Yesaya 40 – CCL & OL

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Yesaya 40:1-31

Mawu a Chitonthozo kwa Anthu a Mulungu

1Atonthozeni, atonthozeni anthu anga,

akutero Mulungu wanu.

2Ayankhuleni moleza mtima anthu a ku Yerusalemu

ndipo muwawuzitse

kuti nthawi ya ukapolo wawo yatha,

tchimo lawo lakhululukidwa.

Ndawalanga mokwanira

chifukwa cha machimo awo onse.

3Mawu a wofuwula mʼchipululu akuti,

“Konzani njira ya Yehova

mʼchipululu;

wongolani njira zake;

msewu owongoka wa Mulungu wathu mʼdziko lopanda kanthu.

4Chigwa chilichonse achidzaze.

Phiri lililonse ndi chitunda chilichonse azitsitse;

Dziko lokumbikakumbika alisalaze,

malo azitundazitunda awasandutse zidikha.

5Ndipo ulemerero wa Yehova udzaonekera,

ndipo mitundu yonse ya anthu idzawuona,

pakuti wanena zimenezi ndi Yehova.”

6Wina ananena kuti, “Lengeza.”

Ndipo ine ndinati, “Kodi ndifuwule chiyani?

“Pakuti anthu onse ali ngati udzu

ndipo kukongola kwawo kuli ngati maluwa akuthengo.

7Udzu umanyala ndipo maluwa amafota

chifukwa cha kuwomba kwa mpweya wa Yehova.”

Mawu aja anatinso, “Ndithudi anthu sasiyana ndi udzu.

8Udzu umanyala ndipo maluwa amafota,

koma mawu a Mulungu wathu adzakhalapo mpaka muyaya.”

9Iwe amene ukulengeza nkhani yabwino ku Ziyoni,

kwera pa phiri lalitali.

Iwe amene ukulengeza nkhani yabwino ku Yerusalemu,

fuwula kwambiri,

kweza mawu, usachite mantha;

uza mizinda ya ku Yuda kuti,

“Mulungu wanu akubwera!”

10Taonani, Ambuye Yehova akubwera mwamphamvu,

ndipo dzanja lake likulamulira,

taonani akubwera ndi mphotho yake

watsogoza zofunkha zako za ku nkhondo.

11Iye adzasamalira nkhosa zake ngati mʼbusa:

Iye adzasonkhanitsa ana ankhosa aakazi mʼmanja mwake

ndipo Iye akuwanyamula pachifuwa chake

ndi kutsogolera bwinobwino nkhosa zoyamwitsa.

12Kodi ndani akhoza kuyeza kuchuluka kwa madzi a mʼnyanja ndi chikhatho chake,

kapena kuyeza kutalika kwa mlengalenga ndi dzanja lake?

Ndani akhoza kuyeza dothi lonse la dziko lapansi mʼdengu,

kapena kuyeza kulemera kwa

mapiri ndi zitunda ndi pasikelo?

13Ndani anapereka malangizo kwa Mzimu wa Yehova

kapena kumuphunzitsa Iye monga phungu wake?

14Kodi Yehova anapemphapo nzeru kwa yani kuti akhale wopenya,

kapena kuti aphunzire njira yoyenera ndi nzeru?

Iye anapempha nzeru kwa yani

ndi njira ya kumvetsa zinthu?

15Ndithudi mitundu ya anthu ili ngati dontho la madzi ochoka mu mtsuko.

Iwo akungoyesedwa ngati fumbi chabe pa sikelo;

mʼmanja mwa Yehova zilumba nʼzopepuka ngati fumbi.

16Nkhalango ya ku Lebanoni singakwanire nkhuni zosonkhera moto pa guwa lansembe,

ngakhale nyama zake sizingakwanire kupereka nsembe zopsereza.

