Estere 1 – CCL & TNCV

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Estere 1:1-22

Vasiti Mkazi wa Mfumu Achotsedwa

1Izi ndi zimene zinachitika pa nthawi ya ufumu wa Ahasiwero, amene analamulira zigawo 127 kuyambira ku India mpaka ku Kusi. 2Pa nthawi imeneyi nʼkuti mfumu Ahasiwero atakhazikika pa mpando wake wa ufumu mu mzinda wa Susa, 3ndipo mʼchaka chachitatu cha ufumu wake anakonza phwando la olemekezeka ndi nduna zake. Atsogoleri a nkhondo a ku Peresiya ndi Mediya, anthu olemekezeka pamodzi ndi nduna za mʼzigawo zonse anasonkhana kwa iye.

4Pa nthawi yomweyi kwa masiku 180 a phwando mfumu inkaonetsa kulemera kwa ulemerero wa ufumu wake ndiponso kukongola ndi kukula kwa ufumu wake. 5Atatha masiku amenewa, kwa masiku ena asanu ndi awiri mfumu inakonzanso phwando la anthu onse okhala mu mzinda wa Susa kuyambira anthu olemekezeka mpaka anthu wamba ku bwalo la munda la nyumba yake yaufumu. 6Bwalo la mundali analikongoletsa ndi makatani a nsalu zoyera ndi za mtundu wamtambo zimene anazimangirira ndi zingwe za nsalu zoyera ndi zapepo ku mphete za siliva zimene anazikoloweka pa nsanamira za maburo. Anayika mipando yopumirapo yagolide ndi siliva pabwalo la miyala yoyala yamtengowapatali yofiira, ya marabulo, ndi yonyezimira. 7Anapereka zakumwa mʼchikho zagolide zamitundumitundu, ndipo vinyo waufumu anali wochuluka kwambiri monga mwa kukoma mtima kwa mfumu. 8Monga mwa lamulo la mfumu aliyense anamwa mʼmene anafunira, pakuti mfumu inawuza otumikira ake kuti apatse aliyense monga mwa kukonda kwake.

9Mkazi wa mfumu Vasiti nayenso anakonzera phwando amayi ku nyumba ya ufumu ya mfumu Ahasiwero.

10Pa tsiku la chisanu ndi chiwiri, pamene mfumu Ahasiwero inaledzera ndi vinyo, inalamula adindo ofulidwa asanu ndi awiri amene ankamutumikira: Mehumani, Bizita, Haribona, Bigita, Abagita, Zetara, ndi Karikasi 11kuti abwere naye mfumukazi Vasiti pamaso pa mfumu atavala chipewa chaufumu. Cholinga cha mfumu chinali choti adzamuonetse kwa anthu onse ndi olemekezeka, chifukwa anali wokongola kwambiri. 12Koma antchito atapereka uthenga wa mfumu kwa mfumukazi, Vasiti anakana kubwera. Tsono mfumu inakwiya ndi kupsa mtima.

13Mfumu inayankhula ndi anthu anzeru ndi ozindikira choyenera kuchita popeza chinali chikhalidwe chake kufunsa uphungu kwa akatswiri pa nkhani za malamulo ndi kuweruza kolungama. 14Anthu amene ankakhala pafupi ndi mfumu anali awa: Karisena, Setara, Adimata, Tarisisi, Meresi, Marisena ndi Memukani, olemekezeka asanu ndi awiri a ku Peresiya ndi Medina amene ankaloledwa mwapadera kuonana ndi mfumu ndipo anali pamwamba kwambiri mu ufumuwo.

15Mfumu inafunsa kuti, “Kodi titani naye mfumukazi Vasiti mwa lamulo, popeza sanamvere lamulo la ine mfumu Ahasiwero limene adindo ofulidwa anakamuwuza?”

16Ndipo Memukani anayankha pa maso pa mfumu ndi olemekezeka anzake kuti, “Mfumukazi Vasiti sanalakwire mfumu yokha, koma walakwiranso olemekezeka onse ndi anthu onse okhala mʼzigawo zonse za mfumu Ahasiwero. 17Pakuti amayi onse adzadziwa zimene wachita mfumukazi ndipo kotero adzapeputsa amuna awo ndi kunena kuti, ‘Mfumu Ahasiwero analamulira kuti abwere naye mfumukazi Vasiti kwa iye koma sanapite.’ 18Lero lomwe lino amayi olemekezeka a ku Peresiya ndi Mediya amene amva zimene wachita mfumukazi adzaganiza zochita chimodzimodzi kwa nduna zonse za mfumu. Ndipo kupeputsana ndi kukongola zidzapitirira.”

