Yesaya 41 – CCL & OL

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Yesaya 41:1-29

Mulungu Thandizo la Israeli

1“Khalani chete pamaso panga, inu mayiko a mʼmbali mwa nyanja!

Alekeni ayandikire ndi kuyankhula;

tiyeni tikhale pamodzi

kuti atiweruze.

2“Ndani anadzutsa wochokera kummawa

uja amene ananka napambana kulikonse kumene ankapita?

Iye amapereka anthu a mitundu ina mʼmanja mwake

ndipo ndi lupanga lake anagonjetsa

ndi kusandutsa mafumu kukhala ngati fumbi

nawamwaza ngati mankhusu ndi uta wake.

3Amawalondola namayenda mosavutika,

mʼnjira imene mapazi ake sanayendemo kale.

4Ndani anachita zimenezi ndi kuzitsiriza,

si uja amene anayambitsa mitundu ya anthu?

Ine Yehova, ndine chiyambi

ndipo potsiriza pake ndidzakhalapo.”

5Mayiko amʼmbali mwa nyanja aona zimenezi ndipo akuopa;

anthu a ku mathero a dziko lapansi akunjenjemera.

Akuyandikira pafupi, akubwera;

6aliyense akuthandiza mnzake

ndipo akuwuza mʼbale wake kuti, “Limba mtima!”

7Mʼmisiri wa matabwa amalimbikitsa mʼmisiri wa golide,

ndipo iye amene amasalaza fano ndi nyundo

amalimbikitsa amene amalisanja pa chipala.

Ponena za kuwotcherera iye amati, “Zili bwino.”

Iye amalikhomerera fanolo ndi misomali kuti lisagwe.

8“Koma Iwe Israeli mtumiki wanga,

Yakobo amene ndakusankha,

Ndiwe chidzukulu cha Abrahamu bwenzi langa.

9Ndinakutengani kuchokera ku mapeto a dziko lapansi,

ndinakuyitanani kuchokera ku mbali za kutali za dziko lapansi.

Ine ndinati, ‘Iwe ndiwe mtumiki wanga;’

Ndinakusankha ndipo sindinakutaye.

10Tsono usaope, pakuti Ine ndili nawe;

usataye mtima chifukwa Ine ndine Mulungu wako.

Ndidzakupatsa mphamvu ndipo ndidzakuthandiza,

ndidzakutchinjiriza ndi dzanja langa lamanja logonjetsa.

11“Onse amene akupsera mtima

adzachita manyazi ndithu ndi kunyazitsidwa;

onse amene akukangana nawe

sadzakhalanso kanthu, adzawonongeka.

12Udzafunafuna adani ako,

koma sadzapezeka.

Iwo amene akuchita nawe nkhondo

sadzakhalanso kanthu.

13Pakuti Ine Yehova, ndine Mulungu wako,

amene ndikukugwira dzanja lako lamanja

ndipo ndikuti, usaope;

ndidzakuthandiza.

14Usachite mantha, iwe Yakobo wofowoka ngati nyongolotsi,

iwe wochepa mphamvu Israeli,

chifukwa Ine ndidzakuthandiza,”

akutero Yehova Mpulumutsi wako, Woyerayo wa Israeli.

15“Taona, ndidzakusandutsa ngati chipangizo chopunthira tirigu

chatsopano, chakunthwa ndi cha mano ambiri.

Udzanyenya mapiri ndi kuwaphwanyaphwanya,

ndipo zitunda adzazisandutsa ngati mankhusu.

16Udzawapeta ndipo adzawuluka ndi mphepo komanso

adzamwazika ndi kamvuluvulu.

Koma iwe udzakondwera chifukwa Ine ndine Mulungu wako,

ndipo udzanyadira chifukwa cha Ine Woyerayo wa Israeli:

17“Pamene amphawi ndi osauka akufunafuna madzi,

koma sakuwapeza;

ndipo kummero kwawo kwawuma ndi ludzu.

