Yobu 37 – CCL & TNCV

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Yobu 37:1-24

1“Mtima wanga ukulumphalumpha pa chimenechinso

ndipo ukuchoka mʼmalo mwake.

2Tamverani! Tamverani kubangula kwa liwu lake,

kugunda kumene kukuchokera mʼkamwa mwake.

3Iye amaponya chingʼaningʼani chake pansi pa thambo lonse

ndipo amachitumiza ku dziko lapansi.

4Pambuyo pake kubangula kwake kumamveka.

Iye amabangula ndi liwu lake laulemerero.

Pamene wabangula,

palibe chimene amalephera kuchita.

5Liwu la Mulungu limabangula mʼnjira zambiri zodabwitsa

Iye amachita zinthu zazikulu zimene sitingathe kuzimvetsa.

6Amalamula chisanu chowundana kuti, ‘Igwa pa dziko lapansi,’

ndipo amalamulanso mvula yamawawa kuti, ‘Khala mvula yamphamvu.’

7Kuti anthu onse amene anawalenga athe kuzindikira ntchito yake.

Iye amalepheretsa anthu kugwira ntchito zawo.

8Zirombo zimakabisala

ndipo zimakhala mʼmaenje mwawo.

9Mphepo yamkuntho imatuluka ku malo ake,

kuzizira kumatuluka mʼmphepo yamkunthoyo.

10Mpweya wa Mulungu umawunditsa madzi

ndipo madzi a mʼnyanja amawuma kuti gwaa.

11Iye amadzaza mitambo ndi madzi a mvula,

amabalalitsa zingʼaningʼani zake kuchokera mʼmitambomo.

12Mulungu amayendetsa mitamboyo

mozungulirazungulira dziko lonse lapansi

kuti ichite zonse zimene Iye akufuna pa dziko lapansi.

13Iye amagwetsa mvula kuti alange anthu,

kapena kubweretsa chinyontho pa dziko lapansi kuti aonetse chikondi chake.

14“Abambo Yobu, tamvani izi;

imani ndipo muganizire ntchito zodabwitsa za Mulungu.

15Kodi mukudziwa momwe Mulungu amayendetsera mitambo

ndi kuchititsa kuti kukhale zingʼaningʼani?

16Kodi mukudziwa momwe Mulungu amayalira mitambo,

ntchito zodabwitsa za Iye amene ndi wanzeru zangwiro?

17Inu amene mʼzovala zanu mumatuluka thukuta

pamene kunja kwatentha chifukwa cha mphepo yakummwera,

18kodi mungathe kuthandizana naye kutambasula thambo

limene ndi lolimba ngati chitsulo?

19“Tiwuzeni ife zoti tikanene kwa Iye;

sitingathe kufotokoza mlandu wathu chifukwa cha mdima umene uli mwa ife.

20Kodi nʼkofunika kumudziwitsa Mulungu kuti ndili naye mawu?

Kodi kutero sikuchita ngati kupempha kuti ndiwonongeke?

21Tsopano munthu sangathe kuyangʼana dzuwa,

ndi kunyezimira mlengalenga,

kuwomba kwa mphepo kutachotsa mitambo yonse.

22Kuwala kwake kumaonekera cha kumpoto;

Mulungu amabwera ndi ulemerero woopsa.

23Wamphamvuzonse sitingathe kumufikira pafupi ndi wa mphamvu zoposa;

pa chiweruzo chake cholungama ndi mʼchilungamo chake chachikulu Iye sapondereza anthu ozunzika.

24Nʼchifukwa chake anthu amamuopa kwambiri,

kodi saganizira za onse amene amaganiza kuti ndi anzeru?”

Thai New Contemporary Bible

โยบ 37:1-24

1“จิตใจของข้าพเจ้าสั่นระรัว

และสะทกสะท้านด้วยข้อนี้

2ฟังสิ! ฟังเสียงกัมปนาทของพระองค์

เสียงดังก้องจากพระโอษฐ์ของพระองค์

3พระองค์ทรงปล่อยฟ้าแลบไปทั่วใต้ฟ้าสวรรค์

และทรงส่งออกไปไกลถึงสุดปลายแผ่นดินโลก

4ติดตามด้วยพระสุรเสียงกึกก้อง

เป็นเสียงกระหึ่มด้วยเดชานุภาพ

เมื่อพระองค์ทรงเปล่งพระสุรเสียง

พระองค์ก็ไม่ได้ทรงหน่วงเหนี่ยวสิ่งใดไว้

5พระสุรเสียงของพระเจ้าดังกึกก้องอย่างน่าอัศจรรย์

ทรงกระทำสิ่งยิ่งใหญ่เกินกว่าเราจะเข้าใจ

6พระองค์ทรงบัญชาหิมะว่า ‘จงตกลงมาบนแผ่นดินโลก’

