Nehemiya 1 – CCL & TNCV

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Nehemiya 1:1-11

Pemphero la Nehemiya

1Awa ndi mawu a Nehemiya mwana wa Hakaliya:

Pa mwezi wa Kisilevi, chaka cha makumi awiri, pamene ndinali mu mzinda wa Susa, 2Hanani mmodzi mwa abale anga, anabwera ndi anthu ena kuchokera ku Yuda, ndipo ine ndinawafunsa za Ayuda otsala amene sanatengedwe ukapolo, ndiponso za mzinda wa Yerusalemu.

3Anandiyankha kuti, “Amene sanatengedwe ukapolo aja ali pa mavuto aakulu ndipo ali ndi manyazi. Khoma la Yerusalemu ndilogamukagamuka ndipo zipata zake zinatenthedwa ndi moto.”

4Nditamva zimenezi, ndinakhala pansi ndi kuyamba kulira. Ndinalira kwa masiku angapo. Ndinkasala zakudya ndi kumapemphera pamaso pa Mulungu Wakumwamba. 5Ndinkati:

“Inu Yehova, Mulungu wakumwamba, Mulungu wamkulu ndi woopsa. Mumasunga pangano ndi kuonetsa chikondi chosasinthika kwa onse amene amakukondani ndi kumvera malamulo anu. 6Tcherani khutu lanu ndi kutsekula maso anu kuti mumve pemphero la mtumiki wanune limene ndikupemphera usana ndi usiku pamaso panu kupempherera Aisraeli, atumiki anu. Ndikuvomereza machimo a Aisraeli amene tinakuchimwirani. Ndithu, ine ndi banja la makolo anga tinakuchimwirani. 7Ife tinakuchitirani zoyipa zambiri. Sitinamvere mawu anu, malamulo ndi malangizo anu amene munapereka kwa mtumiki wanu Mose.

8“Kumbukirani mawu amene munawuza mtumiki wanu Mose akuti, ‘Ngati mukhala osakhulupirika, ndidzakubalalitsani pakati pa mitundu ina. 9Koma mukabwerera kwa Ine, mukamvera malamulo anga ndi kuwatsatadi, ndiye kuti ngakhale anthu anu atabalalika kutali chotani, Ine ndidzawasonkhanitsa kuchokera kumeneko ndi kubwera nawo ku malo amene ndinasankha kuti azidzayitanira dzina langa.’

10“Iwo ndi atumiki anu ndi anthu anu, amene munawawombola ndi mphamvu yanu yayikulu ndi dzanja lanu lamphamvu. 11Inu Ambuye tcherani khutu lanu kuti mumve pemphero la mtumiki wanune ndiponso pemphero la atumiki anu amene amakondwera kuchitira ulemu dzina lanu. Lolani kuti mtumiki wanune zinthu zindiyendere bwino lero ndi kuti mfumu indichitire chifundo.”

Nthawi imeneyi nʼkuti ndili woperekera zakumwa kwa mfumu.

Thai New Contemporary Bible

เนหะมีย์ 1:1-11

คำอธิษฐานของเนหะมีย์

1ถ้อยคำของเนหะมีย์บุตรฮาคาลิยาห์ความว่า

เมื่อข้าพเจ้าอยู่ที่ป้อมเมืองสุสา ในเดือนคิสเลฟ ปีที่ยี่สิบแห่งรัชกาลกษัตริย์อารทาเซอร์ซีส 2ฮานานีพี่น้องคนหนึ่งจากยูดาห์มาเยี่ยมข้าพเจ้าพร้อมกับคนอื่นๆ ข้าพเจ้าจึงซักถามพวกเขาเกี่ยวกับเยรูซาเล็มและชาวยิวที่เหลือซึ่งรอดพ้นจากการเป็นเชลย

3พวกเขาตอบข้าพเจ้าว่า “คนที่เหลือซึ่งรอดพ้นจากการเป็นเชลยและกลับไปยังแว่นแคว้นเดิมนั้นมีความทุกข์และความอัปยศอย่างยิ่ง กำแพงเยรูซาเล็มก็ปรักหักพัง ประตูเมืองก็ถูกเผาไปแล้ว”

4เมื่อข้าพเจ้าได้ยินเช่นนี้ก็นั่งลงร้องไห้ ข้าพเจ้าโศกเศร้า ถืออดอาหาร และอธิษฐานต่อหน้าพระเจ้าแห่งฟ้าสวรรค์อยู่หลายวัน 5แล้วข้าพเจ้าอธิษฐานว่า

“ข้าแต่พระยาห์เวห์พระเจ้าแห่งฟ้าสวรรค์ พระองค์ทรงเป็นพระเจ้าผู้ยิ่งใหญ่และน่าเกรงขาม ผู้ทรงรักษาพันธสัญญาแห่งความรักต่อบรรดาผู้ที่รักและเชื่อฟังพระบัญชาของพระองค์ 6ขอทรงสดับฟังและทอดพระเนตรผู้รับใช้ของพระองค์ซึ่งกำลังทูลอธิษฐานต่อหน้าพระองค์ทั้งวันทั้งคืนเพื่อประชากรอิสราเอลผู้รับใช้ของพระองค์ ข้าพระองค์ขอสารภาพบาปที่เราชาวอิสราเอล รวมทั้งข้าพระองค์และตระกูลของข้าพระองค์ได้ละเมิดต่อพระองค์ 7ข้าพระองค์ทั้งหลายได้ประพฤติตัวเลวทรามต่อพระองค์ ไม่เชื่อฟังพระบัญชา กฎหมาย และบทบัญญัติซึ่งพระองค์ประทานแก่โมเสสผู้รับใช้ของพระองค์

8“โปรดทรงระลึกถึงถ้อยคำของพระองค์ที่ทรงให้โมเสสผู้รับใช้ของพระองค์ไว้ว่า ‘หากพวกเจ้าไม่ซื่อสัตย์ เราจะทำให้เจ้ากระจัดกระจายไปตามชนชาติต่างๆ 9แต่หากเจ้าหันกลับมาหาเราและเชื่อฟังคำสั่งของเรา ถึงแม้เจ้าจะตกเป็นเชลยในแดนไกลสุดขอบฟ้า เราก็จะรวบรวมเจ้าทั้งหลายกลับสู่สถานที่นี้ ซึ่งเราได้เลือกเป็นที่สถาปนานามของเรา’

10“ข้าพระองค์ทั้งหลายเป็นผู้รับใช้และเป็นประชากรของพระองค์ซึ่งพระองค์ได้ทรงไถ่ไว้โดยเดชานุภาพอันยิ่งใหญ่และพระหัตถ์อันเกรียงไกร 11ข้าแต่องค์พระผู้เป็นเจ้าโปรดสดับฟังคำอธิษฐานของผู้รับใช้คนนี้และของบรรดาผู้รับใช้ซึ่งยำเกรงพระนามของพระองค์ด้วยความปีติยินดี โปรดประทานความสำเร็จแก่ผู้รับใช้ของพระองค์ในวันนี้ โดยให้ข้าพระองค์เป็นที่โปรดปรานของชายผู้นี้”

ข้าพเจ้าเป็นผู้เชิญจอกเสวยของกษัตริย์