Ine Yehova ndidzayankha pemphero lawo;

Ine, Mulungu wa Israeli, sindidzawasiya.

18Ndidzayendetsa mitsinje mʼmalo owuma,

ndi akasupe adzatumphuka mu zigwa.

Ndidzasandutsa chipululu kukhala dziwe la madzi

ndipo dziko lowuma kukhala akasupe a madzi.

19Mʼchipululu ndidzameretsa

mkungudza, kasiya mchisu ndi mtengo wa Olivi.

Mʼdziko lowuma ndidzaza mitengo

ya payini, ya mkuyu ndi ya mlombwa,

20kuti anthu aone ndi kudziwa;

inde, alingalire ndi kumvetsa,

kuti Yehova ndiye wachita zimenezi;

kuti Woyera wa Israeli ndiye anakonza zimenezi.

21“Yehova akuwuza milungu ina kuti, ‘Fotokozani mlandu wanu.’

Mfumu ya Yakobo ikuti, ‘Perekani umboni wanu.’

22Bwerani ndi milungu yanu kuti idzatiwuze

zomwe zidzachitike mʼtsogolo.

Tifotokozereni zinthu zamakedzana

tiziganizire

ndi kudziwa zotsatira zake.

Kapena tiwuzeni zimene zidzachitike mʼtsogolo,

23tiwuzeni kuti kutsogolo kuli zotani,

ndipo ife tidziwa kuti ndinu milungu.

Chitani chinthu chabwino kapena choyipa,

ndipo mutidabwitsa ndi kutichititsa mantha.

24Koma inu sindinu kanthu

ndipo zochita zanu nʼzopandapake;

amene amapembedza inu ali ngati chinthu chokanidwa chifukwa ndi choyipa.

25“Ndinawutsa munthu wina kumpoto ndipo anabwera,

munthu wochokera kummawa amene ndinamuyitana.

Amapondaponda olamulira ngati matope,

ngati ndi wowumba mbiya amene akuponda dongo.

26Ndani anawululiratu zimenezi poyamba pomwe, kuti ife tidziwe,

kapena kutiwuziratu zisanachitike kuti ife tinene kuti, ‘Analondola?’

Palibe amene ananena,

palibe analengeza zimenezi,

palibe anamva mawu anu.

27Ine ndinali woyamba kumuwuza Ziyoni kuti, ‘Taona, si awa akubwera apawa!’

Ndinatumiza mthenga wa nkhani yabwino ku Yerusalemu.

28Koma ndikayangʼana palibe ndi mmodzi yemwe,

palibe ndi mmodzi yemwe pakati pawo wotha kupereka uphungu,

palibe woti ayankhe pamene ine ndawafunsa.

29Taonani, milungu yonseyi ndi yachinyengo!

Zochita zawo si kanthu konse;

mafano awo ali ngati mphepo yachabechabe.

O Livro

Isaías 41:1-29

O ajudador de Israel

1“Escutem em silêncio, na minha presença, ó terras para além do mar! Depois venham e falem, apresentem os vossos mais fortes argumentos. O tribunal está pronto a julgar o vosso caso.

2Quem foi que suscitou, para vir lá do oriente, este que alcança vitórias a cada passo? Quem, na verdade, senão Deus? Quem faz com que as nações se lhe submetam e os reis lhe sejam entregues, e com a sua espada os transforme em pó e com o seu arco em palha que o vento arrebata? 3Persegue-os, afasta-os e continua seguro, por um caminho por onde nunca tinha andado. 4Quem é o responsável por tão célebres façanhas? É aquele que anuncia o futuro de antemão. Sou eu, o Senhor, o primeiro e o último! Eu mesmo!”

