Yoswa 18 – CCL & NRT

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Yoswa 18:1-28

Kugawa kwa Madera Otsala a Dziko

1Atagonjetsa dziko lonse Aisraeli anasonkhana ku Silo ndipo anayimikako tenti ya msonkhano. 2Koma pa nthawiyo nʼkuti mafuko asanu ndi awiri a Aisraeli asanalandire cholowa chawo.

3Ndipo Yoswa anati kwa Aisraeli, “Kodi mudikira mpaka liti kuti mulowe ndi kulanda dziko limene Yehova Mulungu wa makolo anu wakupatsani? 4Sankhani amuna atatu kuchokera ku fuko lililonse ndipo ine ndidzawatuma kuti akayendere dzikolo ndi kukalilembera bwino kuti ndiligawe kukhala lawo. Akatero, abwererenso kwa ine. 5Aligawe dzikolo mʼzigawo zisanu ndi ziwiri; fuko la Yuda lidzakhale ndi dziko lake la kummwera ndi nyumba ya Yosefe ikhalebe mʼdziko lawo la kumpoto. 6Mudzalembe mawu ofotokoza za zigawo zisanu ndi ziwiri za dzikolo, ndi kubwera nawo kwa ine. Tsono ineyo ndidzakuchitirani maere pamaso pa Yehova Mulungu wanu. 7Alevi asakhale ndi dziko pakati panu, chifukwa gawo lawo ndi kutumikira Yehova pa ntchito ya unsembe. Ndipo Gadi, Rubeni ndi theka la fuko la Manase analandira kale cholowa chawo kummawa kwa Yorodani. Mose mtumiki wa Yehova ndiye anawapatsa.”

8Anthuwo akupita kukalembera dzikolo, Yoswa anawalangiza kuti, “Pitani mukayendere ndi kulembera dzikolo. Kenaka mukabwere kwa ine, ndidzakuchitirani maere kuno ku Silo pamaso pa Yehova.” 9Ndipo anthu anachoka ndi kukayendera dziko lonse. Iwo analemba bwinobwino mʼbuku za dzikolo, mzinda ndi mzinda. Analigawa magawo asanu ndi awiri, ndipo anabwerera kwa Yoswa ku misasa ya ku Silo. 10Pambuyo pake Yoswa anawachitira maere ku Silo pamaso pa Yehova, ndipo fuko lililonse la Israeli analigawira dziko lake.

Dziko la Benjamini

11Maere anagwera mabanja a fuko la Benjamini. Dziko limene anapatsidwa linali pakati pa fuko la Yuda ndi fuko la Yosefe:

12Mbali ya kumpoto malire awo anayambira ku Yorodani nalowera chakumpoto kwa matsitso a ku Yeriko kulowera cha kumadzulo kwa dziko la ku mapiri ndi kukafika ku chipululu cha Beti-Aveni. 13Kuchokera kumeneko malirewo analoza ku Luzi nadutsa mʼmbali mwa mapiri kummwera kwa Luzi (ndiye Beteli) ndipo anatsika mpaka ku Ataroti Adari, ku mapiri a kummwera kwa Beti-Horoni wa Kumunsi.

14Ndipo malirewo analowanso kwina, analunjika kummwera kuchokera kumadzulo kwake kwa phiri loyangʼanana ndi Beti-Horoni, mpaka ku mzinda wa Kiriyati Baala (ndiye Kiriati Yearimu), mzinda wa anthu a fuko la Yuda. Amenewa ndiye anali malire a mbali ya kumadzulo.

15Malire a kummwera anayambira mʼmphepete mwenimweni mwa Kiriati Yearimu napita kumadzulo mpaka kukafika ku akasupe a Nefitowa. 16Malire anatsikira mʼmphepete mwa phiri loyangʼanana ndi chigwa cha Beni Hinomu, kumpoto kwa chigwa cha Refaimu. Anapitirira kutsikira ku chigwa cha Hinomu kummwera kwa chitunda cha Ayebusi mpaka ku Eni Rogeli. 17Kenaka anakhotera kumpoto kupita ku Eni-Semesi, kupitirira mpaka ku Geliloti amene amayangʼanana ndi pokwera pa Adumimu. Kenaka malire anatsikira ku Mwala wa Bohani, mwana wa Rubeni. 18Anabzola cha kumpoto kwa chitunda cha Beti Araba ndi kutsikabe mpaka ku chigwa cha Yorodani. 19Anabzolanso cha kumpoto kwa chitunda cha Beti-Hogila kukafika cha kumpoto ku gombe la Nyanja ya Mchere kumene mtsinje wa Yorodani umathirirako, cha kummwera kwenikweni. Awa anali malire a kummwera.

20Yorodani ndiye anali malire a mbali ya kummawa.

