Yobu 37 – CCL & NIRV

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Yobu 37:1-24

1“Mtima wanga ukulumphalumpha pa chimenechinso

ndipo ukuchoka mʼmalo mwake.

2Tamverani! Tamverani kubangula kwa liwu lake,

kugunda kumene kukuchokera mʼkamwa mwake.

3Iye amaponya chingʼaningʼani chake pansi pa thambo lonse

ndipo amachitumiza ku dziko lapansi.

4Pambuyo pake kubangula kwake kumamveka.

Iye amabangula ndi liwu lake laulemerero.

Pamene wabangula,

palibe chimene amalephera kuchita.

5Liwu la Mulungu limabangula mʼnjira zambiri zodabwitsa

Iye amachita zinthu zazikulu zimene sitingathe kuzimvetsa.

6Amalamula chisanu chowundana kuti, ‘Igwa pa dziko lapansi,’

ndipo amalamulanso mvula yamawawa kuti, ‘Khala mvula yamphamvu.’

7Kuti anthu onse amene anawalenga athe kuzindikira ntchito yake.

Iye amalepheretsa anthu kugwira ntchito zawo.

8Zirombo zimakabisala

ndipo zimakhala mʼmaenje mwawo.

9Mphepo yamkuntho imatuluka ku malo ake,

kuzizira kumatuluka mʼmphepo yamkunthoyo.

10Mpweya wa Mulungu umawunditsa madzi

ndipo madzi a mʼnyanja amawuma kuti gwaa.

11Iye amadzaza mitambo ndi madzi a mvula,

amabalalitsa zingʼaningʼani zake kuchokera mʼmitambomo.

12Mulungu amayendetsa mitamboyo

mozungulirazungulira dziko lonse lapansi

kuti ichite zonse zimene Iye akufuna pa dziko lapansi.

13Iye amagwetsa mvula kuti alange anthu,

kapena kubweretsa chinyontho pa dziko lapansi kuti aonetse chikondi chake.

14“Abambo Yobu, tamvani izi;

imani ndipo muganizire ntchito zodabwitsa za Mulungu.

15Kodi mukudziwa momwe Mulungu amayendetsera mitambo

ndi kuchititsa kuti kukhale zingʼaningʼani?

16Kodi mukudziwa momwe Mulungu amayalira mitambo,

ntchito zodabwitsa za Iye amene ndi wanzeru zangwiro?

17Inu amene mʼzovala zanu mumatuluka thukuta

pamene kunja kwatentha chifukwa cha mphepo yakummwera,

18kodi mungathe kuthandizana naye kutambasula thambo

limene ndi lolimba ngati chitsulo?

19“Tiwuzeni ife zoti tikanene kwa Iye;

sitingathe kufotokoza mlandu wathu chifukwa cha mdima umene uli mwa ife.

20Kodi nʼkofunika kumudziwitsa Mulungu kuti ndili naye mawu?

Kodi kutero sikuchita ngati kupempha kuti ndiwonongeke?

21Tsopano munthu sangathe kuyangʼana dzuwa,

ndi kunyezimira mlengalenga,

kuwomba kwa mphepo kutachotsa mitambo yonse.

22Kuwala kwake kumaonekera cha kumpoto;

Mulungu amabwera ndi ulemerero woopsa.

23Wamphamvuzonse sitingathe kumufikira pafupi ndi wa mphamvu zoposa;

pa chiweruzo chake cholungama ndi mʼchilungamo chake chachikulu Iye sapondereza anthu ozunzika.

24Nʼchifukwa chake anthu amamuopa kwambiri,

kodi saganizira za onse amene amaganiza kuti ndi anzeru?”

New International Reader’s Version

Job 37:1-24

1“When I hear the thunder, my heart pounds.

It beats faster inside me.

2Listen! Listen to the roar of his voice!

Listen to the thunder that comes from him!

3He sends his lightning across the sky.

It reaches from one end of the earth to the other.

4Next comes the sound of his roaring thunder.

He thunders with his majestic voice.

When his voice fills the air,

he doesn’t hold anything back.

5God’s voice thunders in wonderful ways.

We’ll never understand the great things he does.

6He says to the snow, ‘Fall on the earth.’

He tells the rain, ‘Pour down your mighty waters.’

7He stops everyone from working.

He wants them to see his work.

8The animals go inside.

They remain in their dens.

9The storm comes out of its storeroom in the heavens.

The cold comes from the driving winds.

10The breath of God produces ice.

The shallow water freezes over.

11He loads the clouds with moisture.

He scatters his lightning through them.

12He directs the clouds to circle

above the surface of the whole earth.

They do everything he commands them to do.

13He tells the clouds to punish people.

Or he brings them to water his earth and show his love.

14“Job, listen to me.

Stop and think about the wonderful things God does.

15Do you know how he controls the clouds?

Do you understand how he makes his lightning flash?

16Do you know how the clouds stay up in the sky?

Do you understand the wonders of the God who has perfect knowledge?

17Even your clothes are too hot for you

when the land lies quiet under the south wind.

18Can you help God spread out the skies?

They are as hard as a mirror

that’s made out of bronze.

19“Job, tell us what we should say to God.

We can’t prepare our case

because our minds are dark.

20Should he be told that I want to speak?

Would anyone ask to be destroyed by him?

21No one can look at the sun.

It’s too bright after the wind has swept the skies clean.

22Out of the north, God comes in his shining glory.

He comes in all his wonderful majesty.

23We can’t reach up to the Mighty One.

He is lifted high because of his power.

Everything he does is fair and right.

So he doesn’t crush people.

24That’s why they have respect for him.

He cares about all those who are wise.”