5As terras para além do mar tremem de medo, esperando notícias sobre as novas campanhas de Ciro. Terras distantes estremecem e mobilizam-se para a guerra. 6Cada pessoa encoraja o seu vizinho e diz: “Não te preocupes! Havemos de ganhar!” 7O certo é que correm a fazer um novo ídolo; o artífice de ouro encoraja o entalhador e o escultor ajuda o fundidor. “Está bem!”, dizem eles. “Ficou mesmo bem! Agora vamos fixar-lhe os membros!” Juntam-lhe as diferentes peças e fixam a imagem cuidadosamente ao chão, não vá ela cair!

8“Ouve, Israel, meu servo, povo de Jacob, meu escolhido, descendência de Abraão, o meu amigo! 9Chamei-vos das extremidades da Terra e disse-vos que a ninguém mais deviam servir senão a mim! Fui eu quem vos escolheu, por isso, nunca vos lançarei fora! 10Não temam porque eu estou convosco! Não se espantem, porque eu sou o vosso Deus! Dar-vos-ei força e ajudar-vos-ei; hei de sustentar-vos com a força e a justiça da minha mão vitoriosa.

11Reparem como todos os vossos irritados inimigos ficarão confundidos e frustrados! Todos quantos se vos opõem morrerão! 12Em vão procurarão saber deles, pois todos terão desaparecido. 13Eu, o Senhor, vosso Deus, seguro-vos pela vossa mão direita e digo-vos: Nada receiem! Estou aqui para vos ajudar! 14Ainda que sejam desprezados como vermes, não tenham medo, ó descendência de Jacob, ó Israel, porque eu vos socorrerei! Eu sou o Senhor, o vosso Redentor! Eu sou o Santo de Israel! 15Vou fazer de ti uma debulhadora de dentes agudos, que há de moer todos os vossos inimigos, despedaçando-os, transformando as montanhas em palha. 16Vocês os sacudirão no ar e o vento se encarregará de os levar para longe; remoinhos de ventos tempestuosos os dispersarão. A alegria do Senhor vos encherá e exultarão no Senhor, o Santo de Israel, o qual será a vossa glória.

17Quando os pobres e os necessitados procurarem água, sem a encontrar, e as suas línguas se secarem pela sede, então responderei, quando a mim clamarem. Eu, o Senhor, o Deus de Israel, nunca me esquecerei deles! 18Abrirei rios nos planaltos e dar-lhes-ei fontes de água nos vales. Haverá poços nos desertos e ribeiros alimentados por fontes correrão no meio de terras secas e ressequidas. 19Plantarei cedros, acácias, murtas, oliveiras, ciprestes e pinheiros em terras desertas. 20Toda a gente verá este milagre e compreenderá que foi o Senhor, o Santo de Israel, quem o fez.

21Podem os vossos ídolos fazer coisas semelhantes a estas? Então que venham e mostrem o que podem fazer, diz o Senhor, o Rei de Jacob. 22Que tentem dizer-nos e dar a entender o que ocorreu em anos passados ou o que nos aguarda no futuro. 23Sim, é isso! Se são deuses, então que digam o que irá acontecer nos tempos vindouros ou façam algum milagre poderoso que nos deixe estarrecidos, abismados. 24Mas não! Eles são menos que nada! Não podem fazer coisíssima nenhuma! Se alguém confia neles faz uma coisa abominável!

25Mas eu fiz com que viesse um do noroeste; um que virá contra as nações e que invocará o meu nome; dar-lhe-ei a vitória sobre reis e príncipes; há de esmagá-los como o oleiro pisa e amassa o barro.

26Quem mais vos anunciou que isto iria acontecer, senão eu? Quem mais predisse estas coisas antes de acontecerem, para que verifiquem depois como era verdade? Ninguém mais! Não houve ninguém que tivesse dito uma só palavra! 27Eu fui o primeiro a dizer a Sião: ‘Olhem! Olhem! Já vem a caminho a ajuda!’ A Jerusalém darei um anunciador de boas novas 28Nenhum dos vossos ídolos vos disse tal coisa. Ninguém respondeu quando vos interpelei. 29Vocês bem veem que esses ídolos não passam de coisas ocas, sem valor algum; são tão vazios como o vento.