19“Choncho, ngati chikukomerani mfumu, lamulirani kuti Vasiti asadzaonekerenso pamaso pa mfumu Ahasiwero. Lamuloli lilembedwe mʼmabuku a malamulo a Aperezi ndi Amedi kuti lisadzasinthike. Pamalo pa Vasiti ngati mfumukazi payikidwepo mkazi wina amene ali bwino kuposa iye. 20Ndipo lamulo la mfumuli lilengezedwa mʼdziko lake lonse ngakhale lili lalikulu, amayi onse adzapereka ulemu kwa amuna awo, amuna olemekezeka mpaka amuna wamba.”

21Mfumu ndi nduna zake anakondwera ndi uphungu uwu, kotero mfumu inachita monga momwe ananenera Memukani. 22Mfumu inatumiza makalata ku madera onse a ufumu wake, chigawo chilichonse mʼzilembo zawo ndi ku mtundu uliwonse mʼchiyankhulo chawochawo kulengeza kuti mwamuna ayankhule chilichonse chimene chikumukomera.

Thai New Contemporary Bible

เอสเธอร์ 1:1-22

พระนางวัชทีถูกปลด

1เหตุการณ์นี้เกิดขึ้นในสมัยของกษัตริย์เซอร์ซีส1:1 ภาษาฮีบรูว่าอาหะสุเอรัสเป็นอีกรูปหนึ่งของเซอร์ซีส ซึ่งเป็นชื่อเปอร์เซีย ทั้งในข้อนี้และตลอดพระธรรมเอสเธอร์ผู้ทรงปกครอง 127 มณฑลจากอินเดียถึงคูช1:1 คือ ตอนบนของลุ่มแม่น้ำไนล์ 2ครั้งนั้นกษัตริย์เซอร์ซีสทรงครองราชบัลลังก์ในป้อมเมืองสุสา 3และในปีที่สามแห่งรัชกาลของพระองค์ พระองค์ทรงจัดงานเลี้ยงใหญ่ประทานแก่เหล่าขุนนางและข้าราชบริพาร บรรดาแม่ทัพนายกองแห่งมีเดียและเปอร์เซีย เจ้านายและขุนนางจากทุกมณฑลล้วนมาเข้าเฝ้า

4กษัตริย์ทรงแสดงความมั่งคั่งของราชอาณาจักร พระเกียรติ บารมี และความโอ่อ่าตระการตลอด 180 วัน 5หลังจากนั้นกษัตริย์ทรงจัดงานเลี้ยงเจ็ดวันที่ลานอุทยานของพระราชวังสำหรับทุกคนที่อยู่ในป้อมเมืองสุสา ตั้งแต่ผู้ยิ่งใหญ่ที่สุดลงมาถึงผู้น้อยที่สุด 6ในอุทยานมีม่านลินินสีขาวและสีน้ำเงินร้อยด้วยเชือกลินินสีขาวและสีม่วงเข้ากับห่วงเงินบนเสาหินอ่อน มีตั่งทองคำและเงินตั้งอยู่ตามบาทวิถีซึ่งฝังหินแดง หินอ่อน หอยมุก และพลอยราคาแพงอื่นๆ 7เหล้าองุ่นที่นำออกมาแจกจ่ายบรรจุในภาชนะทองคำ แต่ละใบมีรูปทรงและลวดลายไม่ซ้ำกัน กษัตริย์ทรงประทานเหล้าองุ่นหลวงให้ดื่มอย่างเหลือเฟือ 8แขกแต่ละคนดื่มได้ตามใจชอบ เพราะพระองค์ทรงบัญชาพนักงานฝ่ายเหล้าองุ่นให้นำมาบริการตามความพอใจของทุกคน