Awa anali malire a dziko limene mabanja a fuko la Benjamini analandira.

21Mabanja a fuko la Benjamini anali ndi mizinda iyi;

Yeriko, Beti-Hogila, Emeki Kezizi, 22Beti-Araba, Zemaraimu, Beteli 23Avimu, Para, Ofiri, 24Kefari-Amoni, Ofini ndi Geba, mizinda khumi ndi awiri ndi midzi yake

25Panalinso Gibiyoni, Rama, Beeroti, 26Mizipa, Kefira, Moza 27Rekemu, Iripeeli, Tarala, 28Zera Haelefu, mzinda wa Ayebusi (ndiye kuti Yerusalemu) Gibeya ndi Kiriati, mizinda 14 ndi midzi yake.

Limeneli ndilo dziko limene mabanja a fuko la Benjamini analandira kuti likhale lawo.

New Russian Translation

Навин 18:1-28

Раздел остальной земли

1Все общество израильтян собралось в Шило и поставило там шатер собрания. Страна была покорена ими, 2но семь израильских родов еще не получили своего удела.

3Иисус сказал израильтянам:

– Сколько вы еще будете ждать, прежде чем пойдете и возьмете в удел землю, которую дал вам Господь, Бог ваших отцов? 4Отрядите по три человека из каждого рода. Я отправлю их, чтобы они прошли по земле, описали ее по уделам каждого и вернулись ко мне. 5Разделите землю на семь частей. Иуда пусть останется в своей земле на юге, а дом Иосифа в своей земле на севере. 6Сделав описания семи частей земли, принесите их сюда ко мне, и я брошу о вас жребий перед Господом, нашим Богом. 7Но левиты не получат надела между вами, потому что их удел – священническая служба Господа. А Гад, Рувим и половина рода Манассии уже получили свои наделы на восточной стороне Иордана. Им дал его Моисей, слуга Господа.

8Когда те люди тронулись в путь, чтобы описать землю, Иисус велел им:

– Ступайте, пройдите по земле и опишите ее. Потом возвращайтесь ко мне, и я брошу о вас жребий здесь, в Шило, перед Господом.

9И те люди пошли, прошли по земле, описали ее по городам в семи частях в свитке и вернулись к Иисусу в лагерь в Шило. 10И Иисус бросил о них жребий в Шило перед Господом и распределил израильтянам землю по их родовым разделениям.

Надел Вениамина

11Выпал жребий рода Вениамина по их кланам. Доставшаяся им земля лежала между наделами родов Иуды и Иосифа:

12На севере их граница шла от Иордана по склону к северу от Иерихона и поднималась в нагорья, доходя до пустыни Бет-Авен. 13Оттуда она шла к склону на юге от Луза (то есть Вефиля) и спускалась к Атарот-Аддару и к горе, что к югу от Нижнего Бет-Хорона.

14От холма, что напротив Бет-Хорона, на юге граница поворачивала к югу по западной стороне надела и заканчивалась у Кирьят-Баала (то есть Кирьят-Иеарима), города народа Иуды. Это была западная граница.

15Южная граница шла от предместий Кирьят-Иеарима на западе и оттуда к источнику вод Нефтоах. 16Затем граница спускалась к подножию горы, что напротив долины Бен-Гинном, к северу от долины Рефаим. Она нисходила долиной Гинном по южному склону города иевусеев к Эн-Рогелу. 17Затем она сворачивала на север, шла к Эн-Шемешу, тянулась к Гелилоту, что напротив возвышенности Адуммим, и спускалась к камню Богана, сына Рувима. 18Она тянулась к северному склону Бет-Аравы18:18 Так в одном из древних переводов; в еврейском тексте: «склону напротив Арабы». и спускалась в саму Иорданскую долину. 19Затем она шла к северному склону Бет-Хоглы и доходила до северного залива Соленого моря, у устья Иордана. Такова была северная граница.

20Границей на восточной стороне был Иордан.

Таковы были границы наделов, данных кланам Вениамина.

21Род Вениамина по их кланам владел следующими городами:

Иерихон, Бет-Хогла, Емек-Кециц, 22Бет-Арава, Цемараим, Вефиль, 23Аввим, Фара, Офра, 24Кефар-Аммони, Офни и Гева – двенадцать городов с окрестными поселениями.

25Гаваон, Рама, Беэрот, 26Мицпе, Кефира, Моца, 27Рекем, Ирфеил, Тарала, 28Цела, Елеф, иевусейский город (то есть Иерусалим), Гива и Кирьят-Иеарим18:28 Так в одном из древних переводов; евр.: «Кирьят». – четырнадцать городов с окрестными поселениями.

Таков был удел Вениамина для его кланов.