел.

10И приказал Иисус начальникам народа:

11– Пройдите по лагерю и скажите народу: «Запаситесь едой, потому что через три дня вы переправитесь здесь через Иордан, чтобы войти и завладеть землей, которую Господь, ваш Бог, дает вам во владение».

12Но рувимитам, гадитам и половине рода Манассии Иисус сказал:

13– Помните повеление, которое дал вам Моисей, слуга Господа: «Господь, ваш Бог, дал вам покой и даровал эту землю». 14Ваши жены, дети и скот могут остаться в земле, которую Моисей дал вам к востоку от Иордана, но все ваши воины в полном вооружении должны переправиться впереди ваших братьев. Вы должны помогать вашим братьям, 15пока Господь не даст им покой, как Он сделал это для вас самих, и пока они тоже не завладеют землей, которую Господь, ваш Бог, дает им. После этого вы сможете вернуться и занять свою землю, которую Моисей, слуга Господа, дал вам к востоку от Иордана, к восходу солнца.

16Они ответили Иисусу:

– Мы исполним все, что бы ты ни приказал нам, и куда бы ты ни направил нас, мы пойдем. 17Как мы слушались Моисея, так будем слушаться и тебя. Только пусть Господь, твой Бог, будет с тобой, как Он был с Моисеем. 18Всякий, кто воспротивится твоему приказу и не послушается твоих слов – что бы ты ни приказал, – будет предан смерти. Только будь тверд и мужествен!