Yobu 37 – CCL & CCBT

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Yobu 37:1-24

1“Mtima wanga ukulumphalumpha pa chimenechinso

ndipo ukuchoka mʼmalo mwake.

2Tamverani! Tamverani kubangula kwa liwu lake,

kugunda kumene kukuchokera mʼkamwa mwake.

3Iye amaponya chingʼaningʼani chake pansi pa thambo lonse

ndipo amachitumiza ku dziko lapansi.

4Pambuyo pake kubangula kwake kumamveka.

Iye amabangula ndi liwu lake laulemerero.

Pamene wabangula,

palibe chimene amalephera kuchita.

5Liwu la Mulungu limabangula mʼnjira zambiri zodabwitsa

Iye amachita zinthu zazikulu zimene sitingathe kuzimvetsa.

6Amalamula chisanu chowundana kuti, ‘Igwa pa dziko lapansi,’

ndipo amalamulanso mvula yamawawa kuti, ‘Khala mvula yamphamvu.’

7Kuti anthu onse amene anawalenga athe kuzindikira ntchito yake.

Iye amalepheretsa anthu kugwira ntchito zawo.

8Zirombo zimakabisala

ndipo zimakhala mʼmaenje mwawo.

9Mphepo yamkuntho imatuluka ku malo ake,

kuzizira kumatuluka mʼmphepo yamkunthoyo.

10Mpweya wa Mulungu umawunditsa madzi

ndipo madzi a mʼnyanja amawuma kuti gwaa.

11Iye amadzaza mitambo ndi madzi a mvula,

amabalalitsa zingʼaningʼani zake kuchokera mʼmitambomo.

12Mulungu amayendetsa mitamboyo

mozungulirazungulira dziko lonse lapansi

kuti ichite zonse zimene Iye akufuna pa dziko lapansi.

13Iye amagwetsa mvula kuti alange anthu,

kapena kubweretsa chinyontho pa dziko lapansi kuti aonetse chikondi chake.

14“Abambo Yobu, tamvani izi;

imani ndipo muganizire ntchito zodabwitsa za Mulungu.

15Kodi mukudziwa momwe Mulungu amayendetsera mitambo

ndi kuchititsa kuti kukhale zingʼaningʼani?

16Kodi mukudziwa momwe Mulungu amayalira mitambo,

ntchito zodabwitsa za Iye amene ndi wanzeru zangwiro?

17Inu amene mʼzovala zanu mumatuluka thukuta

pamene kunja kwatentha chifukwa cha mphepo yakummwera,

18kodi mungathe kuthandizana naye kutambasula thambo

limene ndi lolimba ngati chitsulo?

19“Tiwuzeni ife zoti tikanene kwa Iye;

sitingathe kufotokoza mlandu wathu chifukwa cha mdima umene uli mwa ife.

20Kodi nʼkofunika kumudziwitsa Mulungu kuti ndili naye mawu?

Kodi kutero sikuchita ngati kupempha kuti ndiwonongeke?

21Tsopano munthu sangathe kuyangʼana dzuwa,

ndi kunyezimira mlengalenga,

kuwomba kwa mphepo kutachotsa mitambo yonse.

22Kuwala kwake kumaonekera cha kumpoto;

Mulungu amabwera ndi ulemerero woopsa.

23Wamphamvuzonse sitingathe kumufikira pafupi ndi wa mphamvu zoposa;

pa chiweruzo chake cholungama ndi mʼchilungamo chake chachikulu Iye sapondereza anthu ozunzika.

24Nʼchifukwa chake anthu amamuopa kwambiri,

kodi saganizira za onse amene amaganiza kuti ndi anzeru?”

Chinese Contemporary Bible (Traditional)

約伯記 37:1-24

1「因此我心戰慄,

在胸膛跳動。

2請仔細聽祂發出的雷聲,

聽祂口中發出的轟鳴。

3祂使閃電劃過整個天空,

亮光直照到地極。

4隨後雷聲隆隆,

祂發出威嚴之聲。

祂一發聲,雷電交加。

5上帝發出奇妙的雷聲,

我們無法測度祂偉大的作為。

6祂命雪降在大地,

令雨傾盆倒下,

7使人們停下工作,

以便世人都知道祂的作為。

8野獸躲進窩裡,

留在洞中。

9暴風從南天而來,

寒流由北方而至。

10上帝噓氣成冰,

使寬闊的水面凝結。

11祂使密雲佈滿水氣,

從雲端發出閃電。

12雲隨祂的指令旋轉,

在地面之上完成祂的吩咐,

13或為懲罰大地,

或為彰顯慈愛。

14約伯啊,請留心聽,

要駐足沉思上帝的奇妙作為。

15你知道上帝如何發出命令,

使雲中電光閃爍嗎?

16你知道全知者的奇妙作為——

祂如何使雲彩飄浮嗎?

17南風吹來,大地沉寂時,

你就汗濕衣襟,你知道為何嗎?

18你能像祂那樣鋪展堅如銅鏡的穹蒼嗎?

19我們因愚昧而無法陳訴,

請指教我們如何與祂對話。

20我怎敢與祂對話?

豈有人自取滅亡?

21風吹散天空的雲後,

無人能仰視太陽的強光。

22北方出現金色的光芒,

上帝充滿可怕的威嚴。

23我們無法測度全能者,

祂充滿能力,無比正直公義,

不恃強凌弱。

24所以,人們都敬畏祂,

祂不看顧自以為有智慧的人。」