17Pamaso pa Yehova mitundu yonse ya anthu ili ngati chinthu chopandapake;

Iye amayiwerengera ngati chinthu chopanda phindu

ndi cha chabechabe.

18Kodi tsono Mulungu mungamuyerekeze ndi yani?

Kodi mungamufanizire ndi chiyani?

19Likakhala fano, mʼmisiri ndiye analipanga

ndipo mʼmisiri wa golide amalikuta ndi golide

naliveka mkanda wasiliva.

20Mʼmphawi amene sangathe kupeza ngakhale chopereka nsembe chotere

amasankha mtengo umene sudzawola,

nafunafuna mʼmisiri waluso woti

amupangire fano limene silingasunthike.

21Kodi simukudziwa?

Kodi simunamve?

Kodi sanakuwuzeni kuyambira pachiyambi pomwe?

Kodi simunamvetsetse chiyambire cha dziko lapansi?

22Yehova amene amakhala pa mpando wake waufumu kumwamba ndiye analenga dziko lapansi,

Iye amaona anthu a dziko lapansi ngati ziwala.

Ndipo anafunyulula mlengalenga ngati nsalu yotchinga,

nayikunga ngati tenti yokhalamo.

23Amatsitsa pansi mafumu amphamvu

nasandutsa olamula a dziko kukhala achabechabe.

24Inde, iwo ali ngati mbewu zimene zangodzalidwa kumene

kapena kufesedwa chapompano,

ndi kungoyamba kuzika mizu kumene

ndi pamene mphepo imawombapo nʼkuziwumitsa

ndipo kamvuluvulu amaziwulutsa ngati mankhusu.

25Woyera uja akuti, “Kodi mudzandiyerekeza Ine ndi yani?

Kapena kodi alipo wofanana nane?”

26Tayangʼanani mlengalenga ndipo onani.

Kodi ndani analenga zonsezi mukuzionazi?

Yehova ndiye amene amazitsogolera ngati gulu la ankhondo,

nayitana iliyonse ndi dzina lake.

Ndipo popeza Iye ali ndi nyonga zambiri,

palibe ndi imodzi yomwe imene inasowapo.

27Iwe Yakobo, chifukwa chiyani umanena

ndi kumadandaula iwe Israeli, kuti,

“Yehova sakudziwa mavuto anga,

Mulungu wanga sakusamala zomwe zikundichitikira ine?”

28Kodi simukudziwa?

Kodi simunamve?

Yehova ndiye Mulungu wamuyaya,

ndiyenso Mlengi wa dziko lonse lapansi.

Iye sadzatopa kapena kufowoka

ndipo palibe amene angadziwe maganizo ake.

29Iye amalimbitsa ofowoka

ndipo otopa amawawonjezera mphamvu.

30Ngakhale achinyamata amalefuka ndi kufowoka,

ndipo achinyamata amapunthwa ndi kugwa;

31koma iwo amene amakhulupirira Yehova

adzalandira mphamvu zatsopano.

Adzawuluka ngati chiwombankhanga;

adzathamanga koma sadzalefuka,

adzayenda koma sadzatopa konse.

O Livro

Isaías 40:1-31

O consolo para o povo de Deus

1“Consolem o meu povo, diz o vosso Deus. 2Falem ternamente a Jerusalém e digam-lhe que os seus dias de tristeza já se foram. Os seus pecados são perdoados e já recebeu do Senhor o dobro do castigo pelos seus pecados.”

3Ouçam! Eu ouvi a voz de alguém gritando:

“Façam um caminho para o Senhor no deserto.

Façam um caminho direito para o nosso Deus.

4Sejam levantados os vales e nivelados todos os montes e colinas;

sejam aplanados os caminhos tortuosos da montanha,

limpas as veredas pedregosas e tapadas as suas covas.

5A glória do Senhor será vista

por toda a raça humana junta.”

Foi o Senhor quem falou; assim acontecerá.

6Disse a voz: “Clama bem alto!”