และตรัสกับสายฝนว่า ‘จงเทลงมาอย่างหนัก’

7พระเจ้าทรงทำให้มนุษย์หยุดจากงานของพวกเขา37:7 หรือพระเจ้าทำให้ทุกคนเต็มไปด้วยความกลัวโดยฤทธิ์อำนาจของพระองค์

เพื่อมนุษย์ทั้งปวงที่พระองค์ทรงสร้างขึ้นจะรู้ถึงพระราชกิจของพระองค์

8สัตว์ทั้งหลายเข้าสู่ที่กำบัง

พักอยู่ในถ้ำของมัน

9พายุออกมาจากแหล่งของมัน

ความหนาวเย็นมากับลมกล้า

10ลมหายใจของพระเจ้าทรงทำให้เกิดน้ำแข็ง

ทรงทำให้ห้วงน้ำกว้างใหญ่แข็งตัว

11พระองค์ทรงบรรจุความชุ่มชื้นไว้ในเมฆ

และทรงกระจายสายฟ้าแลบออกไป

12เมื่อพระองค์ทรงบัญชา เมฆก็หมุนวนเหนือพื้นผิวของทั้งโลก

มันทำทุกอย่างตามที่ทรงบัญชา

13พระองค์ทรงส่งเมฆมาเพื่อลงโทษมนุษย์

หรือเพื่อรดแผ่นดินโลกของพระองค์37:13 หรือเพื่อทำให้พวกเขาพอใจและแสดงความรักมั่นคงของพระองค์

14“ฟังเถิด โยบเอ๋ย

จงนิ่งพิจารณาสิ่งอัศจรรย์ทั้งปวงของพระเจ้า

15ท่านทราบไหมว่า พระเจ้าทรงควบคุมเมฆ

และทำให้ฟ้าแลบได้อย่างไร?

16ท่านทราบไหมว่าเมฆลอยอยู่ได้อย่างไร?

ท่านทราบการอัศจรรย์ต่างๆ ของพระองค์ผู้ทรงรู้ทุกสิ่งอย่างถ่องแท้หรือ?

17ท่านผู้ร้อนอึดอัดอยู่ในเสื้อผ้า

เมื่อแผ่นดินโลกซบเซาอยู่เพราะลมใต้

18ท่านสามารถช่วยพระเจ้าคลี่ท้องฟ้าออกมา

ซึ่งแข็งเหมือนแผ่นทองสัมฤทธิ์ขัดเงาได้หรือ?

19“บอกเราสิว่าเราจะทูลพระองค์ว่าอย่างไรได้

เราไม่สามารถแถลงคดีของเราเนื่องจากความมืดของเรา

20จะทูลพระองค์ได้หรือว่าข้าพระองค์อยากจะพูด?

มีใครบ้างขอให้ตนเองถูกกลืนกิน?

21ไม่มีใครสามารถมองดูดวงอาทิตย์ได้

ซึ่งส่องแสงเจิดจ้าในท้องฟ้า

ยามที่ลมพัดเมฆผ่านพ้นไป

22พระเจ้าเสด็จมาจากทิศเหนือด้วยแสงทองเจิดจรัส

พระองค์เสด็จมาด้วยพระบารมีอันน่าครั่นคร้าม

23องค์ทรงฤทธิ์สูงส่งเกินกว่าเราจะเอื้อมถึง และฤทธิ์อำนาจของพระองค์เป็นที่เทิดทูน

ถึงกระนั้นโดยความชอบธรรมและความยุติธรรม พระองค์ไม่ได้ทรงกดขี่ข่มเหง

24ฉะนั้นมวลมนุษย์จึงยำเกรงพระองค์

เพราะพระองค์ทรงดูแลทุกคนที่มีปัญญาไม่ใช่หรือ?37:24 หรือพระองค์ไม่ทรงแยแสผู้ใดที่คิดว่าตนเองมีปัญญา