9พระราชินีวัชทีก็ทรงจัดงานเลี้ยงสำหรับเหล่าสตรีในราชสำนักของกษัตริย์เซอร์ซีสด้วย

10ในวันที่เจ็ดเมื่อกษัตริย์เซอร์ซีสสำราญพระทัยด้วยเหล้าองุ่นก็ตรัสเรียกขันทีประจำพระองค์ทั้งเจ็ดคือ เมหุมาน บิสธา ฮารโบนา บิกธา อาบักธา เศธาร์ และคารคัส 11ให้ไปทูลเชิญพระนางวัชทีสวมมงกุฎมาเข้าเฝ้าพระองค์ เพื่อให้ประชาชนและเหล่าขุนนางได้ยลโฉมเพราะพระนางทรงพระสิริโฉมยิ่งนัก 12แต่เมื่อคนเหล่านี้ไปทูลเชิญตามพระบัญชาของกษัตริย์ พระนางไม่ยอมมา กษัตริย์จึงทรงพระพิโรธยิ่งนัก

13เนื่องจากเป็นประเพณีที่กษัตริย์จะต้องปรึกษากับผู้เชี่ยวชาญในเรื่องกฎหมายและความยุติธรรม พระองค์จึงตรัสกับเหล่านักปราชญ์ผู้เข้าใจยุคสมัย 14ซึ่งเป็นผู้ใกล้ชิดกษัตริย์ที่สุดได้แก่ คารเชนา เชธาร์ อัดมาธา ทารชิช เมเรส มารเสนา และเมมูคาน ขุนนางทั้งเจ็ดแห่งมีเดียและเปอร์เซีย ซึ่งเป็นผู้ที่มีสิทธิพิเศษในการเข้าเฝ้ากษัตริย์และเป็นผู้มีอำนาจสูงสุดในราชอาณาจักร

15พระองค์ตรัสถามว่า “กฎหมายระบุให้ทำอย่างไรบ้างกับพระนางวัชทีซึ่งไม่ยอมปฏิบัติตามคำสั่งของกษัตริย์เซอร์ซีสตามที่ให้ขันทีไปเชิญ?”

16แล้วเมมูคานทูลตอบต่อหน้ากษัตริย์และต่อหน้าเหล่าขุนนางว่า “พระนางวัชทีไม่ได้ทรงทำผิดต่อองค์กษัตริย์เท่านั้น แต่ต่อขุนนางและประชาราษฎร์ทั้งปวงในทุกมณฑลของกษัตริย์เซอร์ซีสด้วย 17เพราะหญิงทั้งปวงจะรู้ถึงการกระทำของพระนาง และจะพากันดูแคลนสามี และพูดกันว่า ‘กษัตริย์เซอร์ซีสทรงบัญชาให้พระราชินีวัชทีไปเข้าเฝ้า แต่พระนางไม่ยอมไป’ 18ในวันนี้บรรดาหญิงสูงศักดิ์แห่งมีเดียและเปอร์เซียซึ่งได้ยินการกระทำของพระนางวัชที ก็จะปฏิบัติต่อขุนนางของกษัตริย์ในทำนองเดียวกัน จะทำให้ขาดความเคารพและเกิดความขัดแย้งไม่มีที่สิ้นสุด

19“ฉะนั้นหากฝ่าพระบาททรงดำริชอบ ขอให้ร่างพระราชโองการเป็นกฎหมายของชาวมีเดียและเปอร์เซียซึ่งจะล้มเลิกไม่ได้ ห้ามพระนางวัชทีเข้าเฝ้าฝ่าพระบาทอีก ทั้งให้ฝ่าพระบาทประทานตำแหน่งพระราชินีแก่คนอื่นซึ่งดีกว่าพระนาง 20เมื่อประกาศพระราชโองการนี้ทั่วราชอาณาจักรอันกว้างใหญ่ไพศาลของฝ่าพระบาทแล้ว หญิงทั้งปวงจะเคารพสามี ตั้งแต่ผู้น้อยที่สุดไปจนถึงผู้ใหญ่ที่สุด”

21กษัตริย์และขุนนางทั้งปวงเห็นชอบในคำทูลนี้ ฉะนั้นกษัตริย์ทรงทำตามที่เมมูคานทูลเสนอ 22และมีพระราชสาส์นออกไปยังทุกมณฑลทั่วราชอาณาจักร เป็นภาษาถิ่นครบทุกภาษา ประกาศว่าผู้ชายทุกคนเป็นผู้ปกครองเหนือครัวเรือนของตน