“O que é que eu hei de clamar?”, perguntei.

“Que o ser humano é como a erva e que toda a sua beleza murcha como as flores que morrem. 7A erva seca e as flores murcham sob o sopro do Senhor. E assim é com a frágil criatura humana. 8A erva seca e as flores murcham, contudo, a palavra do nosso Deus permanece para sempre.”

9Tu, ó Sião, anunciador de boas novas, sobe a um alto monte! Tu, anunciador de boas novas a Jerusalém, grita bem alto, não tenhas receio, e diz às cidades de Judá: “Eis aqui o vosso Deus!” 10Sim, o Senhor Deus vem aí com grande poder. Governará com domínio eficaz. Dará a cada um a justa recompensa. 11Alimentará o seu rebanho como um pastor; levará nos braços os cordeirinhos e guiará mansamente as ovelhas que amamentam.

12Quem mais tem poder para segurar nas suas mãos os oceanos e para conhecer os céus em todas as suas medidas? Quem mais conhece perfeitamente o peso de toda a Terra, das montanhas e das cordilheiras? 13Quem conheceu todo o pensamento do Senhor ou quem é seu conselheiro? 14Alguma vez terá precisado de ser instruído quanto ao que é reto, ao que é melhor? Quem é que lhe ensinou a ciência e lhe deu a conhecer a sabedoria?

15Porque os povos do mundo nada são em relação a ele; são como uma gota de água que cai num balde ou como um grão de pó no prato duma balança. Pega nas ilhas como se fossem coisa sem peso. 16As florestas do Líbano juntas não formariam combustível suficiente para consumir um holocausto no seu altar; nem tão-pouco todos os seus animais seriam suficientes para o holocausto. 17Todas as nações são como nada para ele; aos seus olhos, são até menos que nada; são vazio e nulidade.

18Como se poderá então descrever Deus? Com que é que poderá ser comparado? 19Com algum ídolo? Com um ídolo qualquer, feito segundo um molde, pintado de tinta dourada, com cadeias prateadas em volta do pescoço? 20Qualquer pessoa, se não tiver dinheiro bastante para comprar um ídolo desses, pode pegar num pedaço de madeira e procurar um artífice para lhe fazer um ídolo que possa durar!

21Serão vocês assim tão ignorantes? Serão assim tão surdos às palavras de Deus, palavras essas que já foram dadas desde a fundação do mundo? Nunca ouviram nem compreenderam isso? 22É Deus quem se senta acima do globo da Terra, cujos habitantes são para ele como minúsculos gafanhotos. É ele quem estende os céus como uma cortina, como se fizesse com ela a sua tenda. 23Reduz a nada os grandes senhores desta Terra e torna inúteis os seus governantes. 24Dificilmente estabilizam e criam raízes, se Deus soprar sobre eles; as suas obras perdem todo o seu valor, levando-as o vento como à palha.

25“Com quem me hão de comparar então? Quem será semelhante a mim?”, pergunta aquele que é Santo.

26Vejam os céus! Quem foi que criou todas essas estrelas? Tal como um pastor conduz as suas ovelhas, chamando cada uma pelo seu nome, e as conta para ver se alguma se terá perdido ou desviado, assim Deus faz com os astros!

27Ó Jacob, ó Israel, como podes tu dizer que o Senhor não vê as tuas aflições, que não se interessa em fazer-te justiça? 28Não compreendes? Não sabes tu já que o eterno Deus, o Criador das mais distantes partes da Terra, nunca fica cansado nem desfalecido? Ninguém jamais conseguirá descobrir a profundidade do seu pensamento. 29Dá novas forças ao que está cansado e multiplica as energias daquele que está fraco. 30Até mesmo a juventude se cansará; há jovens que acabarão por desistir. 31Mas os que confiam no Senhor renovarão as suas forças. Subirão com asas como águias; correrão e não se cansarão; andarão sem desfalecerem.